< Numeri 20 >

1 Pa mwezi woyamba gulu lonse la Aisraeli linafika ku chipululu cha Zini, ndipo anakhala ku Kadesi. Miriamu anafera kumeneko ndipo anayikidwa mʼmanda.
And they came [the] people of Israel all the congregation [the] wilderness of Zin in the month first and it remained the people in Kadesh and she died there Miriam and she was buried there.
2 Kunalibe madzi woti anthu onse ndi kumwa, choncho anthuwo anasonkhana motsutsana ndi Mose ndi Aaroni.
And not it belonged water to the congregation and they assembled on Moses and on Aaron.
3 Anakangana ndi Mose kuti, “Kunali bwino ifenso tikanangofa pamene abale athu anafa pamaso pa Yehova!
And it quarreled the people with Moses and they said saying and if we had died when died brothers our before Yahweh.
4 Chifukwa chiyani unabweretsa gulu la Yehova mʼchipululu muno, kuti ife ndi ziweto zathu tife kuno?
And why? have you brought [the] assembly of Yahweh into the wilderness this to die there we and livestock our.
5 Nʼchifukwa chiyani unatitulutsa mʼdziko la Igupto ndi kutibweretsa kumalo woyipa ano? Kuno kulibe tirigu kapena nkhuyu, mphesa kapena makangadza. Ndipo kuno kulibenso madzi akumwa!”
And why? have you brought up us from Egypt to bring us to the place the evil this not - a place of seed and fig tree and vine and pomegranate and [is] water there not to drink.
6 Mose ndi Aaroni anachoka mu msonkhano ndi kupita pa khomo la tenti ya msonkhano, nagwa pansi chafufumimba ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera.
And he went Moses and Aaron from before the assembly to [the] entrance of [the] tent of meeting and they fell on faces their and it appeared [the] glory of Yahweh to them.
7 Yehova anati kwa Mose,
And he spoke Yahweh to Moses saying.
8 “Tenga ndodo, ndipo iwe ndi mʼbale wako Aaroni musonkhanitse anthu onse pamodzi. Uyankhule ndi thanthwe ilo iwo akuona ndipo lidzatulutsa madzi ake. Udzatulutsa madzi mʼthanthwe limeneli kuti anthu onse ndi ziweto zawo amwe.”
Take the rod and assemble the congregation you and Aaron brother your and you will speak to the rock to eyes their and it will give water its and you will bring out for them water from the rock and you will give drink to the congregation and livestock their.
9 Choncho Mose anatenga ndodo pamaso pa Yehova monga momwe anamulamulira.
And he took Moses the rod from to before Yahweh just as he had commanded him.
10 Mose ndi Aaroni anasonkhanitsa anthuwo pamodzi ku thanthwelo ndipo Mose anawawuza kuti, “Tamverani osamvera inu, kodi tikupatseni madzi kuchokera ku thanthwe ili?”
And they made assemble Moses and Aaron the assembly to [the] face of the rock and he said to them listen please O rebels ¿ from the rock this will we bring out for you water.
11 Choncho Mose anatukula dzanja lake ndi kumenya thanthwelo kawiri ndi ndodo yake ndipo madzi ambiri anatuluka mwamphamvu, ndipo anthu ndi ziweto zawo anamwa.
And he raised Moses hand his and he struck the rock with rod his two times and they came out waters many and it drank the congregation and livestock their.
12 Koma Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Chifukwa chakuti simunandikhulupirire ndiponso simunandilemekeze monga Woyera pamaso pa Aisraeli, simudzalowetsa anthuwa mʼdziko limene ndikupereka kwa iwo.”
And he said Yahweh to Moses and to Aaron because not you believed me to treat as holy me to [the] eyes of [the] people of Israel therefore not you will bring the assembly this into the land which I have given to them.
13 Awa anali madzi a ku Meriba, kumene Aisraeli anakangana ndi Yehova ndiponso kumene Yehovayo anadzionetsa yekha kuti ndi Woyera pakati pawo.
They [were] [the] waters of Meribah where they quarreled [the] people of Israel with Yahweh and he showed himself holy among them.
14 Mose anatumiza amithenga kuchokera ku Kadesi kupita kwa mfumu ya ku Edomu, kukanena kuti, “Mʼbale wako Israeli akunena izi: Inuyo mukudziwa za mavuto onse amene anatigwera.
And he sent Moses messengers from Kadesh to [the] king of Edom thus he says brother your Israel you you know all the hardship which it has come upon us.
15 Makolo athu anapita ku Igupto ndipo tinakhala kumeneko zaka zambiri. Aigupto anatizunza pamodzi ndi makolo athuwo,
And they went down ancestors our Egypt towards and we dwelt in Egypt days many and they did harm to us Egypt and to ancestors our.
16 koma titalirira Yehova, Iyeyo anamva kulira kwathuko ndipo anatitumizira mngelo amene anatitulutsa ku Igupto.” “Taonani, tsopano tili pano pa Kadesi, mzinda wa mʼmalire a dziko lanu.
And we cried out to Yahweh and he heard voice our and he sent an angel and he brought out us from Egypt and here! we [are] in Kadesh city of [the] outskirt[s] of territory your.
17 Chonde mutilole tidutse mʼdziko lanu. Sitidzera mʼminda yanu kapena mu mpesa wanu, kapenanso kumwa madzi mʼchitsime chilichonse. Tidzayenda kutsata msewu waukulu wa mfumu ndipo sitidzapatukira ku dzanja lamanja kapena lamanzere mpaka titadutsa malire a dziko lanu.”
Let us pass please in land your not we will pass in a field and in a vineyard and not we will drink water of a well [the] way of the king we will go not we will turn aside right and left until that we will pass through territory your.
18 Koma Edomu anayankha kuti, “Musadutse kuno: Mukangoyesera tidzabwera ndi kumenyana nanu ndi lupanga.”
And it said to him Edom not you will pass in me lest with the sword I should come out to meet you.
19 Aisraeli anayankha kuti, “Tidzayenda motsata msewu waukulu. Ndipo ngati ife kapena ziweto zathu tidzamwa madzi anu tidzalipira. Tikungofuna tidutse nawo, palibenso china.”
And they said to him [the] people of Israel on the highway we will go up and if waters your we will drink I and livestock my and I will give price their only there not [is] a thing on feet my let me pass through.
20 Koma Edomu anayankhanso kuti, “Musadutse.” Kenaka Edomu anatuluka ndi gulu lankhondo lalikulu komanso lamphamvu.
And it said not you will pass through and it came out Edom to meet him with a people massive and with a hand strong.
21 Edomu anakaniza Israeli kuti adutse mʼdziko lake, choncho Israeli anabwerera.
And it refused - Edom to permit Israel to pass in territory its and it turned aside Israel from on it.
22 Gulu lonse la Aisraeli linachoka ku Kadesi ndipo linafika ku phiri la Hori.
And they set out from Kadesh and they came [the] people of Israel all the congregation Hor the mountain.
23 Ali pa phiri la Hori, pafupi ndi malire a Edomu, Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni,
And he said Yahweh to Moses and to Aaron at Hor the mountain on [the] border of [the] land of Edom saying.
24 “Aaroni adzakakhala ndi anthu a mtundu wake, sadzalowa mʼdziko limene ndapereka kwa Aisraeli, chifukwa nonse munandiwukira motsutsana ndi malamulo anga ku madzi a ku Meriba.
He will be gathered Aaron to people his for not he will go into the land which I have given to [the] people of Israel on that you rebelled against mouth my to [the] waters of Meribah.
25 Tenga Aaroni ndi mwana wake wamwamuna Eliezara ndipo ukwere nawo ku phiri la Hori.
Take Aaron and Eleazar son his and bring up them Hor the mountain.
26 Uvule Aaroni zovala zake ndipo umuveke mwana wake Eliezara, pakuti Aaroni adzafera komweko, ndipo adzakakhala ndi anthu a mtundu wake.”
And strip off Aaron garments his and you will clothe with them Eleazar son his and Aaron he will be gathered and he will die there.
27 Mose anachita monga Yehova anamulamulira: Anapita ku phiri la Hori gulu lonse likuona.
And he did Moses just as he had commanded Yahweh and they went up to Hor the mountain to [the] eyes of all the congregation.
28 Pamenepo Mose anavula Aaroni zovala zake ndi kuveka mwana wake Eliezara. Aaroni anafa kumeneko pamwamba pa phirilo. Koma Mose ndi Eliezara anatsika ku phiriko,
And he stripped off Moses Aaron garments his and he clothed with them Eleazar son his and he died Aaron there at [the] top of the mountain and he went down Moses and Eleazar from the mountain.
29 ndipo pamene anthu onse anamva kuti Aaroni wafa, nyumba yonse ya Israeli inamulira Aaroniyo masiku makumi atatu.
And they saw all the congregation that he had died Aaron and they wept for Aaron thirty day[s] all [the] house of Israel.

< Numeri 20 >