< Numeri 20 >

1 Pa mwezi woyamba gulu lonse la Aisraeli linafika ku chipululu cha Zini, ndipo anakhala ku Kadesi. Miriamu anafera kumeneko ndipo anayikidwa mʼmanda.
And the sons of Israel, even the whole congregation, came into the wilderness of Zin in the first month, and the people abode in Kadesh. And Miriam died there, and was buried there.
2 Kunalibe madzi woti anthu onse ndi kumwa, choncho anthuwo anasonkhana motsutsana ndi Mose ndi Aaroni.
And there was no water for the congregation, and they assembled themselves together against Moses and against Aaron.
3 Anakangana ndi Mose kuti, “Kunali bwino ifenso tikanangofa pamene abale athu anafa pamaso pa Yehova!
And the people strove with Moses, and spoke, saying, Would that we had died when our brothers died before Jehovah!
4 Chifukwa chiyani unabweretsa gulu la Yehova mʼchipululu muno, kuti ife ndi ziweto zathu tife kuno?
And why have ye brought the assembly of Jehovah into this wilderness, that we should die there, we and our beasts?
5 Nʼchifukwa chiyani unatitulutsa mʼdziko la Igupto ndi kutibweretsa kumalo woyipa ano? Kuno kulibe tirigu kapena nkhuyu, mphesa kapena makangadza. Ndipo kuno kulibenso madzi akumwa!”
And why have ye made us to come up out of Egypt, to bring us in to this evil place? It is no place of seed, or of figs, or of vines, or of pomegranates, neither is there any water to drink.
6 Mose ndi Aaroni anachoka mu msonkhano ndi kupita pa khomo la tenti ya msonkhano, nagwa pansi chafufumimba ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera.
And Moses and Aaron went from the presence of the assembly to the door of the tent of meeting, and fell upon their faces. And the glory of Jehovah appeared to them.
7 Yehova anati kwa Mose,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
8 “Tenga ndodo, ndipo iwe ndi mʼbale wako Aaroni musonkhanitse anthu onse pamodzi. Uyankhule ndi thanthwe ilo iwo akuona ndipo lidzatulutsa madzi ake. Udzatulutsa madzi mʼthanthwe limeneli kuti anthu onse ndi ziweto zawo amwe.”
Take the rod, and assemble the congregation, thou, and Aaron thy brother, and speak ye to the rock before their eyes, that it give forth its water, and thou shall bring forth water to them out of the rock. So thou shall give the congregation and their cattle drink.
9 Choncho Mose anatenga ndodo pamaso pa Yehova monga momwe anamulamulira.
And Moses took the rod from before Jehovah, as he commanded him.
10 Mose ndi Aaroni anasonkhanitsa anthuwo pamodzi ku thanthwelo ndipo Mose anawawuza kuti, “Tamverani osamvera inu, kodi tikupatseni madzi kuchokera ku thanthwe ili?”
And Moses and Aaron gathered the assembly together before the rock, and he said to them, Hear now, ye rebels. Shall we bring forth water to you out of this rock?
11 Choncho Mose anatukula dzanja lake ndi kumenya thanthwelo kawiri ndi ndodo yake ndipo madzi ambiri anatuluka mwamphamvu, ndipo anthu ndi ziweto zawo anamwa.
And Moses lifted up his hand, and smote the rock with his rod twice, and water came forth abundantly. And the congregation drank, and their cattle.
12 Koma Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Chifukwa chakuti simunandikhulupirire ndiponso simunandilemekeze monga Woyera pamaso pa Aisraeli, simudzalowetsa anthuwa mʼdziko limene ndikupereka kwa iwo.”
And Jehovah said to Moses and Aaron, Because ye did not believe in me, to sanctify me in the eyes of the sons of Israel, therefore ye shall not bring this assembly into the land which I have given them.
13 Awa anali madzi a ku Meriba, kumene Aisraeli anakangana ndi Yehova ndiponso kumene Yehovayo anadzionetsa yekha kuti ndi Woyera pakati pawo.
These are the waters of Meribah, because the sons of Israel strove with Jehovah, and he was sanctified in them.
14 Mose anatumiza amithenga kuchokera ku Kadesi kupita kwa mfumu ya ku Edomu, kukanena kuti, “Mʼbale wako Israeli akunena izi: Inuyo mukudziwa za mavuto onse amene anatigwera.
And Moses sent messengers from Kadesh to the king of Edom, Thus says thy brother Israel, Thou know all the travail that has befallen us,
15 Makolo athu anapita ku Igupto ndipo tinakhala kumeneko zaka zambiri. Aigupto anatizunza pamodzi ndi makolo athuwo,
how our fathers went down into Egypt, and we dwelt in Egypt a long time. And the Egyptians dealt ill with us and our fathers.
16 koma titalirira Yehova, Iyeyo anamva kulira kwathuko ndipo anatitumizira mngelo amene anatitulutsa ku Igupto.” “Taonani, tsopano tili pano pa Kadesi, mzinda wa mʼmalire a dziko lanu.
And when we cried to Jehovah, he heard our voice, and sent an agent, and brought us forth out of Egypt. And, behold, we are in Kadesh, a city in the outermost of thy border.
17 Chonde mutilole tidutse mʼdziko lanu. Sitidzera mʼminda yanu kapena mu mpesa wanu, kapenanso kumwa madzi mʼchitsime chilichonse. Tidzayenda kutsata msewu waukulu wa mfumu ndipo sitidzapatukira ku dzanja lamanja kapena lamanzere mpaka titadutsa malire a dziko lanu.”
Let us pass, I pray thee, through thy land. We will not pass through field or through vineyard, neither will we drink of the water of the wells. We will go along the king's highway. We will not turn aside to the right hand nor to the left, until we have passed thy border.
18 Koma Edomu anayankha kuti, “Musadutse kuno: Mukangoyesera tidzabwera ndi kumenyana nanu ndi lupanga.”
And Edom said to him, Thou shall not pass through me, lest I come out with the sword against thee.
19 Aisraeli anayankha kuti, “Tidzayenda motsata msewu waukulu. Ndipo ngati ife kapena ziweto zathu tidzamwa madzi anu tidzalipira. Tikungofuna tidutse nawo, palibenso china.”
And the sons of Israel said to him, We will go up by the highway. And if we drink of thy water, I and my cattle, then will I give the price of it. Only let me, without doing anything, pass through on my feet.
20 Koma Edomu anayankhanso kuti, “Musadutse.” Kenaka Edomu anatuluka ndi gulu lankhondo lalikulu komanso lamphamvu.
And he said, Thou shall not pass through. And Edom came out against him with many people, and with a strong hand.
21 Edomu anakaniza Israeli kuti adutse mʼdziko lake, choncho Israeli anabwerera.
Thus Edom refused to give Israel passage through his border. Therefore Israel turned away from him.
22 Gulu lonse la Aisraeli linachoka ku Kadesi ndipo linafika ku phiri la Hori.
And they journeyed from Kadesh, and the sons of Israel, even the whole congregation, came to mount Hor.
23 Ali pa phiri la Hori, pafupi ndi malire a Edomu, Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni,
And Jehovah spoke to Moses and Aaron in mount Hor, by the border of the land of Edom, saying,
24 “Aaroni adzakakhala ndi anthu a mtundu wake, sadzalowa mʼdziko limene ndapereka kwa Aisraeli, chifukwa nonse munandiwukira motsutsana ndi malamulo anga ku madzi a ku Meriba.
Aaron shall be gathered to his people, for he shall not enter into the land which I have given to the sons of Israel, because ye rebelled against my word at the waters of Meribah.
25 Tenga Aaroni ndi mwana wake wamwamuna Eliezara ndipo ukwere nawo ku phiri la Hori.
Take Aaron and Eleazar his son, and bring them up to mount Hor,
26 Uvule Aaroni zovala zake ndipo umuveke mwana wake Eliezara, pakuti Aaroni adzafera komweko, ndipo adzakakhala ndi anthu a mtundu wake.”
and strip Aaron of his garments, and put them upon Eleazar his son. And Aaron shall be gathered, and shall die there.
27 Mose anachita monga Yehova anamulamulira: Anapita ku phiri la Hori gulu lonse likuona.
And Moses did as Jehovah commanded. And they went up into mount Hor in the sight of all the congregation.
28 Pamenepo Mose anavula Aaroni zovala zake ndi kuveka mwana wake Eliezara. Aaroni anafa kumeneko pamwamba pa phirilo. Koma Mose ndi Eliezara anatsika ku phiriko,
And Moses stripped Aaron of his garments, and put them upon Eleazar his son. And Aaron died there on the top of the mount, and Moses and Eleazar came down from the mount.
29 ndipo pamene anthu onse anamva kuti Aaroni wafa, nyumba yonse ya Israeli inamulira Aaroniyo masiku makumi atatu.
And when all the congregation saw that Aaron was dead, they wept for Aaron thirty days, even all the house of Israel.

< Numeri 20 >