< Numeri 2 >
1 Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
RAB Musa'yla Harun'a, “İsrailliler sancaklarının altında, aile bayraklarıyla Buluşma Çadırı'ndan biraz ötede çepeçevre konaklasın” dedi.
2 “Aisraeli azimanga misasa yawo mozungulira tenti ya msonkhano motalikira pangʼono. Munthu aliyense amange pamene pali mbendera ya fuko lake.”
3 Kummawa, kotulukira dzuwa, magulu a msasa wa Yuda amange pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Ayudawo ndi Naasoni mwana wa Aminadabu.
Doğuda, gündoğusunda konaklayan bölükler Yahuda ordugahının sancağına bağlı olacak. Yahudaoğulları'nın önderi Amminadav oğlu Nahşon olacak.
4 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 74,600.
Bölüğünün sayısı 74 600 kişiydi.
5 Fuko la Isakara lidzamanga pafupi ndi Yuda. Mtsogoleri wa gulu la Isakara ndi Netanieli mwana wa Zuwara.
İssakar oymağı onların bitişiğinde konaklayacak. İssakaroğulları'nın önderi Suar oğlu Netanel olacak.
6 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 54,400.
Bölüğünün sayısı 54 400 kişiydi.
7 Lotsatira lidzakhala fuko la Zebuloni. Mtsogoleri wa gulu la Zebuloni ndi Eliabu mwana wa Heloni.
Sonra Zevulun oymağı konaklayacak. Zevulunoğulları'nın önderi Helon oğlu Eliav olacak.
8 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 57,400.
Bölüğünün sayısı 57 400 kişiydi.
9 Anthu onse aamuna mʼmisasa ya Yuda, chiwerengero chawo ndi 186,400 monga mwa magulu awo. Iwowo ndiwo aziyamba kusamuka.
Yahuda ordugahına ayrılan bölüklerdeki adam sayısı 186 400 kişiydi. Yola ilk çıkacak olanlar bunlardı.
10 Kummwera kudzakhala magulu a msasa wa Rubeni pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu la Rubeni ndi Elizuri mwana wa Sedeuri.
Güneyde Ruben ordugahının sancağı dikilecek, Ruben'e bağlı bölükler orada konaklayacak. Rubenoğulları'nın önderi Şedeur oğlu Elisur olacak.
11 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 46,500.
Bölüğünün sayısı 46 500 kişiydi.
12 Fuko la Simeoni lidzamanga pafupi ndi Rubeni. Mtsogoleri wa gulu la Simeoni ndi Selumieli mwana wa Zurisadai.
Şimon oymağı onların bitişiğinde konaklayacak. Şimonoğulları'nın önderi Surişadday oğlu Şelumiel olacak.
13 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 59,300.
Bölüğünün sayısı 59 300 kişiydi.
14 Lotsatira lidzakhala fuko la Gadi. Mtsogoleri wa gulu la Gadi ndi Eliyasafu mwana wa Deuweli.
Sonra Gad oymağı konaklayacak. Gadoğulları'nın önderi Deuel oğlu Elyasaf olacak.
15 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 45,650.
Bölüğünün sayısı 45 650 kişiydi.
16 Anthu onse aamuna mu msasa wa Rubeni, chiwerengero chawo monga mwa magulu awo, ndi 151,450. Iwowo azikhala achiwiri posamuka.
Ruben ordugahına ayrılan bölüklerdeki adam sayısı 151 450 kişiydi. İkinci sırada yola çıkacak olanlar bunlardı.
17 Tsono tenti ya msonkhano ndi msasa wa Alevi zidzakhala pakati pa misasayo. Iwo adzasamuka monga momwe anamangira misasa yawo, aliyense pa malo ake pamene pali mbendera yake.
Buluşma Çadırı ve Levililer'in ordugahı göç sırasında öbür ordugahların ortasında yola çıkacak. Herkes konakladığı düzende kendi sancağı altında göç edecek.
18 Kumadzulo kudzakhala magulu a msasa wa Efereimu pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Aefereimuwo ndi Elisama mwana wa Amihudi.
Batıda Efrayim ordugahının sancağı dikilecek, Efrayim'e bağlı bölükler orada konaklayacak. Efrayimoğulları'nın önderi Ammihut oğlu Elişama olacak.
19 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 40,500.
Bölüğünün sayısı 40 500 kişiydi.
20 Fuko la Manase lidzakhala pafupi ndi Efereimu. Mtsogoleri wa Amanase ndi Gamalieli mwana wa Pedazuri.
Manaşşe oymağı onlara bitişik olacak. Manaşşeoğulları'nın önderi Pedahsur oğlu Gamliel olacak.
21 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 32,200.
Bölüğünün sayısı 32 200 kişiydi.
22 Lotsatira lidzakhala fuko la Benjamini. Mtsogoleri wa Abenjamini ndi Abidani mwana wa Gideoni.
Sonra Benyamin oymağı konaklayacak. Benyaminoğulları'nın önderi Gidoni oğlu Avidan olacak.
23 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 35,400.
Bölüğünün sayısı 35 400 kişiydi.
24 Anthu onse aamuna mu msasa wa Efereimu, chiwerengero chawo ndi 108,100 monga mwa magulu awo. Iwowo azikhala achitatu posamuka.
Efrayim ordugahına ayrılan bölüklerdeki adam sayısı 108 100 kişiydi. Üçüncü olarak bunlar yola çıkacak.
25 Kumpoto kudzakhala msasa wa magulu a Dani pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Adani ndi Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
Kuzeyde Dan ordugahının sancağı dikilecek, Dan'a bağlı bölükler orada konaklayacak. Danoğulları'nın önderi Ammişadday oğlu Ahiezer olacak.
26 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 62,700.
Bölüğünün sayısı 62 700 kişiydi.
27 Fuko la Aseri lidzamanga pafupi ndi iwowo. Mtsogoleri wa Aaseri ndi Pagieli mwana wa Okirani.
Aşer oymağı onların bitişiğinde konaklayacak. Aşeroğulları'nın önderi Okran oğlu Pagiel olacak.
28 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 41,500.
Bölüğünün sayısı 41 500 kişiydi.
29 Lotsatira lidzakhala fuko la Nafutali. Mtsogoleri wa Anafutali ndi Ahira mwana wa Enani.
Sonra Naftali oymağı konaklayacak. Naftalioğulları'nın önderi Enan oğlu Ahira olacak.
30 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 53,400.
Bölüğünün sayısı 53 400 kişiydi.
31 Anthu onse aamuna mu msasa wa Dani chiwerengero chawo ndi 157,600. Iwo azidzanyamuka pomaliza, ndi mbendera zawo.
Dan ordugahına ayrılan adamların sayısı 157 600 kişiydi. Kendi sancakları altında en son onlar yola çıkacak.
32 Amenewa ndi Aisraeli monga mwa mabanja a makolo awo. Chiwerengero cha Aisraeli onse mʼmisasa chinali 603,550, mwa magulu awo.
Ailelerine göre sayılan İsrailliler bunlardı. Ordugahlardaki bütün bölüklerin toplamı 603 550 kişiydi.
33 Koma Alevi sanawawerenge pamodzi ndi Aisraeli enawo monga momwe Yehova analamulira Mose.
RAB'bin Musa'ya verdiği buyruk uyarınca Levililer öbür İsrailliler'le birlikte sayılmadı.
34 Choncho Aisraeli anachita zonse zomwe Yehova analamulira Mose. Umo ndi momwe amamangira misasa yawo pamene panali mbendera zawo, ndipo ankasamuka monga mwa mafuko a makolo awo.
Böylece İsrailliler RAB'bin Musa'ya buyurduğu gibi yaptılar. Sancakları altında ordugah kurdular. Göç ederken de herkes boyu ve ailesiyle birlikte yola çıktı.