< Numeri 2 >
1 Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
HERREN talede til Moses og, Aron og sagde:
2 “Aisraeli azimanga misasa yawo mozungulira tenti ya msonkhano motalikira pangʼono. Munthu aliyense amange pamene pali mbendera ya fuko lake.”
Israeslitene skal lejre sig hver under sit Felttegn, under sit Fædrene hus's Mærke; i en Kreds om Åbenbaringsteltet skal de lejre sig.
3 Kummawa, kotulukira dzuwa, magulu a msasa wa Yuda amange pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Ayudawo ndi Naasoni mwana wa Aminadabu.
På Forsiden mod Øst skal Juda lejre sig under sin Lejrs Felttegn, Hærafdeling for Hærafdeling, med Nahasjon, Amminadabs Søn, som Øverste over Judæerne;
4 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 74,600.
de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 74600 Mand.
5 Fuko la Isakara lidzamanga pafupi ndi Yuda. Mtsogoleri wa gulu la Isakara ndi Netanieli mwana wa Zuwara.
Ved Siden af ham skal Issakars Stamme lejre sig med Netanel, Zuars Søn, som Øverste over Issakariterne;
6 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 54,400.
de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 54 400 Mand.
7 Lotsatira lidzakhala fuko la Zebuloni. Mtsogoleri wa gulu la Zebuloni ndi Eliabu mwana wa Heloni.
Dernæst Zebulons Stamme med Eliab, Helons Søn, som Øverste over Zebuloniterne;
8 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 57,400.
de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 57 400 Mand.
9 Anthu onse aamuna mʼmisasa ya Yuda, chiwerengero chawo ndi 186,400 monga mwa magulu awo. Iwowo ndiwo aziyamba kusamuka.
De mønstrede i Judas Lejr udgør i alt 186 400 Mand, Hærafdeling for Hærafdeling. De skal bryde op først.
10 Kummwera kudzakhala magulu a msasa wa Rubeni pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu la Rubeni ndi Elizuri mwana wa Sedeuri.
Ruben skal lejre sig under sin Lejrs Felttegn mod Syd, Hærafdeling for Hærafdeling, med Elizur, Sjedeurs Søn, som Øverste over Rubeniterne;
11 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 46,500.
de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 46 500 Mand.
12 Fuko la Simeoni lidzamanga pafupi ndi Rubeni. Mtsogoleri wa gulu la Simeoni ndi Selumieli mwana wa Zurisadai.
Ved Siden af ham skal Simeons Stamme lejre sig med Sjelumiel, Zurisjaddajs Søn, som Øverste over Simeoniterne;
13 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 59,300.
de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 59300 Mand.
14 Lotsatira lidzakhala fuko la Gadi. Mtsogoleri wa gulu la Gadi ndi Eliyasafu mwana wa Deuweli.
Dernæst Gads Stamme med Eljasaf, Reuels Søn, som Øverste over Gadiferne;
15 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 45,650.
de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 45 650 Mand.
16 Anthu onse aamuna mu msasa wa Rubeni, chiwerengero chawo monga mwa magulu awo, ndi 151,450. Iwowo azikhala achiwiri posamuka.
De mønstrede i Rubens Lejr udgør i alt 151 450 Mand, Hærafdeling for Hærafdeling. De skal bryde op i anden Række.
17 Tsono tenti ya msonkhano ndi msasa wa Alevi zidzakhala pakati pa misasayo. Iwo adzasamuka monga momwe anamangira misasa yawo, aliyense pa malo ake pamene pali mbendera yake.
Derpå skal Åbenbaringsteltet, Leviternes Lejr, bryde op midt imellem de andre Lejre; i den Rækkefølge, de lejrer sig, skal de bryde op, hver på sin Plads, Felttegn for Felttegn.
18 Kumadzulo kudzakhala magulu a msasa wa Efereimu pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Aefereimuwo ndi Elisama mwana wa Amihudi.
Efraim skal lejre sig under sin Lejrs Felttegn mod Vest med Elisjama, Ammihuds Søn, som Øverste over Efraimiterne;
19 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 40,500.
de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 40 500 Mand.
20 Fuko la Manase lidzakhala pafupi ndi Efereimu. Mtsogoleri wa Amanase ndi Gamalieli mwana wa Pedazuri.
Ved Siden af ham skal Manasses Stamme lejre sig med Gamliel, Pedazurs Søn, som Øverste over Manassiterne;
21 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 32,200.
de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 32 200 Mand.
22 Lotsatira lidzakhala fuko la Benjamini. Mtsogoleri wa Abenjamini ndi Abidani mwana wa Gideoni.
Dernæst Benjamins Stamme med Abidan, Gidonis Søn, som Øverste over Benjaminiterne;
23 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 35,400.
de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 35 400 Mand.
24 Anthu onse aamuna mu msasa wa Efereimu, chiwerengero chawo ndi 108,100 monga mwa magulu awo. Iwowo azikhala achitatu posamuka.
De mønstrede i Efraims Lejr udgør i alt 108 100 Mand, Hærafdeling for Hærafdeling. De skal bryde op i tredje Række.
25 Kumpoto kudzakhala msasa wa magulu a Dani pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Adani ndi Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
Dan skal lejre sig under sin Lejrs Felttegn mod Nord, Hærafdeling for Hærafdeling, med Ahiezer, Ammisjaddajs Søn, som Øverste over Daniterne;
26 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 62,700.
de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 62 700 Mand.
27 Fuko la Aseri lidzamanga pafupi ndi iwowo. Mtsogoleri wa Aaseri ndi Pagieli mwana wa Okirani.
Ved Siden af ham skal Asers Stamme lejre sig med Pagiel, Okrans Søn, som Øverste over Aseriterne;
28 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 41,500.
de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op til 41 500 Mand.
29 Lotsatira lidzakhala fuko la Nafutali. Mtsogoleri wa Anafutali ndi Ahira mwana wa Enani.
Dernæst Naftalis Stamme med Ahira, Enans Søn, som Øverste over Naftaliterne;
30 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 53,400.
de mønstrede, som udgør hans Hærafdeling, løber op fil 53 400 Mand.
31 Anthu onse aamuna mu msasa wa Dani chiwerengero chawo ndi 157,600. Iwo azidzanyamuka pomaliza, ndi mbendera zawo.
De mønstrede i Dans Lejr udgør i alt 157600 Mand. De skal bryde op sidst, Felttegn for Felttegn.
32 Amenewa ndi Aisraeli monga mwa mabanja a makolo awo. Chiwerengero cha Aisraeli onse mʼmisasa chinali 603,550, mwa magulu awo.
Det var de mønstrede af Israeliterne efter deres Fædrenehuse, alle de mønstrede i Lejrene, Hærafdeling for Hærafdeling, 603 550 Mand.
33 Koma Alevi sanawawerenge pamodzi ndi Aisraeli enawo monga momwe Yehova analamulira Mose.
Men Leviterne mønstredes ikke sammen med de andre Israelitter, således som HERREN havde pålagt Moses.
34 Choncho Aisraeli anachita zonse zomwe Yehova analamulira Mose. Umo ndi momwe amamangira misasa yawo pamene panali mbendera zawo, ndipo ankasamuka monga mwa mafuko a makolo awo.
Og ganske som HERREN havde pålagt Moses, slog Israeliterne Lejr, Felttegn for Felttegn, og i den Rækkefølge brød de op, enhver med sine Slægter, med sit Fædrenehus.