< Numeri 18 >

1 Yehova anawuza Aaroni kuti, “Iwe, ana ako aamuna ndi banja la abambo ako mudzasenza tchimo la malo wopatulika, koma iwe ndi ana ako aamuna okha mudzasenza tchimo lokhudza unsembe wanu.
Potem rzekł Pan do Aarona: Ty i synowie twoi, i dom ojca twego z tobą, poniesiecie nieprawość świątnicy. I ty i synowie twoi z tobą poniesiecie nieprawość kapłaństwa waszego.
2 Ubweretse Alevi, abale ako, kuchokera ku fuko la abambo ako kuti azikhala ndi iwe ndi kumakuthandiza pamodzi ndi ana ako amuna pamene mukutumikira mu tenti ya umboni.
Bracią także twoję, pokolenie Lewiego, ród ojca twego, przypuścisz do siebie, aby byli przy tobie, i posługowali tobie; a ty i synowie twoi z tobą służyć będziecie przed namiotem świadectwa.
3 Iwowo azikutumikirani ndipo azichita ntchito zonse za ku tenti, koma asamafike pafupi ndi zipangizo za ku malo opatulika kapena guwa lansembe, kuopa kuti iwo ndi inu mungafe.
Oni będą przestrzegali rozkazania twego, i pilnowali wszystkiego namiotu; wszakże do naczynia śwątnicy, i do ołtarza, przystępować nie będą, aby nie pomarli, i oni i wy.
4 Azikhala ndi inu ndipo azisamalira ntchito yonse ya mu tenti ya msonkhano koma munthu wina aliyense wapadera sayenera kufika pafupi nanu.
I przyłączą się do ciebie, pilnie strzegąc namiotu zgromadzenia w każdej usłudze namiotu; a nikt obcy niechaj się nie mięsza między was.
5 “Inuyo muzisamalira malo wopatulika ndi guwa lansembe, kuti ukali wa Yehova usawagwerenso Aisraeli.
Wy tedy pilnie strzeżcie świątnicy, i usługi ołtarzowej, by się napotem nie wzruszył gniew przeciwko synom Izraelskim.
6 Ine mwini ndasankha Alevi, abale ako, pakati pa Aisraeli ngati mphatso yako ndipo aperekedwa kwa Yehova kuti azigwira ntchito ku tenti ya msonkhano.
Bom oto ja obrał bracią waszę Lewity, z pośród synów Izraelskich, wam za dar, oddane Panu, aby odprawowali usługę w namiocie zgromadzenia.
7 Koma iwe wekha ndi ana ako aamuna muzitumikira ngati ansembe ndi zina zonse zokhudza pa guwa lansembe ndi za mʼkati mwa malo wopatulika kwambiri. Ndikukupatsani mphatso ya utumiki wa unsembe. Aliyense woyandikira malo wopatulika ayenera kuphedwa.
Ale ty i synowie twoi z tobą, przestrzegać będziecie kapłaństwa waszego przy każdej usłudze ołtarzowej, i za zasłoną służyć będziecie; urząd kapłaństwa waszego dałem wam darmo; gdyby kto obcy przystąpił, umrze.
8 “Kenaka Yehova anati kwa Aaroni, ona, Ine mwini ndikukuyika kuti ukhale woyangʼanira zopereka zobwera kwa Ine; zopereka zonse zopatulika za Aisraeli zimene amapereka kwa ine ndi kuzipereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ngati gawo lanu la nthawi zonse.
Nadto mówił Pan do Aarona: Otom ja dał tobie pod straż ofiary moje podnoszone; wszystkie rzeczy poświęcone od synów Izraelskich tobiem je dał dla pomazania, i synom twoim prawem wiecznem.
9 Uzilandiranso gawo la zopereka zopatulika kwambiri zomwe sizinawotchedwe pa moto. Kuchokera pa mphatso zonse zimene amabweretsa kwa Ine ngati zopatulika kwambiri, nsembe zachakudya kapena nsembe zopepesera machimo, gawo limenelo ndi lako ndi ana ako aamuna.
To będzie twoje z rzeczy poświęconych, które nie bywają palone. Każda ofiara ich, bądź ofiara śniedna ich, bądź ofiara za grzech ich, albo ofiara za występek ich, cokolwiek mi oddawać będą to będzie rzeczą poświęconą tobie i synom twoim,
10 Muzidya zimenezo ngati zinthu zopatulika kwambiri; mwamuna aliyense adyeko. Uzitenge kukhala zopatulika.
Na miejscu najświętszem jadać to będziesz; wszelki mężczyzna będzie jadł z tego; rzeczą poświęconą to będzie tobie.
11 “Izinso ndi zako: chilichonse chopatulidwa kuchokera ku mphatso zoweyula za Aisraeli ndapereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ndi aakazi ngati gawo lako la nthawi zonse. Aliyense wa mʼnyumba mwako amene ali woyeretsedwa monga mwa mwambo angathe kudyako.
To też twoje będzie, ofiara podnoszenia darów ich ze wszystkiemi ofiarami tam i sam obracania synów Izraelskich; tobiem je dał, i synom twoim, i córkom twoim z tobą, prawem wiecznem; każdy czysty w domu twoim będzie je jadł.
12 “Ndikukupatsani mafuta onse abwino kwambiri a olivi ndi vinyo yense watsopano wabwino kwambiri ndi tirigu yense zomwe Aisraeli amapereka kwa Yehova ngati zipatso zoyamba pa zokolola zawo.
Każdą co najprzedniejszą oliwę, i każde co najlepsze wino, i zboże, pierwiastki ich, które ofiarują Panu, tobiem je dał.
13 Zipatso zonse zoyamba kucha za mʼdziko lawo zomwe amapereka kwa Yehova zidzakhala zako. Aliyense mʼnyumba mwako amene ali woyeretsedwa angathe kudyako.
Pierwociny ze wszystkich rzeczy, które będą w ziemi ich, które przyniosą Panu, twoje będą; każdy czysty w domu twoim jadać je będzie.
14 “Chilichonse mu Israeli chomwe chapatulidwira Yehova ndi chako.
Wszystko, cokolwiek jest poślubione w Izraelu, twoje będzie.
15 Chilichonse choyamba kubadwa kwa munthu kaya nyama, chomwe chaperekedwa kwa Yehova ndi chako. Koma uyenera kuwombola mwana aliyense wamwamuna ndi mwana aliyense woyamba wa nyama zodetsedwa.
Cokolwiek otwiera żywot wszelkiego ciała, a bywa ofiarowane Panu, tak z ludzi jako z bydła, twoje będzie; ale pierworodne z ludzi okupisz, także pierworodne nieczystego bydła okupisz.
16 Pamene zili ndi mwezi umodzi wa kubadwa, uziwombole pa mtengo wowombolera wa ndalama zisanu zasiliva, monga mwa ndalama za ku malo wopatulika.
A okup jego, gdy mu miesiąc minie, dasz według szacunku twego pięć syklów srebra według sykla świątnicy; dwadzieścia pieniędzy waży sykiel.
17 “Koma usawombole ana oyamba kubadwa a ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi. Iwo ndi opatulika. Uwaze magazi a nyamazi pa guwa lansembe ndi kutentha mafuta ake ngati nsembe yotentha ndi moto kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova.
Ale pierworodnego od krowy, albo pierworodnego od owcy, albo pierworodnego od kozy, nie dasz na okup; bo poświęcone są; krew ich wylejesz na ołtarz, a tłustość ich zapalisz na ofiarę ognistą dla wdzięcznej wonności Panu.
18 Nyama yake ikhale yanu monga momwe chimakhalira chidale cha nsembe yoweyula ndi ntchafu za miyendo ya kumanja, zonsezi ndi zako.
Ale mięso ich twoje będzie; jako mostek podnoszenia, i jako łopatka prawa, twoje będą.
19 Zonse zimene mwazichotsa ku zopereka zoyera zomwe Aisraeli anapereka kwa Yehova ndazipereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ndi aakazi ngati gawo lanu nthawi zonse. Ili ndi pangano losatha la mchere pamaso pa Yehova kwa iwe ndi ana ako.”
Wszystkie ofiary podnoszenia z rzeczy poświęconych, które przynosić będą synowie Izraelscy Panu, dałem tobie, i synom twym, i córkom twoim z tobą, prawem wiecznem; ustawa to nienaruszona, i wieczna przed Panem, tobie i nasieniu twemu z tobą.
20 Ndipo Yehova anati kwa Aaroni, “Iweyo sudzakhala ndi cholowa mʼdziko lawo, ndiponso sudzalandira gawo lililonse pakati pawo. Ine ndine gawo lako ndi cholowa chako pakati pa Aisraeli.
Potem mówił Pan do Aarona: W ziemi ich dziedzictwa mieć nie będziesz, i działu nie będziesz miał między nimi; Jam dział twój, i dziedzictwo twoje w pośród synów Izraelskich.
21 “Taonani, ndawapatsa Alevi chakhumi chonse mu Israeli ngati cholowa chawo chifukwa cha ntchito ya ku tenti ya msonkhano.
Synom zaś Lewiego otom dał wszystkę dziesięcinę w Izraelu dziedzicznie za służbę ich, którą wykonywają służąc około namiotu zgromadzenia.
22 Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo Aisraeli asamapite pafupi ndi tenti ya msonkhano. Ngati atero adzasenza zotsatira za tchimo lawo ndipo adzafa.
A niechaj nie przystępują więcej synowie Izraelscy do namiotu zgromadzenia, aby nie ponieśli grzechu i nie pomarli;
23 Alevi ndi amene azidzagwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano ndipo adzalangidwa chilichonse chikalakwika. Ili ndi lamulo losatha kwa mibado yawo yonse. Iwowo sadzalandira cholowa pakati pa Aisraeli.
Ale sami Lewitowie odprawować będą usługę około namiotu zgromadzenia, i sami poniosą nieprawość swoję. Ustawa to wieczna będzie w narodziech waszych, aby w pośród synów Izraelskich dziedzictwa nie mieli.
24 Mʼmalo mwake, ndikuwapatsa Aleviwo chakhumi ngati cholowa chawo chimene Aisraeli amapereka kwa Yehova. Nʼchifukwa chake zokhudza iwo ndinati: ‘Sadzakhala ndi cholowa pakati pa Aisraeli.’”
Albowiem dziesięciny synów Izraelskich które przynosić będą na ofiarę podnoszenia Panu, dałem Lewitom za dziedzictwo; przetoż rzekłem do nich: W pośród synów Izraelskich nie będą mieli dziedzictwa.
25 Yehova anati kwa Mose,
Potem rzekł Pan do Mojżesza mówiąc:
26 “Yankhula ndi Alevi ndi kunena nawo kuti, ‘Pamene mulandira chakhumi kuchoka kwa Aisraeli chimene ndimakupatsani ngati cholowa chanu, muyenera kupereka chakhumi cha choperekacho kwa Yehova.
Mów też do Lewitów, a powiedz im: Gdy weźmiecie od synów Izraelskich dziesięciny, którem ja wam dał od nich za dziedzictwo wasze, tedy ofiarować będziecie ofiarę podnoszenia Panu dziesiątą część dziesięcin.
27 Chopereka chanucho chidzawerengedwa kwa inu ngati tirigu wochokera kopunthira kapena ngati mphesa zopsinya kuchokera kopsinyira mphesa.
A poczytana wam będzie ta ofiara wasza jako zboże z bojewiska, i jako obfitość wina z prasy.
28 Mwa njira imeneyi inunso muzipereka chopereka kwa Yehova kuchokera ku chakhumi chanu chilichonse chimene mumalandira kuchokera kwa Aisraeli. Kuchokera ku chakhumicho muziperekako gawo la Yehova kwa Aaroni, wansembe.
Tak wy też ofiarować będziecie ofiarę podnoszenia Panu ze wszystkich dziesięcin waszych, które weźmiecie od synów Izraelskich, a oddacie z nich ofiarę podnoszenia Panu, Aaronowi kapłanowi:
29 Muyenera kupereka monga gawo la Yehova magawo abwino kwambiri ndi opatulika a chilichonse chimene chapatsidwa kwa inu.’
Ze wszystkich dochodów waszych ofiarować będziecie wszelką ofiarę podnoszenia Panu; ze wszystkiego co najlepsze jest, ofiarujecie cząstkę poświęconą.
30 “Nena kwa Alevi: ‘Pamene mupereka gawo labwino lopambana zonse, gawo limenelo lidzawerengedwa kwa inu ngati lochokera popunthira tirigu kapenanso kopsinyira mphesa.
Powiesz im też: Gdy oddawać będziecie z tego, co najlepsze jest, tedy poczytano będzie Lewitom jako urodzaje z bojewiska; i jako urodzaj z prasy.
31 Inu ndi a pa banja panu mungathe kudyera zimenezi paliponse chifukwa ndi malipiro a ntchito yanu ya ku tenti ya msonkhano.
I będziecie to jeść na każdem miejscu, wy i czeladź wasza; albowiem to jest zapłata wasza za służbę waszę przy namiocie zgromadzenia;
32 Popereka gawo labwino kwambirilo simudzapezeka olakwa. Mukatero simudzadetsa zopereka zoyera za Aisraeli, ndipo simudzafa.’”
I nie poniesiecie za to grzechu, gdy ofiarować będziecie co najlepszego jest z tego, i nie splugawicie rzeczy poświęconych od synów Izraelskich, i nie pomrzecie.

< Numeri 18 >