< Numeri 18 >
1 Yehova anawuza Aaroni kuti, “Iwe, ana ako aamuna ndi banja la abambo ako mudzasenza tchimo la malo wopatulika, koma iwe ndi ana ako aamuna okha mudzasenza tchimo lokhudza unsembe wanu.
Yahvé dit à Aaron: « Toi, tes fils et la maison de tes pères avec toi, vous porterez l'iniquité du sanctuaire; toi et tes fils avec toi, vous porterez l'iniquité de votre sacerdoce.
2 Ubweretse Alevi, abale ako, kuchokera ku fuko la abambo ako kuti azikhala ndi iwe ndi kumakuthandiza pamodzi ndi ana ako amuna pamene mukutumikira mu tenti ya umboni.
Fais aussi approcher de toi tes frères, la tribu de Lévi, la tribu de ton père, afin qu'ils soient associés à toi et qu'ils te servent; mais toi et tes fils avec toi, vous serez devant la tente du témoignage.
3 Iwowo azikutumikirani ndipo azichita ntchito zonse za ku tenti, koma asamafike pafupi ndi zipangizo za ku malo opatulika kapena guwa lansembe, kuopa kuti iwo ndi inu mungafe.
Ils observeront tes ordres et les devoirs de toute la tente; seulement, ils ne s'approcheront pas des ustensiles du sanctuaire ni de l'autel, afin qu'ils ne meurent pas, ni eux ni toi.
4 Azikhala ndi inu ndipo azisamalira ntchito yonse ya mu tenti ya msonkhano koma munthu wina aliyense wapadera sayenera kufika pafupi nanu.
Ils s'attacheront à toi et garderont la responsabilité de la Tente de la Rencontre, pour tout le service de la Tente. L'étranger ne s'approchera pas de toi.
5 “Inuyo muzisamalira malo wopatulika ndi guwa lansembe, kuti ukali wa Yehova usawagwerenso Aisraeli.
Vous accomplirez les fonctions du sanctuaire et de l'autel, afin qu'il n'y ait plus de colère contre les enfants d'Israël.
6 Ine mwini ndasankha Alevi, abale ako, pakati pa Aisraeli ngati mphatso yako ndipo aperekedwa kwa Yehova kuti azigwira ntchito ku tenti ya msonkhano.
Voici, j'ai pris moi-même vos frères les Lévites parmi les enfants d'Israël. Ils te sont offerts, ils sont consacrés à l'Éternel, pour faire le service de la Tente de la Rencontre.
7 Koma iwe wekha ndi ana ako aamuna muzitumikira ngati ansembe ndi zina zonse zokhudza pa guwa lansembe ndi za mʼkati mwa malo wopatulika kwambiri. Ndikukupatsani mphatso ya utumiki wa unsembe. Aliyense woyandikira malo wopatulika ayenera kuphedwa.
Toi et tes fils avec toi, vous exercerez votre sacerdoce pour tout ce qui concerne l'autel et ce qui est en deçà du voile. Tu feras le service. Je vous fais don du service de la prêtrise. L'étranger qui s'approchera sera mis à mort. »
8 “Kenaka Yehova anati kwa Aaroni, ona, Ine mwini ndikukuyika kuti ukhale woyangʼanira zopereka zobwera kwa Ine; zopereka zonse zopatulika za Aisraeli zimene amapereka kwa ine ndi kuzipereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ngati gawo lanu la nthawi zonse.
Yahvé parla à Aaron: « Voici, je t'ai donné moi-même l'ordre d'offrir mes offrandes par agitation, toutes les choses saintes des enfants d'Israël. Je te les ai données, à cause de l'onction, ainsi qu'à tes fils, comme une part pour toujours.
9 Uzilandiranso gawo la zopereka zopatulika kwambiri zomwe sizinawotchedwe pa moto. Kuchokera pa mphatso zonse zimene amabweretsa kwa Ine ngati zopatulika kwambiri, nsembe zachakudya kapena nsembe zopepesera machimo, gawo limenelo ndi lako ndi ana ako aamuna.
Voici ce qui vous appartiendra parmi les choses très saintes du feu: toute offrande qu'ils m'offriront, toute offrande de farine, tout sacrifice pour le péché et tout sacrifice de culpabilité, sera très sainte pour vous et pour vos fils.
10 Muzidya zimenezo ngati zinthu zopatulika kwambiri; mwamuna aliyense adyeko. Uzitenge kukhala zopatulika.
Vous en mangerez comme des choses très saintes. Tout mâle en mangera. Ce sera pour vous une chose sainte.
11 “Izinso ndi zako: chilichonse chopatulidwa kuchokera ku mphatso zoweyula za Aisraeli ndapereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ndi aakazi ngati gawo lako la nthawi zonse. Aliyense wa mʼnyumba mwako amene ali woyeretsedwa monga mwa mwambo angathe kudyako.
« Ceci est aussi à toi: l'offrande de leurs dons, toutes les offrandes des enfants d'Israël. Je te les ai données, à toi, à tes fils et à tes filles avec toi, comme une part pour toujours. Tous ceux qui sont purs dans ta maison en mangeront.
12 “Ndikukupatsani mafuta onse abwino kwambiri a olivi ndi vinyo yense watsopano wabwino kwambiri ndi tirigu yense zomwe Aisraeli amapereka kwa Yehova ngati zipatso zoyamba pa zokolola zawo.
« Je te donne tout le meilleur de l'huile, tout le meilleur de la vendange et du blé, les prémices de ce qu'ils apportent à l'Éternel.
13 Zipatso zonse zoyamba kucha za mʼdziko lawo zomwe amapereka kwa Yehova zidzakhala zako. Aliyense mʼnyumba mwako amene ali woyeretsedwa angathe kudyako.
Les prémices de tout ce qui se trouve dans leur pays, qu'ils apporteront à l'Éternel, seront à toi. Tous ceux qui sont propres dans votre maison en mangeront.
14 “Chilichonse mu Israeli chomwe chapatulidwira Yehova ndi chako.
« Tout ce qui est consacré en Israël sera à toi.
15 Chilichonse choyamba kubadwa kwa munthu kaya nyama, chomwe chaperekedwa kwa Yehova ndi chako. Koma uyenera kuwombola mwana aliyense wamwamuna ndi mwana aliyense woyamba wa nyama zodetsedwa.
Tout ce qui ouvre le ventre, de toute chair qu'on offre à l'Éternel, tant des hommes que des animaux, sera à vous. Toutefois, vous rachèterez les premiers-nés des hommes et vous rachèterez les premiers-nés des animaux impurs.
16 Pamene zili ndi mwezi umodzi wa kubadwa, uziwombole pa mtengo wowombolera wa ndalama zisanu zasiliva, monga mwa ndalama za ku malo wopatulika.
Tu rachèteras ceux d'entre eux qui sont âgés d'un mois, selon ton estimation, pour cinq sicles d'argent, selon le sicle du sanctuaire, qui pèse vingt gérachs.
17 “Koma usawombole ana oyamba kubadwa a ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi. Iwo ndi opatulika. Uwaze magazi a nyamazi pa guwa lansembe ndi kutentha mafuta ake ngati nsembe yotentha ndi moto kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova.
« Mais tu ne rachèteras pas le premier-né d'une vache, ni le premier-né d'une brebis, ni le premier-né d'une chèvre. Ils sont saints. Tu feras l'aspersion de leur sang sur l'autel, et tu brûleras leur graisse en offrande consumée par le feu, comme une odeur agréable à Yahvé.
18 Nyama yake ikhale yanu monga momwe chimakhalira chidale cha nsembe yoweyula ndi ntchafu za miyendo ya kumanja, zonsezi ndi zako.
Leur viande sera à toi, comme la poitrine offerte par onction et comme la cuisse droite, elle sera à toi.
19 Zonse zimene mwazichotsa ku zopereka zoyera zomwe Aisraeli anapereka kwa Yehova ndazipereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ndi aakazi ngati gawo lanu nthawi zonse. Ili ndi pangano losatha la mchere pamaso pa Yehova kwa iwe ndi ana ako.”
Toutes les offrandes par ondulation des choses saintes que les enfants d'Israël offrent à l'Éternel, je vous les donne, à vous, à vos fils et à vos filles avec vous, comme une part pour toujours. C'est une alliance de sel pour toujours devant l'Éternel, pour toi et pour ta descendance avec toi. »
20 Ndipo Yehova anati kwa Aaroni, “Iweyo sudzakhala ndi cholowa mʼdziko lawo, ndiponso sudzalandira gawo lililonse pakati pawo. Ine ndine gawo lako ndi cholowa chako pakati pa Aisraeli.
Yahvé dit à Aaron: « Tu n'auras pas d'héritage dans leur pays, et tu n'auras pas de part au milieu d'eux. Je suis ta part et ton héritage parmi les enfants d'Israël.
21 “Taonani, ndawapatsa Alevi chakhumi chonse mu Israeli ngati cholowa chawo chifukwa cha ntchito ya ku tenti ya msonkhano.
« Aux fils de Lévi, voici, j'ai donné en héritage toute la dîme en Israël, en contrepartie du service qu'ils font, le service de la tente d'assignation.
22 Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo Aisraeli asamapite pafupi ndi tenti ya msonkhano. Ngati atero adzasenza zotsatira za tchimo lawo ndipo adzafa.
Désormais, les enfants d'Israël ne s'approcheront plus de la Tente de la Rencontre, de peur de porter le péché et de mourir.
23 Alevi ndi amene azidzagwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano ndipo adzalangidwa chilichonse chikalakwika. Ili ndi lamulo losatha kwa mibado yawo yonse. Iwowo sadzalandira cholowa pakati pa Aisraeli.
Mais les Lévites feront le service de la Tente d'assignation, et ils porteront leur faute. Ce sera une loi pour toujours, de génération en génération. Ils n'auront pas d'héritage parmi les enfants d'Israël.
24 Mʼmalo mwake, ndikuwapatsa Aleviwo chakhumi ngati cholowa chawo chimene Aisraeli amapereka kwa Yehova. Nʼchifukwa chake zokhudza iwo ndinati: ‘Sadzakhala ndi cholowa pakati pa Aisraeli.’”
En revanche, j'ai donné en héritage aux Lévites la dîme des enfants d'Israël, qu'ils offrent en offrande à Yahvé. C'est pourquoi je leur ai dit: « Ils n'auront pas d'héritage parmi les enfants d'Israël. »
25 Yehova anati kwa Mose,
Yahvé parla à Moïse et dit:
26 “Yankhula ndi Alevi ndi kunena nawo kuti, ‘Pamene mulandira chakhumi kuchoka kwa Aisraeli chimene ndimakupatsani ngati cholowa chanu, muyenera kupereka chakhumi cha choperekacho kwa Yehova.
Tu parleras aux Lévites et tu leur diras: « Lorsque vous prélèverez sur les enfants d'Israël la dîme que je vous donne en héritage, vous en ferez une offrande pour Yahvé, la dîme de la dîme.
27 Chopereka chanucho chidzawerengedwa kwa inu ngati tirigu wochokera kopunthira kapena ngati mphesa zopsinya kuchokera kopsinyira mphesa.
Ton offrande ondulatoire te sera créditée comme le grain de l'aire et comme la plénitude de la cuve.
28 Mwa njira imeneyi inunso muzipereka chopereka kwa Yehova kuchokera ku chakhumi chanu chilichonse chimene mumalandira kuchokera kwa Aisraeli. Kuchokera ku chakhumicho muziperekako gawo la Yehova kwa Aaroni, wansembe.
C'est ainsi que tu présenteras à l'Éternel une offrande par ondulation de toutes les dîmes que tu recevras des enfants d'Israël, et tu en donneras une au prêtre Aaron.
29 Muyenera kupereka monga gawo la Yehova magawo abwino kwambiri ndi opatulika a chilichonse chimene chapatsidwa kwa inu.’
De toutes vos offrandes, vous présenterez à Yahvé chaque offrande par ondulation, dans toutes ses parties les meilleures, même la partie sainte.''
30 “Nena kwa Alevi: ‘Pamene mupereka gawo labwino lopambana zonse, gawo limenelo lidzawerengedwa kwa inu ngati lochokera popunthira tirigu kapenanso kopsinyira mphesa.
Tu leur diras: « Lorsque vous en aurez récolté le meilleur, il sera porté au crédit des Lévites comme le produit de l'aire de battage et comme le produit du pressoir.
31 Inu ndi a pa banja panu mungathe kudyera zimenezi paliponse chifukwa ndi malipiro a ntchito yanu ya ku tenti ya msonkhano.
Vous pourrez en manger partout, vous et vos familles, car c'est votre récompense pour votre service dans la Tente de la Rencontre.
32 Popereka gawo labwino kwambirilo simudzapezeka olakwa. Mukatero simudzadetsa zopereka zoyera za Aisraeli, ndipo simudzafa.’”
Tu ne porteras pas de péché à cause d'elle, lorsque tu en auras tiré le meilleur. Tu ne profaneras pas les choses saintes des enfants d'Israël, afin de ne pas mourir.'"