< Numeri 18 >

1 Yehova anawuza Aaroni kuti, “Iwe, ana ako aamuna ndi banja la abambo ako mudzasenza tchimo la malo wopatulika, koma iwe ndi ana ako aamuna okha mudzasenza tchimo lokhudza unsembe wanu.
And the Lord seide to Aaron, Thou, and thi sones, and the hows of thi fadir with thee, schulen bere the wickidnesse of the seyntuarie; and thou and thi sones togidere schulen suffre the synnes of youre preesthod.
2 Ubweretse Alevi, abale ako, kuchokera ku fuko la abambo ako kuti azikhala ndi iwe ndi kumakuthandiza pamodzi ndi ana ako amuna pamene mukutumikira mu tenti ya umboni.
But also take thou with thee thi britheren of the lynage of Leuy, and the power of thi fadir, and be thei redi, that thei mynystre to thee. Forsothe thou and thi sones schulen mynystre in the tabernacle of witnessyng;
3 Iwowo azikutumikirani ndipo azichita ntchito zonse za ku tenti, koma asamafike pafupi ndi zipangizo za ku malo opatulika kapena guwa lansembe, kuopa kuti iwo ndi inu mungafe.
and the dekenes schulen wake at thi comaundementis, and at alle werkis of the tabernacle; so oneli that thei neiye not to the vessels of seyntuarie, and to the autir, lest bothe thei dien, and ye perischen togidere.
4 Azikhala ndi inu ndipo azisamalira ntchito yonse ya mu tenti ya msonkhano koma munthu wina aliyense wapadera sayenera kufika pafupi nanu.
Forsothe be thei with thee, and wake thei in the kepyngis of the tabernacle, and in alle the cerymonyes therof. An alien schal not be meddlid with you.
5 “Inuyo muzisamalira malo wopatulika ndi guwa lansembe, kuti ukali wa Yehova usawagwerenso Aisraeli.
Wake ye in the kepyng of the seyntuarie, and in the seruyce of the auter, lest indignacioun rise on the sones of Israel.
6 Ine mwini ndasankha Alevi, abale ako, pakati pa Aisraeli ngati mphatso yako ndipo aperekedwa kwa Yehova kuti azigwira ntchito ku tenti ya msonkhano.
Lo! Y haue youun `to you youre britheren, dekenes, fro the myddis of the sones of Israel, and Y haue youe a fre yifte to the Lord, that thei serue in the seruyces of his tabernacle.
7 Koma iwe wekha ndi ana ako aamuna muzitumikira ngati ansembe ndi zina zonse zokhudza pa guwa lansembe ndi za mʼkati mwa malo wopatulika kwambiri. Ndikukupatsani mphatso ya utumiki wa unsembe. Aliyense woyandikira malo wopatulika ayenera kuphedwa.
Forsothe thou and thi sones, kepe youre preesthod; and alle thingis that perteynen to the ournyng of the auter, and ben with ynne the veil, schulen be mynystrid bi preestis; if ony straunger neiyeth, he schal be slayn.
8 “Kenaka Yehova anati kwa Aaroni, ona, Ine mwini ndikukuyika kuti ukhale woyangʼanira zopereka zobwera kwa Ine; zopereka zonse zopatulika za Aisraeli zimene amapereka kwa ine ndi kuzipereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ngati gawo lanu la nthawi zonse.
The Lord spak to Aaron, Lo! Y haue youe to thee the kepyng of my firste fruytis; Y haue youe to thee and to thi sones alle thingis, that ben halewid of the sones of Israel, for preestis office euerlastynge lawful thingis.
9 Uzilandiranso gawo la zopereka zopatulika kwambiri zomwe sizinawotchedwe pa moto. Kuchokera pa mphatso zonse zimene amabweretsa kwa Ine ngati zopatulika kwambiri, nsembe zachakudya kapena nsembe zopepesera machimo, gawo limenelo ndi lako ndi ana ako aamuna.
Therfor thou schalt take these thingis of tho thingis that ben halewid, and ben offrid to the Lord; ech offryng, and sacrifice, and what euer thing is yoldun to me for synne and for trespas, and cometh in to hooli of hooli thingis, schal be thin and thi sones.
10 Muzidya zimenezo ngati zinthu zopatulika kwambiri; mwamuna aliyense adyeko. Uzitenge kukhala zopatulika.
Thou schalt ete it in the seyntuarie; malis oneli schulen ete therof, for it is halewid to the Lord.
11 “Izinso ndi zako: chilichonse chopatulidwa kuchokera ku mphatso zoweyula za Aisraeli ndapereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ndi aakazi ngati gawo lako la nthawi zonse. Aliyense wa mʼnyumba mwako amene ali woyeretsedwa monga mwa mwambo angathe kudyako.
Forsothe Y haue youe to thee, and to thi sones and douytris, bi euerlastynge riyt, the firste fruytis whiche the sones of Israel a vowen and offren; he that is clene in thin hous, schal ete tho.
12 “Ndikukupatsani mafuta onse abwino kwambiri a olivi ndi vinyo yense watsopano wabwino kwambiri ndi tirigu yense zomwe Aisraeli amapereka kwa Yehova ngati zipatso zoyamba pa zokolola zawo.
Y yaf to thee al the merowe of oile, and of wyn, and of wheete, what euer thing of the firste fruytis thei schulen offre to the Lord.
13 Zipatso zonse zoyamba kucha za mʼdziko lawo zomwe amapereka kwa Yehova zidzakhala zako. Aliyense mʼnyumba mwako amene ali woyeretsedwa angathe kudyako.
Alle the bigynnyngis of fruytis whiche the erthe bryngith forth, and ben brouyt to the Lord, schulen falle in to thin vsis; he that is cleene in thin hous, schal ete of tho.
14 “Chilichonse mu Israeli chomwe chapatulidwira Yehova ndi chako.
Al thing which the sones of Israel yelden bi avow, schal be thin.
15 Chilichonse choyamba kubadwa kwa munthu kaya nyama, chomwe chaperekedwa kwa Yehova ndi chako. Koma uyenera kuwombola mwana aliyense wamwamuna ndi mwana aliyense woyamba wa nyama zodetsedwa.
What euer thing `schal breke out first of the wombe of al fleisch, which fleisch thei offren to the Lord, whether it is of men, ethir of beestis, it schal be of thi riyt; so oneli that thou take prijs for the firste gendrid child of man, and that thou make ech beeste which is vncleene to be bouyt ayen;
16 Pamene zili ndi mwezi umodzi wa kubadwa, uziwombole pa mtengo wowombolera wa ndalama zisanu zasiliva, monga mwa ndalama za ku malo wopatulika.
whos ayenbiyng schal be aftir o monethe, for fyue siclis of siluer, bi the weiyte of seyntuarie; a sicle hath xx. halpens.
17 “Koma usawombole ana oyamba kubadwa a ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi. Iwo ndi opatulika. Uwaze magazi a nyamazi pa guwa lansembe ndi kutentha mafuta ake ngati nsembe yotentha ndi moto kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova.
Forsothe thou schalt not make the firste gendrid of oxe, and of scheep, and of goet, to be ayen bouyt, for tho ben halewid to the Lord; oneli thou schalt schede the blood of tho on the auter, and thou schalt brenne the ynnere fatnesse in to swettist odour to the Lord.
18 Nyama yake ikhale yanu monga momwe chimakhalira chidale cha nsembe yoweyula ndi ntchafu za miyendo ya kumanja, zonsezi ndi zako.
Forsothe the fleischis schulen falle in to thin vss, as the brest halewid and the riyt schuldur, schulen be thine.
19 Zonse zimene mwazichotsa ku zopereka zoyera zomwe Aisraeli anapereka kwa Yehova ndazipereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ndi aakazi ngati gawo lanu nthawi zonse. Ili ndi pangano losatha la mchere pamaso pa Yehova kwa iwe ndi ana ako.”
Y yaf to the and to thi sones and douytris, bi euerlastynge riyt, alle the firste fruytis of seyntuarie, whiche the sones of Israel offren to the Lord; it is euerlastynge couenant of salt bifor the Lord, to thee, and to thi sones.
20 Ndipo Yehova anati kwa Aaroni, “Iweyo sudzakhala ndi cholowa mʼdziko lawo, ndiponso sudzalandira gawo lililonse pakati pawo. Ine ndine gawo lako ndi cholowa chako pakati pa Aisraeli.
And the Lord seide to Aaron, Ye schulen not welde ony thing in the lond of hem, nether ye schulen haue part among hem; Y am thi part and erytage, in the myddis of the sones of Israel.
21 “Taonani, ndawapatsa Alevi chakhumi chonse mu Israeli ngati cholowa chawo chifukwa cha ntchito ya ku tenti ya msonkhano.
Forsothe Y yaf to the sones of Leuy alle the tithis of Israel in to possessioun, for the seruyce bi whyche thei seruen me in the tabernacle of boond of pees;
22 Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo Aisraeli asamapite pafupi ndi tenti ya msonkhano. Ngati atero adzasenza zotsatira za tchimo lawo ndipo adzafa.
that the sones of Israel neiye no more to the `tabernacle of boond of pees, nether do dedli synne.
23 Alevi ndi amene azidzagwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano ndipo adzalangidwa chilichonse chikalakwika. Ili ndi lamulo losatha kwa mibado yawo yonse. Iwowo sadzalandira cholowa pakati pa Aisraeli.
To the sones aloone of Leuy, seruynge me in the tabernacle, and berynge the `synnes of the puple, it schal be a lawful thing euerlastynge in youre generaciouns.
24 Mʼmalo mwake, ndikuwapatsa Aleviwo chakhumi ngati cholowa chawo chimene Aisraeli amapereka kwa Yehova. Nʼchifukwa chake zokhudza iwo ndinati: ‘Sadzakhala ndi cholowa pakati pa Aisraeli.’”
Thei schulen welde noon other thing, and thei schulen be apeied with the offryng of tithis, whiche Y departide in to vsis and necessaries of hem.
25 Yehova anati kwa Mose,
And the Lord spak to Moises and seide,
26 “Yankhula ndi Alevi ndi kunena nawo kuti, ‘Pamene mulandira chakhumi kuchoka kwa Aisraeli chimene ndimakupatsani ngati cholowa chanu, muyenera kupereka chakhumi cha choperekacho kwa Yehova.
Comaunde thou, and denounse to the dekenes, Whanne ye han take tithis of the sones of Israel, whiche Y yaf to you, offre ye the firste fruytis of tho to the Lord, that is, the tenthe part of the dyme,
27 Chopereka chanucho chidzawerengedwa kwa inu ngati tirigu wochokera kopunthira kapena ngati mphesa zopsinya kuchokera kopsinyira mphesa.
that it be arettid to you in to offryng of the firste fruytis, as wel of corn flooris as of pressis;
28 Mwa njira imeneyi inunso muzipereka chopereka kwa Yehova kuchokera ku chakhumi chanu chilichonse chimene mumalandira kuchokera kwa Aisraeli. Kuchokera ku chakhumicho muziperekako gawo la Yehova kwa Aaroni, wansembe.
and of alle thingis of whiche ye taken tithis, offre ye the firste fruytis to the Lord, and yyue ye to Aaron, preest.
29 Muyenera kupereka monga gawo la Yehova magawo abwino kwambiri ndi opatulika a chilichonse chimene chapatsidwa kwa inu.’
Alle thingis whiche ye schulen offre of tithis, and schulen departe in to the yiftis of the Lord, schulen be the beste, and alle chosun thingis.
30 “Nena kwa Alevi: ‘Pamene mupereka gawo labwino lopambana zonse, gawo limenelo lidzawerengedwa kwa inu ngati lochokera popunthira tirigu kapenanso kopsinyira mphesa.
And thou schalt seye to hem, If ye offren to the Lord alle the clere and betere thingis of tithis, it schal be arettid to you, as if ye yauen the firste fruitis of the corn floor and presse.
31 Inu ndi a pa banja panu mungathe kudyera zimenezi paliponse chifukwa ndi malipiro a ntchito yanu ya ku tenti ya msonkhano.
And ye schulen ete tho tithis in alle youre placis, as wel ye as youre meynees, for it is the prijs for the seruyce, in whiche ye seruen in the tabernacle of witnessyng.
32 Popereka gawo labwino kwambirilo simudzapezeka olakwa. Mukatero simudzadetsa zopereka zoyera za Aisraeli, ndipo simudzafa.’”
And ye schulen not do synne on this thing, `and resserue noble thingis and fat to you, lest ye defoulen the offryngis of the sones of Israel, and ye dien.

< Numeri 18 >