< Numeri 18 >

1 Yehova anawuza Aaroni kuti, “Iwe, ana ako aamuna ndi banja la abambo ako mudzasenza tchimo la malo wopatulika, koma iwe ndi ana ako aamuna okha mudzasenza tchimo lokhudza unsembe wanu.
And the Lord spoke to Aaron, saying, You and your sons and your father's house shall bear the sins of the holy things, and you and your sons shall bear the iniquity of your priesthood.
2 Ubweretse Alevi, abale ako, kuchokera ku fuko la abambo ako kuti azikhala ndi iwe ndi kumakuthandiza pamodzi ndi ana ako amuna pamene mukutumikira mu tenti ya umboni.
And take to yourself your brethren the tribe of Levi, the family of your father, and let them be joined to you, and let them minister to you; and you and your sons with you [shall minister] before the tabernacle of witness.
3 Iwowo azikutumikirani ndipo azichita ntchito zonse za ku tenti, koma asamafike pafupi ndi zipangizo za ku malo opatulika kapena guwa lansembe, kuopa kuti iwo ndi inu mungafe.
And they shall keep your charges, and the charges of the tabernacle; only they shall not approach the holy vessels and the altar, so both they and you shall not die.
4 Azikhala ndi inu ndipo azisamalira ntchito yonse ya mu tenti ya msonkhano koma munthu wina aliyense wapadera sayenera kufika pafupi nanu.
And they shall be joined to you, and shall keep the charges of the tabernacle of witness, in all the services of the tabernacle; and a stranger shall not approach to you.
5 “Inuyo muzisamalira malo wopatulika ndi guwa lansembe, kuti ukali wa Yehova usawagwerenso Aisraeli.
And you shall keep the charges of the holy things, and the charges of the altar, and [so] there shall not be anger among the children of Israel.
6 Ine mwini ndasankha Alevi, abale ako, pakati pa Aisraeli ngati mphatso yako ndipo aperekedwa kwa Yehova kuti azigwira ntchito ku tenti ya msonkhano.
And I have taken your brethren the Levites out of the midst of the children of Israel, a present given to the Lord, to minister in the services of the tabernacle of witness.
7 Koma iwe wekha ndi ana ako aamuna muzitumikira ngati ansembe ndi zina zonse zokhudza pa guwa lansembe ndi za mʼkati mwa malo wopatulika kwambiri. Ndikukupatsani mphatso ya utumiki wa unsembe. Aliyense woyandikira malo wopatulika ayenera kuphedwa.
And you and your sons after you shall keep up your priestly ministration, according to the whole manner of the altar, and that which is within the veil; and you shall minister in the services as the office of your priesthood; and the stranger that comes near shall die.
8 “Kenaka Yehova anati kwa Aaroni, ona, Ine mwini ndikukuyika kuti ukhale woyangʼanira zopereka zobwera kwa Ine; zopereka zonse zopatulika za Aisraeli zimene amapereka kwa ine ndi kuzipereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ngati gawo lanu la nthawi zonse.
And the Lord said to Aaron, And, behold, I have given you the charge of the first fruits of all things consecrated to me by the children of Israel; and I have given them to you as an honor, and to your sons after you for a perpetual ordinance.
9 Uzilandiranso gawo la zopereka zopatulika kwambiri zomwe sizinawotchedwe pa moto. Kuchokera pa mphatso zonse zimene amabweretsa kwa Ine ngati zopatulika kwambiri, nsembe zachakudya kapena nsembe zopepesera machimo, gawo limenelo ndi lako ndi ana ako aamuna.
And let this be to you from all the holy things that are consecrated [to me, even] the burnt offerings, from all their gifts, and from all their sacrifices, and from every trespass-offering of theirs, and from all their sin-offerings, whatever things they give to me of all their holy things, they shall be your and your sons'.
10 Muzidya zimenezo ngati zinthu zopatulika kwambiri; mwamuna aliyense adyeko. Uzitenge kukhala zopatulika.
In the most holy place shall you eat them; every male shall eat them, you and your sons: they shall be holy to you.
11 “Izinso ndi zako: chilichonse chopatulidwa kuchokera ku mphatso zoweyula za Aisraeli ndapereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ndi aakazi ngati gawo lako la nthawi zonse. Aliyense wa mʼnyumba mwako amene ali woyeretsedwa monga mwa mwambo angathe kudyako.
And this shall be to you of the first fruits of their gifts, of all the wave-offerings of the children of Israel; to you have I given them and to your sons and your daughters with you, a perpetual ordinance; every clean person in your house shall eat them.
12 “Ndikukupatsani mafuta onse abwino kwambiri a olivi ndi vinyo yense watsopano wabwino kwambiri ndi tirigu yense zomwe Aisraeli amapereka kwa Yehova ngati zipatso zoyamba pa zokolola zawo.
Every first-offering of oil, and every first-offering of wine, their first fruits of corn, whatever they may give to the Lord, to you have I given them.
13 Zipatso zonse zoyamba kucha za mʼdziko lawo zomwe amapereka kwa Yehova zidzakhala zako. Aliyense mʼnyumba mwako amene ali woyeretsedwa angathe kudyako.
All the first fruits that are in their land, whatever they shall offer to the Lord, shall be your: every clean person in your house shall eat them.
14 “Chilichonse mu Israeli chomwe chapatulidwira Yehova ndi chako.
Every devoted thing among the children of Israel shall be your.
15 Chilichonse choyamba kubadwa kwa munthu kaya nyama, chomwe chaperekedwa kwa Yehova ndi chako. Koma uyenera kuwombola mwana aliyense wamwamuna ndi mwana aliyense woyamba wa nyama zodetsedwa.
And every thing that opens the womb of all flesh, whatever they bring to the Lord, whether man or beast, shall be your: only the firstborn of men shall be surely redeemed, and you shall redeem the firstborn of unclean cattle.
16 Pamene zili ndi mwezi umodzi wa kubadwa, uziwombole pa mtengo wowombolera wa ndalama zisanu zasiliva, monga mwa ndalama za ku malo wopatulika.
And the redemption of them [shall be] from a month old; their valuation of five shekels—it is twenty oboli according to the holy shekel.
17 “Koma usawombole ana oyamba kubadwa a ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi. Iwo ndi opatulika. Uwaze magazi a nyamazi pa guwa lansembe ndi kutentha mafuta ake ngati nsembe yotentha ndi moto kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova.
But you shall not redeem the firstborn of calves and the firstborn of sheep and the firstborn of goats; they are holy: and you shall pour their blood upon the altar, and you shall offer the fat as a burnt offering for a smell of sweet savor to the Lord.
18 Nyama yake ikhale yanu monga momwe chimakhalira chidale cha nsembe yoweyula ndi ntchafu za miyendo ya kumanja, zonsezi ndi zako.
And the flesh shall be your, as also the breast of the wave-offering and as the right shoulder, it shall be your.
19 Zonse zimene mwazichotsa ku zopereka zoyera zomwe Aisraeli anapereka kwa Yehova ndazipereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ndi aakazi ngati gawo lanu nthawi zonse. Ili ndi pangano losatha la mchere pamaso pa Yehova kwa iwe ndi ana ako.”
Every special offering of the holy things, whatever the children of Israel shall specially offer to the Lord, I have given to you and to your sons and to your daughters with you, a perpetual ordinance: it is a covenant of salt for ever before the Lord, for you and your seed after you.
20 Ndipo Yehova anati kwa Aaroni, “Iweyo sudzakhala ndi cholowa mʼdziko lawo, ndiponso sudzalandira gawo lililonse pakati pawo. Ine ndine gawo lako ndi cholowa chako pakati pa Aisraeli.
And the Lord said to Aaron, You shall have no inheritance in their land, neither shall you have any portion among them; for I [am] your portion and your inheritance in the midst of the children of Israel.
21 “Taonani, ndawapatsa Alevi chakhumi chonse mu Israeli ngati cholowa chawo chifukwa cha ntchito ya ku tenti ya msonkhano.
And, behold, I have given to the sons of Levi every tithe in Israel for an inheritance for their services, whenever they perform ministry in the tabernacle of witness.
22 Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo Aisraeli asamapite pafupi ndi tenti ya msonkhano. Ngati atero adzasenza zotsatira za tchimo lawo ndipo adzafa.
And the children of Israel shall no more draw near to the tabernacle of witness to incur fatal guilt.
23 Alevi ndi amene azidzagwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano ndipo adzalangidwa chilichonse chikalakwika. Ili ndi lamulo losatha kwa mibado yawo yonse. Iwowo sadzalandira cholowa pakati pa Aisraeli.
And the Levite himself shall perform the service of the tabernacle of witness; and they shall bear their iniquities, it is a perpetual statute throughout their generations; and in the midst of the children of Israel they shall not receive an inheritance.
24 Mʼmalo mwake, ndikuwapatsa Aleviwo chakhumi ngati cholowa chawo chimene Aisraeli amapereka kwa Yehova. Nʼchifukwa chake zokhudza iwo ndinati: ‘Sadzakhala ndi cholowa pakati pa Aisraeli.’”
Because I have given as a distinct portion to the Levites for an inheritance the tithes of the children of Israel, whatever they shall offer to the Lord; therefore I said to them, In the midst of the children of Israel they shall have no inheritance.
25 Yehova anati kwa Mose,
And the Lord spoke to Moses, saying,
26 “Yankhula ndi Alevi ndi kunena nawo kuti, ‘Pamene mulandira chakhumi kuchoka kwa Aisraeli chimene ndimakupatsani ngati cholowa chanu, muyenera kupereka chakhumi cha choperekacho kwa Yehova.
You shall also speak to the Levites, and shall say to them, If you take the tithe from the children of Israel, which I have given you from them for an inheritance, then shall you separate from it a heave-offering to the Lord, a tenth of the tenth.
27 Chopereka chanucho chidzawerengedwa kwa inu ngati tirigu wochokera kopunthira kapena ngati mphesa zopsinya kuchokera kopsinyira mphesa.
And your heave-offerings shall be reckoned to you as corn from the floor, and an offering from the wine-press.
28 Mwa njira imeneyi inunso muzipereka chopereka kwa Yehova kuchokera ku chakhumi chanu chilichonse chimene mumalandira kuchokera kwa Aisraeli. Kuchokera ku chakhumicho muziperekako gawo la Yehova kwa Aaroni, wansembe.
So shall you also separate them from all the offerings of the Lord out of all your tithes, whatever you shall receive from the children of Israel; and you shall give of them an offering to the Lord to Aaron the priest.
29 Muyenera kupereka monga gawo la Yehova magawo abwino kwambiri ndi opatulika a chilichonse chimene chapatsidwa kwa inu.’
Of all your gifts you shall offer an offering to the Lord, and of every first-fruit the consecrated part from it.
30 “Nena kwa Alevi: ‘Pamene mupereka gawo labwino lopambana zonse, gawo limenelo lidzawerengedwa kwa inu ngati lochokera popunthira tirigu kapenanso kopsinyira mphesa.
And you shall say to them, When you shall offer the first fruits from it, then shall it be reckoned to the Levites as produce from the threshing floor, and as produce from the wine-press.
31 Inu ndi a pa banja panu mungathe kudyera zimenezi paliponse chifukwa ndi malipiro a ntchito yanu ya ku tenti ya msonkhano.
And you shall eat it in any place, you and your families; for this is your reward for your services in the tabernacle of witness.
32 Popereka gawo labwino kwambirilo simudzapezeka olakwa. Mukatero simudzadetsa zopereka zoyera za Aisraeli, ndipo simudzafa.’”
And you shall not bear sin by reason of it, for you shall have offered an offering of first fruits from it, and you shall not profane the holy things of the children of Israel, that you die not.

< Numeri 18 >