< Numeri 18 >

1 Yehova anawuza Aaroni kuti, “Iwe, ana ako aamuna ndi banja la abambo ako mudzasenza tchimo la malo wopatulika, koma iwe ndi ana ako aamuna okha mudzasenza tchimo lokhudza unsembe wanu.
A protož řekl Hospodin Aronovi: Ty a synové tvoji i dům otce tvého s tebou ponesete nepravost svatyně; ty také i synové tvoji s tebou ponesete nepravost kněžství svého.
2 Ubweretse Alevi, abale ako, kuchokera ku fuko la abambo ako kuti azikhala ndi iwe ndi kumakuthandiza pamodzi ndi ana ako amuna pamene mukutumikira mu tenti ya umboni.
Bratří také své, pokolení Léví, čeled otce svého připoj k sobě, ať jsou při tobě a posluhují tobě; ty pak a synové tvoji s tebou před stánkem svědectví sloužiti budete.
3 Iwowo azikutumikirani ndipo azichita ntchito zonse za ku tenti, koma asamafike pafupi ndi zipangizo za ku malo opatulika kapena guwa lansembe, kuopa kuti iwo ndi inu mungafe.
A pilně ostříhati budou rozkázaní tvého, bedlivi jsouce při všem stánku; a však ať k nádobám svatyně a k oltáři nepřistupují, aby nezemřeli i oni i vy.
4 Azikhala ndi inu ndipo azisamalira ntchito yonse ya mu tenti ya msonkhano koma munthu wina aliyense wapadera sayenera kufika pafupi nanu.
A přídržeti se budou tebe, pilně ostříhajíce stánku úmluvy při všech službách jeho; a cizí žádný nepřistupuj k vám.
5 “Inuyo muzisamalira malo wopatulika ndi guwa lansembe, kuti ukali wa Yehova usawagwerenso Aisraeli.
Protož pilně ostříhejte svatyně i služby oltáře, ať nepřichází více zůřivá prchlivost na syny Izraelské,
6 Ine mwini ndasankha Alevi, abale ako, pakati pa Aisraeli ngati mphatso yako ndipo aperekedwa kwa Yehova kuti azigwira ntchito ku tenti ya msonkhano.
Poněvadž jsem já vybral bratří vaše Levíty z synů Izraelských vám, za dar dané Hospodinu, aby konali službu při stánku úmluvy.
7 Koma iwe wekha ndi ana ako aamuna muzitumikira ngati ansembe ndi zina zonse zokhudza pa guwa lansembe ndi za mʼkati mwa malo wopatulika kwambiri. Ndikukupatsani mphatso ya utumiki wa unsembe. Aliyense woyandikira malo wopatulika ayenera kuphedwa.
Ty pak a synové tvoji s tebou ostříhati budete kněžství svého při všech věcech přináležejících k oltáři, a kteréž jsou za oponou, a sloužiti budete. Úřad kněžství vašeho darem jsem vám dal, protož, přistoupil-li by kdo cizí, umře.
8 “Kenaka Yehova anati kwa Aaroni, ona, Ine mwini ndikukuyika kuti ukhale woyangʼanira zopereka zobwera kwa Ine; zopereka zonse zopatulika za Aisraeli zimene amapereka kwa ine ndi kuzipereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ngati gawo lanu la nthawi zonse.
Mluvil také Hospodin k Aronovi: Aj, já dal jsem tobě k ostříhání oběti své, kteréž se vzhůru pozdvihují; všecko také, což se posvěcuje od synů Izraelských, tobě jsem dal pro pomazání i synům tvým ustanovením věčným.
9 Uzilandiranso gawo la zopereka zopatulika kwambiri zomwe sizinawotchedwe pa moto. Kuchokera pa mphatso zonse zimene amabweretsa kwa Ine ngati zopatulika kwambiri, nsembe zachakudya kapena nsembe zopepesera machimo, gawo limenelo ndi lako ndi ana ako aamuna.
Toto bude tvé z věcí posvěcených, kteréž nepřicházejí na oheň: Všeliká obět jejich, buď suchá obět jejich, neb obět za hřích jejich, aneb obět za provinění jejich, kteréž mi dávati budou, svatosvaté tobě bude to i synům tvým.
10 Muzidya zimenezo ngati zinthu zopatulika kwambiri; mwamuna aliyense adyeko. Uzitenge kukhala zopatulika.
V svatyni budeš je jísti, každý pohlaví mužského bude je jísti; svaté bude tobě.
11 “Izinso ndi zako: chilichonse chopatulidwa kuchokera ku mphatso zoweyula za Aisraeli ndapereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ndi aakazi ngati gawo lako la nthawi zonse. Aliyense wa mʼnyumba mwako amene ali woyeretsedwa monga mwa mwambo angathe kudyako.
Tvá tedy bude obět darů jejich, kteráž vzhůru pozdvižena bývá; každou také obět synů Izraelských, kteráž sem i tam obracína bývá, tobě jsem dal a synům tvým, i dcerám tvým s tebou ustanovením věčným. Každý, kdož jest čistý v domě tvém, bude je jísti.
12 “Ndikukupatsani mafuta onse abwino kwambiri a olivi ndi vinyo yense watsopano wabwino kwambiri ndi tirigu yense zomwe Aisraeli amapereka kwa Yehova ngati zipatso zoyamba pa zokolola zawo.
Všecko, což předního jest z oleje, a což nejlepšího jest vína a obilé, prvotiny těch věcí, kteréž dají Hospodinu, dal jsem tobě.
13 Zipatso zonse zoyamba kucha za mʼdziko lawo zomwe amapereka kwa Yehova zidzakhala zako. Aliyense mʼnyumba mwako amene ali woyeretsedwa angathe kudyako.
Prvotiny všech věcí, kteréž rostly v zemi jejich, ty přinesou Hospodinu, a tvé budou. Každý, kdož jest čistý v domě tvém, jísti je bude.
14 “Chilichonse mu Israeli chomwe chapatulidwira Yehova ndi chako.
Všecko oddané Bohu v Izraeli tvé bude.
15 Chilichonse choyamba kubadwa kwa munthu kaya nyama, chomwe chaperekedwa kwa Yehova ndi chako. Koma uyenera kuwombola mwana aliyense wamwamuna ndi mwana aliyense woyamba wa nyama zodetsedwa.
Cožkoli otvírá život všelikého těla, kteréž obětováno bývá Hospodinu, tak z lidí jako z hovad, tvé bude; prvorozené však z lidí, vyplaceno bude, prvorozené také z nečistých hovad vyplatiti kážeš.
16 Pamene zili ndi mwezi umodzi wa kubadwa, uziwombole pa mtengo wowombolera wa ndalama zisanu zasiliva, monga mwa ndalama za ku malo wopatulika.
Výplata pak jeho, když mu již jeden měsíc bude, vedlé ceny tvé bude pěti loty stříbra podlé lotu svatyně; dvadceti peněz váží lot.
17 “Koma usawombole ana oyamba kubadwa a ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi. Iwo ndi opatulika. Uwaze magazi a nyamazi pa guwa lansembe ndi kutentha mafuta ake ngati nsembe yotentha ndi moto kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova.
Ale prvorozeného z volů, neb z ovcí, neb z koz, nedáš vyplatiti; nebo posvěceny jsou. Krev jejich vykropíš na oltář, a tuk jejich zapálíš, aby byl obětí ohnivou vůně spokojující Hospodina.
18 Nyama yake ikhale yanu monga momwe chimakhalira chidale cha nsembe yoweyula ndi ntchafu za miyendo ya kumanja, zonsezi ndi zako.
Maso pak jejich tvé bude; jako hrudí z oběti sem i tam obracení, a jako plece pravé tvé bude.
19 Zonse zimene mwazichotsa ku zopereka zoyera zomwe Aisraeli anapereka kwa Yehova ndazipereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ndi aakazi ngati gawo lanu nthawi zonse. Ili ndi pangano losatha la mchere pamaso pa Yehova kwa iwe ndi ana ako.”
Každou obět vzhůru pozdvižení z věcí posvěcených, kteréž přinášejí synové Izraelští Hospodinu, dal jsem tobě, a synům tvým, i dcerám tvým s tebou ustanovením věčným, smlouvou trvánlivou a věčnou před Hospodinem, tobě i semeni tvému s tebou.
20 Ndipo Yehova anati kwa Aaroni, “Iweyo sudzakhala ndi cholowa mʼdziko lawo, ndiponso sudzalandira gawo lililonse pakati pawo. Ine ndine gawo lako ndi cholowa chako pakati pa Aisraeli.
Mluvil také Hospodin k Aronovi: V zemi jejich, dědictví ani dílu svého mezi nimi nebudeš míti; já jsem díl tvůj, a dědictví tvé u prostřed synů Izraelských.
21 “Taonani, ndawapatsa Alevi chakhumi chonse mu Israeli ngati cholowa chawo chifukwa cha ntchito ya ku tenti ya msonkhano.
Synům pak Léví, aj, dal jsem všecky desátky v Izraeli za dědictví, za službu jejich, kterouž vykonávají, sloužíce při stánku úmluvy.
22 Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo Aisraeli asamapite pafupi ndi tenti ya msonkhano. Ngati atero adzasenza zotsatira za tchimo lawo ndipo adzafa.
A synové Izraelští nechať nepřistupují k stánku úmluvy, aby nenesli hříchu a nezemřeli.
23 Alevi ndi amene azidzagwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano ndipo adzalangidwa chilichonse chikalakwika. Ili ndi lamulo losatha kwa mibado yawo yonse. Iwowo sadzalandira cholowa pakati pa Aisraeli.
Ale sami Levítové konati budou službu při stánku úmluvy, a sami ponesou nepravost svou. Ustanovení věčné v pronárodech vašich to bude, aby dědictví nemívali mezi syny Izraelskými.
24 Mʼmalo mwake, ndikuwapatsa Aleviwo chakhumi ngati cholowa chawo chimene Aisraeli amapereka kwa Yehova. Nʼchifukwa chake zokhudza iwo ndinati: ‘Sadzakhala ndi cholowa pakati pa Aisraeli.’”
Nebo desátky synů Izraelských, kteréž přinášeti budou Hospodinu v obět vzhůru pozdvižení, dal jsem Levítům za dědictví; protož jsem o nich řekl: U prostřed synů Izraelských nebudou míti dědictví.
25 Yehova anati kwa Mose,
I mluvil Hospodin k Mojžíšovi, řka:
26 “Yankhula ndi Alevi ndi kunena nawo kuti, ‘Pamene mulandira chakhumi kuchoka kwa Aisraeli chimene ndimakupatsani ngati cholowa chanu, muyenera kupereka chakhumi cha choperekacho kwa Yehova.
Mluv k Levítům a rci jim: Když vezmete desátky od synů Izraelských, kteréž jsem vám dal od nich za dědictví vaše, tedy přinesete z nich obět vzhůru pozdvižení Hospodinu, desátky z desátků.
27 Chopereka chanucho chidzawerengedwa kwa inu ngati tirigu wochokera kopunthira kapena ngati mphesa zopsinya kuchokera kopsinyira mphesa.
A počtena vám bude ta obět vaše jako obilí z humna, a jako víno od presu.
28 Mwa njira imeneyi inunso muzipereka chopereka kwa Yehova kuchokera ku chakhumi chanu chilichonse chimene mumalandira kuchokera kwa Aisraeli. Kuchokera ku chakhumicho muziperekako gawo la Yehova kwa Aaroni, wansembe.
Tak vy také přinesete obět vzhůru pozdvižení Hospodinu ze všech desátků svých, kteréž vezmete od synů Izraelských, a dáte z nich obět Hospodinovu Aronovi knězi.
29 Muyenera kupereka monga gawo la Yehova magawo abwino kwambiri ndi opatulika a chilichonse chimene chapatsidwa kwa inu.’
Ze všech darů svých přinesete každou obět vzhůru pozdvižení Hospodinu, díl posvěcený všeho, což nejlepšího jest.
30 “Nena kwa Alevi: ‘Pamene mupereka gawo labwino lopambana zonse, gawo limenelo lidzawerengedwa kwa inu ngati lochokera popunthira tirigu kapenanso kopsinyira mphesa.
Díš jim také: Když obětovati budete z toho, což nejlepšího jest, počteno bude Levítům jako úrody z humna, a jako úrody od presu.
31 Inu ndi a pa banja panu mungathe kudyera zimenezi paliponse chifukwa ndi malipiro a ntchito yanu ya ku tenti ya msonkhano.
Jísti pak budete ty desátky na všelikém místě vy i čeled vaše; nebo mzda vaše jest za službu vaši při stánku úmluvy.
32 Popereka gawo labwino kwambirilo simudzapezeka olakwa. Mukatero simudzadetsa zopereka zoyera za Aisraeli, ndipo simudzafa.’”
A neponesete pro to hříchu, když obětovati budete to, což nejlepšího jest; a tak nepoškvrníte věcí posvěcených od synů Izraelských, a nezemřete.

< Numeri 18 >