< Numeri 18 >
1 Yehova anawuza Aaroni kuti, “Iwe, ana ako aamuna ndi banja la abambo ako mudzasenza tchimo la malo wopatulika, koma iwe ndi ana ako aamuna okha mudzasenza tchimo lokhudza unsembe wanu.
Tada Jahve reče Aronu: “Ti, tvoji sinovi i tvoj pradjedovski dom s tobom bit ćete odgovorni za grijehe u Svetištu; ti i tvoji sinovi s tobom bit ćete odgovorni za grijehe svoga svećeništva.
2 Ubweretse Alevi, abale ako, kuchokera ku fuko la abambo ako kuti azikhala ndi iwe ndi kumakuthandiza pamodzi ndi ana ako amuna pamene mukutumikira mu tenti ya umboni.
Pridruži k sebi i svoju braću od Levijeva plemena - tvoga pradjedovskog doma - neka ti se priključe da ti poslužuju, tebi i tvojim sinovima s tobom, pred Šatorom svjedočanstva.
3 Iwowo azikutumikirani ndipo azichita ntchito zonse za ku tenti, koma asamafike pafupi ndi zipangizo za ku malo opatulika kapena guwa lansembe, kuopa kuti iwo ndi inu mungafe.
Neka stoje na službu tebi i svemu Šatoru, ali neka se ne približuju pokućstvu u Svetištu niti žrtveniku, da ne poginu i oni i vi.
4 Azikhala ndi inu ndipo azisamalira ntchito yonse ya mu tenti ya msonkhano koma munthu wina aliyense wapadera sayenera kufika pafupi nanu.
Neka su, dakle, tebi pridruženi i neka preuzmu brigu za Šator sastanka, svaku službu oko Šatora. I neka se ni jedan svjetovnjak ne približuje vama,
5 “Inuyo muzisamalira malo wopatulika ndi guwa lansembe, kuti ukali wa Yehova usawagwerenso Aisraeli.
a vi vršite službu u Svetištu i službu oko žrtvenika da se više ne izlijeva gnjev na Izraelce.
6 Ine mwini ndasankha Alevi, abale ako, pakati pa Aisraeli ngati mphatso yako ndipo aperekedwa kwa Yehova kuti azigwira ntchito ku tenti ya msonkhano.
Uzeh, evo, vašu braću levite između Izraelaca vama za dar; kao darovani pripadaju Jahvi da obavljaju službu oko Šatora sastanka.
7 Koma iwe wekha ndi ana ako aamuna muzitumikira ngati ansembe ndi zina zonse zokhudza pa guwa lansembe ndi za mʼkati mwa malo wopatulika kwambiri. Ndikukupatsani mphatso ya utumiki wa unsembe. Aliyense woyandikira malo wopatulika ayenera kuphedwa.
Ti i tvoji sinovi s tobom preuzmite svećeničke poslove oko svega što spada na žrtvenik i iza zavjese. Službu koju dajem na dar vašem svećeništvu vi obavljajte. A svjetovnjak koji se primakne neka se pogubi.”
8 “Kenaka Yehova anati kwa Aaroni, ona, Ine mwini ndikukuyika kuti ukhale woyangʼanira zopereka zobwera kwa Ine; zopereka zonse zopatulika za Aisraeli zimene amapereka kwa ine ndi kuzipereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ngati gawo lanu la nthawi zonse.
Još reče Jahve Aronu: “Tebi, evo, povjeravam brigu o onom što se meni prinosi. Sve što Izraelci posvećuju dodjeljujem tebi i tvojim sinovima kao baštinu trajnim zakonom.
9 Uzilandiranso gawo la zopereka zopatulika kwambiri zomwe sizinawotchedwe pa moto. Kuchokera pa mphatso zonse zimene amabweretsa kwa Ine ngati zopatulika kwambiri, nsembe zachakudya kapena nsembe zopepesera machimo, gawo limenelo ndi lako ndi ana ako aamuna.
Ovo neka pripadne tebi od svetinja nad svetinjama: od paljenih žrtava svi njihovi darovi, za sve njihove prinosnice, za sve njihove okajnice i za sve njihove naknadnice što ih budu meni uzvraćali; ta vrlo sveta stvar neka pripadne tebi i tvojim sinovima!
10 Muzidya zimenezo ngati zinthu zopatulika kwambiri; mwamuna aliyense adyeko. Uzitenge kukhala zopatulika.
Blagujte ih kao najveće svetinje! Svaki muškarac može ih jesti. Neka ti budu svete!
11 “Izinso ndi zako: chilichonse chopatulidwa kuchokera ku mphatso zoweyula za Aisraeli ndapereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ndi aakazi ngati gawo lako la nthawi zonse. Aliyense wa mʼnyumba mwako amene ali woyeretsedwa monga mwa mwambo angathe kudyako.
I ovo neka bude za te: ono što se uzima od izraelskih prinosa da se prinese kao prikaznica - trajnim zakonom predajem tebi, tvojim sinovima i tvojim kćerima s tobom. Svatko tko u tvome domu bude čist može od toga jesti.
12 “Ndikukupatsani mafuta onse abwino kwambiri a olivi ndi vinyo yense watsopano wabwino kwambiri ndi tirigu yense zomwe Aisraeli amapereka kwa Yehova ngati zipatso zoyamba pa zokolola zawo.
Najbolje od novoga ulja i najbolje od novoga vina i žita - prvine koje se prinose Jahvi - predajem tebi.
13 Zipatso zonse zoyamba kucha za mʼdziko lawo zomwe amapereka kwa Yehova zidzakhala zako. Aliyense mʼnyumba mwako amene ali woyeretsedwa angathe kudyako.
Prvi rodovi svega u njihovoj zemlji što ih budu donosili Jahvi neka budu tvoji. Tko je god čist u tvome domu može ih jesti.
14 “Chilichonse mu Israeli chomwe chapatulidwira Yehova ndi chako.
Sve što u Izraelu bude određeno za 'herem' neka je tvoje.
15 Chilichonse choyamba kubadwa kwa munthu kaya nyama, chomwe chaperekedwa kwa Yehova ndi chako. Koma uyenera kuwombola mwana aliyense wamwamuna ndi mwana aliyense woyamba wa nyama zodetsedwa.
Svako prvorođenče svih bića - kako ljudi tako i životinja - što se prinose Jahvi neka bude tvoje. Samo pusti da se otkupi prvenac od ljudi i prvenče od nečiste stoke.
16 Pamene zili ndi mwezi umodzi wa kubadwa, uziwombole pa mtengo wowombolera wa ndalama zisanu zasiliva, monga mwa ndalama za ku malo wopatulika.
Kad budu stari mjesec dana, pusti da ih otkupljuju. A njihovu otkupnu cijenu odredi: pet srebrnih šekela, prema hramskom šekelu, a to je dvadeset gera.
17 “Koma usawombole ana oyamba kubadwa a ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi. Iwo ndi opatulika. Uwaze magazi a nyamazi pa guwa lansembe ndi kutentha mafuta ake ngati nsembe yotentha ndi moto kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova.
Ali prvenče kravlje, prvenče ovčje i prvenče kozje neka se ne otkupljuje. Oni su svetinja. Krv njihovu izlij na žrtvenik, a pretilinu njihovu sažeži u kad kao žrtvu spaljenu na ugodan miris Jahvi.
18 Nyama yake ikhale yanu monga momwe chimakhalira chidale cha nsembe yoweyula ndi ntchafu za miyendo ya kumanja, zonsezi ndi zako.
Njihovo meso neka pripadne tebi; kao i grudi žrtve prikaznice i desno pleće.
19 Zonse zimene mwazichotsa ku zopereka zoyera zomwe Aisraeli anapereka kwa Yehova ndazipereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ndi aakazi ngati gawo lanu nthawi zonse. Ili ndi pangano losatha la mchere pamaso pa Yehova kwa iwe ndi ana ako.”
Sve posvećene prinose što ih Izraelci podižu Jahvi predajem trajnim zakonom tebi, tvojim sinovima i tvojim kćerima s tobom. To je savez osoljen, trajan pred Jahvom, tebi i tvome potomstvu s tobom.”
20 Ndipo Yehova anati kwa Aaroni, “Iweyo sudzakhala ndi cholowa mʼdziko lawo, ndiponso sudzalandira gawo lililonse pakati pawo. Ine ndine gawo lako ndi cholowa chako pakati pa Aisraeli.
“Nemoj imati baštine u zemlji njihovoj”, reče Jahve Aronu, “niti sebi stječi posjeda među njima! Ja sam tvoj dio i tvoja baština među Izraelcima.”
21 “Taonani, ndawapatsa Alevi chakhumi chonse mu Israeli ngati cholowa chawo chifukwa cha ntchito ya ku tenti ya msonkhano.
“Levijevim sinovima, evo, predajem u baštinu sve desetine u Izraelu za njihovu službu - za službu što je obavljaju u Šatoru sastanka.
22 Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo Aisraeli asamapite pafupi ndi tenti ya msonkhano. Ngati atero adzasenza zotsatira za tchimo lawo ndipo adzafa.
A Izraelci neka se više ne primiču Šatoru sastanka, da ne navuku na se grijeh i ne poginu.
23 Alevi ndi amene azidzagwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano ndipo adzalangidwa chilichonse chikalakwika. Ili ndi lamulo losatha kwa mibado yawo yonse. Iwowo sadzalandira cholowa pakati pa Aisraeli.
Neka samo leviti obavljaju službu u Šatoru sastanka; i neka oni budu odgovorni za svoj grijeh. Trajna je to odredba za vaše naraštaje; među Izraelcima neka nemaju posjeda,
24 Mʼmalo mwake, ndikuwapatsa Aleviwo chakhumi ngati cholowa chawo chimene Aisraeli amapereka kwa Yehova. Nʼchifukwa chake zokhudza iwo ndinati: ‘Sadzakhala ndi cholowa pakati pa Aisraeli.’”
jer ja im predajem u posjed desetine što ih Izraelci prinose na dar Jahvi. Stoga sam za njih rekao: neka oni nemaju posjeda među Izraelcima.”
25 Yehova anati kwa Mose,
Jahve reče Mojsiju:
26 “Yankhula ndi Alevi ndi kunena nawo kuti, ‘Pamene mulandira chakhumi kuchoka kwa Aisraeli chimene ndimakupatsani ngati cholowa chanu, muyenera kupereka chakhumi cha choperekacho kwa Yehova.
“Levitima govori i reci im: 'Kad od Izraelaca primate desetinu, koju ja od njih dajem vama u baštinu, od toga onda vi prinesite podizanicu Jahvi: desetinu od desetine.
27 Chopereka chanucho chidzawerengedwa kwa inu ngati tirigu wochokera kopunthira kapena ngati mphesa zopsinya kuchokera kopsinyira mphesa.
Prinos će vam biti zaračunan kao da je prinos s gumna i Óotoka iz badnja.
28 Mwa njira imeneyi inunso muzipereka chopereka kwa Yehova kuchokera ku chakhumi chanu chilichonse chimene mumalandira kuchokera kwa Aisraeli. Kuchokera ku chakhumicho muziperekako gawo la Yehova kwa Aaroni, wansembe.
Tako isto prinosite podizanicu Jahvi i od svih svojih desetina što ih primate od Izraelaca. Od toga davajte podizanicu Jahvinu svećeniku Aronu.
29 Muyenera kupereka monga gawo la Yehova magawo abwino kwambiri ndi opatulika a chilichonse chimene chapatsidwa kwa inu.’
Od svih darova koje budete primali podižite podizanicu Jahvi; od svega ono najbolje - onaj dio koji treba posvećivati.'
30 “Nena kwa Alevi: ‘Pamene mupereka gawo labwino lopambana zonse, gawo limenelo lidzawerengedwa kwa inu ngati lochokera popunthira tirigu kapenanso kopsinyira mphesa.
Još im reci: 'Pošto od toga prinesete najbolji dio, neka se to levitima uračuna kao prihod s gumna i prihod iz badnja.
31 Inu ndi a pa banja panu mungathe kudyera zimenezi paliponse chifukwa ndi malipiro a ntchito yanu ya ku tenti ya msonkhano.
Na svakome ga mjestu možete jesti, i vi i vaši ukućani, jer to vam je nagrada za vašu službu u Šatoru sastanka.
32 Popereka gawo labwino kwambirilo simudzapezeka olakwa. Mukatero simudzadetsa zopereka zoyera za Aisraeli, ndipo simudzafa.’”
Pošto prinesete njegov najbolji dio, nećete navući na se grijeha; svetinja Izraelaca nećete oskvrnjivati te nećete ginuti.'”