< Numeri 17 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
Le Seigneur parla encore à Moïse, disant:
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo akupatse ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse. Ulembe dzina la munthu aliyense pa ndodo yake.
Parle aux enfants d’Israël, et prends d’eux des verges, une à une, selon leur parenté, de tous les princes des tribus, douze verges; et tu écriras le nom de chacun d’eux sur sa verge:
3 Pa ndodo ya Levi ulembepo dzina la Aaroni, chifukwa pafunika ndodo imodzi ya mtsogoleri pa fuko lililonse.
Mais le nom d’Aaron sera dans la tribu de Lévi, et chaque verge contiendra séparément toutes les familles;
4 Uyike ndodozo mu tenti ya msonkhano, kutsogolo kwa Bokosi la Umboni, kumene ndimakumana nawe.
Tu les déposeras dans le tabernacle d’alliance, devant le témoignage, où je te parlerai.
5 Ndodo ya munthu amene ndamusankha idzachita maluwa potero ndidzaletsa madandawulo osatha a Aisraeli otsutsana nawe.”
Celui d’entre eux que j’aurai choisi, c’est celui dont la verge fleurira: j’arrêterai ainsi les plaintes des enfants d’Israël qui les font murmurer contre vous.
6 Choncho Mose anayankhula ndi Aisraeli, ndipo atsogoleri awo anapereka ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse ndipo ndodo ya Aaroni inali pakati pa ndodo zawozo.
Et Moïse parla aux enfants d’Israël; et tous les princes lui donnèrent des verges, une par chaque tribu: ainsi il y eut douze verges sans la verge d’Aaron.
7 Mose anayika ndodozo pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano.
Moïse les ayant déposées devant le Seigneur, dans le tabernacle du témoignage,
8 Pa tsiku lotsatira Mose analowa mu tenti ya msonkhanoyo ndipo anaona kuti ndodo ya Aaroni, yomwe inkayimira fuko la Levi, sinangophuka masamba chabe, komanso inachita maluwa nʼkubala zipatso za alimondi.
Et, le Jour suivant, étant revenu, il trouva que la verge d’Aaron dans la famille de Lévi avait germé, et que des bourgeons s’étant développés, il était sorti des fleurs, qui, des feuilles s’étant ouvertes, s’étaient formées en amandes.
9 Choncho Mose anatulutsa ndodo zonse pamaso pa Yehova napita nazo kwa Aisraeli onse. Iwowo anaziona ndipo munthu aliyense anatenga ndodo yake.
Moïse donc porta les verges de la présence du Seigneur à tous les enfants d’Israël; ils virent et reçurent chacun leur verge.
10 Yehova anawuza Mose kuti, “Bwezera ndodo ya Aaroni patsogolo pa Bokosi la Umboni, kuti chikhale chizindikiro cha kuwukira kwawo. Zimenezi zidzathetsa kudandaula kwawo kotsutsana nane, kuopa kuti angafe.”
Or, le Seigneur dit à Moïse: Reporte la verge d’Aaron dans le tabernacle du témoignage, afin qu’elle y soit gardée comme un signe de la rébellion des enfants d’Israël, et que leurs plaintes se taisent devant moi, pour ne pas qu’ils meurent.
11 Mose anachita monga Yehova anamulamulira.
Et Moïse fit, comme avait ordonné le Seigneur.
12 Aisraeli anati kwa Mose, “Tikufa! Tatayika, tonse tatayika!
Mais les enfants d’Israël dirent à Moïse: Voici que nous sommes consumés et que tous nous périssons.
13 Aliyense woyandikira chihema adzafa. Kodi ndiye kuti tonse tikufa?”
Quiconque approche du tabernacle du Seigneur, meurt; est-ce jusqu’à une entière extermination, que nous devons être détruits?