< Numeri 17 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
L’Éternel parla ainsi à Moïse:
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo akupatse ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse. Ulembe dzina la munthu aliyense pa ndodo yake.
"Annonce aux enfants d’Israël que tu dois recevoir d’eux une verge respectivement par famille paternelle, de la part de tous leurs chefs de familles paternelles, ensemble douze verges; le nom de chacun, tu l’écriras sur sa verge.
3 Pa ndodo ya Levi ulembepo dzina la Aaroni, chifukwa pafunika ndodo imodzi ya mtsogoleri pa fuko lililonse.
Et le nom d’Aaron, tu l’écriras sur la verge de Lévi, car il faut une seule verge par chef de famille paternelle.
4 Uyike ndodozo mu tenti ya msonkhano, kutsogolo kwa Bokosi la Umboni, kumene ndimakumana nawe.
Tu les déposeras dans la tente d’assignation, devant le statut où je vous donne habituellement rendez-vous.
5 Ndodo ya munthu amene ndamusankha idzachita maluwa potero ndidzaletsa madandawulo osatha a Aisraeli otsutsana nawe.”
Or, l’homme que j’aurai élu, sa verge fleurira, et ainsi mettrai-je fin à ces murmures contre moi, que les enfants d’Israël profèrent à cause de vous."
6 Choncho Mose anayankhula ndi Aisraeli, ndipo atsogoleri awo anapereka ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse ndipo ndodo ya Aaroni inali pakati pa ndodo zawozo.
Moïse parla aux enfants d’Israël; et tous leurs phylarques lui remirent chacun une verge, selon leurs familles paternelles, ensemble douze verges; et la verge d’Aaron fut jointe aux leurs.
7 Mose anayika ndodozo pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano.
Moïse déposa ces verges devant le Seigneur, dans la tente du statut.
8 Pa tsiku lotsatira Mose analowa mu tenti ya msonkhanoyo ndipo anaona kuti ndodo ya Aaroni, yomwe inkayimira fuko la Levi, sinangophuka masamba chabe, komanso inachita maluwa nʼkubala zipatso za alimondi.
Or, le lendemain, Moïse entra dans la tente du statut, et voici qu’avait fleuri la verge d’Aaron, déposée pour la famille de Lévi: il y avait germé des boutons, éclos des fleurs, mûri des amandes.
9 Choncho Mose anatulutsa ndodo zonse pamaso pa Yehova napita nazo kwa Aisraeli onse. Iwowo anaziona ndipo munthu aliyense anatenga ndodo yake.
Moïse retira toutes les verges de devant le Seigneur et les exposa devant les enfants d’Israël: ils les regardèrent, et reprirent chacun la sienne.
10 Yehova anawuza Mose kuti, “Bwezera ndodo ya Aaroni patsogolo pa Bokosi la Umboni, kuti chikhale chizindikiro cha kuwukira kwawo. Zimenezi zidzathetsa kudandaula kwawo kotsutsana nane, kuopa kuti angafe.”
Et l’Éternel dit à Moïse: "Replace la verge d’Aaron devant le statut, comme signe durable à l’encontre des rebelles; tu feras cesser par là leurs murmures contre moi, et ils ne mourront point."
11 Mose anachita monga Yehova anamulamulira.
Moïse obéit: comme l’Éternel lui avait ordonné, ainsi fit-il.
12 Aisraeli anati kwa Mose, “Tikufa! Tatayika, tonse tatayika!
Les enfants d’Israël parlèrent ainsi à Moïse: "Certes, c’est fait de nous, nous sommes perdus, tous perdus!
13 Aliyense woyandikira chihema adzafa. Kodi ndiye kuti tonse tikufa?”
Quiconque s’approche tant soit peu de la résidence du Seigneur est frappé de mort: sommes-nous donc tous destinés à périr?"

< Numeri 17 >