< Numeri 17 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the LORD spoke to Moses, saying,
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo akupatse ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse. Ulembe dzina la munthu aliyense pa ndodo yake.
Speak to the children of Israel, and take of every one of them a rod according to the house of their fathers, of all their princes according to the house of their fathers twelve rods: write thou every man’s name upon his rod.
3 Pa ndodo ya Levi ulembepo dzina la Aaroni, chifukwa pafunika ndodo imodzi ya mtsogoleri pa fuko lililonse.
And thou shalt write Aaron’s name upon the rod of Levi: for one rod shall be for the head of the house of their fathers.
4 Uyike ndodozo mu tenti ya msonkhano, kutsogolo kwa Bokosi la Umboni, kumene ndimakumana nawe.
And thou shalt lay them in the tabernacle of the congregation before the testimony, where I will meet with you.
5 Ndodo ya munthu amene ndamusankha idzachita maluwa potero ndidzaletsa madandawulo osatha a Aisraeli otsutsana nawe.”
And it shall come to pass, that the man’s rod, whom I shall choose, shall blossom: and I will make to cease from me the murmurings of the children of Israel, by which they murmur against you.
6 Choncho Mose anayankhula ndi Aisraeli, ndipo atsogoleri awo anapereka ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse ndipo ndodo ya Aaroni inali pakati pa ndodo zawozo.
And Moses spoke to the children of Israel, and every one of their princes gave him a rod apiece, for each prince one, according to their fathers’ houses, even twelve rods: and the rod of Aaron was among their rods.
7 Mose anayika ndodozo pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano.
And Moses laid the rods before the LORD in the tabernacle of witness.
8 Pa tsiku lotsatira Mose analowa mu tenti ya msonkhanoyo ndipo anaona kuti ndodo ya Aaroni, yomwe inkayimira fuko la Levi, sinangophuka masamba chabe, komanso inachita maluwa nʼkubala zipatso za alimondi.
And it came to pass, that on the next day Moses went into the tabernacle of witness; and, behold, the rod of Aaron for the house of Levi had budded, and brought forth buds, and bloomed blossoms, and yielded almonds.
9 Choncho Mose anatulutsa ndodo zonse pamaso pa Yehova napita nazo kwa Aisraeli onse. Iwowo anaziona ndipo munthu aliyense anatenga ndodo yake.
And Moses brought out all the rods from before the LORD to all the children of Israel: and they looked, and took every man his rod.
10 Yehova anawuza Mose kuti, “Bwezera ndodo ya Aaroni patsogolo pa Bokosi la Umboni, kuti chikhale chizindikiro cha kuwukira kwawo. Zimenezi zidzathetsa kudandaula kwawo kotsutsana nane, kuopa kuti angafe.”
And the LORD said to Moses, Bring Aaron’s rod again before the testimony, to be kept for a sign against the rebels; and thou shalt quite take away their murmurings from me, that they die not.
11 Mose anachita monga Yehova anamulamulira.
And Moses did so: as the LORD commanded him, so did he.
12 Aisraeli anati kwa Mose, “Tikufa! Tatayika, tonse tatayika!
And the children of Israel spoke to Moses, saying, Behold, we die, we perish, we all perish.
13 Aliyense woyandikira chihema adzafa. Kodi ndiye kuti tonse tikufa?”
Whoever approacheth the tabernacle of the LORD shall die: shall we be consumed with dying?

< Numeri 17 >