< Numeri 17 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the LORD spake unto Moses, saying,
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo akupatse ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse. Ulembe dzina la munthu aliyense pa ndodo yake.
Speak unto the children of Israel, and take of them rods, one for each fathers’ house, of all their princes according to their fathers’ houses, twelve rods: write thou every man’s name upon his rod.
3 Pa ndodo ya Levi ulembepo dzina la Aaroni, chifukwa pafunika ndodo imodzi ya mtsogoleri pa fuko lililonse.
And thou shalt write Aaron’s name upon the rod of Levi: for there shall be one rod for each head of their fathers’ houses.
4 Uyike ndodozo mu tenti ya msonkhano, kutsogolo kwa Bokosi la Umboni, kumene ndimakumana nawe.
And thou shalt lay them up in the tent of meeting before the testimony, where I meet with you.
5 Ndodo ya munthu amene ndamusankha idzachita maluwa potero ndidzaletsa madandawulo osatha a Aisraeli otsutsana nawe.”
And it shall come to pass, that the man whom I shall choose, his rod shall bud: and I will make to cease from me the murmurings of the children of Israel, which they murmur against you.
6 Choncho Mose anayankhula ndi Aisraeli, ndipo atsogoleri awo anapereka ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse ndipo ndodo ya Aaroni inali pakati pa ndodo zawozo.
And Moses spake unto the children of Israel, and all their princes gave him rods, for each prince one, according to their fathers’ houses, even twelve rods: and the rod of Aaron was among their rods.
7 Mose anayika ndodozo pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano.
And Moses laid up the rods before the LORD in the tent of the testimony.
8 Pa tsiku lotsatira Mose analowa mu tenti ya msonkhanoyo ndipo anaona kuti ndodo ya Aaroni, yomwe inkayimira fuko la Levi, sinangophuka masamba chabe, komanso inachita maluwa nʼkubala zipatso za alimondi.
And it came to pass on the morrow, that Moses went into the tent of the testimony; and, behold, the rod of Aaron for the house of Levi was budded, and put forth buds, and bloomed blossoms, and bare ripe almonds.
9 Choncho Mose anatulutsa ndodo zonse pamaso pa Yehova napita nazo kwa Aisraeli onse. Iwowo anaziona ndipo munthu aliyense anatenga ndodo yake.
And Moses brought out all the rods from before the LORD unto all the children of Israel: and they looked, and took every man his rod.
10 Yehova anawuza Mose kuti, “Bwezera ndodo ya Aaroni patsogolo pa Bokosi la Umboni, kuti chikhale chizindikiro cha kuwukira kwawo. Zimenezi zidzathetsa kudandaula kwawo kotsutsana nane, kuopa kuti angafe.”
And the LORD said unto Moses, Put back the rod of Aaron before the testimony, to be kept for a token against the children of rebellion; that thou mayest make an end of their murmurings against me, that they die not.
11 Mose anachita monga Yehova anamulamulira.
Thus did Moses: as the LORD commanded him, so did he.
12 Aisraeli anati kwa Mose, “Tikufa! Tatayika, tonse tatayika!
And the children of Israel spake unto Moses, saying, Behold, we perish, we are undone, we are all undone.
13 Aliyense woyandikira chihema adzafa. Kodi ndiye kuti tonse tikufa?”
Every one that cometh near, that cometh near unto the tabernacle of the LORD, dieth: shall we perish all of us?