< Numeri 17 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke unto Moses, saying,
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo akupatse ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse. Ulembe dzina la munthu aliyense pa ndodo yake.
Speak unto the children of Israel, and take from them one staff each for a family division, from all their princes, according to their family divisions, twelve staves: the name of each man shalt thou write upon his staff.
3 Pa ndodo ya Levi ulembepo dzina la Aaroni, chifukwa pafunika ndodo imodzi ya mtsogoleri pa fuko lililonse.
And the name of Aaron shalt thou write upon the staff of Levi; for there shall be but one staff for the head of their family division.
4 Uyike ndodozo mu tenti ya msonkhano, kutsogolo kwa Bokosi la Umboni, kumene ndimakumana nawe.
And thou shalt lay them down in the tabernacle of the congregation before the testimony, where I usually meet with you.
5 Ndodo ya munthu amene ndamusankha idzachita maluwa potero ndidzaletsa madandawulo osatha a Aisraeli otsutsana nawe.”
And it shall come to pass, that the staff of the man whom I shall choose, shall blossom: and I will allay from around me the murmurings of the children of Israel, which they murmur against you.
6 Choncho Mose anayankhula ndi Aisraeli, ndipo atsogoleri awo anapereka ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse ndipo ndodo ya Aaroni inali pakati pa ndodo zawozo.
And Moses spoke unto the children of Israel, and all their princes gave him each a staff, one for every prince, according to their family divisions, twelve staves: and the staff of Aaron was among their staves.
7 Mose anayika ndodozo pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano.
And Moses laid down the staves before the Lord in the tabernacle of the testimony.
8 Pa tsiku lotsatira Mose analowa mu tenti ya msonkhanoyo ndipo anaona kuti ndodo ya Aaroni, yomwe inkayimira fuko la Levi, sinangophuka masamba chabe, komanso inachita maluwa nʼkubala zipatso za alimondi.
And it came to pass on the morrow, that as Moses went into the tabernacle of the testimony, behold, the staff of Aaron for the house of Levi had budded; and it brought forth buds, and produced blossoms, and yielded ripe almonds.
9 Choncho Mose anatulutsa ndodo zonse pamaso pa Yehova napita nazo kwa Aisraeli onse. Iwowo anaziona ndipo munthu aliyense anatenga ndodo yake.
And Moses brought out all the staves from before the Lord unto all the children of Israel; and they looked [at them], and took away every one his staff.
10 Yehova anawuza Mose kuti, “Bwezera ndodo ya Aaroni patsogolo pa Bokosi la Umboni, kuti chikhale chizindikiro cha kuwukira kwawo. Zimenezi zidzathetsa kudandaula kwawo kotsutsana nane, kuopa kuti angafe.”
And the Lord said unto Moses, Carry back the staff of Aaron before the testimony, to be kept as a token against the children of rebellion, that there may be an end of their murmurings from around me, and they die not.
11 Mose anachita monga Yehova anamulamulira.
And Moses did so; as the Lord had commanded him, so did he.
12 Aisraeli anati kwa Mose, “Tikufa! Tatayika, tonse tatayika!
And the children of Israel said unto Moses, thus, Behold, we perish, we are lost, we are all lost.
13 Aliyense woyandikira chihema adzafa. Kodi ndiye kuti tonse tikufa?”
Every one that cometh near at all unto the tabernacle of the Lord must die: shall we totally perish?

< Numeri 17 >