< Numeri 16 >

1 Kora mwana wa Izihari, mwana wa Kohati, mwana wa Levi ndi Datani ndi Abiramu ana a Eliabu, pamodzi ndi Oni mwana wa Perezi, ana a Rubeni, anayamba kudzikuza,
و قورح بن یصهار بن قهات بن لاوی وداتان و ابیرام پسران الیاب و اون بن فالت پسران روبین (کسان ) گرفته،۱
2 ndipo anawukira Mose. Mʼgulu mwawo munali atsogoleri a Aisraeli 250, anthu otchuka amene anasankhidwa ndi anthu pa msonkhano.
با بعضی ازبنی‌اسرائیل، یعنی دویست و پنجاه نفر ازسروران جماعت که برگزیدگان شورا و مردان معروف بودند، به حضور موسی برخاستند.۲
3 Iwo anasonkhana kudzatsutsana ndi Mose ndi Aaroni nawawuza kuti, “Mwawonjeza! Anthu onsewa ndi oyera, aliyense wa iwo, ndipo Yehova ali pakati pawo. Chifukwa chiyani mukudzikuza pakati pa gulu lonse la Yehova?”
و به مقابل موسی و هارون جمع شده، به ایشان گفتند: «شما از حد خود تجاوز می‌نمایید، زیرا تمامی جماعت هریک از ایشان مقدس‌اند، و خداوند درمیان ایشان است. پس چرا خویشتن را بر جماعت خداوند برمی افرازید؟»۳
4 Mose atamva izi, anagwa chafufumimba.
و چون موسی این راشنید به روی خود درافتاد.۴
5 Ndipo iye anawuza Kora ndi anthu onse amene ankamutsatira kuti, “Yehova mawa mmawa adzasonyeza yemwe ndi wake ndiponso amene ndi woyera mtima. Munthuyo adzabwera pafupi ndi Iye. Munthu amene adzamusankheyo adzamusendeza pafupi.
و قورح و تمامی جمعیت او را خطاب کرده، گفت: «بامدادان خداوند نشان خواهد داد که چه کس از آن وی وچه کس مقدس است، و او را نزد خود خواهدآورد، و هرکه را برای خود برگزیده است، او رانزد خود خواهد آورد.۵
6 Iwe Kora pamodzi ndi onse amene akukutsatira chitani izi: Tengani zofukizira
این را بکنید که مجمرهابرای خود بگیرید، ای قورح و تمامی جمعیت تو.۶
7 ndipo mawa muyikemo moto ndi lubani pamaso pa Yehova. Munthu amene Yehova amusankhe ndiye amene ali woyera. Alevi inu mwawonjeza kwambiri!”
و آتش در آنها گذارده، فردا به حضورخداوند بخور در آنها بریزید، و آن کس که خداوند برگزیده است، مقدس خواهد شد. ای پسران لاوی شما از حد خود تجاوز می‌نمایید!»۷
8 Mose anawuzanso Kora kuti, “Inu Alevi, tsopano tamverani!
و موسی به قورح گفت: «ای بنی لاوی بشنوید!۸
9 Kodi sizinakukwanireni kuti Mulungu wa Israeli anakupatulani pakati pa gulu lonse la Aisraeli ndi kukubweretsani pafupi ndi Iye, kuti muzigwira ntchito ku nyumba ya Yehova ndi kumayima pamaso pa gulu, kumatumikira?
آیا نزد شما کم است که خدای اسرائیل شما رااز جماعت اسرائیل ممتاز کرده است، تا شما رانزد خود بیاورد تا در مسکن خداوندخدمت نمایید، و به حضور جماعت برای خدمت ایشان بایستید؟۹
10 Wakubweretsa iwe pamodzi ndi Alevi anzako kufupi ndi Iye mwini. Koma tsopano ukufuna kutenganso unsembe.
و تو را و جمیع برادرانت بنی لاوی رابا تو نزدیک آورد، و آیا کهانت را نیز می‌طلبید؟۱۰
11 Nʼkulakwira Yehova kuti iwe ndi gulu lako lonseli mwasonkhana kuti mutsutsane ndi Yehova. Kodi Aaroni ndani kuti muzikangana naye?”
از این جهت تو و تمامی جمعیت تو به ضدخداوند جمع شده‌اید، و اما هارون چیست که براو همهمه می‌کنید؟»۱۱
12 Kenaka Mose anayitana Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu koma iwo anati, “Sitibwera!
و موسی فرستاد تا داتان و ابیرام پسران الیاب را بخواند، و ایشان گفتند: «نمی آییم!۱۲
13 Kodi sikukwanira kuti unatitulutsa, kutichotsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kuti udzatiphe mʼchipululu muno? Kodi tsopano ukufunanso kutilemetsa?
آیاکم است که ما را از زمینی که به شیر و شهد جاری است، بیرون آوردی تا ما را در صحرا نیز هلاک سازی که می‌خواهی خود را بر ما حکمران سازی؟۱۳
14 Kuwonjezera apo, sunatilowetse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kapena kutipatsa malo wolima ndi minda ya mpesa. Kodi ukufuna kuchotsa maso a anthuwa? Ayi, sitibwera!”
و ما را هم به زمینی که به شیر و شهدجاری است درنیاوردی و ملکیتی از مزرعه‌ها وتاکستانها به ما ندادی. آیا چشمان این مردمان رامی کنی؟ نخواهیم آمد!»۱۴
15 Pamenepo Mose anakwiya kwambiri ndipo anati kwa Yehova, “Musalandire chopereka chawo. Sindinatenge kalikonse kwa iwo ngakhale bulu, ndiponso sindinalakwire wina aliyense wa iwo.”
و موسی بسیار خشمناک شده، به خداوندگفت: «هدیه ایشان را منظور منما، یک خر ازایشان نگرفتم، و به یکی از ایشان زیان نرساندم.»۱۵
16 Mose anati kwa Kora, “Iwe ndi okutsatira onse mudzaonekere pamaso pa Yehova mawa, iweyo ndi iwowo pamodzi ndi Aaroni.
و موسی به قورح گفت: «تو با تمامی جمعیت خود فردا به حضور خداوند حاضر شوید، تو وایشان و هارون.۱۶
17 Munthu aliyense akatenge chofukizira ndi kuyikamo lubani, zofukizira 250 zonse pamodzi ndi kuzibweretsa pamaso pa Yehova. Iwe ndi Aaroni mudzabweretsenso zofukizira zanu.”
و هر کس مجمر خود راگرفته، بخور بر آنها بگذارد و شما هر کس مجمرخود، یعنی دویست و پنجاه مجمر به حضورخداوند بیاورید، تو نیز و هارون هر یک مجمرخود را بیاورید.»۱۷
18 Choncho munthu aliyense anatenga chofukizira chake nayikamo moto ndi lubani, ndipo anayima pamodzi ndi Mose ndi Aaroni pa khomo la tenti ya msonkhano.
پس هر کس مجمر خود راگرفته، و آتش در آنها نهاده، و بخور بر آنهاگذارده، نزد دروازه خیمه اجتماع، با موسی وهارون ایستادند.۱۸
19 Kora atasonkhanitsa omutsatira ake onse amene amatsutsa nawo pa khomo la tenti ya msonkhano, ulemerero wa Yehova unaonekera kwa gulu lonselo.
و قورح تمامی جماعت را به مقابل ایشان نزد در خیمه اجتماع جمع کرد، وجلال خداوند بر تمامی جماعت ظاهرشد.۱۹
20 Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
و خداوند موسی و هارون را خطاب کرده، گفت:۲۰
21 “Chokani pakati pa gulu ili kuti ndithetse mkanganowu kamodzinʼkamodzi.”
«خود را از این جماعت دور کنید تاایشان را در لحظه‌ای هلاک کنم.»۲۱
22 Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa chafufumimba ndipo analira mokweza, “Chonde Mulungu, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, kodi mudzakwiyira gulu lonse pamene munthu mmodzi yekha ndiye amene wachimwa?”
پس ایشان به روی در‌افتاده، گفتند: «ای خدا که خدای روحهای تمام بشر هستی، آیا یک نفر گناه ورزد وبر تمام جماعت غضبناک شوی؟»۲۲
23 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti,
و خداوند موسی را خطاب کرده، گفت:۲۳
24 “Uza gulu lonse kuti, ‘Khalani kutali ndi matenti a Kora, Datani ndi Abiramu.’”
«جماعت را خطاب کرده، بگو از اطراف مسکن قورح و داتان و ابیرام دور شوید.»۲۴
25 Mose anayimirira napita kwa Datani, Abiramu ndi kwa akuluakulu a Israeli amene ankamutsatira.
پس موسی برخاسته، نزد داتان و ابیرام رفت و مشایخ اسرائیل در عقب وی رفتند.۲۵
26 Anachenjeza gulu lonse kuti, “Khalani kutali ndi matenti a anthu oyipawa! Musakhudze kanthu kawo kalikonse, mukatero mudzawonongedwa limodzi nawo chifukwa cha machimo awo.”
و جماعت راخطاب کرده، گفت: «از نزد خیمه های این مردمان شریر دور شوید، و چیزی را که از آن ایشان است لمس منمایید، مبادا در همه گناهان ایشان هلاک شوید.»۲۶
27 Choncho anthuwo anachokadi ku matenti a Kora, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali atatuluka nayima pamodzi ndi akazi awo, ana awo ndi makanda awo pa makomo a matenti awo.
پس از اطراف مسکن قورح و داتان وابیرام دور شدند، و داتان و ابیرام بیرون آمده، بازنان و پسران و اطفال خود به در خیمه های خودایستادند.۲۷
28 Tsono Mose anati, “Umu ndi mmene mudzadziwire kuti Yehova ndiye amene anandituma kuti ndichite zinthu zonsezi ndipo kuti si maganizo anga.
و موسی گفت: «از این خواهیددانست که خداوند مرا فرستاده است تا همه این کارها را بکنم و به اراده من نبوده است.۲۸
29 Ngati anthu awa afa ndi imfa ya chilengedwe ndi kuwachitikira zomwe zimachitikira munthu aliyense, ndiye kuti Yehova sananditume.
اگر این کسان مثل موت سایر بنی آدم بمیرند و اگر مثل وقایع جمیع بنی آدم بر ایشان واقع شود، خداوندمرا نفرستاده است.۲۹
30 Koma Yehova akachita china chake chachilendo, nthaka nitsekula pakamwa pake ndi kuwameza iwo pamodzi ndi zonse zimene ali nazo, iwowa nʼkulowa mʼmanda ali moyo, pamenepo mudzazindikira kuti anthu amenewa ananyoza Yehova.” (Sheol h7585)
و اما اگر خداوند چیزتازه‌ای بنماید و زمین دهان خود را گشاده، ایشان را با جمیع مایملک ایشان ببلعد که به گور زنده فرود روند، آنگاه بدانید که این مردمان خداوند رااهانت نموده‌اند.» (Sheol h7585)۳۰
31 Atangotsiriza kuyankhula zimenezi, nthaka ya pamene anayimapo inagawikana
و چون از گفتن همه این سخنان فارغ شد، زمینی که زیر ایشان بود، شکافته شد.۳۱
32 ndipo dziko linatsekula pakamwa pake ndi kuwameza pamodzi ndi nyumba zawo ndi anthu onse a Kora ndi katundu wawo yense.
و زمین دهان خود را گشوده، ایشان را و خانه های ایشان و همه کسان را که تعلق به قورح داشتند، با تمامی اموال ایشان بلعید.۳۲
33 Analowa mʼmanda amoyo pamodzi ndi zonse zimene anali nazo. Nthaka inawatsekera ndi kuwawononga ndipo sanaonekenso. (Sheol h7585)
و ایشان با هرچه به ایشان تعلق داشت، زنده به گور فرورفتند، و زمین برایشان به هم آمد که از میان جماعت هلاک شدند. (Sheol h7585)۳۳
34 Atamva kulira kwawo, Aisraeli onse amene anali pafupi ndi anthuwo anathawa akufuwula kuti, “Nthaka imezanso ife!”
و جمیع اسرائیلیان که به اطراف ایشان بودند، از نعره ایشان گریختند، زیرا گفتند مبادا زمین ما رانیز ببلعد.۳۴
35 Ndipo moto wochokera kwa Yehova unabwera nʼkunyeketsa anthu 250 amene ankapereka nsembe yofukiza aja.
و آتش از حضور خداوند بدر‌آمده، دویست و پنجاه نفر را که بخور می‌گذرانیدند، سوزانید.۳۵
36 Yehova anawuza Mose kuti,
و خداوند موسی را خطاب کرده، گفت:۳۶
37 “Uza Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe kuti atenge zofukizirazo pakati pa mitembo yopsererayo ndipo amwazire makalawo kutali chifukwa zofukizirazo nʼzopatulika.
«به العازار بن هارون کاهن بگو که مجمرها را ازمیان آتش بردار، و آتش را به آن طرف بپاش زیراکه آنها مقدس است.۳۷
38 Izi ndi zofukizira za anthu omwe anafa chifukwa cha uchimo wawo. Musule zofukizirazo kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe, chifukwa zinaperekedwa kwa Yehova ndipo ndi zopatulika. Zimenezi zikhale chizindikiro kwa Aisraeli.”
یعنی مجمرهای این گناهکاران را به ضد جان ایشان و از آنها تختهای پهن برای پوشش مذبح بسازند، زیرا چونکه آنهارا به حضور خداوند گذرانیده‌اند مقدس شده است، تا برای بنی‌اسرائیل آیتی باشد.»۳۸
39 Choncho Eliezara, wansembe, anasonkhanitsa zofukizira zamkuwa zija zomwe anthu opsererawo anabwera nazo ndipo anazisula kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe,
پس العازار کاهن مجمرهای برنجین را که سوخته شدگان گذرانیده بودند گرفته، از آنها پوشش مذبح ساختند.۳۹
40 monga momwe Yehova anamulangizira kudzera mwa Mose. Chimenechi chinali chikumbutso kwa Aisraeli kuti munthu wina aliyense, kupatula zidzukulu za Aaroni, sayenera kupsereza lubani pamaso pa Yehova, kuopa kuti munthu woteroyo angakhale ngati Kora ndi omutsatira ake.
تا برای بنی‌اسرائیل یادگارباشد تا هیچ غریبی که از اولاد هارون نباشدبجهت سوزانیدن بخور به حضور خداوند نزدیک نیاید، مبادا مثل قورح و جمعیتش بشود، چنانکه خداوند به واسطه موسی او را امر فرموده بود.۴۰
41 Tsiku lotsatira, gulu lonse la Aisraeli linatsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Iwo anati, “Inu mwapha anthu a Yehova.”
و در فردای آن روز تمامی جماعت بنی‌اسرائیل بر موسی و هارون همهمه کرده، گفتند که شما قوم خداوند را کشتید.۴۱
42 Koma pamene anthuwo anasonkhana kuti atsutsane ndi Mose ndi Aaroni, atatembenuka kuyangʼana ku tenti ya msonkhano, mwadzidzidzi mtambo unaphimba tentiyo ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera.
و چون جماعت بر موسی و هارون جمع شدند، به سوی خیمه اجتماع نگریستند، و اینک ابر آن راپوشانید و جلال خداوند ظاهر شد.۴۲
43 Pamenepo Mose ndi Aaroni anapita patsogolo pa tenti ya msonkhano ija
و موسی وهارون پیش خیمه اجتماع آمدند.۴۳
44 ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
و خداوندموسی را خطاب کرده، گفت:۴۴
45 “Chokani pakati pa gulu la anthuwa kuti ndiwawononge kamodzinʼkamodzi.” Ndipo iwo anagwa pansi chafufumimba.
«از میان این جماعت دور شوید تا ایشان را ناگهان هلاک سازم.» و ایشان به روی خود درافتادند.۴۵
46 Kenaka Mose anawuza Aaroni kuti, “Tenga chofukizira chako ndipo ikamo lubani pamodzi ndi moto wochokera pa guwa lansembe, fulumira, pita pa gulu la anthuwo ndipo ukachite nsembe yopepesera machimo awo popeza mkwiyo wa Yehova wafika, mliri wayamba.”
و موسی به هارون گفت: «مجمر خود راگرفته، آتش از روی مذبح در آن بگذار، و بخور برآن بریز، و به زودی به سوی جماعت رفته، برای ایشان کفاره کن، زیرا غضب از حضور خداوندبرآمده، و وبا شروع شده است.»۴۶
47 Ndipo Aaroni anachita monga ananenera Mose, nathamangira mʼkatikati mwa gulu la anthuwo. Pamenepo nʼkuti mliri utayamba kale pakati pa anthu aja ndipo Aaroni anafukiza lubani ndi kupereka nsembe yopepesera machimo awo.
پس هارون به نحوی که موسی گفته بود آن را گرفته، در میان جماعت دوید و اینک وبا در میان قوم شروع شده بود، پس بخور را بریخت و بجهت قوم کفاره نمود.۴۷
48 Iye anayimirira pakati pa anthu amoyo ndi akufa ndipo mliri unaleka.
و او در میان مردگان و زندگان ایستاد ووبا بازداشته شد.۴۸
49 Komabe anthu 14, 700 anafa ndi mliriwo, kuwonjezera pa aja amene anafa chifukwa cha Kora.
و عدد کسانی که از وبا مردندچهارده هزار و هفتصد بود، سوای آنانی که درحادثه قورح هلاک شدند.۴۹
50 Ndipo Aaroni anabwerera kwa Mose ku khomo la tenti ya msonkhano, chifukwa mliriwo unali utatha.
پس هارون نزدموسی به در خیمه اجتماع برگشت و وبا رفع شد.۵۰

< Numeri 16 >