< Numeri 16 >

1 Kora mwana wa Izihari, mwana wa Kohati, mwana wa Levi ndi Datani ndi Abiramu ana a Eliabu, pamodzi ndi Oni mwana wa Perezi, ana a Rubeni, anayamba kudzikuza,
UKora indodana kaIzihari indodana kaKohathi indodana kaLevi, loDathani loAbiramu amadodana kaEliyabi, loOni indodana kaPelethi, amadodana kaRubeni, basebethatha amadoda.
2 ndipo anawukira Mose. Mʼgulu mwawo munali atsogoleri a Aisraeli 250, anthu otchuka amene anasankhidwa ndi anthu pa msonkhano.
Basebesukuma phambi kukaMozisi, lamadoda abantwana bakoIsrayeli, abangamakhulu amabili lamatshumi amahlanu, abangabakhokheli benhlangano, abakhethiweyo bomhlangano, amadoda alebizo.
3 Iwo anasonkhana kudzatsutsana ndi Mose ndi Aaroni nawawuza kuti, “Mwawonjeza! Anthu onsewa ndi oyera, aliyense wa iwo, ndipo Yehova ali pakati pawo. Chifukwa chiyani mukudzikuza pakati pa gulu lonse la Yehova?”
Bahlangana bamelana loMozisi bamelana loAroni, bathi kubo: Seledlulise amalawulo! Ngoba inhlangano yonke, bonke bangcwele, leNkosi iphakathi kwabo. Pho, liziphakamiselani phezu kwebandla leNkosi?
4 Mose atamva izi, anagwa chafufumimba.
Kwathi uMozisi esekuzwile, wathi mbo ngobuso bakhe phansi.
5 Ndipo iye anawuza Kora ndi anthu onse amene ankamutsatira kuti, “Yehova mawa mmawa adzasonyeza yemwe ndi wake ndiponso amene ndi woyera mtima. Munthuyo adzabwera pafupi ndi Iye. Munthu amene adzamusankheyo adzamusendeza pafupi.
Wasekhuluma kuKora lakuqembu lakhe lonke esithi: Kusisa, khona iNkosi izatshengisa ukuthi ngubani ongowayo lokuthi ngubani ongcwele, izamsondeza kuyo, lalowo emkhethileyo izamsondeza kuyo.
6 Iwe Kora pamodzi ndi onse amene akukutsatira chitani izi: Tengani zofukizira
Yenzani lokhu: Zithatheleni imiganu yokutshisela impepha, uKora, leqembu lakhe lonke,
7 ndipo mawa muyikemo moto ndi lubani pamaso pa Yehova. Munthu amene Yehova amusankhe ndiye amene ali woyera. Alevi inu mwawonjeza kwambiri!”
lifake kiyo umlilo, libeke kiyo impepha phambi kweNkosi kusasa. Kuzakuthi indoda iNkosi eyikhethayo, yiyo engcwele. Seledlulise amalawulo, madodana kaLevi!
8 Mose anawuzanso Kora kuti, “Inu Alevi, tsopano tamverani!
UMozisi wasesithi kuKora: Ake lizwe, madodana kaLevi;
9 Kodi sizinakukwanireni kuti Mulungu wa Israeli anakupatulani pakati pa gulu lonse la Aisraeli ndi kukubweretsani pafupi ndi Iye, kuti muzigwira ntchito ku nyumba ya Yehova ndi kumayima pamaso pa gulu, kumatumikira?
kuyinto encinyane kini yini ukuthi uNkulunkulu kaIsrayeli ulehlukanisile lenhlangano yakoIsrayeli ukuze alisondeze kuye ukuthi lenze inkonzo yethabhanekele leNkosi, lokuthi lime phambi kwenhlangano ukubakhonza?
10 Wakubweretsa iwe pamodzi ndi Alevi anzako kufupi ndi Iye mwini. Koma tsopano ukufuna kutenganso unsembe.
Ukusondezile, labafowenu bonke, amadodana kaLevi, kanye lawe; selifuna lobupristi yini?
11 Nʼkulakwira Yehova kuti iwe ndi gulu lako lonseli mwasonkhana kuti mutsutsane ndi Yehova. Kodi Aaroni ndani kuti muzikangana naye?”
Ngalokho wena leqembu lakho lonke selihlangene ukumelana leNkosi. Ngoba uAroni uyini ukuthi limngungunele?
12 Kenaka Mose anayitana Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu koma iwo anati, “Sitibwera!
UMozisi wasethuma ukubiza uDathani loAbiramu, amadodana kaEliyabi. Kodwa bathi: Kasiyikwenyuka;
13 Kodi sikukwanira kuti unatitulutsa, kutichotsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kuti udzatiphe mʼchipululu muno? Kodi tsopano ukufunanso kutilemetsa?
kuyinto encinyane yini ukuthi wasenyusa sivela elizweni eligeleza uchago loluju ukusibulala enkangala, kanti lawe usuzenza umbusi phezu kwethu?
14 Kuwonjezera apo, sunatilowetse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kapena kutipatsa malo wolima ndi minda ya mpesa. Kodi ukufuna kuchotsa maso a anthuwa? Ayi, sitibwera!”
Futhi kawusingenisanga elizweni eligeleza uchago loluju, loba ukusinika ilifa lamasimu lezivini. Amehlo ala amadoda ungawakopola yini? Asiyikwenyuka.
15 Pamenepo Mose anakwiya kwambiri ndipo anati kwa Yehova, “Musalandire chopereka chawo. Sindinatenge kalikonse kwa iwo ngakhale bulu, ndiponso sindinalakwire wina aliyense wa iwo.”
UMozisi wasethukuthela kakhulu, wathi eNkosini: Unganaki umnikelo wabo. Kangithathanga ubabhemi oyedwa wabo, futhi kangenzanga okubi komunye wabo.
16 Mose anati kwa Kora, “Iwe ndi okutsatira onse mudzaonekere pamaso pa Yehova mawa, iweyo ndi iwowo pamodzi ndi Aaroni.
UMozisi wasesithi kuKora: Wena leqembu lakho lonke banini phambi kweNkosi, wena, labo, loAroni, kusasa;
17 Munthu aliyense akatenge chofukizira ndi kuyikamo lubani, zofukizira 250 zonse pamodzi ndi kuzibweretsa pamaso pa Yehova. Iwe ndi Aaroni mudzabweretsenso zofukizira zanu.”
thathani, omunye lomunye umganu wakhe wokutshisela impepha, lifake kuyo impepha, liyisondeze phambi kweNkosi, kube ngulowo lalowo umganu wakhe wokutshisela impepha, imiganu yokutshisela impepha engamakhulu amabili lamatshumi amahlanu; lawe loAroni, ngulowo lalowo umganu wakhe wokutshisela impepha.
18 Choncho munthu aliyense anatenga chofukizira chake nayikamo moto ndi lubani, ndipo anayima pamodzi ndi Mose ndi Aaroni pa khomo la tenti ya msonkhano.
Basebethatha, ngulowo lalowo umganu wakhe wokutshisela impepha, bafaka umlilo kuyo, babeka impepha kuyo, bema emnyango wethente lenhlangano, loMozisi loAroni.
19 Kora atasonkhanitsa omutsatira ake onse amene amatsutsa nawo pa khomo la tenti ya msonkhano, ulemerero wa Yehova unaonekera kwa gulu lonselo.
UKora wasebuthanisa inhlangano yonke ukumelana labo emnyango wethente lenhlangano. Inkazimulo yeNkosi yasibonakala ebandleni lonke.
20 Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
INkosi yasikhuluma kuMozisi lakuAroni isithi:
21 “Chokani pakati pa gulu ili kuti ndithetse mkanganowu kamodzinʼkamodzi.”
Zehlukaniseni liphume phakathi kwalinhlangano ukuze ngibaqede ngokucwayiza kwelihlo.
22 Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa chafufumimba ndipo analira mokweza, “Chonde Mulungu, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, kodi mudzakwiyira gulu lonse pamene munthu mmodzi yekha ndiye amene wachimwa?”
Basebesithi mbo ngobuso babo phansi bathi: Nkulunkulu, Nkulunkulu wemimoya yayo yonke inyama, kona umuntu oyedwa, ubusuthukuthelela inhlangano yonke yini?
23 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti,
INkosi yasikhuluma kuMozisi isithi:
24 “Uza gulu lonse kuti, ‘Khalani kutali ndi matenti a Kora, Datani ndi Abiramu.’”
Tshono enhlanganweni uthi: Yenyukani lisuke kunhlangothi zonke zomuzi kaKora, uDathani, loAbiramu.
25 Mose anayimirira napita kwa Datani, Abiramu ndi kwa akuluakulu a Israeli amene ankamutsatira.
UMozisi wasesukuma, waya kuDathani loAbiramu, labadala bakoIsrayeli bamlandela.
26 Anachenjeza gulu lonse kuti, “Khalani kutali ndi matenti a anthu oyipawa! Musakhudze kanthu kawo kalikonse, mukatero mudzawonongedwa limodzi nawo chifukwa cha machimo awo.”
Wasekhuluma enhlanganweni esithi: Ake lisuke emathenteni alamadoda amabi, lingathinti lutho olungolwabo, hlezi liphetshulwe ezonweni zabo zonke.
27 Choncho anthuwo anachokadi ku matenti a Kora, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali atatuluka nayima pamodzi ndi akazi awo, ana awo ndi makanda awo pa makomo a matenti awo.
Basebesenyuka besuka emzini yaboKora, uDathani loAbiramu enhlangothini zonke; oDathani loAbiramu basebephuma, bema emnyango wamathente abo labomkabo lamadodana abo labantwanyana babo.
28 Tsono Mose anati, “Umu ndi mmene mudzadziwire kuti Yehova ndiye amene anandituma kuti ndichite zinthu zonsezi ndipo kuti si maganizo anga.
UMozisi wasesithi: Ngalokhu lizakwazi ukuthi iNkosi ingithumile ukwenza yonke limisebenzi, lokuthi kakusikho okwengqondo yami.
29 Ngati anthu awa afa ndi imfa ya chilengedwe ndi kuwachitikira zomwe zimachitikira munthu aliyense, ndiye kuti Yehova sananditume.
Uba laba besifa njengokufa kwabantu bonke, kumbe behlelwe njengokwehlelwa kwabantu bonke, iNkosi kayingithumanga.
30 Koma Yehova akachita china chake chachilendo, nthaka nitsekula pakamwa pake ndi kuwameza iwo pamodzi ndi zonse zimene ali nazo, iwowa nʼkulowa mʼmanda ali moyo, pamenepo mudzazindikira kuti anthu amenewa ananyoza Yehova.” (Sheol h7585)
Kodwa uba iNkosi idala into entsha, ukuthi umhlaba uvule umlomo wawo, ubaginye lakho konke okwabo, behlele emgodini bephila, lizaqedisisa ukuthi lamadoda ayidelele iNkosi. (Sheol h7585)
31 Atangotsiriza kuyankhula zimenezi, nthaka ya pamene anayimapo inagawikana
Kwasekusithi eseqedile ukukhuluma wonke la amazwi, umhlaba owawungaphansi kwabo waqhekezeka,
32 ndipo dziko linatsekula pakamwa pake ndi kuwameza pamodzi ndi nyumba zawo ndi anthu onse a Kora ndi katundu wawo yense.
lomhlaba wavula umlomo wawo, wabaginya lezindlu zabo, labo bonke abantu ababengabakaKora, lempahla yabo yonke.
33 Analowa mʼmanda amoyo pamodzi ndi zonse zimene anali nazo. Nthaka inawatsekera ndi kuwawononga ndipo sanaonekenso. (Sheol h7585)
Basebetshona emgodini bephila bona lakho konke okwabo; umhlaba wabagqibela, babhubha besuka phakathi kwebandla. (Sheol h7585)
34 Atamva kulira kwawo, Aisraeli onse amene anali pafupi ndi anthuwo anathawa akufuwula kuti, “Nthaka imezanso ife!”
UIsrayeli wonke owayebazingelezele wasebaleka ekukhaleni kwabo, ngoba bathi: Hlezi umhlaba usiginye.
35 Ndipo moto wochokera kwa Yehova unabwera nʼkunyeketsa anthu 250 amene ankapereka nsembe yofukiza aja.
Kwasekuphuma umlilo eNkosini, waqothula amadoda angamakhulu amabili lamatshumi amahlanu ayenikele impepha.
36 Yehova anawuza Mose kuti,
INkosi yasikhuluma kuMozisi isithi:
37 “Uza Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe kuti atenge zofukizirazo pakati pa mitembo yopsererayo ndipo amwazire makalawo kutali chifukwa zofukizirazo nʼzopatulika.
Tshono kuEleyazare, indodana kaAroni umpristi, ukuthi athathe imiganu yokutshisela impepha phakathi kokutsha; uwuchithachithele umlilo laphayana, ngoba ingcwele.
38 Izi ndi zofukizira za anthu omwe anafa chifukwa cha uchimo wawo. Musule zofukizirazo kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe, chifukwa zinaperekedwa kwa Yehova ndipo ndi zopatulika. Zimenezi zikhale chizindikiro kwa Aisraeli.”
Imiganu yokutshisela impepha yalezizoni imelene lemiphefumulo yazo, kabayenze ibe yizicecedu ezibanzi zibe yisisibekelo selathi; ngoba bayinikele phambi kweNkosi, ngakho ingcwele; njalo izakuba yisibonakaliso ebantwaneni bakoIsrayeli.
39 Choncho Eliezara, wansembe, anasonkhanitsa zofukizira zamkuwa zija zomwe anthu opsererawo anabwera nazo ndipo anazisula kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe,
UEleyazare umpristi wasethatha imiganu yethusi yokutshisela impepha ababenikele ngayo abatshisiweyo, basebeyikhanda yaba yizicecedu zokusibekela ilathi,
40 monga momwe Yehova anamulangizira kudzera mwa Mose. Chimenechi chinali chikumbutso kwa Aisraeli kuti munthu wina aliyense, kupatula zidzukulu za Aaroni, sayenera kupsereza lubani pamaso pa Yehova, kuopa kuti munthu woteroyo angakhale ngati Kora ndi omutsatira ake.
kube yisikhumbuzo ebantwaneni bakoIsrayeli ukuze kungabi lowemzini, ongesuye owenzalo kaAroni, osondela ukutshisa impepha phambi kweNkosi, ukuze angabi njengoKora lanjengexuku lakhe, njengoba iNkosi yakhuluma kuye ngesandla sikaMozisi.
41 Tsiku lotsatira, gulu lonse la Aisraeli linatsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Iwo anati, “Inu mwapha anthu a Yehova.”
Kodwa kusisa inhlangano yonke yabantwana bakoIsrayeli yabasola oMozisi loAroni, isithi: Lina libabulele abantu beNkosi.
42 Koma pamene anthuwo anasonkhana kuti atsutsane ndi Mose ndi Aaroni, atatembenuka kuyangʼana ku tenti ya msonkhano, mwadzidzidzi mtambo unaphimba tentiyo ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera.
Kwasekusithi inhlangano isihlangene imelene loMozisi njalo imelene loAroni, baphendukela ethenteni lenhlangano, khangela-ke iyezi lalilisibekele lenkazimulo yeNkosi yabonakala.
43 Pamenepo Mose ndi Aaroni anapita patsogolo pa tenti ya msonkhano ija
UMozisi loAroni basebesiza ngaphambi kwethente lenhlangano.
44 ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
INkosi yasikhuluma kuMozisi isithi:
45 “Chokani pakati pa gulu la anthuwa kuti ndiwawononge kamodzinʼkamodzi.” Ndipo iwo anagwa pansi chafufumimba.
Yenyukani lisuke phakathi kwalinhlangano, ukuze ngibaqede njengokucwayiza kwelihlo. Basebesithi mbo ngobuso babo phansi.
46 Kenaka Mose anawuza Aaroni kuti, “Tenga chofukizira chako ndipo ikamo lubani pamodzi ndi moto wochokera pa guwa lansembe, fulumira, pita pa gulu la anthuwo ndipo ukachite nsembe yopepesera machimo awo popeza mkwiyo wa Yehova wafika, mliri wayamba.”
UMozisi wasesithi kuAroni: Thatha umganu wokutshisela impepha, ufake kuwo umlilo ovela elathini, ubeke kuwo impepha, uye ngokuphangisa enhlanganweni, ubenzele inhlawulo yokuthula; ngoba ulaka seluphumile lusuka phambi kweNkosi, inhlupheko isiqalisile.
47 Ndipo Aaroni anachita monga ananenera Mose, nathamangira mʼkatikati mwa gulu la anthuwo. Pamenepo nʼkuti mliri utayamba kale pakati pa anthu aja ndipo Aaroni anafukiza lubani ndi kupereka nsembe yopepesera machimo awo.
UAroni wasekuthatha njengokutsho kukaMozisi, wagijimela phakathi kwebandla, khangela-ke, inhlupheko yayisiqalisile phakathi kwabantu. Wafaka impepha, wabenzela abantu inhlawulo yokuthula.
48 Iye anayimirira pakati pa anthu amoyo ndi akufa ndipo mliri unaleka.
Wasesima phakathi kwabafileyo labaphilayo. Inhlupheko yasimiswa.
49 Komabe anthu 14, 700 anafa ndi mliriwo, kuwonjezera pa aja amene anafa chifukwa cha Kora.
Labafayo enhluphekweni babeyizinkulungwane ezilitshumi lane lamakhulu ayisikhombisa, ngaphandle kwalabo abafa ngendaba kaKora.
50 Ndipo Aaroni anabwerera kwa Mose ku khomo la tenti ya msonkhano, chifukwa mliriwo unali utatha.
UAroni wasebuyela kuMozisi emnyango wethente lenhlangano; lenhlupheko yayisimisiwe.

< Numeri 16 >