< Numeri 16 >

1 Kora mwana wa Izihari, mwana wa Kohati, mwana wa Levi ndi Datani ndi Abiramu ana a Eliabu, pamodzi ndi Oni mwana wa Perezi, ana a Rubeni, anayamba kudzikuza,
UKhora indodana ka-Izihari, indodana kaKhohathi, indodana kaLevi, labathile abakoRubheni, uDathani kanye lo-Abhiramu, amadodana ka-Eliyabi, kanye lo-Oni indodana kaPhelethi baqala ukuba yiziqholo
2 ndipo anawukira Mose. Mʼgulu mwawo munali atsogoleri a Aisraeli 250, anthu otchuka amene anasankhidwa ndi anthu pa msonkhano.
bavukela uMosi. Bakwenza lokhu bendawonye lamanye amadoda angamakhulu amabili alamatshumi amahlanu ako-Israyeli, abakhokheli abadumileyo babantu bakuleyondawo ababekhethelwe ukuthi babe ngamalunga enkundla.
3 Iwo anasonkhana kudzatsutsana ndi Mose ndi Aaroni nawawuza kuti, “Mwawonjeza! Anthu onsewa ndi oyera, aliyense wa iwo, ndipo Yehova ali pakati pawo. Chifukwa chiyani mukudzikuza pakati pa gulu lonse la Yehova?”
Beza beliqembu ukuzomelana loMosi lo-Aroni bathi kubo, “Seledlulise amalawulo! Abantu bonke bako-Israyeli bangcwele, bonke ngamunye wabo, njalo uThixo uyabasekela. Pho kungani liziphakamisa ngaphezu kwabantu bakaThixo na?”
4 Mose atamva izi, anagwa chafufumimba.
UMosi wathi ekuzwa lokhu, wawela phansi ngobuso.
5 Ndipo iye anawuza Kora ndi anthu onse amene ankamutsatira kuti, “Yehova mawa mmawa adzasonyeza yemwe ndi wake ndiponso amene ndi woyera mtima. Munthuyo adzabwera pafupi ndi Iye. Munthu amene adzamusankheyo adzamusendeza pafupi.
Wasesithi kuKhora lakubalandeli bakhe: “Kusasa ekuseni uThixo uzaveza obala ukuthi ngubani ongowakhe lokuthi ngubani ongcwele, njalo uzamvumela lowomuntu ukuthi asondele kuye. Indoda azayikhetha uzayivumela ukuthi isondele phansi kwakhe.
6 Iwe Kora pamodzi ndi onse amene akukutsatira chitani izi: Tengani zofukizira
Wena, Khora, kanye labalandeli bakho yenzani lokhu: Thathani indengezi
7 ndipo mawa muyikemo moto ndi lubani pamaso pa Yehova. Munthu amene Yehova amusankhe ndiye amene ali woyera. Alevi inu mwawonjeza kwambiri!”
kuthi kusasa libasele umlilo njalo litshisele impepha kuzo phambi kukaThixo. Indoda ezakhethwa nguThixo yiyo engcwele. Lina baLevi seledlulise amalawulo!”
8 Mose anawuzanso Kora kuti, “Inu Alevi, tsopano tamverani!
UMosi wabuye wathi kuKhora, “Khathesi lalelani-ke, lina baLevi!
9 Kodi sizinakukwanireni kuti Mulungu wa Israeli anakupatulani pakati pa gulu lonse la Aisraeli ndi kukubweretsani pafupi ndi Iye, kuti muzigwira ntchito ku nyumba ya Yehova ndi kumayima pamaso pa gulu, kumatumikira?
Kanti akulanelisanga yini ukuthi uNkulunkulu ka-Israyeli ulikhethile phakathi kwabo bonke abako-Israyeli njalo walisondeza phansi kwakhe ukuze lenze umsebenzi ethabanikeleni likaThixo lokuthi lizakuma phambi kwesizwe lisenzele inkonzo na?
10 Wakubweretsa iwe pamodzi ndi Alevi anzako kufupi ndi Iye mwini. Koma tsopano ukufuna kutenganso unsembe.
Ukusondezile wena kanye labanye bakho abangabaLevi phansi kwakhe, kodwa-ke khathesi selifuna lobuphristi.
11 Nʼkulakwira Yehova kuti iwe ndi gulu lako lonseli mwasonkhana kuti mutsutsane ndi Yehova. Kodi Aaroni ndani kuti muzikangana naye?”
Ukubambana kwakho kanye labalandeli bakho kuyikumelana loThixo limphikisa. Kambe ungubani u-Aroni elingakhonona ngaye?”
12 Kenaka Mose anayitana Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu koma iwo anati, “Sitibwera!
Ngakho uMosi wabiza uDathani lo-Abhiramu amadodana ka-Eliyabi. Kodwa bona bathi, “Vele kasibuyi!
13 Kodi sikukwanira kuti unatitulutsa, kutichotsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kuti udzatiphe mʼchipululu muno? Kodi tsopano ukufunanso kutilemetsa?
Kambe bekungenelanga yini ukuthi wasikhipha elizweni eligeleza uchago loluju ukuzasibulalela enkangala na? Khathesi usufuna lokuba yinkosi phezu kwethu?
14 Kuwonjezera apo, sunatilowetse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kapena kutipatsa malo wolima ndi minda ya mpesa. Kodi ukufuna kuchotsa maso a anthuwa? Ayi, sitibwera!”
Kunjalo-nje, awukasingenisi elizweni eligeleza uchago loluju kumbe ukusipha ilifa lamasimu kanye lezivini. Ufuna ukukopola amehlo amadoda la na? Hatshi, kasibuyi!”
15 Pamenepo Mose anakwiya kwambiri ndipo anati kwa Yehova, “Musalandire chopereka chawo. Sindinatenge kalikonse kwa iwo ngakhale bulu, ndiponso sindinalakwire wina aliyense wa iwo.”
Ngalokho uMosi wathukuthela kakhulu wasesithi kuThixo, “Ungawemukeli umnikelo wabo. Angithathanga lutho kubo ngitsho lobabhemi kodwa lokhu, njalo kakho loyedwa engimoneleyo.”
16 Mose anati kwa Kora, “Iwe ndi okutsatira onse mudzaonekere pamaso pa Yehova mawa, iweyo ndi iwowo pamodzi ndi Aaroni.
UMosi wathi kuKhora, “Wena kanye labo bonke abalandeli bakho kumele lime phambi kukaThixo kusasa, wena, bona kanye lo-Aroni.
17 Munthu aliyense akatenge chofukizira ndi kuyikamo lubani, zofukizira 250 zonse pamodzi ndi kuzibweretsa pamaso pa Yehova. Iwe ndi Aaroni mudzabweretsenso zofukizira zanu.”
Indoda inye nganye kumele ithathe udengezi ifake impepha kulo, indengezi ezingamakhulu amabili alamatshumi amahlanu, njalo iwethule phambi kukaThixo. Wena kanye lo-Aroni lani kufanele liveze ezenu indengezi.”
18 Choncho munthu aliyense anatenga chofukizira chake nayikamo moto ndi lubani, ndipo anayima pamodzi ndi Mose ndi Aaroni pa khomo la tenti ya msonkhano.
Ngakho indoda inye ngayinye yathatha udengezi lwayo, yafaka umlilo kanye lempepha kulo, njalo yema loMosi lo-Aroni esangweni lethente lokuhlangana.
19 Kora atasonkhanitsa omutsatira ake onse amene amatsutsa nawo pa khomo la tenti ya msonkhano, ulemerero wa Yehova unaonekera kwa gulu lonselo.
Kwathi uKhora esebaqoqile abalandeli bakhe bephikisana labo esangweni lethente lokuhlangana, inkazimulo kaThixo yabonakala kubo bonke abantu ababebuthene kuleyondawo.
20 Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
UThixo wathi kuMosi lo-Aroni,
21 “Chokani pakati pa gulu ili kuti ndithetse mkanganowu kamodzinʼkamodzi.”
“Sukani phakathi kwalaba ababutheneyo ukuze ngibabhubhise khathesi.”
22 Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa chafufumimba ndipo analira mokweza, “Chonde Mulungu, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, kodi mudzakwiyira gulu lonse pamene munthu mmodzi yekha ndiye amene wachimwa?”
Kodwa uMosi lo-Aroni bawa phansi ngobuso bakhala bathi, “Oh Nkulunkulu, Nkulunkulu wemiphefumulo yabantu bonke, uzathukuthelela abantu bonke jikelele ngenxa yomuntu oyedwa owonileyo na?”
23 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti,
Ngakho uThixo wathi kuMosi,
24 “Uza gulu lonse kuti, ‘Khalani kutali ndi matenti a Kora, Datani ndi Abiramu.’”
“Tshela ibandla uthi, ‘Sukani eduze kwamathente aboKhora, loDathani lo-Abhiramu.’”
25 Mose anayimirira napita kwa Datani, Abiramu ndi kwa akuluakulu a Israeli amene ankamutsatira.
UMosi wasukuma waya kuDathani lo-Abhiramu, kwathi labadala bako-Israyeli bamlandela.
26 Anachenjeza gulu lonse kuti, “Khalani kutali ndi matenti a anthu oyipawa! Musakhudze kanthu kawo kalikonse, mukatero mudzawonongedwa limodzi nawo chifukwa cha machimo awo.”
Waqonqosela ibandla wathi, “Buyelani emuva lisuke emathenteni abantu laba ababi! Lingathinti lutho olungolwabo ngoba lingenzenjalo lizakhuculwa ngenxa yezono zabo.”
27 Choncho anthuwo anachokadi ku matenti a Kora, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali atatuluka nayima pamodzi ndi akazi awo, ana awo ndi makanda awo pa makomo a matenti awo.
Ngakho basuka emathenteni kaKhora, uDathani lo-Abhiramu. UDathani lo-Abhiramu basebephume phandle bemi labomkabo, labantwababo kanye labancane emasangweni amathente abo.
28 Tsono Mose anati, “Umu ndi mmene mudzadziwire kuti Yehova ndiye amene anandituma kuti ndichite zinthu zonsezi ndipo kuti si maganizo anga.
UMosi wasesithi, “Nansi indlela elizabona ngayo ukuthi uThixo ungithumile ukuzokwenza konke lokhu engikwenzayo kanye lokuthi akusingqondo yami.
29 Ngati anthu awa afa ndi imfa ya chilengedwe ndi kuwachitikira zomwe zimachitikira munthu aliyense, ndiye kuti Yehova sananditume.
Nxa amadoda la ezazifela ngendlela abantu abazifela ngayo, kumbe nxa bengethekelelwa emva kokwethekelela kwabantu bonke kuzabe kusitsho ukuthi uThixo kangithumanga.
30 Koma Yehova akachita china chake chachilendo, nthaka nitsekula pakamwa pake ndi kuwameza iwo pamodzi ndi zonse zimene ali nazo, iwowa nʼkulowa mʼmanda ali moyo, pamenepo mudzazindikira kuti anthu amenewa ananyoza Yehova.” (Sheol h7585)
Kodwa nxa uThixo ezakwenza esingakaze sikubone okunye okutsha kwenzakale ukuthi umhlaba uvuleke ubaginye kanye lakho konke okungokwabo, bangene bephila engcwabeni, kulapho elizakwazi khona ukuthi amadoda la ameyisile uThixo.” (Sheol h7585)
31 Atangotsiriza kuyankhula zimenezi, nthaka ya pamene anayimapo inagawikana
Kwathi eqeda ukutsho lokhu, umhlaba wavuleka ngaphansi kwabo,
32 ndipo dziko linatsekula pakamwa pake ndi kuwameza pamodzi ndi nyumba zawo ndi anthu onse a Kora ndi katundu wawo yense.
wavuleka wabaginya bona, kanye labantwababo lamadoda wonke ayekhokhelwa nguKhora kanye lempahla zawo.
33 Analowa mʼmanda amoyo pamodzi ndi zonse zimene anali nazo. Nthaka inawatsekera ndi kuwawononga ndipo sanaonekenso. (Sheol h7585)
Batshona engcwabeni bephila, lakho konke okwakungokwabo; umhlabathi wabambokotha, kwaba yikutshabalala kwabo, basuswa kwabakibo. (Sheol h7585)
34 Atamva kulira kwawo, Aisraeli onse amene anali pafupi ndi anthuwo anathawa akufuwula kuti, “Nthaka imezanso ife!”
Besizwa ukukhala kwabo, bonke abako-Israyeli ababelapho babaleka, beklabalala besithi, “Umhlaba uzasiginya lathi!”
35 Ndipo moto wochokera kwa Yehova unabwera nʼkunyeketsa anthu 250 amene ankapereka nsembe yofukiza aja.
Kwavela umlilo kuThixo watshaya waqothula amadoda angamakhulu amabili alamatshumi amahlanu ayenikela ngempepha.
36 Yehova anawuza Mose kuti,
UThixo wathi kuMosi,
37 “Uza Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe kuti atenge zofukizirazo pakati pa mitembo yopsererayo ndipo amwazire makalawo kutali chifukwa zofukizirazo nʼzopatulika.
“Tshela u-Eliyazari indodana ka-Aroni, umphristi, ukuthi athathe indengezi azikhiphe emlotheni achithele amalahle endaweni ekhatshana, ngoba indengezi lezi zingcwele,
38 Izi ndi zofukizira za anthu omwe anafa chifukwa cha uchimo wawo. Musule zofukizirazo kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe, chifukwa zinaperekedwa kwa Yehova ndipo ndi zopatulika. Zimenezi zikhale chizindikiro kwa Aisraeli.”
indengezi zamadoda onileyo aze alahlekelwa yimpilo yawo. Khanda lezondengezi ukuze zendlaleke e-alithareni, ngoba zethulwa phambi kukaThixo zaba ngezingcwele. Azibe yisibonakaliso kwabako-Israyeli.”
39 Choncho Eliezara, wansembe, anasonkhanitsa zofukizira zamkuwa zija zomwe anthu opsererawo anabwera nazo ndipo anazisula kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe,
Ngakho u-Eliyazari umphristi wabutha indengezi zethusi ezazilethwe yilabo abatshayo, walungisa ukuba zikhandwe zendlalwe e-alithareni,
40 monga momwe Yehova anamulangizira kudzera mwa Mose. Chimenechi chinali chikumbutso kwa Aisraeli kuti munthu wina aliyense, kupatula zidzukulu za Aaroni, sayenera kupsereza lubani pamaso pa Yehova, kuopa kuti munthu woteroyo angakhale ngati Kora ndi omutsatira ake.
njengokulaywa kukaMosi nguThixo. Lokhu kwakuzakhumbuza abako-Israyeli ukuthi kakho ovunyelwayo ukutshisa impepha phambi kukaThixo ngaphandle kuka-Aroni lesizukulwane sakhe, funa abe njengoKhora labalandeli bakhe.
41 Tsiku lotsatira, gulu lonse la Aisraeli linatsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Iwo anati, “Inu mwapha anthu a Yehova.”
Ngosuku olulandelayo abako-Israyeli bonke bakhonona basola uMosi lo-Aroni. Bathi, “Selibulele abantu bakaThixo.”
42 Koma pamene anthuwo anasonkhana kuti atsutsane ndi Mose ndi Aaroni, atatembenuka kuyangʼana ku tenti ya msonkhano, mwadzidzidzi mtambo unaphimba tentiyo ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera.
Kodwa kwathi ibandla selibuthene bephikisa uMosi lo-Aroni njalo sebekhangele ethenteni lokuhlangana, masinyane iyezi lalisibekela kwavela inkazimulo kaThixo.
43 Pamenepo Mose ndi Aaroni anapita patsogolo pa tenti ya msonkhano ija
Ngakho uMosi lo-Aroni baya phambi kwethente lokuhlangana,
44 ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
uThixo wasesithi kuMosi,
45 “Chokani pakati pa gulu la anthuwa kuti ndiwawononge kamodzinʼkamodzi.” Ndipo iwo anagwa pansi chafufumimba.
“Suka kulelibandla ukuze ngibatshabalalise.” Ngakho bawa phansi ngobuso.
46 Kenaka Mose anawuza Aaroni kuti, “Tenga chofukizira chako ndipo ikamo lubani pamodzi ndi moto wochokera pa guwa lansembe, fulumira, pita pa gulu la anthuwo ndipo ukachite nsembe yopepesera machimo awo popeza mkwiyo wa Yehova wafika, mliri wayamba.”
Kusenjalo uMosi wathi ku-Aroni, “Thatha udengezi lwakho uthele impepha kulo, ndawonye lomlilo ovela e-alithareni, uphange uye ebandleni ukuze ubenzele indlela yokubuyisana. Ulaka lukaThixo lubonakele; isifo sesiqalisile.”
47 Ndipo Aaroni anachita monga ananenera Mose, nathamangira mʼkatikati mwa gulu la anthuwo. Pamenepo nʼkuti mliri utayamba kale pakati pa anthu aja ndipo Aaroni anafukiza lubani ndi kupereka nsembe yopepesera machimo awo.
U-Aroni wenza okwakutshiwo nguMosi, waphanga wangena phakathi kwebandla. Isifo sesivele sesiqalisile ebantwini, kodwa u-Aroni wanikela impepha wabenzela indlela yokubuyisana.
48 Iye anayimirira pakati pa anthu amoyo ndi akufa ndipo mliri unaleka.
Wema phakathi kwabaphilayo lasebefile, isifo saphela.
49 Komabe anthu 14, 700 anafa ndi mliriwo, kuwonjezera pa aja amene anafa chifukwa cha Kora.
Kodwa kwasekufe abantu abazinkulungwane ezilitshumi lane lamakhulu ayisikhombisa bebulawa yisifo, phezu kwalabo ababefe ngenxa kaKhora.
50 Ndipo Aaroni anabwerera kwa Mose ku khomo la tenti ya msonkhano, chifukwa mliriwo unali utatha.
Ngemva kwalokho u-Aroni wabuyela kuMosi esangweni lethente lokuhlangana, njengoba isifo sasesiphelile.

< Numeri 16 >