< Numeri 16 >
1 Kora mwana wa Izihari, mwana wa Kohati, mwana wa Levi ndi Datani ndi Abiramu ana a Eliabu, pamodzi ndi Oni mwana wa Perezi, ana a Rubeni, anayamba kudzikuza,
Then took Korah, son of Izhar son of Kohath son of Levi, —and Dathan and Abiram sons of Eliab, and On, son of Peleth sons of Reuben;
2 ndipo anawukira Mose. Mʼgulu mwawo munali atsogoleri a Aisraeli 250, anthu otchuka amene anasankhidwa ndi anthu pa msonkhano.
and rose up before Moses, with certain men of the sons of Israel, two hundred and fifty, —princes of assembly, called to the stated meeting, men of renown;
3 Iwo anasonkhana kudzatsutsana ndi Mose ndi Aaroni nawawuza kuti, “Mwawonjeza! Anthu onsewa ndi oyera, aliyense wa iwo, ndipo Yehova ali pakati pawo. Chifukwa chiyani mukudzikuza pakati pa gulu lonse la Yehova?”
and gathered themselves together against Moses and against Aaron and said unto them Too much for you, when, all the assembly, are, all of them, holy, and in the midst of them, is Yahweh, —Wherefore, then, should ye set yourselves up, above the convocation of Yahweh?
4 Mose atamva izi, anagwa chafufumimba.
And, when Moses heard it, he fell upon his face.
5 Ndipo iye anawuza Kora ndi anthu onse amene ankamutsatira kuti, “Yehova mawa mmawa adzasonyeza yemwe ndi wake ndiponso amene ndi woyera mtima. Munthuyo adzabwera pafupi ndi Iye. Munthu amene adzamusankheyo adzamusendeza pafupi.
Then spake he unto Korah, and unto all his assembly, saying, In the morning, will Yahweh make known who are his, and who is the holy one and will cause him to come near unto himself, —yea him whom he shall choose, will he cause to come near unto himself.
6 Iwe Kora pamodzi ndi onse amene akukutsatira chitani izi: Tengani zofukizira
This do, —Take to you censers, Korah and all his assembly;
7 ndipo mawa muyikemo moto ndi lubani pamaso pa Yehova. Munthu amene Yehova amusankhe ndiye amene ali woyera. Alevi inu mwawonjeza kwambiri!”
and place therein fire, and put thereon incense before Yahweh, to-morrow, So shall it be—that, the man whom Yahweh shall choose, he shall be the holy one. Too much for you ye sons of Levi!
8 Mose anawuzanso Kora kuti, “Inu Alevi, tsopano tamverani!
And Moses said unto Korah, —Hear, I pray you, ye sons of Levi!
9 Kodi sizinakukwanireni kuti Mulungu wa Israeli anakupatulani pakati pa gulu lonse la Aisraeli ndi kukubweretsani pafupi ndi Iye, kuti muzigwira ntchito ku nyumba ya Yehova ndi kumayima pamaso pa gulu, kumatumikira?
Is it too small a thing for you that the God of Israel hath separated you from the assembly of Israel, to bring you near unto himself, —to do the laborious work of the habitation of Yahweh, and to stand before the assembly, to wait upon them?
10 Wakubweretsa iwe pamodzi ndi Alevi anzako kufupi ndi Iye mwini. Koma tsopano ukufuna kutenganso unsembe.
But having brought thee near, and all thy brethren the sons of Levi with thee, must ye seek priesthood also?
11 Nʼkulakwira Yehova kuti iwe ndi gulu lako lonseli mwasonkhana kuti mutsutsane ndi Yehova. Kodi Aaroni ndani kuti muzikangana naye?”
Wherefore thou and all thine assembly, are conspiring against Yahweh, —But Aaron, what is he, that ye should murmur against him?
12 Kenaka Mose anayitana Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu koma iwo anati, “Sitibwera!
Then sent Moses, to call for Dathan and for Abiram sons of Eliab, —and they said We will not come up:
13 Kodi sikukwanira kuti unatitulutsa, kutichotsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kuti udzatiphe mʼchipululu muno? Kodi tsopano ukufunanso kutilemetsa?
Was it, a small thing, that thou didst bring us up out of a land flowing with milk and honey, to put us to death in the desert but thou must, continue even to lord it, over us?
14 Kuwonjezera apo, sunatilowetse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kapena kutipatsa malo wolima ndi minda ya mpesa. Kodi ukufuna kuchotsa maso a anthuwa? Ayi, sitibwera!”
Certainly not into a land flowing with milk and honey, hast thou brought us, nor given unto us an inheritance of field and vineyard, —The eyes of those men, wilt thou dig out? We will not come up.
15 Pamenepo Mose anakwiya kwambiri ndipo anati kwa Yehova, “Musalandire chopereka chawo. Sindinatenge kalikonse kwa iwo ngakhale bulu, ndiponso sindinalakwire wina aliyense wa iwo.”
Then was Moses very angry, and he said unto Yahweh, Do not thou have respect unto their meal-offering. Not one ass, from them, have I taken, neither have I wronged one of them.
16 Mose anati kwa Kora, “Iwe ndi okutsatira onse mudzaonekere pamaso pa Yehova mawa, iweyo ndi iwowo pamodzi ndi Aaroni.
And Moses said unto Korah, Thou, and all thine assembly, come ye before Yahweh, —thou, and they, and Aaron to-morrow.
17 Munthu aliyense akatenge chofukizira ndi kuyikamo lubani, zofukizira 250 zonse pamodzi ndi kuzibweretsa pamaso pa Yehova. Iwe ndi Aaroni mudzabweretsenso zofukizira zanu.”
And take ye each man his censer and put thereon incense, then shall ye bring near before Yahweh, each man his censer, two hundred and fifty Censers, —and, thou and Aaron, each man his censer.
18 Choncho munthu aliyense anatenga chofukizira chake nayikamo moto ndi lubani, ndipo anayima pamodzi ndi Mose ndi Aaroni pa khomo la tenti ya msonkhano.
So they took each man his censer and put thereon fire, and placed thereon incense, —and took their stand at the entrance of the tent of meeting with Moses and Aaron.
19 Kora atasonkhanitsa omutsatira ake onse amene amatsutsa nawo pa khomo la tenti ya msonkhano, ulemerero wa Yehova unaonekera kwa gulu lonselo.
And Korah gathered together against them all the assembly, unto the entrance of the tent of meeting, —then appeared the glory of Yahweh, unto all the assembly.
20 Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
Then spake Yahweh unto Moses and unto Aaron, saying:
21 “Chokani pakati pa gulu ili kuti ndithetse mkanganowu kamodzinʼkamodzi.”
Separate yourselves out of the midst of this assembly, —that I may consume them in a moment.
22 Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa chafufumimba ndipo analira mokweza, “Chonde Mulungu, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, kodi mudzakwiyira gulu lonse pamene munthu mmodzi yekha ndiye amene wachimwa?”
And they fell upon their faces and said, O GOD, the God of the spirits of all flesh, —shall, one man, sin, and against all the assembly, wilt thou be wroth.
23 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti,
And Yahweh spake unto Moses, saying,
24 “Uza gulu lonse kuti, ‘Khalani kutali ndi matenti a Kora, Datani ndi Abiramu.’”
Speak unto the assembly, saying, —Get ye up from round about the habitation of Korah, Dathan and Abiram.
25 Mose anayimirira napita kwa Datani, Abiramu ndi kwa akuluakulu a Israeli amene ankamutsatira.
So Moses rose up, and went, unto Dathan and Abiram, —then went, after him the elders of Israel.
26 Anachenjeza gulu lonse kuti, “Khalani kutali ndi matenti a anthu oyipawa! Musakhudze kanthu kawo kalikonse, mukatero mudzawonongedwa limodzi nawo chifukwa cha machimo awo.”
And he spake unto the assembly, saying—Remove I pray you from beside the tents of these lawless men, and do not touch aught that pertaineth unto them, —lest ye be carried off, in all their sins.
27 Choncho anthuwo anachokadi ku matenti a Kora, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali atatuluka nayima pamodzi ndi akazi awo, ana awo ndi makanda awo pa makomo a matenti awo.
So they went up from beside the habitation of Korah, Dathan and Abiram on every side, —and, Dathan and Abiram, came out and stationed themselves at the entrance of their tents, with their wives and their sons and their little ones.
28 Tsono Mose anati, “Umu ndi mmene mudzadziwire kuti Yehova ndiye amene anandituma kuti ndichite zinthu zonsezi ndipo kuti si maganizo anga.
Then said Moses, Hereby, shall ye know, that, Yahweh hath sent me, to do all these works, —verily, not out of my own heart:
29 Ngati anthu awa afa ndi imfa ya chilengedwe ndi kuwachitikira zomwe zimachitikira munthu aliyense, ndiye kuti Yehova sananditume.
If, as all human beings die, these do die, and the visitation of all human beings, be visited upon them, Yahweh, hath not sent me.
30 Koma Yehova akachita china chake chachilendo, nthaka nitsekula pakamwa pake ndi kuwameza iwo pamodzi ndi zonse zimene ali nazo, iwowa nʼkulowa mʼmanda ali moyo, pamenepo mudzazindikira kuti anthu amenewa ananyoza Yehova.” (Sheol )
But, if, a creation, Yahweh create, and the ground open wide her mouth and swallow them up, with all that pertain unto them, and so they go down alive unto hades, then shall ye know, that these men have despised Yahweh. (Sheol )
31 Atangotsiriza kuyankhula zimenezi, nthaka ya pamene anayimapo inagawikana
And it came to pass as he made an end of speaking all these words, that the ground which was under them, clave asunder;
32 ndipo dziko linatsekula pakamwa pake ndi kuwameza pamodzi ndi nyumba zawo ndi anthu onse a Kora ndi katundu wawo yense.
and the earth opened her mouth, and swallowed up them, and their households, —and all the human beings who pertained unto Korah, with all their goods:
33 Analowa mʼmanda amoyo pamodzi ndi zonse zimene anali nazo. Nthaka inawatsekera ndi kuwawononga ndipo sanaonekenso. (Sheol )
so, they, and all that pertained unto them, went down, alive unto hades, —and the earth, closed upon them, and they perished out of the midst of the convocation. (Sheol )
34 Atamva kulira kwawo, Aisraeli onse amene anali pafupi ndi anthuwo anathawa akufuwula kuti, “Nthaka imezanso ife!”
And, all Israel who were round about them, fled at their cry, —for they said, Lest the earth swallow us up.
35 Ndipo moto wochokera kwa Yehova unabwera nʼkunyeketsa anthu 250 amene ankapereka nsembe yofukiza aja.
Fire also came forth, from Yahweh, —and consumed the two hundred and fifty men, who offered the incense.
36 Yehova anawuza Mose kuti,
Then spake Yahweh unto Moses, saying:
37 “Uza Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe kuti atenge zofukizirazo pakati pa mitembo yopsererayo ndipo amwazire makalawo kutali chifukwa zofukizirazo nʼzopatulika.
Say unto Eleazar, son of Aaron the priest, that he take up the censers out of the midst of the burning, and the fire, scatter thou yonder, —for they have been hallowed.
38 Izi ndi zofukizira za anthu omwe anafa chifukwa cha uchimo wawo. Musule zofukizirazo kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe, chifukwa zinaperekedwa kwa Yehova ndipo ndi zopatulika. Zimenezi zikhale chizindikiro kwa Aisraeli.”
As for the censers of these sinners against their own persons, they shall be made into beaten-out plates as an overlay for the altar, for they had brought them near before Yahweh and hallowed them, —so shall they become a sign unto the sons of Israel.
39 Choncho Eliezara, wansembe, anasonkhanitsa zofukizira zamkuwa zija zomwe anthu opsererawo anabwera nazo ndipo anazisula kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe,
And Eleazar the priest took the censers of bronze, which the consumed men had brought near, —and beat them out into plates for overlaying the altar:
40 monga momwe Yehova anamulangizira kudzera mwa Mose. Chimenechi chinali chikumbutso kwa Aisraeli kuti munthu wina aliyense, kupatula zidzukulu za Aaroni, sayenera kupsereza lubani pamaso pa Yehova, kuopa kuti munthu woteroyo angakhale ngati Kora ndi omutsatira ake.
a memorial unto the sons of Israel, That no stranger, who is not of the seed of Aaron, shall draw near to offer incense before Yahweh, —lest he become like Korah and like his assembly, As spake Yahweh by the hand of Moses with regard thereto.
41 Tsiku lotsatira, gulu lonse la Aisraeli linatsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Iwo anati, “Inu mwapha anthu a Yehova.”
And all the assembly of the sons of Israel murmured, on the morrow, against Moses and against, Aaron, saying, —Ye, have caused the death of the people of Yahweh.
42 Koma pamene anthuwo anasonkhana kuti atsutsane ndi Mose ndi Aaroni, atatembenuka kuyangʼana ku tenti ya msonkhano, mwadzidzidzi mtambo unaphimba tentiyo ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera.
And it came to pass, when the assembly gathered themselves together against Moses and against Aaron, that they turned towards the tent of meeting, and lo! the cloud had covered it: and the glory of Yahweh, appeared.
43 Pamenepo Mose ndi Aaroni anapita patsogolo pa tenti ya msonkhano ija
And Moses and Aaron came in, before the tent of meeting.
44 ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
Then spake Yahweh unto Moses, saying:
45 “Chokani pakati pa gulu la anthuwa kuti ndiwawononge kamodzinʼkamodzi.” Ndipo iwo anagwa pansi chafufumimba.
Lift yourselves up out of the midst of this assembly, that I may consume them, as in a moment, —And they fell upon their faces.
46 Kenaka Mose anawuza Aaroni kuti, “Tenga chofukizira chako ndipo ikamo lubani pamodzi ndi moto wochokera pa guwa lansembe, fulumira, pita pa gulu la anthuwo ndipo ukachite nsembe yopepesera machimo awo popeza mkwiyo wa Yehova wafika, mliri wayamba.”
Then said Moses unto Aaron—Take the censer and place thereon fire, from off the altar, and put incense [thereon], and, going quickly into the assembly, put a propitiatory-covering over them, —for wrath hath gone forth from before Yahweh the plague, hath begun.
47 Ndipo Aaroni anachita monga ananenera Mose, nathamangira mʼkatikati mwa gulu la anthuwo. Pamenepo nʼkuti mliri utayamba kale pakati pa anthu aja ndipo Aaroni anafukiza lubani ndi kupereka nsembe yopepesera machimo awo.
Then took Aaron, as Moses spake, and ran into the midst of the convocation, and lo! the plague had begun among the people, —so he placed the incense, and put a propitiatory-covering over the people:
48 Iye anayimirira pakati pa anthu amoyo ndi akufa ndipo mliri unaleka.
thus did he take his stand between the dead and the living, —and the plague was restrained.
49 Komabe anthu 14, 700 anafa ndi mliriwo, kuwonjezera pa aja amene anafa chifukwa cha Kora.
And so it was that they who died in the plague were fourteen thousand and seven hundred, —besides them who died over the matter of Korah.
50 Ndipo Aaroni anabwerera kwa Mose ku khomo la tenti ya msonkhano, chifukwa mliriwo unali utatha.
And Aaron returned unto Moses, unto the entrance of the tent of meeting, —when, the plague, had been restrained.