< Numeri 16 >

1 Kora mwana wa Izihari, mwana wa Kohati, mwana wa Levi ndi Datani ndi Abiramu ana a Eliabu, pamodzi ndi Oni mwana wa Perezi, ana a Rubeni, anayamba kudzikuza,
Chóre pak syn Izarův, syna Kahat z pokolení Léví, vytrhl se z jiných, tolikéž Dátan a Abiron, synové Eliabovi, také Hon, syn Feletův, z synů Rubenových,
2 ndipo anawukira Mose. Mʼgulu mwawo munali atsogoleri a Aisraeli 250, anthu otchuka amene anasankhidwa ndi anthu pa msonkhano.
A povstali proti Mojžíšovi, i jiných mužů z synů Izraelských dvě stě a padesáte, knížata shromáždění, kteříž svoláváni byli do rady, muži slovoutní.
3 Iwo anasonkhana kudzatsutsana ndi Mose ndi Aaroni nawawuza kuti, “Mwawonjeza! Anthu onsewa ndi oyera, aliyense wa iwo, ndipo Yehova ali pakati pawo. Chifukwa chiyani mukudzikuza pakati pa gulu lonse la Yehova?”
A sebravše se proti Mojžíšovi a proti Aronovi, řekli jim: Příliště to již na vás; všecko zajisté množství toto, všickni tito svatí jsou, a u prostřed nich jest Hospodin. Pročež se tedy vyzdvihujete nad shromážděním Hospodinovým?
4 Mose atamva izi, anagwa chafufumimba.
To když uslyšel Mojžíš, padl na tvář svou,
5 Ndipo iye anawuza Kora ndi anthu onse amene ankamutsatira kuti, “Yehova mawa mmawa adzasonyeza yemwe ndi wake ndiponso amene ndi woyera mtima. Munthuyo adzabwera pafupi ndi Iye. Munthu amene adzamusankheyo adzamusendeza pafupi.
A mluvil k Chóre a ke vší rotě jeho, řka: Ráno ukáže Hospodin, kdo jsou jeho, a kdo jest svatý, i kdo před něj předstupovati má; nebo kohožkoli vyvolil, tomu rozkáže přistoupiti k sobě.
6 Iwe Kora pamodzi ndi onse amene akukutsatira chitani izi: Tengani zofukizira
Toto učiňte: Vezměte sobě kadidlnice, ty Chóre i všecko shromáždění tvé,
7 ndipo mawa muyikemo moto ndi lubani pamaso pa Yehova. Munthu amene Yehova amusankhe ndiye amene ali woyera. Alevi inu mwawonjeza kwambiri!”
A naklaďte do nich uhlí, a vložte na ně kadidla před Hospodinem zítra; i stane se, že kohožkoli vyvolí Hospodin, ten bude svatý. Příliště to již na vás, synové Léví.
8 Mose anawuzanso Kora kuti, “Inu Alevi, tsopano tamverani!
I řekl Mojžíš k Chóre: Slyšte, prosím, synové Léví.
9 Kodi sizinakukwanireni kuti Mulungu wa Israeli anakupatulani pakati pa gulu lonse la Aisraeli ndi kukubweretsani pafupi ndi Iye, kuti muzigwira ntchito ku nyumba ya Yehova ndi kumayima pamaso pa gulu, kumatumikira?
Zdaliž málo vám to jest, že vás oddělil Bůh Izraelský ode všeho množství Izraelského, a rozkázal vám přistupovati k sobě, abyste vykonávali službu příbytku Hospodinova, a abyste stáli před shromážděním, a sloužili jim,
10 Wakubweretsa iwe pamodzi ndi Alevi anzako kufupi ndi Iye mwini. Koma tsopano ukufuna kutenganso unsembe.
A vzal tě sobě, a všecky bratří tvé syny Léví s tebou, a že ještě přes to i kněžství hledáte?
11 Nʼkulakwira Yehova kuti iwe ndi gulu lako lonseli mwasonkhana kuti mutsutsane ndi Yehova. Kodi Aaroni ndani kuti muzikangana naye?”
Protož věz, že ty a všickni tvoji jste ti, kteříž se rotíte proti Hospodinu; nebo Aron co jest, že jste reptali proti němu?
12 Kenaka Mose anayitana Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu koma iwo anati, “Sitibwera!
Tedy poslal Mojžíš, aby zavolali Dátana a Abirona, synů Eliabových. Kteříž odpověděli: Nepůjdem.
13 Kodi sikukwanira kuti unatitulutsa, kutichotsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kuti udzatiphe mʼchipululu muno? Kodi tsopano ukufunanso kutilemetsa?
Cožť se ještě málo zdá, že jsi vyvedl nás z země oplývající mlékem a strdí, abys nás zmořil na poušti, že také chceš i panovati nad námi, a rozkazovati nám?
14 Kuwonjezera apo, sunatilowetse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kapena kutipatsa malo wolima ndi minda ya mpesa. Kodi ukufuna kuchotsa maso a anthuwa? Ayi, sitibwera!”
A ještě jsi nás neuvedl do země oplývající mlékem a strdí, aniž jsi nám dal v dědictví rolí a vinic. Zdali oči mužům těmto vyloupiti chceš? Nepůjdeme.
15 Pamenepo Mose anakwiya kwambiri ndipo anati kwa Yehova, “Musalandire chopereka chawo. Sindinatenge kalikonse kwa iwo ngakhale bulu, ndiponso sindinalakwire wina aliyense wa iwo.”
I rozhněval se Mojžíš velmi, a řekl k Hospodinu: Nepatřiž na oběti jejich. Ani jednoho osla od nich jsem nevzal, aniž jsem komu z nich co zlého učinil.
16 Mose anati kwa Kora, “Iwe ndi okutsatira onse mudzaonekere pamaso pa Yehova mawa, iweyo ndi iwowo pamodzi ndi Aaroni.
Potom řekl Mojžíš k Chóre: Ty a všickni tvoji, postavte se zítra před Hospodinem, ty i oni, též i Aron.
17 Munthu aliyense akatenge chofukizira ndi kuyikamo lubani, zofukizira 250 zonse pamodzi ndi kuzibweretsa pamaso pa Yehova. Iwe ndi Aaroni mudzabweretsenso zofukizira zanu.”
A vezmouce jeden každý kadidlnici svou, dáte do nich kadidla, a postavíte se před Hospodinem, jeden každý s kadidlnicí svou; dvě stě a padesáte kadidlnic bude, ty také i Aron, každý s kadidlnicí svou.
18 Choncho munthu aliyense anatenga chofukizira chake nayikamo moto ndi lubani, ndipo anayima pamodzi ndi Mose ndi Aaroni pa khomo la tenti ya msonkhano.
Tedy vzal jeden každý kadidlnici svou, a nabravše do nich uhlí, vložili na ně i kadidla, a stáli u dveří stánku úmluvy, i Mojžíš i Aron.
19 Kora atasonkhanitsa omutsatira ake onse amene amatsutsa nawo pa khomo la tenti ya msonkhano, ulemerero wa Yehova unaonekera kwa gulu lonselo.
Chóre pak již byl sebral proti nim všecko množství ke dveřím stánku úmluvy; i ukázala se sláva Hospodinova všemu množství.
20 Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
I mluvil Hospodin k Mojžíšovi a k Aronovi, řka:
21 “Chokani pakati pa gulu ili kuti ndithetse mkanganowu kamodzinʼkamodzi.”
Oddělte se z prostředku množství tohoto, ať je v okamžení zahladím.
22 Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa chafufumimba ndipo analira mokweza, “Chonde Mulungu, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, kodi mudzakwiyira gulu lonse pamene munthu mmodzi yekha ndiye amene wachimwa?”
Kteřížto padše na tváři své, řekli: Bože silný, Bože duchů i všelikého těla, jediný tento člověk zhřešil, a což na všecko shromáždění hněvati se budeš?
23 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti,
Tedy mluvil Hospodin k Mojžíšovi, řka:
24 “Uza gulu lonse kuti, ‘Khalani kutali ndi matenti a Kora, Datani ndi Abiramu.’”
Mluv k množství a rci: Odstupte od příbytku Chóre, Dátana a Abirona.
25 Mose anayimirira napita kwa Datani, Abiramu ndi kwa akuluakulu a Israeli amene ankamutsatira.
A vstav Mojžíš, šel k Dátanovi a Abironovi; i šli za ním starší Izraelští.
26 Anachenjeza gulu lonse kuti, “Khalani kutali ndi matenti a anthu oyipawa! Musakhudze kanthu kawo kalikonse, mukatero mudzawonongedwa limodzi nawo chifukwa cha machimo awo.”
A mluvil k množství, řka: Odstupte, prosím, od stanů bezbožných mužů těchto, aniž se čeho dotýkejte, což jejich jest, abyste nebyli zachváceni ve všech hříších jejich.
27 Choncho anthuwo anachokadi ku matenti a Kora, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali atatuluka nayima pamodzi ndi akazi awo, ana awo ndi makanda awo pa makomo a matenti awo.
I odstoupili se všech stran od příbytku Chóre, Dátana a Abirona; ale Dátan a Abiron vyšedše, stáli u dveří stanů svých, i ženy jejich a synové jejich, i maličcí jejich.
28 Tsono Mose anati, “Umu ndi mmene mudzadziwire kuti Yehova ndiye amene anandituma kuti ndichite zinthu zonsezi ndipo kuti si maganizo anga.
Tedy řekl Mojžíš: Po tomto poznáte, že Hospodin poslal mne, abych činil všecky skutky tyto, a že nic o své ujmě ne činím:
29 Ngati anthu awa afa ndi imfa ya chilengedwe ndi kuwachitikira zomwe zimachitikira munthu aliyense, ndiye kuti Yehova sananditume.
Jestliže tak jako jiní lidé mrou, zemrou i tito, a navštívením obecným všechněm lidem jestliže navštíveni budou, neposlal mne Hospodin.
30 Koma Yehova akachita china chake chachilendo, nthaka nitsekula pakamwa pake ndi kuwameza iwo pamodzi ndi zonse zimene ali nazo, iwowa nʼkulowa mʼmanda ali moyo, pamenepo mudzazindikira kuti anthu amenewa ananyoza Yehova.” (Sheol h7585)
Pakliť něco nového učiní Hospodin, a země, otevra ústa svá, požře je se vším, což mají, a sstoupí-li za živa do pekla, tedy poznáte, že jsou popouzeli muži ti Hospodina. (Sheol h7585)
31 Atangotsiriza kuyankhula zimenezi, nthaka ya pamene anayimapo inagawikana
I stalo se, když přestal mluviti slov těch, že rozstoupila se země pod nimi.
32 ndipo dziko linatsekula pakamwa pake ndi kuwameza pamodzi ndi nyumba zawo ndi anthu onse a Kora ndi katundu wawo yense.
A otevřevši země ústa svá, požřela je i domy jejich i všecky lidi, kteříž byli s Chóre, i všecken statek jejich.
33 Analowa mʼmanda amoyo pamodzi ndi zonse zimene anali nazo. Nthaka inawatsekera ndi kuwawononga ndipo sanaonekenso. (Sheol h7585)
A tak sstoupili oni se vším, což měli, za živa do pekla, a přikryla je země; i zahynuli z prostředku shromáždění. (Sheol h7585)
34 Atamva kulira kwawo, Aisraeli onse amene anali pafupi ndi anthuwo anathawa akufuwula kuti, “Nthaka imezanso ife!”
Všickni pak Izraelští, kteříž byli vůkol nich, utíkali, slyšíce křik jejich; nebo řekli: Utecme, aby i nás nesehltila země.
35 Ndipo moto wochokera kwa Yehova unabwera nʼkunyeketsa anthu 250 amene ankapereka nsembe yofukiza aja.
Vyšel také oheň od Hospodina, a spálil těch dvě stě a padesáte mužů, kteříž kadili.
36 Yehova anawuza Mose kuti,
Tedy mluvil Hospodin k Mojžíšovi, řka:
37 “Uza Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe kuti atenge zofukizirazo pakati pa mitembo yopsererayo ndipo amwazire makalawo kutali chifukwa zofukizirazo nʼzopatulika.
Rci Eleazarovi, synu Arona kněze, ať sbéře kadidlnice z toho spáleniště, a uhlí z nich pryč rozmece, nebo posvěceny jsou,
38 Izi ndi zofukizira za anthu omwe anafa chifukwa cha uchimo wawo. Musule zofukizirazo kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe, chifukwa zinaperekedwa kwa Yehova ndipo ndi zopatulika. Zimenezi zikhale chizindikiro kwa Aisraeli.”
Kadidlnice totiž těch, kteříž proti svým dušem hřešili, a ať je rozkuje na plechy k obložení oltáře; nebo kadili jimi před Hospodinem, protož posvěceny jsou, a budou na znamení synům Izraelským.
39 Choncho Eliezara, wansembe, anasonkhanitsa zofukizira zamkuwa zija zomwe anthu opsererawo anabwera nazo ndipo anazisula kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe,
I sebral Eleazar kněz kadidlnice měděné, jimiž kadili ti, kteříž spáleni jsou, a rozkovali je k obložení oltáře,
40 monga momwe Yehova anamulangizira kudzera mwa Mose. Chimenechi chinali chikumbutso kwa Aisraeli kuti munthu wina aliyense, kupatula zidzukulu za Aaroni, sayenera kupsereza lubani pamaso pa Yehova, kuopa kuti munthu woteroyo angakhale ngati Kora ndi omutsatira ake.
Pro budoucí pamět synům Izraelským, aby nepřistupoval žádný jiný, kdož by nebyl z rodu Aronova, k kadění před Hospodinem, aby se mu nestalo jako Chóre a jako rotě jeho, jakož byl mluvil jemu Hospodin skrze Mojžíše.
41 Tsiku lotsatira, gulu lonse la Aisraeli linatsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Iwo anati, “Inu mwapha anthu a Yehova.”
Nazejtří pak reptalo všecko množství synů Izraelských na Mojžíše a na Arona, řkouce: Vy jste příčinou smrti lidu Hospodinova.
42 Koma pamene anthuwo anasonkhana kuti atsutsane ndi Mose ndi Aaroni, atatembenuka kuyangʼana ku tenti ya msonkhano, mwadzidzidzi mtambo unaphimba tentiyo ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera.
I stalo se, když se opět sbíral lid proti Mojžíšovi a proti Aronovi, že se ohlédli k stánku úmluvy, a aj, přikryl jej oblak, a ukázala se sláva Hospodinova.
43 Pamenepo Mose ndi Aaroni anapita patsogolo pa tenti ya msonkhano ija
Přišel také Mojžíš s Aronem před stánek úmluvy.
44 ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
I mluvil Hospodin k Mojžíšovi, řka:
45 “Chokani pakati pa gulu la anthuwa kuti ndiwawononge kamodzinʼkamodzi.” Ndipo iwo anagwa pansi chafufumimba.
Vyjděte z prostředku množství tohoto, a zahladím je v okamžení. I padli na tváři své.
46 Kenaka Mose anawuza Aaroni kuti, “Tenga chofukizira chako ndipo ikamo lubani pamodzi ndi moto wochokera pa guwa lansembe, fulumira, pita pa gulu la anthuwo ndipo ukachite nsembe yopepesera machimo awo popeza mkwiyo wa Yehova wafika, mliri wayamba.”
Tedy řekl Mojžíš Aronovi: Vezma kadidlnici, dej do ní uhlí z oltáře, a vlož kadidla, a běž rychle k množství a očisť je; nebo vyšla prchlivost od tváři Hospodinovy, a již rána se začala.
47 Ndipo Aaroni anachita monga ananenera Mose, nathamangira mʼkatikati mwa gulu la anthuwo. Pamenepo nʼkuti mliri utayamba kale pakati pa anthu aja ndipo Aaroni anafukiza lubani ndi kupereka nsembe yopepesera machimo awo.
I vzav Aron kadidlnici, jakž rozkázal Mojžíš, běžel do prostřed shromáždění, (a aj, rána již se byla začala v lidu, ) a zakadiv, očistil lid.
48 Iye anayimirira pakati pa anthu amoyo ndi akufa ndipo mliri unaleka.
A stál mezi mrtvými a živými; i zastavena jest rána.
49 Komabe anthu 14, 700 anafa ndi mliriwo, kuwonjezera pa aja amene anafa chifukwa cha Kora.
Bylo pak těch, kteříž od té rány zemřeli, čtrnácte tisíců a sedm set, kromě těch, jenž zemřeli příčinou Chóre.
50 Ndipo Aaroni anabwerera kwa Mose ku khomo la tenti ya msonkhano, chifukwa mliriwo unali utatha.
I navrátil se Aron k Mojžíšovi, ke dveřím stánku úmluvy, když ta rána přetržena byla.

< Numeri 16 >