< Numeri 15 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Entonces el Señor le dijo a Moisés:
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo,
“Dile a los israelitas, ‘Estas son la instrucciones sobre lo que deben hacer una vez que lleguen al país que les doy para vivir:
3 ndipo mukamadzapereka kwa Yehova, nsembe yotentha pa moto ya ngʼombe kapena nkhosa monga fungo lokoma kwa Yehova, kaya ndi nsembe yopsereza kapena nsembe zina, nsembe yapadera chifukwa cha lumbiro kapena nsembe yoperekedwa mwaufulu kapenanso yoperekedwa pa chikondwerero,
Cuando traiga una ofrenda al Señor de tu ganado o rebaño (ya sea un holocausto, un sacrificio para cumplir una promesa que hiciste, o una ofrenda de libre albedrío o de fiesta) que sea aceptable para el Señor,
4 munthu amene akubweretsa zopereka zake, azikapereka kwa Yehova chopereka chachakudya cholemera kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta wokwana lita imodzi.
entonces también presentarás una ofrenda de grano de una décima parte de un efa de la mejor harina mezclada con un cuarto de hin de aceite de oliva.
5 Pamodzi ndi mwana wankhosa aliyense wa nsembe yopsereza kapena nsembe ina, muzikakonzanso lita imodzi la vinyo ngati chopereka cha chakumwa.’”
Añade un cuarto de hin de vino como ofrenda de bebida al holocausto o al sacrificio de un cordero.
6 “Pamodzi ndi nkhosa yayimuna, muzikakonzanso chopereka cha chakudya cholemera makilogalamu awiri a ufa wosalala, wosakaniza ndi mafuta okwanira lita imodzi ndi theka,
“Cuando se trate de un carnero, presenta una ofrenda de grano de dos décimas de efa de la mejor harina mezclada con un tercio de hin de aceite de oliva,
7 ndi vinyo wokwanira lita imodzi ndi theka ngati chopereka cha chakumwa. Muzikapereka monga nsembe yopereka fungo lokoma kwa Yehova.
junto con un tercio de hin de vino como ofrenda de bebida, todo ello para ser aceptable al Señor.
8 “‘Pamene mukukonza mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse: ya lumbiro lapadera kapena nsembe yachiyanjano kwa Yehova,
“Cuando traigas un novillo como holocausto o sacrificio para cumplir una promesa que hiciste o como ofrenda de paz al Señor,
9 pamodzi ndi mwana wangʼombe wamwamunayo muzibweretsa nsembe yachakudya yolemera makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta okwana malita awiri.
también llevarás con el novillo una ofrenda de grano de tres décimas de efa de la mejor harina mezclada con medio hin de aceite de oliva.
10 Komanso muzibweretsa vinyo wokwanira malita awiri monga chopereka chachakumwa. Imeneyi idzakhala chopereka chotentha pa moto kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova.
Añade medio hin de vino como ofrenda de bebida. Todo esto es una ofrenda para ser aceptable al Señor.
11 Ngʼombe yayimuna iliyonse kapena nkhosa yayimuna iliyonse, mwana wankhosa aliyense kapena mbuzi yayingʼono, zizikonzedwa motere.
“Esto debe hacerse por cada toro, carnero, cordero o cabra que se traiga como ofrenda.
12 Ngakhale zingachuluke chotani, chitani izi kwa iliyonse ya nyamazo.
Esto es lo que tienes que hacer para cada uno, sin importar cuántos sean.
13 “‘Mbadwa iliyonse ya mu Israeli izichita zimenezi pamene ibweretsa nsembe yotentha pa moto kuti ikhale fungo lokoma kwa Yehova.
Todo israelita debe seguir estas instrucciones cuando presente una ofrenda que sea aceptable para el Señor.
14 Ku mibado yanu yonse ya mʼtsogolo, pamene mlendo kapena wina aliyense wokhala pakati panu apereka chopereka chotentha pa moto kuti chikhale fungo lokoma kwa Yehova, azichita mofanana ndi momwe inu mumachitira.
Esto también se aplica a todas las generaciones futuras que si un extranjero que vive entre ustedes o cualquier otra persona entre ustedes desea presentar una ofrenda aceptable para el Señor: deben hacer exactamente lo que ustedes hacen.
15 Gulu lonse likhale ndi malamulo ofanana a inu kapena mlendo wokhala pakati panu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya kwa mibado imene ikubwera. Inuyo ndi mlendo mudzakhala wofanana pamaso pa Yehova.
Toda la congregación debe tener las mismas reglas para ustedes y para el extranjero que vive entre ustedes. Esta es una ley permanente para todas las generaciones futuras. Tú y el extranjero deben ser tratados de la misma manera ante la ley.
16 Mudzakhale ndi malamulo ndi miyambo yofanana, inuyo ndi mlendo wokhala pakati panu.’”
Las mismas reglas y normas se aplican a ustedes y al extranjero que vive entre ustedes’”.
17 Yehova anawuza Mose kuti,
El Señor le dijo a Moisés:
18 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo unene kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukutengeraniko
“Diles a los israelitas: ‘Cuando lleguen al país al que yo los llevo
19 ndipo mukakadya chakudya cha mʼdzikolo, mukapereke gawo lina kwa Yehova monga chopereka.
y cománde los alimentos que allí se producen, darán parte de ellos como ofrenda al Señor.
20 Pa buledi wanu woyamba, mukapereke mmodzi monga nsembe, ngati chopereka chochokera ku malo wopunthira tirigu.
Darán como ofrenda una parte de la harina que usen para hacer los panes, y la presentarás como una ofrenda de la era.
21 Pa mibado yanu yonse muzidzapereka chopereka ichi kwa Yehova kuchokera ku zakudya zanu zoyamba za mʼnthaka.
Para todas las generaciones futuras, darás al Señor una ofrenda de la primera de tus harinas.
22 “‘Ndipo ngati muchimwa mosadziwa posasunga ena mwa malamulo awa amene Yehova wapereka kwa Mose,
“Ahora bien, si pecan colectivamente sin querer y no siguen todas estas instrucciones que el Señor ha dado a Moisés,
23 lina lililonse mwa malamulo a Yehova amene wapereka kwa inu kudzera mwa Mose, kuyambira tsiku limene Yehova anawapereka mpaka mibado ya mʼtsogolo,
s decir, todo lo que el Señor les ha ordenado hacer a través de Moisés desde el momento en que el Señor les dio y para todas las generaciones futuras,
24 ndipo ngati zimenezi zachitika osati mwadala ndipo gulu lonse silinadziwe, zikatero gulu lonselo lipereke mwana wangʼombe wamwamuna monga nsembe yopsereza kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova pamodzinso ndi chopereka chachakudya ndi chopereka cha chakumwa ndi mbuzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo potsata zimene zinalamulidwa.
y si se hizo sin querer y sin que todos lo supieran, entonces toda la congregación debe presentar un novillo como holocausto para ser aceptado por el Señor, junto con su ofrenda de grano y su libación presentada según las reglas, así como un macho cabrío como ofrenda por el pecado.
25 Wansembe apereke nsembe yopepesera machimo a gulu lonse la Aisraeli, ndipo adzakhululukidwa, pakuti linali tchimo lochita mosadziwa. Ndipo chifukwa cha tchimo lawolo, abweretse kwa Yehova nsembe yotentha pa moto ndi nsembe yopepesera machimo.
De esta manera el sacerdote debe hacer que toda la congregación de Israel esté bien con el Señor para que puedan ser perdonados, porque el pecado fue involuntario y han presentado al Señor un holocausto y una ofrenda por el pecado, ofrecida ante el Señor por su pecado involuntario.
26 Gulu lonse la Aisraeli ndi alendo okhala pakati pawo adzakhululukidwa chifukwa anthu onsewo anachimwa mosadziwa.
Entonces toda la congregación de Israel y los extranjeros que viven entre ellos serán perdonados, porque el pueblo pecó sin intención.
27 “‘Koma ngati munthu mmodzi achimwa mosadziwa, ayenera kubweretsa mbuzi yayikazi ya chaka chimodzi kuti ikhale nsembe yopepesera machimo.
“En el caso de un individuo que peca sin intención, deben presentar una cabra hembra de un año como ofrenda por el pecado.
28 Wansembe apereke nsembe yopepesera machimowo pamaso pa Yehova chifukwa cha munthu yemwe anachimwa mosadziwayo. Nsembe yopepesera tchimo lakelo ikaperekedwa, munthuyo adzakhululukidwa.
El sacerdote hará que la persona que pecó sin querer esté en su derecho ante el Señor. Una vez que hayan sido expiados, serán perdonados.
29 Lamulo lomweli ligwiritsidwe ntchito kwa aliyense wochimwa mosadziwa, kaya ndi mbadwa ya mu Israeli kapena mlendo.
Aplicarás la misma ley para el que peca por error a un israelita o a un extranjero que viva entre ustedes.
30 “‘Koma aliyense amene achimwa mwadala, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, nachitira chipongwe Yehova, ameneyo achotsedwe ndithu pakati pa anthu ake.
“Pero la persona que peca a manera de desafío, ya sea un israelita o un extranjero, está blasfemando al Señor. Serán expulsados de su pueblo.
31 Popeza wanyoza mawu a Yehova ndi kuphwanya malamulo ake. Munthu ameneyo achotsedwe ndithu, kuchimwa kwake kudzakhala pa iyeyo.’”
Deben ser expulsados, porque han tratado la palabra del Señor con desprecio y han quebrantado su mandamiento. Son responsables de las consecuencias de su propia culpa’”.
32 Aisraeli ali mʼchipululu, munthu wina anapezeka akutola nkhuni tsiku la Sabata.
Durante el tiempo en que los israelitas vagaban por el desierto, un hombre fue sorprendido recogiendo leña en el día Sábado.
33 Amene anamupeza akutola nkhunizo anabwera naye kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa gulu lonse
Las personas que lo encontraron recogiendo leña lo llevaron ante Moisés, Aarón y el resto de los israelitas.
34 ndipo anamutsekera mʼndende chifukwa sankadziwa choti achite naye.
Lo pusieron bajo vigilancia porque no estaba claro qué le iba a pasar.
35 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Munthu ameneyu ayenera kuphedwa. Gulu lonse liyenera kumugenda ndi miyala kunja kwa msasa.”
El Señor le dijo a Moisés: “Este hombre tiene que ser ejecutado. Todos los israelitas deben apedrearlo fuera del campamento”.
36 Choncho gululo linamutengera kunja kwa msasa ndi kumupha pomugenda ndi miyala, monga momwe Yehova analamulira Mose.
Así que todos tomaron al hombre fuera del campamento y lo apedrearon hasta la muerte como el Señor había ordenado a Moisés.
37 Yehova anawuza Mose kuti,
Poco después el Señor le dijo a Moisés:
38 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pa mibado yanu yonse muzisokerera mphonje pa ngodya za zovala zanu ndipo pa ngodya ya mphonje iliyonse azisokererapo chingwe chobiriwira.
“Diles a los israelitas que para todas las generaciones futuras harán borlas para los dobladillos de tu ropa y deberán atarlas con un cordón azul.
39 Mudzakhala ndi mphonje zimenezi kuti mukaziona muzikakumbukira malamulo onse a Yehova ndi kuwamvera kuti musamatsatenso zilakolako za mʼmitima mwanu ndi za maso anu.
Cuando miren estas borlas recordarán que deben guardar todos los mandamientos del Señor y que no sean infieles, siguiendo sus propios pensamientos y deseos.
40 Motero mudzakumbukira kumvera malamulo anga ndipo mudzakhala opatulikira a Mulungu wanu.
De esta manera serecordarán que deben guardar todos mis mandamientos y serán santos para Dios. Yo soy el Señor su Dios que los sacó de Egipto para ser su Dios.
41 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
¡Yo soy el Señor su Dios!”

< Numeri 15 >