< Numeri 15 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah speaketh unto Moses, saying,
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo,
'Speak unto the sons of Israel, and thou hast said unto them, When ye come in unto the land of your dwellings, which I am giving to you,
3 ndipo mukamadzapereka kwa Yehova, nsembe yotentha pa moto ya ngʼombe kapena nkhosa monga fungo lokoma kwa Yehova, kaya ndi nsembe yopsereza kapena nsembe zina, nsembe yapadera chifukwa cha lumbiro kapena nsembe yoperekedwa mwaufulu kapenanso yoperekedwa pa chikondwerero,
then ye have prepared a fire-offering to Jehovah, a burnt-offering, or a sacrifice, at separating a vow or free-will-offering, or in your appointed things, to make a sweet fragrance to Jehovah, out of the herd, or out of the flock.
4 munthu amene akubweretsa zopereka zake, azikapereka kwa Yehova chopereka chachakudya cholemera kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta wokwana lita imodzi.
'And he who is bringing near his offering to Jehovah hath brought near a present of flour, a tenth deal, mixed with a fourth of the hin of oil;
5 Pamodzi ndi mwana wankhosa aliyense wa nsembe yopsereza kapena nsembe ina, muzikakonzanso lita imodzi la vinyo ngati chopereka cha chakumwa.’”
and wine for a libation, a fourth of the hin thou dost prepare for the burnt-offering or for a sacrifice, for the one lamb;
6 “Pamodzi ndi nkhosa yayimuna, muzikakonzanso chopereka cha chakudya cholemera makilogalamu awiri a ufa wosalala, wosakaniza ndi mafuta okwanira lita imodzi ndi theka,
or for a ram thou dost prepare a present of flour, two-tenth deals, mixed with oil, a third of the hin;
7 ndi vinyo wokwanira lita imodzi ndi theka ngati chopereka cha chakumwa. Muzikapereka monga nsembe yopereka fungo lokoma kwa Yehova.
and wine for a libation, a third part of the hin, thou dost bring near — a sweet fragrance to Jehovah.
8 “‘Pamene mukukonza mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse: ya lumbiro lapadera kapena nsembe yachiyanjano kwa Yehova,
'And when thou makest a son of the herd a burnt-offering or a sacrifice, at separating a vow or peace-offerings to Jehovah,
9 pamodzi ndi mwana wangʼombe wamwamunayo muzibweretsa nsembe yachakudya yolemera makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta okwana malita awiri.
then he hath brought near for the son of the herd a present of flour, three-tenth deals, mixed with oil, a half of the hin;
10 Komanso muzibweretsa vinyo wokwanira malita awiri monga chopereka chachakumwa. Imeneyi idzakhala chopereka chotentha pa moto kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova.
and wine thou bringest near for a libation, a half of the hin — a fire-offering of sweet fragrance to Jehovah;
11 Ngʼombe yayimuna iliyonse kapena nkhosa yayimuna iliyonse, mwana wankhosa aliyense kapena mbuzi yayingʼono, zizikonzedwa motere.
thus it is done for the one ox, or for the one ram, or for a lamb of the sheep or of the goats.
12 Ngakhale zingachuluke chotani, chitani izi kwa iliyonse ya nyamazo.
'According to the number that ye prepare, so ye do to each, according to their number;
13 “‘Mbadwa iliyonse ya mu Israeli izichita zimenezi pamene ibweretsa nsembe yotentha pa moto kuti ikhale fungo lokoma kwa Yehova.
every native doth thus with these, at bringing near a fire-offering of sweet fragrance to Jehovah;
14 Ku mibado yanu yonse ya mʼtsogolo, pamene mlendo kapena wina aliyense wokhala pakati panu apereka chopereka chotentha pa moto kuti chikhale fungo lokoma kwa Yehova, azichita mofanana ndi momwe inu mumachitira.
and when a sojourner sojourneth with you, or whoso [is] in your midst to your generations, and he hath made a fire-offering of sweet fragrance to Jehovah, as ye do so he doth.
15 Gulu lonse likhale ndi malamulo ofanana a inu kapena mlendo wokhala pakati panu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya kwa mibado imene ikubwera. Inuyo ndi mlendo mudzakhala wofanana pamaso pa Yehova.
'One statute is for you of the congregation and for the sojourner who is sojourning, a statute age-during to your generations: as ye [are] so is the sojourner before Jehovah;
16 Mudzakhale ndi malamulo ndi miyambo yofanana, inuyo ndi mlendo wokhala pakati panu.’”
one law and one ordinance is to you and to the sojourner who is sojourning with you.'
17 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah speaketh unto Moses, saying,
18 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo unene kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukutengeraniko
'Speak unto the sons of Israel, and thou hast said unto them, In your coming in unto the land whither I am bringing you in,
19 ndipo mukakadya chakudya cha mʼdzikolo, mukapereke gawo lina kwa Yehova monga chopereka.
then it hath been, in your eating of the bread of the land, ye heave up a heave-offering to Jehovah;
20 Pa buledi wanu woyamba, mukapereke mmodzi monga nsembe, ngati chopereka chochokera ku malo wopunthira tirigu.
the beginning of your dough a cake ye heave up — a heave-offering; as the heave-offering of a threshing-floor, so ye do heave it.
21 Pa mibado yanu yonse muzidzapereka chopereka ichi kwa Yehova kuchokera ku zakudya zanu zoyamba za mʼnthaka.
Of the beginning of your dough ye do give to Jehovah a heave-offering — to your generations.
22 “‘Ndipo ngati muchimwa mosadziwa posasunga ena mwa malamulo awa amene Yehova wapereka kwa Mose,
'And when ye err, and do not all these commands which Jehovah hath spoken unto Moses,
23 lina lililonse mwa malamulo a Yehova amene wapereka kwa inu kudzera mwa Mose, kuyambira tsiku limene Yehova anawapereka mpaka mibado ya mʼtsogolo,
the whole that Jehovah hath charged upon you by the hand of Moses, from the day that Jehovah hath commanded, and henceforth, to your generations,
24 ndipo ngati zimenezi zachitika osati mwadala ndipo gulu lonse silinadziwe, zikatero gulu lonselo lipereke mwana wangʼombe wamwamuna monga nsembe yopsereza kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova pamodzinso ndi chopereka chachakudya ndi chopereka cha chakumwa ndi mbuzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo potsata zimene zinalamulidwa.
then it hath been, if from the eyes of the company it hath been done in ignorance, that all the company have prepared one bullock, a son of the herd, for a burnt-offering, for sweet fragrance to Jehovah, and its present, and its libation, according to the ordinance, and one kid of the goats for a sin-offering.
25 Wansembe apereke nsembe yopepesera machimo a gulu lonse la Aisraeli, ndipo adzakhululukidwa, pakuti linali tchimo lochita mosadziwa. Ndipo chifukwa cha tchimo lawolo, abweretse kwa Yehova nsembe yotentha pa moto ndi nsembe yopepesera machimo.
'And the priest hath made atonement for all the company of the sons of Israel, and it hath been forgiven them, for it [is] ignorance, and they — they have brought in their offering, a fire-offering to Jehovah, even their sin-offering before Jehovah for their ignorance;
26 Gulu lonse la Aisraeli ndi alendo okhala pakati pawo adzakhululukidwa chifukwa anthu onsewo anachimwa mosadziwa.
and it hath been forgiven to all the company of the sons of Israel, and to the sojourner who is sojourning in their midst; for to all the company [it is done] in ignorance.
27 “‘Koma ngati munthu mmodzi achimwa mosadziwa, ayenera kubweretsa mbuzi yayikazi ya chaka chimodzi kuti ikhale nsembe yopepesera machimo.
'And if one person sin in ignorance, then he hath brought near a she-goat, daughter of a year, for a sin-offering;
28 Wansembe apereke nsembe yopepesera machimowo pamaso pa Yehova chifukwa cha munthu yemwe anachimwa mosadziwayo. Nsembe yopepesera tchimo lakelo ikaperekedwa, munthuyo adzakhululukidwa.
and the priest hath made atonement for the person who is erring, in his sinning in ignorance before Jehovah, by making atonement for him, and it hath been forgiven him;
29 Lamulo lomweli ligwiritsidwe ntchito kwa aliyense wochimwa mosadziwa, kaya ndi mbadwa ya mu Israeli kapena mlendo.
for the native among the sons of Israel, and for the sojourner who is sojourning in their midst — one law is to you, for him who is doing [anything] through ignorance.
30 “‘Koma aliyense amene achimwa mwadala, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, nachitira chipongwe Yehova, ameneyo achotsedwe ndithu pakati pa anthu ake.
'And the person who doth [aught] with a high hand — of the native or of the sojourner — Jehovah he is reviling, and that person hath been cut off from the midst of his people;
31 Popeza wanyoza mawu a Yehova ndi kuphwanya malamulo ake. Munthu ameneyo achotsedwe ndithu, kuchimwa kwake kudzakhala pa iyeyo.’”
because the word of Jehovah he despised, and His command hath broken — that person is certainly cut off; his iniquity [is] on him.'
32 Aisraeli ali mʼchipululu, munthu wina anapezeka akutola nkhuni tsiku la Sabata.
And the sons of Israel are in the wilderness, and they find a man gathering wood on the sabbath-day,
33 Amene anamupeza akutola nkhunizo anabwera naye kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa gulu lonse
and those finding him gathering wood bring him near unto Moses, and unto Aaron, and unto all the company,
34 ndipo anamutsekera mʼndende chifukwa sankadziwa choti achite naye.
and they place him in ward, for it [is] not explained what is [to be] done to him.
35 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Munthu ameneyu ayenera kuphedwa. Gulu lonse liyenera kumugenda ndi miyala kunja kwa msasa.”
And Jehovah saith unto Moses, 'The man is certainly put to death, all the company stoning him with stones, at the outside of the camp.'
36 Choncho gululo linamutengera kunja kwa msasa ndi kumupha pomugenda ndi miyala, monga momwe Yehova analamulira Mose.
And all the company bring him out unto the outside of the camp, and stone him with stones, and he dieth, as Jehovah hath commanded Moses.
37 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah speaketh unto Moses, saying,
38 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pa mibado yanu yonse muzisokerera mphonje pa ngodya za zovala zanu ndipo pa ngodya ya mphonje iliyonse azisokererapo chingwe chobiriwira.
'Speak unto the sons of Israel, and thou hast said unto them, and they have made for themselves fringes on the skirts of their garments, to their generations, and they have put on the fringe of the skirt a ribbon of blue,
39 Mudzakhala ndi mphonje zimenezi kuti mukaziona muzikakumbukira malamulo onse a Yehova ndi kuwamvera kuti musamatsatenso zilakolako za mʼmitima mwanu ndi za maso anu.
and it hath been to you for a fringe, and ye have seen it, and have remembered all the commands of Jehovah, and have done them, and ye search not after your heart, and after your eyes, after which ye are going a-whoring;
40 Motero mudzakumbukira kumvera malamulo anga ndipo mudzakhala opatulikira a Mulungu wanu.
so that ye remember and have done all My commands, and ye have been holy to your God;
41 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
I [am] Jehovah your God, who hath brought you out from the land of Egypt to become your God; I, Jehovah, [am] your God.'

< Numeri 15 >