< Numeri 14 >

1 Usiku umenewo gulu lonse la Aisraeli linalira mofuwula kwambiri.
Lenhlangano yonke yasiziphakamisa, yazwakalisa ilizwi layo; abantu basebekhala inyembezi ngalobobusuku.
2 Ndipo Aisraeli onse anayankhula motsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Gulu lonse linanena kwa iwo kuti, “Kunali bwino tikanafera ku Igupto kapena mʼchipululu muno!
Bonke abantwana bakoIsrayeli basebengunguna bemelene loMozisi loAroni; lenhlangano yonke yathi kubo: Kungathi ngabe safela elizweni leGibhithe, kumbe kungathi ngabe safela kule inkangala!
3 Nʼchifukwa chiyani Yehova akutilowetsa mʼdziko limenelo? Kodi kuti tikaphedwe ndi lupanga? Kuti akazi ndi ana athu akatengedwe ngati katundu wolanda ku nkhondo? Kodi sikungakhale bwino kuti tibwerere ku Igupto?”
Njalo kungani iNkosi isilethe kulelilizwe ukuthi siwe ngenkemba? Omkethu labantwanyana bethu bazakuba yimpango. Bekungebe ngcono kithi ukubuyela eGibhithe yini?
4 Ndipo anawuzana wina ndi mnzake kuti, “Tiyeni tisankhe mtsogoleri ndipo tibwerere ku Igupto.”
Basebesithi omunye komunye: Asimiseni inhloko, sibuyele eGibhithe.
5 Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa pansi chafufumimba pamaso pa Aisraeli onse omwe anasonkhana pamenepo.
UMozisi loAroni basebesithi mbo ngobuso babo phambi kwebandla lonke lenhlangano yabantwana bakoIsrayeli.
6 Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune, omwe anali amodzi mwa amene anakazonda nawo dziko, anangʼamba zovala zawo
UJoshuwa indodana kaNuni loKalebi indodana kaJefune ababengabalabo abahlola ilizwe, basebedabula izembatho zabo,
7 ndipo anati kwa gulu lonse la Aisraeli, “Dziko limene tinakayendamo ndi kuliona ndi labwino kwambiri zedi.
bakhuluma kunhlangano yonke yabantwana bakoIsrayeli besithi: Ilizwe esadabula kulo ukuze silihlole yilizwe elihle kakhulukazi.
8 Ngati Yehova akukondwera nafe, adzatitsogolera kulowa mʼdziko limenelo. Dziko loyenda mkaka ndi uchi adzalipereka kwa ife,
Uba iNkosi ithokoza ngathi, izasingenisa kulelilizwe, isinike lona, ilizwe eligeleza uchago loluju.
9 koma musawukire Yehova. Komanso musaope anthu a mʼdzikomo, pakuti tidzawagonjetsa. Chitetezo chawachokera, koma ife Yehova ali nafe. Musawaope.”
Kuphela lingayivukeli iNkosi; futhi lina lingesabi abantu belizwe, ngoba bayikudla kwethu. Umthunzi wabo usukile kubo; leNkosi ilathi; lingabesabi.
10 Koma gulu lonse linayankhula zofuna kuwagenda miyala. Pamenepo ulemerero wa Yehova unaonekera kwa Aisraeli onse ku tenti ya msonkhano.
Kodwa inhlangano yonke yathi kabakhandwe ngamatshe. Inkazimulo yeNkosi yasibonakala ethenteni lenhlangano kubo bonke abantwana bakoIsrayeli.
11 Yehova anawuza Mose kuti, “Anthu awa adzandinyoza mpaka liti? Sadzandikhulupirira mpaka liti, ngakhale ndachita zizindikiro zozizwitsa zonsezi pakati pawo?
INkosi yasisithi kuMozisi: Koze kube nini lababantu bengidelela? Koze kube nini bengangikholwa, ngazo zonke izibonakaliso engizenze phakathi kwabo?
12 Ndidzawakantha ndi mliri ndi kuwawononga. Koma ndidzakusandutsa iwe mtundu waukulu ndi wamphamvu kuposa iwo.”
Ngizabatshaya ngomatshayabhuqe wesifo, ngibathathele ilifa, ngikwenze ube yisizwe esikhulu lesilamandla kulabo.
13 Mose anati kwa Yehova, “Aigupto adzamva zimenezi! Mwa mphamvu yanu munawatulutsa anthu amenewa pakati pawo.
UMozisi wasesithi eNkosini: Khona amaGibhithe azakuzwa; ngoba wenyuse lababantu phakathi kwawo ngamandla akho.
14 Ndipo iwowo adzawuza anthu okhala mʼdziko lino zimenezi. Anthuwa amva kale kuti Inu Yehova mumakhala pakati pa anthu amenewa ndi kuti Inuyo Yehova mwawaonekera maso ndi maso. Mtambo wanu umakhala pamwamba pawo ndiponso mumayenda nawo mu mtambo woyima, masana ndi moto woyima, usiku.
Njalo azatshela abahlali balelilizwe. Bazwile ukuthi wena Nkosi uphakathi kwalababantu, ukuthi wena Nkosi ubonwa ubuso ngobuso, lokuthi iyezi lakho lima phezu kwabo, uhamba phambi kwabo usensikeni yeyezi emini lensikeni yomlilo ebusuku.
15 Tsono mukawapha anthu onsewa nthawi imodzi, mayiko amene anamva za Inu adzati,
Uba ubulala lababantu njengomuntu oyedwa, izizwe ezizwe ngendumela yakho zizakhuluma zisithi:
16 ‘Yehova walephera kuwalowetsa anthuwo mʼdziko lomwe anawalonjeza molumbira, ndipo wawapha mʼchipululu.’
Ngoba iNkosi yayingelakho ukungenisa lababantu elizweni eyabafungela lona, ngakho ibabulele enkangala.
17 “Chonde Ambuye wonetsani mphamvu yanu monga munalonjezera kuti,
Khathesi-ke, ngiyancenga, kawabe makhulu amandla eNkosi yami, njengokutsho kwakho usithi:
18 ‘Yehova sakwiya msanga, ndipo ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika, wokhululukira tchimo ndi kuwukira. Koma Iye sadzaleka kulanga ochimwa. Iyeyo amalanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo kufikira mʼbado wachitatu ndi wachinayi.’
INkosi iyaphuza ukuthukuthela, njalo inkulu emuseni, ithethelela ububi leziphambeko, kodwa engayikumyekela lokumyekela olecala, iphindisela ububi baboyise phezu kwabantwana kwesesithathu lesesine isizukulwana.
19 Chifukwa cha kukula kwa chikondi chanu chosasinthika, akhululukireni anthuwa tchimo lawo monga mwakhala mukuwakhululukira kuchokera pa nthawi imene anachoka ku Igupto mpaka tsopano.”
Thethelela, ngiyancenga, ububi balababantu njengobukhulu bomusa wakho, lanjengalokho ubathethelele lababantu kusukela eGibhithe kuze kube khathesi.
20 Yehova anayankha kuti, “Ndawakhululukira monga wapemphera.
INkosi yasisithi: Sengibathethelele njengokwelizwi lakho.
21 Komabe, ndikunenetsa kuti pali Ine, ndiponso pamene dziko lapansi ladzaza ndi ulemerero wa Yehova,
Kodwa isibili, njengalokhu ngiphila, umhlaba wonke uzagcwala ngenkazimulo yeNkosi.
22 palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu amene anaona ulemerero wanga ndi zizindikiro zozizwitsa zimene ndinazichita ku Igupto ndi mʼchipululu muno, koma osandimvera ndi kundiyesa kokwanira kakhumi,
Ngoba wonke amadoda abone inkazimulo yami lezibonakaliso zami engazenza eGibhithe lenkangala, langilingileyo lezizikhathi ezilitshumi, kawezwanga ilizwi lami,
23 palibe ndi mmodzi yemwe wa anthu amenewa amene adzaone dziko limene ndinalonjeza ndi lumbiro kwa makolo awo. Aliyense amene anandinyoza sadzaliona dzikolo.
isibili kabayikubona ilizwe engalifungela oyise; futhi kakho owalabo abangideleleyo ozalibona.
24 Koma mtumiki wanga Kalebe, pakuti ali ndi mtima wosiyana ndi ena ndiponso amanditsatira ndi mtima wonse, ndidzamulowetsa mʼdziko limene anapitamolo ndipo zidzukulu zake zidzalandira dzikolo ngati cholowa chawo.
Kodwa inceku yami uKalebi, ngoba omunye umoya ubulaye, wangilandela ngokupheleleyo; ngakho ngizamngenisa elizweni ayengene kilo; lenzalo yakhe izakudla ilifa lalo.
25 Ndipo popeza kuti Aamaleki ndi Akanaani akukhala ku chigwa, mawa mubwerere ndipo mupite ku chipululu podzera ku Nyanja Yofiira.”
(AmaAmaleki lamaKhanani ahlala-ke esigodini.) Kusasa phendukani, lisuke liziyele enkangala ngendlela yoLwandle oluBomvu.
26 Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
INkosi yasikhuluma kuMozisi lakuAroni isithi:
27 “Kodi anthu oyipawa adzangʼungʼudza ndi kutsutsana nane mpaka liti? Ndamva madandawulo a Aisraeli ongʼungʼudzawa.
Koze kube nini ngilalinhlangano embi, engingungunelayo? Ngizwile ukungunguna kwabantwana bakoIsrayeli abangunguna ngakho bemelene lami.
28 Tsono awuze kuti, ‘Ndikulumbira pali Ine,’ akutero Yehova, ‘Ndidzakuchitirani zinthu zonse zimene ndamva inu mukunena:
Tshono kibo uthi: Sibili njengoba ngiphila, kutsho iNkosi, njengalokhu likhulume endlebeni zami, ngizakwenza njalo kini.
29 Mitembo yanu idzakhala ili ngundangunda mʼchipululu muno; mtembo wa munthu aliyense pakati panu amene ali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, amene anawerengedwa pa chiwerengero chija ndipo anangʼungʼudza motsutsana nane.
Izidumbu zenu zizawela enkangala le, labo bonke ababaliweyo benu, njengokwenani lonke lenu, kusukela koleminyaka engamatshumi amabili langaphezulu, lina abangingunguneleyo;
30 Palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene adzalowe mʼdziko lomwe ndinalumbira mokweza manja kuti likhale lanu, kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.
sibili lina kaliyikungena elizweni engiliphakamisele isandla sami ukulihlalisa kulo, ngaphandle kukaKalebi indodana kaJefune loJoshuwa indodana kaNuni.
31 Koma ana anu amene mukunena kuti adzatengedwa ngati katundu wolanda ku nkhondo, Ine ndidzawalowetsa kuti akasangalale mʼdziko limene munalikana.
Kodwa abantwanyana benu elathi ngabo bazakuba yimpango, ngizabangenisa, bazalazi ilizwe elalilahlayo.
32 Koma inu mitembo yanu idzakhala ngundangunda mʼchipululu muno.
Lina-ke, izidumbu zenu zizawela kulinkangala.
33 Ana anu adzakhala abusa mʼchipululu muno zaka makumi anayi, kuvutika chifukwa cha kusakhulupirika kwanu, mpaka munthu womaliza mwa inu atafa mʼchipululu muno.
Labantwana benu bazakuba ngabelusi enkangala iminyaka engamatshumi amane, bathwale ukuphinga kwenu, izidumbu zenu zize ziphele enkangala.
34 Mudzavutika chifukwa cha machimo anu kwa zaka makumi anayi Chaka chimodzi chikuyimira tsiku limodzi la masiku makumi anayi amene munakazonda dziko lija ndipo mudzadziwa kuyipa kwake kwa kukangana ndi Ine.’
Njengokwenani lezinsuku elahlola ngazo ilizwe, insuku ezingamatshumi amane, usuku ngomnyaka, usuku ngomnyaka, lizathwala ububi benu, iminyaka engamatshumi amane, lazi ukufulathela kwami.
35 Ine Yehova, ndanena, ndidzachitadi zimenezi kwa anthu onse oyipawa, amene agwirizana kunditsutsa. Adzathera mʼchipululu momwe muno, adzafera muno basi.”
Mina Nkosi ngikhulumile. Isibili ngizakwenza lokhu kulinhlangano yonke embi ebuthene imelene lami; kulinkangala bazaphela, bafele khona.
36 Ndipo anthu amene Mose anawatuma kukazonda dziko aja anachoka pamaso pake nachititsa gulu lonse la anthu kuwukira Moseyo chifukwa chofalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo.
Njalo amadoda uMozisi awathumayo ukuhlola ilizwe, esephenduka, enza inhlangano yonke yamngungunela ngokuletha umbiko omubi mayelana lelizwe,
37 Anthu amene ankafalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo anakanthidwa ndi mliri ndipo anafa pamaso pa Yehova.
lamadoda aletha umbiko omubi ngelizwe afa ngenhlupheko phambi kweNkosi.
38 Mwa anthu amene anakaona dzikolo, Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune ndi okhawo amene anapulumuka.
Kodwa uJoshuwa indodana kaNuni loKalebi indodana kaJefune, kulawomadoda ayeyehlola ilizwe, asala ephila.
39 Mose atafotokoza izi kwa Aisraeli onse, anthuwo analira kwambiri.
Njalo uMozisi wakhuluma la amazwi kubo bonke abantwana bakoIsrayeli; abantu basebelila kakhulu.
40 Mmamawa tsiku linalo anapita mbali ya ku dziko la mapiri. Iwo anati, “Tachimwa, tipita ku dziko limene Yehova anatilonjeza.”
Basebevuka ekuseni kakhulu, benyukela engqongeni yentaba, besithi: Khangelani silapha, sizakwenyukela endaweni iNkosi eyithembisileyo; ngoba sonile.
41 Koma Mose anati, “Chifukwa chiyani simukumvera lamulo la Yehova? Zimenezi sizitheka!
Kodwa uMozisi wathi: Kungani-ke liseqa umlayo weNkosi? Ngoba kakuyikuphumelela.
42 Musapite chifukwa Yehova sali pakati panu. Mudzagonjetsedwa ndi adani anu
Lingenyuki, ngoba iNkosi kayikho phakathi kwenu, ukuze lingatshaywa phambi kwezitha zenu.
43 chifukwa kumeneko mukakumana ndi Aamaleki ndi Akanaani. Popeza mwaleka kutsata Yehova, Iyeyo sadzakhala nanu ndipo mudzaphedwa ndi lupanga.”
Ngoba amaAmaleki lamaKhanani alapho phambi kwenu; njalo lizakuwa ngenkemba, ngoba njengoba liphendukile ekulandeleni iNkosi, iNkosi kayiyikuba lani.
44 Komabe mwa maganizo awo anapita molunjika dziko la mapiri ngakhale kuti Mose sanachoke ndi Bokosi la Chipangano la Yehova pa msasa.
Kodwa ngokuziqhenya benyukela engqongeni yentaba, kodwa umtshokotsho wesivumelwano seNkosi loMozisi kawuphumanga phakathi kwenkamba.
45 Koma Aamaleki ndi Akanaani amene ankakhala ku dziko lamapirilo anatsika ndi kumenyana nawo ndipo anawakantha mʼnjira yonse mpaka ku Horima.
AmaAmaleki asesehla, lamaKhanani ahlala kulezozintaba, abatshaya, abahlakaza kwaze kwaba seHorma.

< Numeri 14 >