< Numeri 14 >

1 Usiku umenewo gulu lonse la Aisraeli linalira mofuwula kwambiri.
Ainsi toute la multitude vociférant, pleura cette nuit-là.
2 Ndipo Aisraeli onse anayankhula motsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Gulu lonse linanena kwa iwo kuti, “Kunali bwino tikanafera ku Igupto kapena mʼchipululu muno!
Et tous les enfants d’Israël murmurèrent contre Moïse et Aaron, disant:
3 Nʼchifukwa chiyani Yehova akutilowetsa mʼdziko limenelo? Kodi kuti tikaphedwe ndi lupanga? Kuti akazi ndi ana athu akatengedwe ngati katundu wolanda ku nkhondo? Kodi sikungakhale bwino kuti tibwerere ku Igupto?”
Plût Dieu que nous fussions morts en Egypte! et plût à Dieu que nous périssions dans cette vaste solitude, et que le Seigneur ne nous conduise pas dans cette terre, afin que nous ne tombions point sous le glaive, et que nos femmes et nos enfants ne soient pas amenés captifs! Ne vaut-il pas mieux retourner en Egypte?
4 Ndipo anawuzana wina ndi mnzake kuti, “Tiyeni tisankhe mtsogoleri ndipo tibwerere ku Igupto.”
Et ils se dirent l’un à l’autre: Etablissons-nous un chef, et retournons en Egypte.
5 Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa pansi chafufumimba pamaso pa Aisraeli onse omwe anasonkhana pamenepo.
Ce qu’ayant entendu. Moïse et Aaron tombèrent inclinés vers la terre devant toute la multitude des enfants d’Israël.
6 Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune, omwe anali amodzi mwa amene anakazonda nawo dziko, anangʼamba zovala zawo
Mais Josué, fils de Nun, et Caleb, fils de Jéphoné, qui avaient aussi eux-mêmes parcouru la terre, déchirèrent leurs vêtements,
7 ndipo anati kwa gulu lonse la Aisraeli, “Dziko limene tinakayendamo ndi kuliona ndi labwino kwambiri zedi.
Et dirent à toute la multitude des enfants d’Israël: La terre dont nous avons fait le tour est très bonne.
8 Ngati Yehova akukondwera nafe, adzatitsogolera kulowa mʼdziko limenelo. Dziko loyenda mkaka ndi uchi adzalipereka kwa ife,
Si le Seigneur est propice, il nous y conduira et nous donnera ce sol où coulent du lait et du miel.
9 koma musawukire Yehova. Komanso musaope anthu a mʼdzikomo, pakuti tidzawagonjetsa. Chitetezo chawachokera, koma ife Yehova ali nafe. Musawaope.”
Ne soyez point rebelles contre le Seigneur, et ne craignez point le peuple de cette terre, parce que nous pouvons les dévorer comme du pain: tout secours les a abandonnés: le Seigneur est avec nous; ne craignez point.
10 Koma gulu lonse linayankhula zofuna kuwagenda miyala. Pamenepo ulemerero wa Yehova unaonekera kwa Aisraeli onse ku tenti ya msonkhano.
Et, comme toute la multitude criait et voulait les lapider, la gloire du Seigneur apparut sur le toit d’alliance à tous les enfants d’Israël.
11 Yehova anawuza Mose kuti, “Anthu awa adzandinyoza mpaka liti? Sadzandikhulupirira mpaka liti, ngakhale ndachita zizindikiro zozizwitsa zonsezi pakati pawo?
Et le Seigneur dit à Moïse: Jusqu’à quand ce peuple m’outragera-t-il? Jusqu’à quand ne me croiront-ils pas, après tous les miracles que j’ai faits devant eux?
12 Ndidzawakantha ndi mliri ndi kuwawononga. Koma ndidzakusandutsa iwe mtundu waukulu ndi wamphamvu kuposa iwo.”
Je les frapperai donc de la peste, et je les détruirai entièrement: et pour toi, je te ferai prince sur une nation grande, et plus forte que n’est celle-ci.
13 Mose anati kwa Yehova, “Aigupto adzamva zimenezi! Mwa mphamvu yanu munawatulutsa anthu amenewa pakati pawo.
Et Moïse répondit au Seigneur: C’est donc pour que les Egyptiens du milieu desquels vous avez retiré ce peuple, apprennent, eux
14 Ndipo iwowo adzawuza anthu okhala mʼdziko lino zimenezi. Anthuwa amva kale kuti Inu Yehova mumakhala pakati pa anthu amenewa ndi kuti Inuyo Yehova mwawaonekera maso ndi maso. Mtambo wanu umakhala pamwamba pawo ndiponso mumayenda nawo mu mtambo woyima, masana ndi moto woyima, usiku.
Et les habitants de cette terre (qui ont ouï dire que vous, Seigneur, vous êtes au milieu de ce peuple, que vous y êtes vu face à face, que votre nuée les couvre, que vous les précédez dans une colonne de nuée pendant le jour, et dans une colonne de feu pendant la nuit),
15 Tsono mukawapha anthu onsewa nthawi imodzi, mayiko amene anamva za Inu adzati,
Que vous avez fait mourir une si grande multitude comme un seul homme, et qu’ils disent:
16 ‘Yehova walephera kuwalowetsa anthuwo mʼdziko lomwe anawalonjeza molumbira, ndipo wawapha mʼchipululu.’
Il ne pouvait pas introduire ce peuple dans la terre au sujet de laquelle il avait juré. C’est pourquoi il les a fait mourir dans le désert.
17 “Chonde Ambuye wonetsani mphamvu yanu monga munalonjezera kuti,
Que la force du Seigneur soit donc glorifiée, comme vous l’avez juré, disant:
18 ‘Yehova sakwiya msanga, ndipo ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika, wokhululukira tchimo ndi kuwukira. Koma Iye sadzaleka kulanga ochimwa. Iyeyo amalanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo kufikira mʼbado wachitatu ndi wachinayi.’
Le Seigneur est patient et d’une abondante miséricorde, effaçant l’iniquité et les crimes, et ne délaissant aucun innocent; vous qui visitez les péchés des pères dans les fils jusqu’à la troisième et quatrième génération,
19 Chifukwa cha kukula kwa chikondi chanu chosasinthika, akhululukireni anthuwa tchimo lawo monga mwakhala mukuwakhululukira kuchokera pa nthawi imene anachoka ku Igupto mpaka tsopano.”
Remettez, je vous conjure, le péché de ce peuple, selon la grandeur de votre miséricorde, comme vous leur avez été propice depuis qu’ils sortirent de l’Egypte jusqu’en ce lieu.
20 Yehova anayankha kuti, “Ndawakhululukira monga wapemphera.
Et le Seigneur reprit: Je l’ai remis selon ta parole.
21 Komabe, ndikunenetsa kuti pali Ine, ndiponso pamene dziko lapansi ladzaza ndi ulemerero wa Yehova,
Je vis, moi: et toute la terre sera remplie de la gloire du Seigneur.
22 palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu amene anaona ulemerero wanga ndi zizindikiro zozizwitsa zimene ndinazichita ku Igupto ndi mʼchipululu muno, koma osandimvera ndi kundiyesa kokwanira kakhumi,
Mais cependant tous les hommes qui ont vu ma majesté et les miracles que j’ai faits en Egypte et dans le désert, qui m’ont déjà tenté par dix fois, et n’ont pas obéi à ma voix,
23 palibe ndi mmodzi yemwe wa anthu amenewa amene adzaone dziko limene ndinalonjeza ndi lumbiro kwa makolo awo. Aliyense amene anandinyoza sadzaliona dzikolo.
Ne verront pas la terre au sujet de laquelle j’ai juré à leurs pères, et qui que ce soit d’entre eux qui m’a outragé ne la verra pas.
24 Koma mtumiki wanga Kalebe, pakuti ali ndi mtima wosiyana ndi ena ndiponso amanditsatira ndi mtima wonse, ndidzamulowetsa mʼdziko limene anapitamolo ndipo zidzukulu zake zidzalandira dzikolo ngati cholowa chawo.
Quant à mon serviteur Caleb, qui, plein d’un autre esprit, m’a suivi, je l’introduirai dans cette terre dont il a fait le tour; et sa postérité la possédera.
25 Ndipo popeza kuti Aamaleki ndi Akanaani akukhala ku chigwa, mawa mubwerere ndipo mupite ku chipululu podzera ku Nyanja Yofiira.”
Parce que l’Amalécite et le Chananéen habitent dans les vallées, demain levez le camp et retournez au désert par le chemin de la mer Rouge.
26 Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
Le Seigneur parla encore à Moïse et à Aaron, disant:
27 “Kodi anthu oyipawa adzangʼungʼudza ndi kutsutsana nane mpaka liti? Ndamva madandawulo a Aisraeli ongʼungʼudzawa.
Jusqu’à quand cette multitude très méchante murmurera-t-elle contre moi? j’ai ouï les plaintes des enfants d’Israël.
28 Tsono awuze kuti, ‘Ndikulumbira pali Ine,’ akutero Yehova, ‘Ndidzakuchitirani zinthu zonse zimene ndamva inu mukunena:
Dis leur donc: Je vis, moi, dit le Seigneur: Comme vous avez parlé, moi l’entendant, ainsi je vous ferai.
29 Mitembo yanu idzakhala ili ngundangunda mʼchipululu muno; mtembo wa munthu aliyense pakati panu amene ali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, amene anawerengedwa pa chiwerengero chija ndipo anangʼungʼudza motsutsana nane.
C’est dans cette solitude que gésiront vos cadavres. Vous tous qui avez été dénombrés depuis vingt ans et au-dessus, et qui avez murmuré contre moi,
30 Palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene adzalowe mʼdziko lomwe ndinalumbira mokweza manja kuti likhale lanu, kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.
Vous n’entrerez point dans la terre sur laquelle j’ai levé ma main, que je vous la ferais habiter, excepté Caleb, fils de Jéphoné et Josué, fils de Nun.
31 Koma ana anu amene mukunena kuti adzatengedwa ngati katundu wolanda ku nkhondo, Ine ndidzawalowetsa kuti akasangalale mʼdziko limene munalikana.
Mais vos petits-enfants dont vous avez dit qu’ils seraient en proie aux ennemis, je les y introduirai, afin qu’ils voient la terre qui vous a déplu.
32 Koma inu mitembo yanu idzakhala ngundangunda mʼchipululu muno.
Vos cadavres gésiront dans cette solitude.
33 Ana anu adzakhala abusa mʼchipululu muno zaka makumi anayi, kuvutika chifukwa cha kusakhulupirika kwanu, mpaka munthu womaliza mwa inu atafa mʼchipululu muno.
Vos enfants seront errants dans le désert pendant quarante ans, ils porteront votre fornication, jusqu’à ce que soient consumés les cadavres de leurs pères dans le désert,
34 Mudzavutika chifukwa cha machimo anu kwa zaka makumi anayi Chaka chimodzi chikuyimira tsiku limodzi la masiku makumi anayi amene munakazonda dziko lija ndipo mudzadziwa kuyipa kwake kwa kukangana ndi Ine.’
Selon le nombre des quarante jours pendant lesquels vous avez considéré la terre: un an sera compté pour un jour. Et pendant quarante ans vous recevrez la peine de vos iniquités, et vous saurez ma vengeance;
35 Ine Yehova, ndanena, ndidzachitadi zimenezi kwa anthu onse oyipawa, amene agwirizana kunditsutsa. Adzathera mʼchipululu momwe muno, adzafera muno basi.”
Parce que, comme j’ai parlé, ainsi je ferai à toute cette multitude très méchante, qui s’est élevée contre moi: elle défaillira dans cette solitude et elle mourra.
36 Ndipo anthu amene Mose anawatuma kukazonda dziko aja anachoka pamaso pake nachititsa gulu lonse la anthu kuwukira Moseyo chifukwa chofalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo.
Ainsi, tous les hommes qu’avait envoyés Moïse pour considérer la terre et qui, revenus, avaient fait murmurer contre lui toute la multitude, décriant la terre comme si elle était mauvaise,
37 Anthu amene ankafalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo anakanthidwa ndi mliri ndipo anafa pamaso pa Yehova.
Moururent, ayant été frappés en la présence du Seigneur.
38 Mwa anthu amene anakaona dzikolo, Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune ndi okhawo amene anapulumuka.
Mais Josué, fils de Nun, et Caleb, fils de Jéphoné, vécurent seuls de tous ceux qui étaient allés pour considérer la terre.
39 Mose atafotokoza izi kwa Aisraeli onse, anthuwo analira kwambiri.
Or Moïse dit toutes ces paroles à tous les enfants d’Israël, et le peuple se lamenta beaucoup.
40 Mmamawa tsiku linalo anapita mbali ya ku dziko la mapiri. Iwo anati, “Tachimwa, tipita ku dziko limene Yehova anatilonjeza.”
Et voilà que, se levant de grand matin, ils montèrent sur le sommet de la montagne, et dirent: Nous sommes prêts à monter au lieu dont le Seigneur a parlé, parce que nous avons péché.
41 Koma Mose anati, “Chifukwa chiyani simukumvera lamulo la Yehova? Zimenezi sizitheka!
Pourquoi, leur dit Moïse, transgressez-vous la parole du Seigneur, ce qui ne vous tournera pas à bien?
42 Musapite chifukwa Yehova sali pakati panu. Mudzagonjetsedwa ndi adani anu
Ne montez point (car le Seigneur n’est point avec vous), de peur que vous ne succombiez devant vos ennemis.
43 chifukwa kumeneko mukakumana ndi Aamaleki ndi Akanaani. Popeza mwaleka kutsata Yehova, Iyeyo sadzakhala nanu ndipo mudzaphedwa ndi lupanga.”
L’Amalécite et le Chananéen sont devant vous; vous succomberez sous leur glaive, parce que vous n’avez pas voulu obéir au Seigneur, et le Seigneur ne sera pas avec vous.
44 Komabe mwa maganizo awo anapita molunjika dziko la mapiri ngakhale kuti Mose sanachoke ndi Bokosi la Chipangano la Yehova pa msasa.
Mais eux, couverts de ténèbres, montèrent sur le sommet de la montagne. Mais l’arche d’alliance du Seigneur et Moïse ne sortirent point du camp.
45 Koma Aamaleki ndi Akanaani amene ankakhala ku dziko lamapirilo anatsika ndi kumenyana nawo ndipo anawakantha mʼnjira yonse mpaka ku Horima.
Alors descendirent l’Amalécite et le Chananéen, qui habitaient sur la montagne, et les frappant et les taillant en pièces, ils les poursuivirent jusqu’à Horma.

< Numeri 14 >