< Numeri 14 >

1 Usiku umenewo gulu lonse la Aisraeli linalira mofuwula kwambiri.
Alors toute l'assemblée s'éleva, et se mit à jeter des cris, et le peuple pleura cette nuit-là.
2 Ndipo Aisraeli onse anayankhula motsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Gulu lonse linanena kwa iwo kuti, “Kunali bwino tikanafera ku Igupto kapena mʼchipululu muno!
Et tous les enfants d'Israël murmurèrent contre Moïse et contre Aaron; et toute l'assemblée leur dit: Plût à Dieu que nous fussions morts au pays d'Egypte, ou en ce désert! plût à Dieu que nous fussions morts!
3 Nʼchifukwa chiyani Yehova akutilowetsa mʼdziko limenelo? Kodi kuti tikaphedwe ndi lupanga? Kuti akazi ndi ana athu akatengedwe ngati katundu wolanda ku nkhondo? Kodi sikungakhale bwino kuti tibwerere ku Igupto?”
Et pourquoi l'Eternel nous conduit-il vers ce pays-là, pour y tomber par l'épée; nos femmes et nos petits enfants seront en proie. Ne nous vaudrait-il pas mieux retourner en Egypte?
4 Ndipo anawuzana wina ndi mnzake kuti, “Tiyeni tisankhe mtsogoleri ndipo tibwerere ku Igupto.”
Et ils se dirent l'un à l'autre: Etablissons-nous un chef, et retournons en Egypte.
5 Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa pansi chafufumimba pamaso pa Aisraeli onse omwe anasonkhana pamenepo.
Alors Moïse et Aaron tombèrent sur leurs visages devant toute l'assemblée des enfants d'Israël.
6 Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune, omwe anali amodzi mwa amene anakazonda nawo dziko, anangʼamba zovala zawo
Et Josué, fils de Nun, et Caleb, fils de Jéphunné, qui étaient de ceux qui avaient examiné le pays, déchirèrent leurs vêtements;
7 ndipo anati kwa gulu lonse la Aisraeli, “Dziko limene tinakayendamo ndi kuliona ndi labwino kwambiri zedi.
Et parlèrent à toute l'assemblée des enfants d'Israël, en disant: Le pays par lequel nous avons passé pour le reconnaître est un fort bon pays.
8 Ngati Yehova akukondwera nafe, adzatitsogolera kulowa mʼdziko limenelo. Dziko loyenda mkaka ndi uchi adzalipereka kwa ife,
Si nous sommes agréables à l'Eternel, il nous fera entrer en ce pays-là, et il nous le donnera. C'est un pays découlant de lait et de miel.
9 koma musawukire Yehova. Komanso musaope anthu a mʼdzikomo, pakuti tidzawagonjetsa. Chitetezo chawachokera, koma ife Yehova ali nafe. Musawaope.”
Seulement ne soyez point rebelles contre l'Eternel, et ne craignez point le peuple de ce pays-là; car ils seront notre pain; leur protection s'est retirée de dessus eux, et l'Eternel est avec nous; ne les craignez point.
10 Koma gulu lonse linayankhula zofuna kuwagenda miyala. Pamenepo ulemerero wa Yehova unaonekera kwa Aisraeli onse ku tenti ya msonkhano.
Alors toute l'assemblée parla de les lapider; mais la gloire de l'Eternel apparut à tous les enfants d'Israël au Tabernacle d'assignation.
11 Yehova anawuza Mose kuti, “Anthu awa adzandinyoza mpaka liti? Sadzandikhulupirira mpaka liti, ngakhale ndachita zizindikiro zozizwitsa zonsezi pakati pawo?
Et l'Eternel dit à Moïse: Jusques-à quand ce peuple-ci m'irritera-t-il par mépris, et jusques-à quand ne croira-t-il point en moi, après tous les signes que j'ai faits au milieu de lui?
12 Ndidzawakantha ndi mliri ndi kuwawononga. Koma ndidzakusandutsa iwe mtundu waukulu ndi wamphamvu kuposa iwo.”
Je le frapperai de mortalité, et je le détruirai; mais je te ferai devenir un peuple plus grand et plus fort qu'il n'est.
13 Mose anati kwa Yehova, “Aigupto adzamva zimenezi! Mwa mphamvu yanu munawatulutsa anthu amenewa pakati pawo.
Et Moïse dit à l'Eternel: Mais les Egyptiens l'entendront, car tu as fait monter par ta force ce peuple-ci du milieu d'eux.
14 Ndipo iwowo adzawuza anthu okhala mʼdziko lino zimenezi. Anthuwa amva kale kuti Inu Yehova mumakhala pakati pa anthu amenewa ndi kuti Inuyo Yehova mwawaonekera maso ndi maso. Mtambo wanu umakhala pamwamba pawo ndiponso mumayenda nawo mu mtambo woyima, masana ndi moto woyima, usiku.
Et ils diront avec les habitants de ce pays qui auront entendu que tu étais, ô Eternel! au milieu de ce peuple, et que tu apparaissais, ô Eternel! à vue d'œil, que ta nuée s'arrêtait sur eux, et que tu marchais devant eux le jour dans la colonne de nuée, et la nuit dans la colonne de feu;
15 Tsono mukawapha anthu onsewa nthawi imodzi, mayiko amene anamva za Inu adzati,
Quand tu auras fait mourir ce peuple, comme un seul homme, les nations qui auront entendu parler de ton Nom, tiendront ce langage.
16 ‘Yehova walephera kuwalowetsa anthuwo mʼdziko lomwe anawalonjeza molumbira, ndipo wawapha mʼchipululu.’
Parce que l'Eternel ne pouvait faire entrer ce peuple au pays qu il avait juré de leur donner, il les a tués au désert.
17 “Chonde Ambuye wonetsani mphamvu yanu monga munalonjezera kuti,
Or maintenant, je te prie, que la puissance du Seigneur soit magnifiée, comme tu as parlé, en disant:
18 ‘Yehova sakwiya msanga, ndipo ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika, wokhululukira tchimo ndi kuwukira. Koma Iye sadzaleka kulanga ochimwa. Iyeyo amalanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo kufikira mʼbado wachitatu ndi wachinayi.’
L'Eternel est tardif à colère, et abondant en gratuité, ôtant l'iniquité, et le péché, et qui ne tient nullement le coupable pour innocent, punissant l'iniquité des pères sur les enfants, jusqu'à la troisième et à la quatrième [génération].
19 Chifukwa cha kukula kwa chikondi chanu chosasinthika, akhululukireni anthuwa tchimo lawo monga mwakhala mukuwakhululukira kuchokera pa nthawi imene anachoka ku Igupto mpaka tsopano.”
Pardonne, je te prie, l'iniquité de ce peuple, selon la grandeur de ta gratuité, comme tu as pardonné à ce peuple, depuis l'Egypte jusqu'ici.
20 Yehova anayankha kuti, “Ndawakhululukira monga wapemphera.
Et l'Eternel dit: J'ai pardonné selon ta parole.
21 Komabe, ndikunenetsa kuti pali Ine, ndiponso pamene dziko lapansi ladzaza ndi ulemerero wa Yehova,
Mais certainement je suis vivant, et la gloire de l'Eternel remplira toute la terre.
22 palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu amene anaona ulemerero wanga ndi zizindikiro zozizwitsa zimene ndinazichita ku Igupto ndi mʼchipululu muno, koma osandimvera ndi kundiyesa kokwanira kakhumi,
Car quant à tous les hommes qui ont vu ma gloire, et les signes que j ai faits en Egypte et au désert qui m'ont déjà tenté par dix fois, et qui n ont point obéi à ma voix;
23 palibe ndi mmodzi yemwe wa anthu amenewa amene adzaone dziko limene ndinalonjeza ndi lumbiro kwa makolo awo. Aliyense amene anandinyoza sadzaliona dzikolo.
S'ils voient [jamais] le pays que j'avais juré à leurs pères de leur donner, tous ceux, dis-je, qui m'ont irrité par mépris, ne le verront point.
24 Koma mtumiki wanga Kalebe, pakuti ali ndi mtima wosiyana ndi ena ndiponso amanditsatira ndi mtima wonse, ndidzamulowetsa mʼdziko limene anapitamolo ndipo zidzukulu zake zidzalandira dzikolo ngati cholowa chawo.
Mais parce que mon serviteur Caleb a été animé d'un autre esprit, et qu'il a persévéré à me suivre, aussi le ferai-je entrer au pays où il a été, et sa postérité le possédera en héritage.
25 Ndipo popeza kuti Aamaleki ndi Akanaani akukhala ku chigwa, mawa mubwerere ndipo mupite ku chipululu podzera ku Nyanja Yofiira.”
Or les Hamalécites et les Cananéens habitent en la vallée; retournez demain en arrière, et vous en allez au désert par le chemin de la mer Rouge.
26 Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
L'Eternel parla aussi à Moïse et à Aaron, en disant:
27 “Kodi anthu oyipawa adzangʼungʼudza ndi kutsutsana nane mpaka liti? Ndamva madandawulo a Aisraeli ongʼungʼudzawa.
Jusques à quand [continuera] cette méchante assemblée qui murmure contre moi? J'ai entendu les murmures des enfants d'Israël, par lesquels ils murmurent contre moi.
28 Tsono awuze kuti, ‘Ndikulumbira pali Ine,’ akutero Yehova, ‘Ndidzakuchitirani zinthu zonse zimene ndamva inu mukunena:
Dis-leur: Je suis vivant, dit l'Eternel, si je ne vous fais ainsi que vous avez parlé, et comme je l'ai ouï.
29 Mitembo yanu idzakhala ili ngundangunda mʼchipululu muno; mtembo wa munthu aliyense pakati panu amene ali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, amene anawerengedwa pa chiwerengero chija ndipo anangʼungʼudza motsutsana nane.
Vos charognes tomberont dans ce désert, et tous ceux d'entre vous qui ont été dénombrés selon tout le compte que vous en avez fait, depuis l'âge de vingt ans, et au dessus, vous tous qui avez murmuré contre moi;
30 Palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene adzalowe mʼdziko lomwe ndinalumbira mokweza manja kuti likhale lanu, kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.
Si vous entrez au pays, pour lequel j'avais levé ma main, [jurant] que je vous y ferais habiter, excepté Caleb, fils de Jéphunné, et Josué, fils de Nun.
31 Koma ana anu amene mukunena kuti adzatengedwa ngati katundu wolanda ku nkhondo, Ine ndidzawalowetsa kuti akasangalale mʼdziko limene munalikana.
Et quant à vos petits enfants, dont vous avez dit qu'ils seraient en proie, je les y ferai entrer, et ils sauront quel est ce pays que vous avez méprisé.
32 Koma inu mitembo yanu idzakhala ngundangunda mʼchipululu muno.
Mais quant à vous, vos charognes tomberont dans ce désert.
33 Ana anu adzakhala abusa mʼchipululu muno zaka makumi anayi, kuvutika chifukwa cha kusakhulupirika kwanu, mpaka munthu womaliza mwa inu atafa mʼchipululu muno.
Mais vos enfants seront paissant dans ce désert quarante ans; et ils porteront [la peine de] vos paillardises, jusqu'à ce que vos charognes soient consumés au désert.
34 Mudzavutika chifukwa cha machimo anu kwa zaka makumi anayi Chaka chimodzi chikuyimira tsiku limodzi la masiku makumi anayi amene munakazonda dziko lija ndipo mudzadziwa kuyipa kwake kwa kukangana ndi Ine.’
Selon le nombre des jours que vous avez mis à reconnaître le pays, qui ont été quarante jours, un jour pour une année, vous porterez [la peine de] vos iniquités quarante ans, et vous connaîtrez que j'ai rompu le cours de mes bénédictions sur vous.
35 Ine Yehova, ndanena, ndidzachitadi zimenezi kwa anthu onse oyipawa, amene agwirizana kunditsutsa. Adzathera mʼchipululu momwe muno, adzafera muno basi.”
Je suis l'Eternel qui ai parlé, si je ne fais ceci à toute cette méchante assemblée, à ceux qui se sont assemblés contre moi; ils seront consumés en ce désert, et ils y mourront.
36 Ndipo anthu amene Mose anawatuma kukazonda dziko aja anachoka pamaso pake nachititsa gulu lonse la anthu kuwukira Moseyo chifukwa chofalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo.
Les hommes donc que Moïse avait envoyés pour épier le pays, et qui étant de retour avaient fait murmurer contre lui toute l'assemblée, en diffamant le pays;
37 Anthu amene ankafalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo anakanthidwa ndi mliri ndipo anafa pamaso pa Yehova.
Ces hommes-là qui avaient décrié le pays, moururent de plaie devant l'Eternel.
38 Mwa anthu amene anakaona dzikolo, Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune ndi okhawo amene anapulumuka.
Mais Josué, fils de Nun, et Caleb, fils de Jéphunné, vécurent d'entre ceux qui étaient allés reconnaître le pays.
39 Mose atafotokoza izi kwa Aisraeli onse, anthuwo analira kwambiri.
Or Moïse dit ces choses-là à tous les enfants d'Israël, et le peuple en mena un fort grand deuil.
40 Mmamawa tsiku linalo anapita mbali ya ku dziko la mapiri. Iwo anati, “Tachimwa, tipita ku dziko limene Yehova anatilonjeza.”
Puis s'étant levés de bon matin, ils montèrent sur le haut de la montagne, en disant: Nous voici, et nous monterons au lieu dont l'Eternel a parlé; car nous avons péché.
41 Koma Mose anati, “Chifukwa chiyani simukumvera lamulo la Yehova? Zimenezi sizitheka!
Mais Moïse leur dit: Pourquoi transgressez-vous le commandement de l'Eternel? cela ne réussira point.
42 Musapite chifukwa Yehova sali pakati panu. Mudzagonjetsedwa ndi adani anu
N'y montez point; car l'Eternel n'est point au milieu de vous; afin que vous ne soyez pas battus devant vos ennemis.
43 chifukwa kumeneko mukakumana ndi Aamaleki ndi Akanaani. Popeza mwaleka kutsata Yehova, Iyeyo sadzakhala nanu ndipo mudzaphedwa ndi lupanga.”
Car les Hamalécites et les Cananéens sont là devant vous, et vous tomberez par l'épée; à cause que vous avez cessé de suivre l'Eternel, l'Eternel aussi ne sera point avec vous.
44 Komabe mwa maganizo awo anapita molunjika dziko la mapiri ngakhale kuti Mose sanachoke ndi Bokosi la Chipangano la Yehova pa msasa.
Toutefois ils s'obstinèrent de monter sur le haut de la montagne, mais l'Arche de l'alliance de l'Eternel et Moïse ne bougèrent point du milieu du camp.
45 Koma Aamaleki ndi Akanaani amene ankakhala ku dziko lamapirilo anatsika ndi kumenyana nawo ndipo anawakantha mʼnjira yonse mpaka ku Horima.
Alors les Hamalécites et les Cananéens qui habitaient en cette montagne-là, descendirent, et les battirent, et les mirent en déroute jusqu'en Horma.

< Numeri 14 >