< Numeri 14 >

1 Usiku umenewo gulu lonse la Aisraeli linalira mofuwula kwambiri.
Toute l'assemblée éleva la voix et poussa des cris, et le peuple pleura cette nuit-là.
2 Ndipo Aisraeli onse anayankhula motsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Gulu lonse linanena kwa iwo kuti, “Kunali bwino tikanafera ku Igupto kapena mʼchipululu muno!
Tous les enfants d'Israël murmurèrent contre Moïse et contre Aaron. Toute l'assemblée leur dit: « Nous aurions voulu mourir au pays d'Égypte, ou mourir dans ce désert!
3 Nʼchifukwa chiyani Yehova akutilowetsa mʼdziko limenelo? Kodi kuti tikaphedwe ndi lupanga? Kuti akazi ndi ana athu akatengedwe ngati katundu wolanda ku nkhondo? Kodi sikungakhale bwino kuti tibwerere ku Igupto?”
Pourquoi Yahvé nous fait-il venir dans ce pays, pour que nous tombions par l'épée? Nos femmes et nos petits enfants seront capturés ou tués! Ne vaudrait-il pas mieux pour nous de retourner en Égypte? »
4 Ndipo anawuzana wina ndi mnzake kuti, “Tiyeni tisankhe mtsogoleri ndipo tibwerere ku Igupto.”
Ils se dirent les uns aux autres: « Choisissons un chef et retournons en Égypte. »
5 Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa pansi chafufumimba pamaso pa Aisraeli onse omwe anasonkhana pamenepo.
Et Moïse et Aaron tombèrent sur leur visage devant toute l'assemblée des enfants d'Israël.
6 Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune, omwe anali amodzi mwa amene anakazonda nawo dziko, anangʼamba zovala zawo
Josué, fils de Nun, et Caleb, fils de Jephunné, qui étaient de ceux qui avaient exploré le pays, déchirèrent leurs vêtements.
7 ndipo anati kwa gulu lonse la Aisraeli, “Dziko limene tinakayendamo ndi kuliona ndi labwino kwambiri zedi.
Ils parlèrent à toute l'assemblée des enfants d'Israël, en disant: « Le pays que nous avons traversé pour l'explorer est un pays extrêmement bon.
8 Ngati Yehova akukondwera nafe, adzatitsogolera kulowa mʼdziko limenelo. Dziko loyenda mkaka ndi uchi adzalipereka kwa ife,
Si Yahvé se plaît en nous, il nous fera entrer dans ce pays et nous le donnera: un pays où coulent le lait et le miel.
9 koma musawukire Yehova. Komanso musaope anthu a mʼdzikomo, pakuti tidzawagonjetsa. Chitetezo chawachokera, koma ife Yehova ali nafe. Musawaope.”
Seulement, ne vous révoltez pas contre Yahvé, et ne craignez pas les habitants du pays, car ils sont notre pain. Leur défense s'est retirée au-dessus d'eux, et Yahvé est avec nous. Ne les craignez pas. »
10 Koma gulu lonse linayankhula zofuna kuwagenda miyala. Pamenepo ulemerero wa Yehova unaonekera kwa Aisraeli onse ku tenti ya msonkhano.
Mais toute la congrégation menaçait de les lapider. La gloire de Yahvé apparut dans la Tente de la Rencontre à tous les enfants d'Israël.
11 Yehova anawuza Mose kuti, “Anthu awa adzandinyoza mpaka liti? Sadzandikhulupirira mpaka liti, ngakhale ndachita zizindikiro zozizwitsa zonsezi pakati pawo?
Yahvé dit à Moïse: « Jusques à quand ce peuple me méprisera-t-il? Jusques à quand ne croiront-ils pas en moi, à cause de tous les signes que j'ai accomplis au milieu d'eux?
12 Ndidzawakantha ndi mliri ndi kuwawononga. Koma ndidzakusandutsa iwe mtundu waukulu ndi wamphamvu kuposa iwo.”
Je les frapperai de la peste, je les déshériterai et je ferai de vous une nation plus grande et plus puissante qu'eux. »
13 Mose anati kwa Yehova, “Aigupto adzamva zimenezi! Mwa mphamvu yanu munawatulutsa anthu amenewa pakati pawo.
Moïse dit à Yahvé: « Les Égyptiens l'entendront, car c'est par ta puissance que tu as fait sortir ce peuple du milieu d'eux.
14 Ndipo iwowo adzawuza anthu okhala mʼdziko lino zimenezi. Anthuwa amva kale kuti Inu Yehova mumakhala pakati pa anthu amenewa ndi kuti Inuyo Yehova mwawaonekera maso ndi maso. Mtambo wanu umakhala pamwamba pawo ndiponso mumayenda nawo mu mtambo woyima, masana ndi moto woyima, usiku.
Ils le diront aux habitants de ce pays. Ils ont appris que toi, Yahvé, tu es au milieu de ce peuple, car on te voit face à face, et ta nuée se tient au-dessus d'eux, et tu marches devant eux, dans une colonne de nuée le jour, et dans une colonne de feu la nuit.
15 Tsono mukawapha anthu onsewa nthawi imodzi, mayiko amene anamva za Inu adzati,
Si tu as tué ce peuple comme un seul homme, les nations qui ont entendu parler de toi diront:
16 ‘Yehova walephera kuwalowetsa anthuwo mʼdziko lomwe anawalonjeza molumbira, ndipo wawapha mʼchipululu.’
« Parce que l'Éternel n'a pas pu faire entrer ce peuple dans le pays qu'il lui avait promis, il l'a tué dans le désert ».
17 “Chonde Ambuye wonetsani mphamvu yanu monga munalonjezera kuti,
Maintenant, que la puissance de l'Éternel soit grande, comme vous l'avez dit, en disant:
18 ‘Yehova sakwiya msanga, ndipo ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika, wokhululukira tchimo ndi kuwukira. Koma Iye sadzaleka kulanga ochimwa. Iyeyo amalanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo kufikira mʼbado wachitatu ndi wachinayi.’
« L'Éternel est lent à la colère et riche en bonté, il pardonne l'iniquité et la désobéissance; il ne pardonne pas les coupables, il fait retomber l'iniquité des pères sur les enfants, sur la troisième et la quatrième génération.
19 Chifukwa cha kukula kwa chikondi chanu chosasinthika, akhululukireni anthuwa tchimo lawo monga mwakhala mukuwakhululukira kuchokera pa nthawi imene anachoka ku Igupto mpaka tsopano.”
Pardonne, je te prie, l'iniquité de ce peuple, selon la grandeur de ta bonté, et comme tu as pardonné à ce peuple, depuis l'Égypte jusqu'à maintenant. »
20 Yehova anayankha kuti, “Ndawakhululukira monga wapemphera.
L'Éternel dit: J'ai pardonné selon ta parole;
21 Komabe, ndikunenetsa kuti pali Ine, ndiponso pamene dziko lapansi ladzaza ndi ulemerero wa Yehova,
mais, en vérité, comme je suis vivant et que toute la terre sera remplie de la gloire de l'Éternel,
22 palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu amene anaona ulemerero wanga ndi zizindikiro zozizwitsa zimene ndinazichita ku Igupto ndi mʼchipululu muno, koma osandimvera ndi kundiyesa kokwanira kakhumi,
parce que tous ces hommes qui ont vu ma gloire et les signes que j'ai opérés en Égypte et dans le désert, m'ont tenté dix fois et n'ont pas écouté ma voix,
23 palibe ndi mmodzi yemwe wa anthu amenewa amene adzaone dziko limene ndinalonjeza ndi lumbiro kwa makolo awo. Aliyense amene anandinyoza sadzaliona dzikolo.
ils ne verront pas le pays que j'ai juré à leurs pères, et aucun de ceux qui m'ont méprisé ne le verra.
24 Koma mtumiki wanga Kalebe, pakuti ali ndi mtima wosiyana ndi ena ndiponso amanditsatira ndi mtima wonse, ndidzamulowetsa mʼdziko limene anapitamolo ndipo zidzukulu zake zidzalandira dzikolo ngati cholowa chawo.
Mais mon serviteur Caleb, parce qu'il avait avec lui un autre esprit et qu'il m'a entièrement suivi, lui, je le ferai entrer dans le pays où il est allé. Sa descendance le possédera.
25 Ndipo popeza kuti Aamaleki ndi Akanaani akukhala ku chigwa, mawa mubwerere ndipo mupite ku chipululu podzera ku Nyanja Yofiira.”
Puisque l'Amalécite et le Cananéen habitent dans la vallée, demain, tournez-vous et allez dans le désert par le chemin de la mer Rouge. »
26 Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
Yahvé parla à Moïse et à Aaron, et dit:
27 “Kodi anthu oyipawa adzangʼungʼudza ndi kutsutsana nane mpaka liti? Ndamva madandawulo a Aisraeli ongʼungʼudzawa.
« Jusqu'à quand supporterai-je cette méchante assemblée qui se plaint de moi? J'ai entendu les plaintes des enfants d'Israël, qui se plaignent de moi.
28 Tsono awuze kuti, ‘Ndikulumbira pali Ine,’ akutero Yehova, ‘Ndidzakuchitirani zinthu zonse zimene ndamva inu mukunena:
Dis-leur: Je suis vivant, dit l'Éternel, et je vous ferai ce que vous avez dit à mes oreilles.
29 Mitembo yanu idzakhala ili ngundangunda mʼchipululu muno; mtembo wa munthu aliyense pakati panu amene ali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, amene anawerengedwa pa chiwerengero chija ndipo anangʼungʼudza motsutsana nane.
Vos cadavres tomberont dans ce désert; et tous ceux d'entre vous qui ont été comptés, selon votre nombre total, depuis l'âge de vingt ans et au-dessus, et qui se sont plaints de moi,
30 Palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene adzalowe mʼdziko lomwe ndinalumbira mokweza manja kuti likhale lanu, kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.
vous n'entrerez pas dans le pays que j'ai juré de vous faire habiter, excepté Caleb, fils de Jephunné, et Josué, fils de Nun.
31 Koma ana anu amene mukunena kuti adzatengedwa ngati katundu wolanda ku nkhondo, Ine ndidzawalowetsa kuti akasangalale mʼdziko limene munalikana.
Mais je ferai venir vos petits enfants que vous avez dit devoir être capturés ou tués, et ils connaîtront le pays que vous avez rejeté.
32 Koma inu mitembo yanu idzakhala ngundangunda mʼchipululu muno.
Mais quant à vous, vos cadavres tomberont dans ce désert.
33 Ana anu adzakhala abusa mʼchipululu muno zaka makumi anayi, kuvutika chifukwa cha kusakhulupirika kwanu, mpaka munthu womaliza mwa inu atafa mʼchipululu muno.
Vos enfants seront errants dans le désert pendant quarante ans, et porteront votre prostitution, jusqu'à ce que vos cadavres soient consumés dans le désert.
34 Mudzavutika chifukwa cha machimo anu kwa zaka makumi anayi Chaka chimodzi chikuyimira tsiku limodzi la masiku makumi anayi amene munakazonda dziko lija ndipo mudzadziwa kuyipa kwake kwa kukangana ndi Ine.’
Après le nombre de jours pendant lesquels vous avez exploré le pays, quarante jours, car chaque jour est une année, vous porterez vos fautes, quarante ans, et vous connaîtrez mon aliénation'.
35 Ine Yehova, ndanena, ndidzachitadi zimenezi kwa anthu onse oyipawa, amene agwirizana kunditsutsa. Adzathera mʼchipululu momwe muno, adzafera muno basi.”
Moi, Yahvé, j'ai parlé. Je vais faire cela à toute cette méchante assemblée qui s'est réunie contre moi. Dans ce désert, ils seront consumés, et c'est là qu'ils mourront. »
36 Ndipo anthu amene Mose anawatuma kukazonda dziko aja anachoka pamaso pake nachititsa gulu lonse la anthu kuwukira Moseyo chifukwa chofalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo.
Les hommes que Moïse avait envoyés pour explorer le pays et qui, à leur retour, avaient poussé toute l'assemblée à murmurer contre lui en rapportant un mauvais rapport sur le pays,
37 Anthu amene ankafalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo anakanthidwa ndi mliri ndipo anafa pamaso pa Yehova.
ces hommes qui avaient rapporté un mauvais rapport sur le pays, moururent par la peste devant Yahvé.
38 Mwa anthu amene anakaona dzikolo, Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune ndi okhawo amene anapulumuka.
Mais Josué, fils de Nun, et Caleb, fils de Jephunné, restèrent en vie parmi les hommes qui étaient allés explorer le pays.
39 Mose atafotokoza izi kwa Aisraeli onse, anthuwo analira kwambiri.
Moïse rapporta ces paroles à tous les enfants d'Israël, et le peuple se lamenta beaucoup.
40 Mmamawa tsiku linalo anapita mbali ya ku dziko la mapiri. Iwo anati, “Tachimwa, tipita ku dziko limene Yehova anatilonjeza.”
Ils se levèrent de bon matin et montèrent au sommet de la montagne, en disant: « Voici, nous sommes ici, et nous monterons au lieu que l'Éternel a promis, car nous avons péché. »
41 Koma Mose anati, “Chifukwa chiyani simukumvera lamulo la Yehova? Zimenezi sizitheka!
Moïse dit: « Pourquoi désobéissez-vous maintenant au commandement de l'Éternel, puisqu'il ne prospérera pas?
42 Musapite chifukwa Yehova sali pakati panu. Mudzagonjetsedwa ndi adani anu
Ne montez pas, car l'Éternel n'est pas au milieu de vous; ainsi, vous ne serez pas terrassés devant vos ennemis.
43 chifukwa kumeneko mukakumana ndi Aamaleki ndi Akanaani. Popeza mwaleka kutsata Yehova, Iyeyo sadzakhala nanu ndipo mudzaphedwa ndi lupanga.”
Car là, l'Amalécite et le Cananéen sont devant toi, et tu tomberas par l'épée parce que tu t'es détourné de suivre l'Yahvé; c'est pourquoi l'Yahvé ne sera pas avec toi. »
44 Komabe mwa maganizo awo anapita molunjika dziko la mapiri ngakhale kuti Mose sanachoke ndi Bokosi la Chipangano la Yehova pa msasa.
Mais ils s'enhardirent à monter au sommet de la montagne. Néanmoins, l'arche de l'alliance de Yahvé et Moïse ne sortirent pas du camp.
45 Koma Aamaleki ndi Akanaani amene ankakhala ku dziko lamapirilo anatsika ndi kumenyana nawo ndipo anawakantha mʼnjira yonse mpaka ku Horima.
Alors les Amalécites descendirent, ainsi que les Cananéens qui habitaient cette montagne, et ils les frappèrent et les battirent jusqu'à Horma.

< Numeri 14 >