< Numeri 13 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
UThixo wathi kuMosi,
2 “Tuma anthu kuti akazonde dziko la Kanaani limene ndikupereka kwa Aisraeli. Kuchokera pa fuko lililonse utume munthu mmodzi amene ndi mtsogoleri wawo.”
“Thuma amadoda athile ukuba ayehlola ilizwe laseKhenani, engilinika abako-Israyeli. Kusendo ngalunye lwesizwe thuma umkhokheli oyedwa.”
3 Monga mwa mawu a Yehova, Mose anawatuma kuchokera ku chipululu cha Parani. Onsewo anali atsogoleri a Aisraeli.
Ngakho ngokulaya kukaThixo uMosi wabakhupha labo enkangala yePharani. Bonke babengabakhokheli bako-Israyeli.
4 Mayina awo ndi awa: kuchokera ku fuko la Rubeni, Samuwa mwana wa Zakuri;
Nanka amabizo abo: esizweni sikaRubheni, kwakunguShamuwa indodana kaZakhuri;
5 kuchokera ku fuko la Simeoni, Safati mwana wa Hori;
esizweni sikaSimiyoni, kwakunguShafathi indodana kaHori;
6 kuchokera ku fuko la Yuda, Kalebe mwana wa Yefune;
esizweni sikaJuda, kwakunguKhalebi indodana kaJefune;
7 kuchokera ku fuko la Isakara, Igala mwana wa Yosefe;
esizweni sika-Isakhari, kwakungu-Igali indodana kaJosefa;
8 kuchokera ku fuko la Efereimu, Hoseya mwana wa Nuni;
esizweni sika-Efrayimi, kwakunguHosheya indodana kaNuni;
9 kuchokera ku fuko la Benjamini, Paliti mwana wa Rafu;
esizweni sikaBhenjamini, kwakunguPhalithi indodana kaRafu;
10 kuchokera ku fuko la Zebuloni, Gadieli mwana wa Sodi;
esizweni sikaZebhuluni, kwakunguGadiyeli indodana kaSodi;
11 kuchokera ku fuko la Manase (fuko la Yosefe), Gadi mwana wa Susi;
esizweni sikaManase (owesizwe sikaJosefa), kwakunguGadi indodana kaSusi;
12 kuchokera ku fuko la Dani, Amieli mwana wa Gemali;
esizweni sikaDani, kwakungu-Amiyeli indodana kaGemali;
13 kuchokera ku fuko la Aseri, Seturi mwana wa Mikayeli;
esizweni sika-Asheri, kwakunguSethuri indodana kaMikhayeli;
14 kuchokera ku fuko la Nafutali, Naabi mwana wa Vofisi;
esizweni sikaNafithali, kwakunguNabhi indodana kaVofisi;
15 kuchokera ku fuko la Gadi, Geuweli mwana wa Maki.
esizweni sikaGadi, kwakunguGewuweli indodana kaMakhi.
16 Amenewa ndiwo mayina a anthu amene Mose anawatuma kukazonda dzikolo. (Hoseya mwana wa Nuni, Mose anamupatsa dzina loti Yoswa).
La ngamabizo alawomadoda athunywa nguMosi ukuyahlola ilizwe. (UMosi wetha uHosheya indodana kaNuni ibizo elithi Joshuwa.)
17 Mose atawatuma kuti akazonde Kanaani anati, “Mupite kudzera ku Negevi, mukapitirire mpaka ku dziko la mapiri.
Ekubathumeni kwakhe ukuyahlola ilizwe laseKhenani, uMosi wathi kubo, “Hambani liye eNegebi likhuphukele elizweni lezintaba.
18 Mukaone dzikolo kuti ndi lotani ndi anthu okhala mʼmenemo ngati ndi amphamvu kapena ofowoka, ochepa kapena ambiri.
Likhangele ukuthi ilizwe lakhona linjani njalo lokuthi abantu bakhona balamandla kumbe babuthakathaka, balutshwana kumbe banengi.
19 Nanga dziko limene akukhalako ndi lotani? Ndi labwino kapena loyipa? Mizinda imene akukhalamo ndi yotani? Kodi ilibe malinga kapena ndi ya malinga?
Ilizwe abahlala kulo linjani? Lihle na loba libi? Amadolobho abahlala kuwo anjani? Agonjolozelwe ngemiduli loba asegcekeni nje?
20 Nthaka yake ndi yotani? Yachonde kapena yopanda chonde? Kodi dzikolo lili ndi mitengo kapena lilibe mitengo? Mukayesetse kubweretsako zipatso za mʼdzikomo.” (Inali nthawi yamphesa zoyamba kupsa).
Umhlabathi wakhona unjani? Uvundile na loba ulugwadule? Langabe lilezihlahla loba hayi? Yenzani ubungcono benu libuye lezinye zezithelo zakulelolizwe.” (Kwakuyisikhathi sokuvuthwa kwezithelo zakuqala zevini.)
21 Choncho anapita kukazonda dzikolo kuchokera ku chipululu cha Zini mpaka ku Rehobu, mopenyana ndi Lebo Hamati.
Ngakho bahamba ukuyahlola ilizwe besukela eNkangala yaseZini kuze kuyefika eRehobhi, ngokuya eLebho Hamathi.
22 Anapita kudzera ku Negevi ndi kukafika ku Hebroni, kumene Ahimani, Sesai ndi Talimai, ana a Anaki ankakhala. (Anamanga Hebroni zaka zisanu ndi ziwiri asanamange Zowani ku Igupto).
Bahamba-ke badabula eNegebi baze bayafika eHebhroni, lapho okwakuhlala khona u-Ahimani, loSheshayi kanye loThalimayi, izizukulwane zika-Anakhi. (IHebhroni yakhiwa iminyaka eyisikhombisa kungakakhiwa idolobho laseZowani eGibhithe.)
23 Atafika ku chigwa cha Esikolo, anadulako nthambi ya mpesa ya phava limodzi la mphesa ndipo anthu awiri ananyamulizana, natenganso makangadza ndi nkhuyu.
Bathi befika esihotsheni sase-Eshikholi baquma ugatsha olwalulesixha sezithelo zevini. Ababili babo basithwala besigaxe egodweni ndawonye lamaphomegranathi kanye lomkhiwa.
24 Malo amenewo anawatcha chigwa cha Esikolo chifukwa cha phava la mphesa limene Aisraeli anadula kumeneko.
Lindawo yabizwa ngokuthi yisihotsha sase-Eshikholi ngenxa yesixha sezithelo zevini esaqunywa khona ngabako-Israyeli.
25 Patapita masiku makumi anayi, anthu aja anabwerako kokazonda dziko lija.
Ngemva kwensuku ezingamatshumi amane zokuhlola ilizwe inhloli zabuyela emuva.
26 Ndipo atabwerako anapita kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa Aisraeli onse ku Kadesi mʼchipululu cha Parani. Kumeneko anafotokozera anthu onse nawaonetsanso zipatso za mʼdzikolo.
Babuyela kuMosi lo-Aroni lakuso sonke isizwe sako-Israyeli eKhadeshi, enkangala yasePharani. Babikela uMosi lo-Aroni kanye labo bonke abako-Israyeli njalo batshengisa lezithelo zakulelolizwe.
27 Anthuwo anafotokozera Mose kuti, “Tinapita ku dziko komwe munatituma. Dzikolo ndi loyenda mkaka ndi uchi ndipo zipatso zake ndi izi.
Balandisela uMosi bathi: “Sihambile elizweni lelo obukade usithume kulo, ngempela ligeleza uchago loluju! Nanzi izithelo zalo.
28 Koma anthu amene amakhala mʼdzikomo ndi amphamvu, mizinda yawo ndi ya malinga aakulu kwambiri. Tinaonanso Aanaki kumeneko.
Kodwa abantu abahlala khona balamandla kanti lamadolobho akhona makhulu njalo avikelwe. Size sabona lezizukulwane zika-Anakhi khonale.
29 Aamaleki amakhala ku Negevi, Ahiti, Ayebusi ndi Aamori amakhala mʼdziko la mapiri ndipo Akanaani amakhala pafupi ndi nyanja, mʼmbali mwa Yorodani.”
Ama-Amaleki ahlala eNegebi; amaHithi, lamaJebusi lama-Amori bahlala elizweni lezintaba, amaKhenani wona ahlala eduzane lolwandle esekele umfula uJodani.”
30 Koma Kalebe anawakhalitsa chete anthuwo pamaso pa Mose, ndipo anati, “Tiyeni tipite ndithu ndi kutenga dzikolo, pakuti tingathe kulitenga.”
Emva kwalokho uKhalebi wathulisa abantu phambi kukaMosi wasesithi, “Kufanele ukuthi sihambe siyethatha ilizwe leli libe ngelethu, ngoba singakwenza sibili.”
31 Koma anthu aja amene anapita naye anati, “Sitingathe kulimbana ndi anthuwo popeza ndi amphamvu kuposa ifeyo.”
Kodwa amadoda lawo ayehambe laye athi, “Asingeke sibahlasele abantu labo; balamandla kulathi.”
32 Choncho anthuwo anafalitsa pakati pa Aisraeli mbiri yoyipa ya dziko lomwe anakalionalo. Iwo anati, “Dziko limene tinapita kukalizonda limawononga anthu okhala mʼmenemo. Ndipo anthu onse amene tinakawaona kumeneko ndi ataliatali.
Basebetshela abantu bako-Israyeli umbiko omubi ngelizwe ababelihlolile. Bathi, “Ilizwe esilihlolileyo liyabagabhela labantu abahlala kulo. Bonke abantu esibabone khonale yiziqhwaga.
33 Kumeneko tinaona Anefili (ana a Aanaki ochokera kwa Nefili). Ifeyo timangodziona ngati ziwala mʼmaso mwawo, ndipo kwa iwo timaonekadi motero ndithu.”
Sibone khona amaNefilimi (isizukulwane sika-Anakhi sivela kumaNefilimi.) Emehlweni ethu besingangentethe phambi kwabo, lasemehlweni abo besinjalo.”