< Numeri 13 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Et l'Eternel parla à Moïse, en disant:
2 “Tuma anthu kuti akazonde dziko la Kanaani limene ndikupereka kwa Aisraeli. Kuchokera pa fuko lililonse utume munthu mmodzi amene ndi mtsogoleri wawo.”
Envoie des hommes pour reconnaître le pays de Canaan, que je donne aux enfants d'Israël. Vous enverrez un homme de chaque Tribu de leurs pères, tous des principaux d'entr'eux.
3 Monga mwa mawu a Yehova, Mose anawatuma kuchokera ku chipululu cha Parani. Onsewo anali atsogoleri a Aisraeli.
Moïse donc les envoya du désert de Paran, selon le commandement de l'Eternel; et tous ces hommes étaient chefs des enfants d'Israël.
4 Mayina awo ndi awa: kuchokera ku fuko la Rubeni, Samuwa mwana wa Zakuri;
Et ce sont ici leurs noms: De la Tribu de Ruben, Sammuah, fils de Zaccur.
5 kuchokera ku fuko la Simeoni, Safati mwana wa Hori;
De la Tribu de Siméon, Saphat, fils de Hori.
6 kuchokera ku fuko la Yuda, Kalebe mwana wa Yefune;
De la Tribu de Juda, Caleb, fils de Jéphunné.
7 kuchokera ku fuko la Isakara, Igala mwana wa Yosefe;
De la Tribu d'Issacar, Jigueal, fils de Joseph.
8 kuchokera ku fuko la Efereimu, Hoseya mwana wa Nuni;
De la Tribu d'Ephraïm, Osée, fils de Nun.
9 kuchokera ku fuko la Benjamini, Paliti mwana wa Rafu;
De la Tribu de Benjamin, Palti, fils de Raphu.
10 kuchokera ku fuko la Zebuloni, Gadieli mwana wa Sodi;
De la Tribu de Zabulon, Gaddiel, fils de Sodi.
11 kuchokera ku fuko la Manase (fuko la Yosefe), Gadi mwana wa Susi;
De l'autre Tribu de Joseph, [savoir] de la Tribu de Manassé, Gaddi, fils de Susi.
12 kuchokera ku fuko la Dani, Amieli mwana wa Gemali;
De la Tribu de Dan, Hammiel, fils de Guemalli.
13 kuchokera ku fuko la Aseri, Seturi mwana wa Mikayeli;
De la Tribu d'Aser, Séthur, fils de Micaël.
14 kuchokera ku fuko la Nafutali, Naabi mwana wa Vofisi;
De la Tribu de Nephthali, Nahbi, fils de Vaphsi.
15 kuchokera ku fuko la Gadi, Geuweli mwana wa Maki.
De la Tribu de Gad, Guéuel, fils de Maki.
16 Amenewa ndiwo mayina a anthu amene Mose anawatuma kukazonda dzikolo. (Hoseya mwana wa Nuni, Mose anamupatsa dzina loti Yoswa).
Ce [sont] là les noms des hommes que Moïse envoya pour reconnaître le pays. Or Moïse avait nommé Osée, fils de Nun, Josué.
17 Mose atawatuma kuti akazonde Kanaani anati, “Mupite kudzera ku Negevi, mukapitirire mpaka ku dziko la mapiri.
Moïse donc les envoya pour reconnaître le pays de Canaan, et il leur dit: Montez de ce côté vers le Midi, puis vous monterez sur la montagne.
18 Mukaone dzikolo kuti ndi lotani ndi anthu okhala mʼmenemo ngati ndi amphamvu kapena ofowoka, ochepa kapena ambiri.
Et vous verrez quel est ce pays-là, et quel est le peuple qui l'habite, s'il est fort, ou faible; s'il est en petit ou en grand nombre.
19 Nanga dziko limene akukhalako ndi lotani? Ndi labwino kapena loyipa? Mizinda imene akukhalamo ndi yotani? Kodi ilibe malinga kapena ndi ya malinga?
Et quel est le pays où il habite, s'il est bon ou mauvais; et quelles [sont] les villes dans lesquelles il habite, si c'est dans des tentes, ou dans des villes closes.
20 Nthaka yake ndi yotani? Yachonde kapena yopanda chonde? Kodi dzikolo lili ndi mitengo kapena lilibe mitengo? Mukayesetse kubweretsako zipatso za mʼdzikomo.” (Inali nthawi yamphesa zoyamba kupsa).
Et quel est le terroir, s'il est gras ou maigre, s'il y a des arbres, ou non. Ayez bon courage, et prenez du fruit du pays. Or c'était alors le temps des premiers raisins.
21 Choncho anapita kukazonda dzikolo kuchokera ku chipululu cha Zini mpaka ku Rehobu, mopenyana ndi Lebo Hamati.
Etant donc partis, ils examinèrent le pays, depuis le désert de Tsin jusqu'à Réhob, à l'entrée de Hamath.
22 Anapita kudzera ku Negevi ndi kukafika ku Hebroni, kumene Ahimani, Sesai ndi Talimai, ana a Anaki ankakhala. (Anamanga Hebroni zaka zisanu ndi ziwiri asanamange Zowani ku Igupto).
Ils montèrent donc vers le Midi, et vinrent jusqu'à Hébron, où étaient Ahiman, Sésaï, et Talmaï, issus de Hanak. Or Hébron avait été bâtie sept ans avant Tsohan d'Egypte.
23 Atafika ku chigwa cha Esikolo, anadulako nthambi ya mpesa ya phava limodzi la mphesa ndipo anthu awiri ananyamulizana, natenganso makangadza ndi nkhuyu.
Et ils vinrent jusqu'au torrent d'Escol, et coupèrent de là un sarment de vigne, avec une grappe de raisins; et ils étaient deux à le porter avec un levier. Ils apportèrent aussi des grenades et des figues.
24 Malo amenewo anawatcha chigwa cha Esikolo chifukwa cha phava la mphesa limene Aisraeli anadula kumeneko.
Et on appela ce lieu-là Nahal-Escol; à l'occasion de la grappe que les enfants d'Israël y coupèrent.
25 Patapita masiku makumi anayi, anthu aja anabwerako kokazonda dziko lija.
Et au bout de quarante jours ils furent de retour du pays qu'ils étaient allés reconnaître.
26 Ndipo atabwerako anapita kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa Aisraeli onse ku Kadesi mʼchipululu cha Parani. Kumeneko anafotokozera anthu onse nawaonetsanso zipatso za mʼdzikolo.
Et étant arrivés, ils vinrent vers Moïse et Aaron, et vers toute l'assemblée des enfants d'Israël, au désert de Padan en Kadès; et leur ayant fait leur rapport, et à toute l'assemblée, ils leur montrèrent du fruit du pays.
27 Anthuwo anafotokozera Mose kuti, “Tinapita ku dziko komwe munatituma. Dzikolo ndi loyenda mkaka ndi uchi ndipo zipatso zake ndi izi.
Ils firent donc leur rapport à Moïse, et lui dirent: Nous avons été au pays où tu nous avais envoyés; et véritablement c'est un pays découlant de lait et de miel, et c'est ici de son fruit.
28 Koma anthu amene amakhala mʼdzikomo ndi amphamvu, mizinda yawo ndi ya malinga aakulu kwambiri. Tinaonanso Aanaki kumeneko.
Il y a seulement ceci, que le peuple qui habite au pays est robuste, et les villes sont closes, [et] fort grandes; nous y avons vu aussi les enfants de Hanak.
29 Aamaleki amakhala ku Negevi, Ahiti, Ayebusi ndi Aamori amakhala mʼdziko la mapiri ndipo Akanaani amakhala pafupi ndi nyanja, mʼmbali mwa Yorodani.”
Les Hamalécites habitent au pays du Midi; et les Héthiens, les Jébusiens, et les Amorrhéens habitent en la montagne; et les Cananéens habitent le long de la mer, et vers le rivage du Jourdain.
30 Koma Kalebe anawakhalitsa chete anthuwo pamaso pa Mose, ndipo anati, “Tiyeni tipite ndithu ndi kutenga dzikolo, pakuti tingathe kulitenga.”
Alors Caleb fit taire le peuple devant Moïse, et dit: Montons hardiment, et possédons ce pays-là, car certainement nous y serons les plus forts.
31 Koma anthu aja amene anapita naye anati, “Sitingathe kulimbana ndi anthuwo popeza ndi amphamvu kuposa ifeyo.”
Mais les hommes qui étaient montés avec lui, dirent: Nous ne saurions monter contre ce peuple-là, car il est plus fort que nous.
32 Choncho anthuwo anafalitsa pakati pa Aisraeli mbiri yoyipa ya dziko lomwe anakalionalo. Iwo anati, “Dziko limene tinapita kukalizonda limawononga anthu okhala mʼmenemo. Ndipo anthu onse amene tinakawaona kumeneko ndi ataliatali.
Et ils décrièrent devant les enfants d'Israël le pays qu'ils avaient examiné, en disant: Le pays par lequel nous sommes passés pour le reconnaître [est] un pays qui consume ses habitants, et tous le peuple que nous y avons vus, sont des gens de grande stature.
33 Kumeneko tinaona Anefili (ana a Aanaki ochokera kwa Nefili). Ifeyo timangodziona ngati ziwala mʼmaso mwawo, ndipo kwa iwo timaonekadi motero ndithu.”
Nous y avons vu aussi des géants, des enfants de Hanak, de la race des géants; et nous ne paraissions auprès d'eux que comme des sauterelles.

< Numeri 13 >