< Numeri 13 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
And he spoke Yahweh to Moses saying.
2 “Tuma anthu kuti akazonde dziko la Kanaani limene ndikupereka kwa Aisraeli. Kuchokera pa fuko lililonse utume munthu mmodzi amene ndi mtsogoleri wawo.”
Send for yourself men so they may spy out [the] land of Canaan which I [am] about to give to [the] people of Israel a man one a man one for [the] tribe of ancestors his you will send every [one] a leader among them.
3 Monga mwa mawu a Yehova, Mose anawatuma kuchokera ku chipululu cha Parani. Onsewo anali atsogoleri a Aisraeli.
And he sent them Moses from [the] wilderness of Paran on [the] mouth of Yahweh all of them [were] men [who were] [the] heads of [the] people of Israel they.
4 Mayina awo ndi awa: kuchokera ku fuko la Rubeni, Samuwa mwana wa Zakuri;
And these [are] names their for [the] tribe of Reuben Shammua [the] son of Zaccur.
5 kuchokera ku fuko la Simeoni, Safati mwana wa Hori;
For [the] tribe of Simeon Shaphat [the] son of Hori.
6 kuchokera ku fuko la Yuda, Kalebe mwana wa Yefune;
For [the] tribe of Judah Caleb [the] son of Jephunneh.
7 kuchokera ku fuko la Isakara, Igala mwana wa Yosefe;
For [the] tribe of Issachar Igal [the] son of Joseph.
8 kuchokera ku fuko la Efereimu, Hoseya mwana wa Nuni;
For [the] tribe of Ephraim Hoshea [the] son of Nun.
9 kuchokera ku fuko la Benjamini, Paliti mwana wa Rafu;
For [the] tribe of Benjamin Palti [the] son of Raphu.
10 kuchokera ku fuko la Zebuloni, Gadieli mwana wa Sodi;
For [the] tribe of Zebulun Gaddiel [the] son of Sodi.
11 kuchokera ku fuko la Manase (fuko la Yosefe), Gadi mwana wa Susi;
For [the] tribe of Joseph for [the] tribe of Manasseh Gaddi [the] son of Susi.
12 kuchokera ku fuko la Dani, Amieli mwana wa Gemali;
For [the] tribe of Dan Ammiel [the] son of Gemalli.
13 kuchokera ku fuko la Aseri, Seturi mwana wa Mikayeli;
For [the] tribe of Asher Sethur [the] son of Michael.
14 kuchokera ku fuko la Nafutali, Naabi mwana wa Vofisi;
For [the] tribe of Naphtali Nahbi [the] son of Vopshi.
15 kuchokera ku fuko la Gadi, Geuweli mwana wa Maki.
For [the] tribe of Gad Geuel [the] son of Maki.
16 Amenewa ndiwo mayina a anthu amene Mose anawatuma kukazonda dzikolo. (Hoseya mwana wa Nuni, Mose anamupatsa dzina loti Yoswa).
These [are] [the] names of the men whom he sent Moses to spy out the land and he called Moses Hoshea [the] son of Nun Joshua.
17 Mose atawatuma kuti akazonde Kanaani anati, “Mupite kudzera ku Negevi, mukapitirire mpaka ku dziko la mapiri.
And he sent them Moses to spy out [the] land of Canaan and he said to them go up this in the Negev and you will go up the hill country.
18 Mukaone dzikolo kuti ndi lotani ndi anthu okhala mʼmenemo ngati ndi amphamvu kapena ofowoka, ochepa kapena ambiri.
And you will see the land what? [is] it and the people which dwells on it ¿ strong [is] it ¿ feeble ¿ few [is] it or? many.
19 Nanga dziko limene akukhalako ndi lotani? Ndi labwino kapena loyipa? Mizinda imene akukhalamo ndi yotani? Kodi ilibe malinga kapena ndi ya malinga?
And what? [is] the land which it [is] dwelling in it ¿ good [is] it or? bad and what? [are] the cities which it [is] dwelling in them ¿ in camps or? in fortresses.
20 Nthaka yake ndi yotani? Yachonde kapena yopanda chonde? Kodi dzikolo lili ndi mitengo kapena lilibe mitengo? Mukayesetse kubweretsako zipatso za mʼdzikomo.” (Inali nthawi yamphesa zoyamba kupsa).
And what? [is] the land ¿ fat [is] it or? lean ¿ [is] there in it wood or? not and you will show yourselves strong and you will take some of [the] fruit of the land and the days [were the] days of [the] first-fruits of grapes.
21 Choncho anapita kukazonda dzikolo kuchokera ku chipululu cha Zini mpaka ku Rehobu, mopenyana ndi Lebo Hamati.
And they went up and they spied out the land from [the] wilderness of Zin to Rehob Lebo Hamath.
22 Anapita kudzera ku Negevi ndi kukafika ku Hebroni, kumene Ahimani, Sesai ndi Talimai, ana a Anaki ankakhala. (Anamanga Hebroni zaka zisanu ndi ziwiri asanamange Zowani ku Igupto).
And they went up in the Negev and he came to Hebron and [were] there Ahiman Sheshai and Talmai those born of Anak and Hebron seven years it was built before Zoan Egypt.
23 Atafika ku chigwa cha Esikolo, anadulako nthambi ya mpesa ya phava limodzi la mphesa ndipo anthu awiri ananyamulizana, natenganso makangadza ndi nkhuyu.
And they came to [the] wadi of Eshcol and they cut down from there a branch and a cluster of grapes one and they carried it on the pole two and some of the pomegranates and some of the figs.
24 Malo amenewo anawatcha chigwa cha Esikolo chifukwa cha phava la mphesa limene Aisraeli anadula kumeneko.
the Place that someone called [the] wadi of Eshcol on [the] causes of the cluster which they cut down from there [the] people of Israel.
25 Patapita masiku makumi anayi, anthu aja anabwerako kokazonda dziko lija.
And they returned from spying out the land from [the] end of forty day[s].
26 Ndipo atabwerako anapita kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa Aisraeli onse ku Kadesi mʼchipululu cha Parani. Kumeneko anafotokozera anthu onse nawaonetsanso zipatso za mʼdzikolo.
And they went and they came to Moses and to Aaron and to all [the] congregation of [the] people of Israel to [the] wilderness of Paran Kadesh towards and they brought back them word and all the congregation and they showed them [the] fruit of the land.
27 Anthuwo anafotokozera Mose kuti, “Tinapita ku dziko komwe munatituma. Dzikolo ndi loyenda mkaka ndi uchi ndipo zipatso zake ndi izi.
And they recounted to him and they said we went into the land which you sent us and also [is] flowing of milk and honey it and this [is] fruit its.
28 Koma anthu amene amakhala mʼdzikomo ndi amphamvu, mizinda yawo ndi ya malinga aakulu kwambiri. Tinaonanso Aanaki kumeneko.
Nevertheless for [is] strong the people which dwells in the land and the cities [are] fortified large very and also those born of Anak we saw there.
29 Aamaleki amakhala ku Negevi, Ahiti, Ayebusi ndi Aamori amakhala mʼdziko la mapiri ndipo Akanaani amakhala pafupi ndi nyanja, mʼmbali mwa Yorodani.”
Amalek [is] dwelling in [the] land of the Negev and the Hittite[s] and the Jebusite[s] and the Amorite[s] [is] dwelling in the hill country and the Canaanite[s] [is] dwelling at the sea and on [the] side of the Jordan.
30 Koma Kalebe anawakhalitsa chete anthuwo pamaso pa Mose, ndipo anati, “Tiyeni tipite ndithu ndi kutenga dzikolo, pakuti tingathe kulitenga.”
And he silenced Caleb the people to Moses and he said certainly we will go up and we will take possession of it for certainly we will prevail to it.
31 Koma anthu aja amene anapita naye anati, “Sitingathe kulimbana ndi anthuwo popeza ndi amphamvu kuposa ifeyo.”
And the men who they had gone up with him they said not we are able to go up against the people for [is] strong it more than us.
32 Choncho anthuwo anafalitsa pakati pa Aisraeli mbiri yoyipa ya dziko lomwe anakalionalo. Iwo anati, “Dziko limene tinapita kukalizonda limawononga anthu okhala mʼmenemo. Ndipo anthu onse amene tinakawaona kumeneko ndi ataliatali.
And they brought out bad report of the land which they had spied out it to [the] people of Israel saying the land which we passed in it to spy out it [is] a land [which] devours inhabitants its it and all the people which we saw in [the] midst of it [were] men of stature.
33 Kumeneko tinaona Anefili (ana a Aanaki ochokera kwa Nefili). Ifeyo timangodziona ngati ziwala mʼmaso mwawo, ndipo kwa iwo timaonekadi motero ndithu.”
And there we saw the Nephilim [the] descendants of Anak [were] from the Nephilim and we were in own eyes our like grasshoppers and thus we were in view their.