< Numeri 13 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
The LORD spoke to Moses, saying,
2 “Tuma anthu kuti akazonde dziko la Kanaani limene ndikupereka kwa Aisraeli. Kuchokera pa fuko lililonse utume munthu mmodzi amene ndi mtsogoleri wawo.”
"Send men, that they may spy out the land of Canaan, which I give to the children of Israel. Of every tribe of their fathers, you shall send a man, every one a prince among them."
3 Monga mwa mawu a Yehova, Mose anawatuma kuchokera ku chipululu cha Parani. Onsewo anali atsogoleri a Aisraeli.
Moses sent them from the wilderness of Paran according to the commandment of the LORD: all of them men who were heads of the children of Israel.
4 Mayina awo ndi awa: kuchokera ku fuko la Rubeni, Samuwa mwana wa Zakuri;
These were their names: Of the tribe of Reuben, Shammua the son of Zakkur.
5 kuchokera ku fuko la Simeoni, Safati mwana wa Hori;
Of the tribe of Simeon, Shaphat the son of Hori.
6 kuchokera ku fuko la Yuda, Kalebe mwana wa Yefune;
Of the tribe of Judah, Caleb the son of Jephunneh.
7 kuchokera ku fuko la Isakara, Igala mwana wa Yosefe;
Of the tribe of Issachar, Igal the son of Joseph.
8 kuchokera ku fuko la Efereimu, Hoseya mwana wa Nuni;
Of the tribe of Ephraim, Hoshea the son of Nun.
9 kuchokera ku fuko la Benjamini, Paliti mwana wa Rafu;
Of the tribe of Benjamin, Palti the son of Raphu.
10 kuchokera ku fuko la Zebuloni, Gadieli mwana wa Sodi;
Of the tribe of Zebulun, Gaddiel the son of Sodi.
11 kuchokera ku fuko la Manase (fuko la Yosefe), Gadi mwana wa Susi;
Of the tribe of Joseph, of the tribe of Manasseh, Gaddi the son of Susi.
12 kuchokera ku fuko la Dani, Amieli mwana wa Gemali;
Of the tribe of Dan, Ammiel the son of Gemalli.
13 kuchokera ku fuko la Aseri, Seturi mwana wa Mikayeli;
Of the tribe of Asher, Sethur the son of Michael.
14 kuchokera ku fuko la Nafutali, Naabi mwana wa Vofisi;
Of the tribe of Naphtali, Nahbi the son of Vophsi.
15 kuchokera ku fuko la Gadi, Geuweli mwana wa Maki.
Of the tribe of Gad, Geuel the son of Maki.
16 Amenewa ndiwo mayina a anthu amene Mose anawatuma kukazonda dzikolo. (Hoseya mwana wa Nuni, Mose anamupatsa dzina loti Yoswa).
These are the names of the men who Moses sent to spy out the land. Moses called Hoshea the son of Nun Joshua.
17 Mose atawatuma kuti akazonde Kanaani anati, “Mupite kudzera ku Negevi, mukapitirire mpaka ku dziko la mapiri.
Moses sent them to spy out the land of Canaan, and said to them, "Go up this way by the Negev, and go up into the hill country:
18 Mukaone dzikolo kuti ndi lotani ndi anthu okhala mʼmenemo ngati ndi amphamvu kapena ofowoka, ochepa kapena ambiri.
and see the land, what it is; and the people who dwell in it, whether they are strong or weak, whether they are few or many;
19 Nanga dziko limene akukhalako ndi lotani? Ndi labwino kapena loyipa? Mizinda imene akukhalamo ndi yotani? Kodi ilibe malinga kapena ndi ya malinga?
and what the land is that they dwell in, whether it is good or bad; and what cities they are that they dwell in, whether in camps, or in strongholds;
20 Nthaka yake ndi yotani? Yachonde kapena yopanda chonde? Kodi dzikolo lili ndi mitengo kapena lilibe mitengo? Mukayesetse kubweretsako zipatso za mʼdzikomo.” (Inali nthawi yamphesa zoyamba kupsa).
and what the land is, whether it is fat or lean, whether there is wood in it, or not. Be courageous, and bring of the fruit of the land. Now the time was the time of the first-ripe grapes."
21 Choncho anapita kukazonda dzikolo kuchokera ku chipululu cha Zini mpaka ku Rehobu, mopenyana ndi Lebo Hamati.
So they went up, and spied out the land from the wilderness of Zin to Rehob, to Lebo Hamath.
22 Anapita kudzera ku Negevi ndi kukafika ku Hebroni, kumene Ahimani, Sesai ndi Talimai, ana a Anaki ankakhala. (Anamanga Hebroni zaka zisanu ndi ziwiri asanamange Zowani ku Igupto).
They went up by the Negev, and came to Hebron; and Ahiman, Sheshai, and Talmai, the descendants of Anak, were there. (Now Hebron was built seven years before Zoan in Egypt.)
23 Atafika ku chigwa cha Esikolo, anadulako nthambi ya mpesa ya phava limodzi la mphesa ndipo anthu awiri ananyamulizana, natenganso makangadza ndi nkhuyu.
They came to the Valley of Eshcol, and cut down from there a branch with one cluster of grapes on it, and they bore it on a staff between two. They also brought some of the pomegranates and figs.
24 Malo amenewo anawatcha chigwa cha Esikolo chifukwa cha phava la mphesa limene Aisraeli anadula kumeneko.
That place was called the Valley of Eshcol, because of the cluster which the children of Israel cut down from there.
25 Patapita masiku makumi anayi, anthu aja anabwerako kokazonda dziko lija.
They returned from spying out the land at the end of forty days.
26 Ndipo atabwerako anapita kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa Aisraeli onse ku Kadesi mʼchipululu cha Parani. Kumeneko anafotokozera anthu onse nawaonetsanso zipatso za mʼdzikolo.
They went and came to Moses, and to Aaron, and to all the congregation of the children of Israel, to the wilderness of Paran, to Kadesh; and brought back word to them, and to all the congregation, and showed them the fruit of the land.
27 Anthuwo anafotokozera Mose kuti, “Tinapita ku dziko komwe munatituma. Dzikolo ndi loyenda mkaka ndi uchi ndipo zipatso zake ndi izi.
They told him, and said, "We came to the land where you sent us; and surely it flows with milk and honey; and this is its fruit.
28 Koma anthu amene amakhala mʼdzikomo ndi amphamvu, mizinda yawo ndi ya malinga aakulu kwambiri. Tinaonanso Aanaki kumeneko.
However the people who dwell in the land are strong, and the cities are fortified and very large. Moreover, we saw the descendants of Anak there.
29 Aamaleki amakhala ku Negevi, Ahiti, Ayebusi ndi Aamori amakhala mʼdziko la mapiri ndipo Akanaani amakhala pafupi ndi nyanja, mʼmbali mwa Yorodani.”
Amalek dwells in the land of the Negev: and the Hethites, and the Hivites, and the Jebusites, and the Amorites, dwell in the hill country; and the Canaanite dwells by the sea, and along by the side of the Jordan."
30 Koma Kalebe anawakhalitsa chete anthuwo pamaso pa Mose, ndipo anati, “Tiyeni tipite ndithu ndi kutenga dzikolo, pakuti tingathe kulitenga.”
Caleb stilled the people before Moses, and said, "Let us go up at once, and possess it; for we are well able to overcome it."
31 Koma anthu aja amene anapita naye anati, “Sitingathe kulimbana ndi anthuwo popeza ndi amphamvu kuposa ifeyo.”
But the men who went up with him said, "We aren't able to go up against the people; for they are stronger than we."
32 Choncho anthuwo anafalitsa pakati pa Aisraeli mbiri yoyipa ya dziko lomwe anakalionalo. Iwo anati, “Dziko limene tinapita kukalizonda limawononga anthu okhala mʼmenemo. Ndipo anthu onse amene tinakawaona kumeneko ndi ataliatali.
They brought up an evil report of the land which they had spied out to the children of Israel, saying, "The land, through which we have gone to spy it out, is a land that eats up its inhabitants; and all the people who we saw in it are men of great stature.
33 Kumeneko tinaona Anefili (ana a Aanaki ochokera kwa Nefili). Ifeyo timangodziona ngati ziwala mʼmaso mwawo, ndipo kwa iwo timaonekadi motero ndithu.”
There we saw the Nephilim, the sons of Anak, who come of the Nephilim: and we were in our own sight as grasshoppers, and so we were in their sight."

< Numeri 13 >