< Numeri 13 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord said to Moses,
2 “Tuma anthu kuti akazonde dziko la Kanaani limene ndikupereka kwa Aisraeli. Kuchokera pa fuko lililonse utume munthu mmodzi amene ndi mtsogoleri wawo.”
Send men to get knowledge about the land of Canaan, which I am giving to the children of Israel; from every tribe of their fathers you are to send a man, every one a chief among them.
3 Monga mwa mawu a Yehova, Mose anawatuma kuchokera ku chipululu cha Parani. Onsewo anali atsogoleri a Aisraeli.
And Moses sent them from the waste land of Paran as the Lord gave orders, all of them men who were heads of the children of Israel.
4 Mayina awo ndi awa: kuchokera ku fuko la Rubeni, Samuwa mwana wa Zakuri;
And these were their names: of the tribe of Reuben, Shammua, the son of Zaccur.
5 kuchokera ku fuko la Simeoni, Safati mwana wa Hori;
Of the tribe of Simeon, Shaphat, the son of Hori.
6 kuchokera ku fuko la Yuda, Kalebe mwana wa Yefune;
Of the tribe of Judah, Caleb, the son of Jephunneh.
7 kuchokera ku fuko la Isakara, Igala mwana wa Yosefe;
Of the tribe of Issachar, Igal, the son of Joseph.
8 kuchokera ku fuko la Efereimu, Hoseya mwana wa Nuni;
Of the tribe of Ephraim, Hoshea, the son of Nun.
9 kuchokera ku fuko la Benjamini, Paliti mwana wa Rafu;
Of the tribe of Benjamin, Palti, the son of Raphu.
10 kuchokera ku fuko la Zebuloni, Gadieli mwana wa Sodi;
Of the tribe of Zebulun, Gaddiel, the son of Sodi.
11 kuchokera ku fuko la Manase (fuko la Yosefe), Gadi mwana wa Susi;
Of the tribe of Joseph, that is of the family of Manasseh, Gaddi, the son of Susi.
12 kuchokera ku fuko la Dani, Amieli mwana wa Gemali;
Of the tribe of Dan, Ammiel, the son of Gemalli.
13 kuchokera ku fuko la Aseri, Seturi mwana wa Mikayeli;
Of the tribe of Asher, Sethur, the son of Michael
14 kuchokera ku fuko la Nafutali, Naabi mwana wa Vofisi;
Of the tribe of Naphtali, Nahbi, the son of Vophsi.
15 kuchokera ku fuko la Gadi, Geuweli mwana wa Maki.
Of the tribe of Gad, Gevel, the son of Machi.
16 Amenewa ndiwo mayina a anthu amene Mose anawatuma kukazonda dzikolo. (Hoseya mwana wa Nuni, Mose anamupatsa dzina loti Yoswa).
These are the names of the men whom Moses sent to get knowledge about the land. And Moses gave to Hoshea, the son of Nun, the name of Joshua.
17 Mose atawatuma kuti akazonde Kanaani anati, “Mupite kudzera ku Negevi, mukapitirire mpaka ku dziko la mapiri.
So Moses sent them to have a look at the land of Canaan, and said to them, Go up into the South and into the hill-country;
18 Mukaone dzikolo kuti ndi lotani ndi anthu okhala mʼmenemo ngati ndi amphamvu kapena ofowoka, ochepa kapena ambiri.
And see what the land is like; and if the people living in it are strong or feeble, small or great in number;
19 Nanga dziko limene akukhalako ndi lotani? Ndi labwino kapena loyipa? Mizinda imene akukhalamo ndi yotani? Kodi ilibe malinga kapena ndi ya malinga?
And what sort of land they are living in, if it is good or bad; and what their living-places are, tent-circles or walled towns;
20 Nthaka yake ndi yotani? Yachonde kapena yopanda chonde? Kodi dzikolo lili ndi mitengo kapena lilibe mitengo? Mukayesetse kubweretsako zipatso za mʼdzikomo.” (Inali nthawi yamphesa zoyamba kupsa).
And if the land is fertile or poor, and if there is wood in it or not. And be of good heart, and come back with some of the produce of the land. Now it was the time when the first grapes were ready.
21 Choncho anapita kukazonda dzikolo kuchokera ku chipululu cha Zini mpaka ku Rehobu, mopenyana ndi Lebo Hamati.
So they went up and got a view of the land, from the waste land of Zin to Rehob, on the way to Hamath.
22 Anapita kudzera ku Negevi ndi kukafika ku Hebroni, kumene Ahimani, Sesai ndi Talimai, ana a Anaki ankakhala. (Anamanga Hebroni zaka zisanu ndi ziwiri asanamange Zowani ku Igupto).
They went up into the South and came to Hebron; and Ahiman and Sheshai and Talmai, the children of Anak, were living there. (Now the building of Hebron took place seven years before that of Zoan in Egypt.)
23 Atafika ku chigwa cha Esikolo, anadulako nthambi ya mpesa ya phava limodzi la mphesa ndipo anthu awiri ananyamulizana, natenganso makangadza ndi nkhuyu.
And they came to the valley of Eshcol, and cutting down a vine-branch with its grapes, two of them took it on a rod between them; and they took some pomegranates and figs.
24 Malo amenewo anawatcha chigwa cha Esikolo chifukwa cha phava la mphesa limene Aisraeli anadula kumeneko.
That place was named the valley of Eshcol because of the grapes which the children of Israel took from there.
25 Patapita masiku makumi anayi, anthu aja anabwerako kokazonda dziko lija.
At the end of forty days they came back from viewing the land.
26 Ndipo atabwerako anapita kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa Aisraeli onse ku Kadesi mʼchipululu cha Parani. Kumeneko anafotokozera anthu onse nawaonetsanso zipatso za mʼdzikolo.
And they came back to Moses and Aaron and all the children of Israel, to Kadesh in the waste land of Paran; and gave an account to them and to all the people and let them see the produce of the land.
27 Anthuwo anafotokozera Mose kuti, “Tinapita ku dziko komwe munatituma. Dzikolo ndi loyenda mkaka ndi uchi ndipo zipatso zake ndi izi.
And they said, We came to the land where you sent us, and truly it is flowing with milk and honey: and here is some of the produce of it.
28 Koma anthu amene amakhala mʼdzikomo ndi amphamvu, mizinda yawo ndi ya malinga aakulu kwambiri. Tinaonanso Aanaki kumeneko.
But the people living in the land are strong, and the towns are walled and very great; further, we saw the children of Anak there.
29 Aamaleki amakhala ku Negevi, Ahiti, Ayebusi ndi Aamori amakhala mʼdziko la mapiri ndipo Akanaani amakhala pafupi ndi nyanja, mʼmbali mwa Yorodani.”
And the Amalekites are in the South; and the Hittites and the Jebusites and the Amorites are living in the hill-country; and the Canaanites by the sea and by the side of Jordan.
30 Koma Kalebe anawakhalitsa chete anthuwo pamaso pa Mose, ndipo anati, “Tiyeni tipite ndithu ndi kutenga dzikolo, pakuti tingathe kulitenga.”
Then Caleb made signs to the people to keep quiet, and said to Moses, Let us go up straight away and take this land; for we are well able to overcome it.
31 Koma anthu aja amene anapita naye anati, “Sitingathe kulimbana ndi anthuwo popeza ndi amphamvu kuposa ifeyo.”
But the men who had gone up with him said, We are not able to go up against the people, for they are stronger than we.
32 Choncho anthuwo anafalitsa pakati pa Aisraeli mbiri yoyipa ya dziko lomwe anakalionalo. Iwo anati, “Dziko limene tinapita kukalizonda limawononga anthu okhala mʼmenemo. Ndipo anthu onse amene tinakawaona kumeneko ndi ataliatali.
And they gave the children of Israel a bad account of the land they had been to see, saying, This land through which we went is a land causing destruction to those living in it; and all the people we saw there are men of more than common size.
33 Kumeneko tinaona Anefili (ana a Aanaki ochokera kwa Nefili). Ifeyo timangodziona ngati ziwala mʼmaso mwawo, ndipo kwa iwo timaonekadi motero ndithu.”
There we saw those great men, the sons of Anak, offspring of the Nephilim: and we seemed to ourselves no more than insects, and so we seemed to them.