< Numeri 13 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
HERREN talede fremdeles til Moses og sagde:
2 “Tuma anthu kuti akazonde dziko la Kanaani limene ndikupereka kwa Aisraeli. Kuchokera pa fuko lililonse utume munthu mmodzi amene ndi mtsogoleri wawo.”
»Send nogle Mænd af Sted for at undersøge Kana'ans Land, som jeg vil give Israeliterne; een Mand af hver Fædrenestamme skal I sende, og kun Mænd, der er Øverster iblandt dem!«
3 Monga mwa mawu a Yehova, Mose anawatuma kuchokera ku chipululu cha Parani. Onsewo anali atsogoleri a Aisraeli.
Da udsendte Moses dem fra Parans Ørken paa HERRENS Bud, Mænd, der alle var Overhoveder for Israeliterne.
4 Mayina awo ndi awa: kuchokera ku fuko la Rubeni, Samuwa mwana wa Zakuri;
Deres Navne var følgende: Af Rubens Stamme Sjammua, Zakkurs Søn,
5 kuchokera ku fuko la Simeoni, Safati mwana wa Hori;
af Simeons Stamme Sjafat, Horis Søn,
6 kuchokera ku fuko la Yuda, Kalebe mwana wa Yefune;
af Judas Stamme Kaleb, Jefunnes Søn,
7 kuchokera ku fuko la Isakara, Igala mwana wa Yosefe;
af Issakars Stamme Jig'al, Josefs Søn,
8 kuchokera ku fuko la Efereimu, Hoseya mwana wa Nuni;
af Efraims Stamme Hosea, Nuns Søn,
9 kuchokera ku fuko la Benjamini, Paliti mwana wa Rafu;
af Benjamins Stamme Palti, Rafus Søn,
10 kuchokera ku fuko la Zebuloni, Gadieli mwana wa Sodi;
af Zebulons Stamme Gaddiel, Sodis Søn,
11 kuchokera ku fuko la Manase (fuko la Yosefe), Gadi mwana wa Susi;
af Josefs Stamme, det er Manasses Stamme, Gaddi, Susis Søn,
12 kuchokera ku fuko la Dani, Amieli mwana wa Gemali;
af Dans Stamme Ammiel, Gemallis Søn,
13 kuchokera ku fuko la Aseri, Seturi mwana wa Mikayeli;
af Asers Stamme Setur, Mikaels Søn,
14 kuchokera ku fuko la Nafutali, Naabi mwana wa Vofisi;
af Naftalis Stamme Nabi, Vofsis Søn,
15 kuchokera ku fuko la Gadi, Geuweli mwana wa Maki.
af Gads Stamme Ge'uel, Makis Søn.
16 Amenewa ndiwo mayina a anthu amene Mose anawatuma kukazonda dzikolo. (Hoseya mwana wa Nuni, Mose anamupatsa dzina loti Yoswa).
Det var Navnene paa de Mænd, Moses udsendte for at undersøge Landet. Men Moses gav Hosea, Nuns Søn, Navnet Josua.
17 Mose atawatuma kuti akazonde Kanaani anati, “Mupite kudzera ku Negevi, mukapitirire mpaka ku dziko la mapiri.
Og Moses sendte dem af Sted for at undersøge Kana'ans Land. Og han sagde til dem: »Drag herfra op i Sydlandet og drag op i Bjergene
18 Mukaone dzikolo kuti ndi lotani ndi anthu okhala mʼmenemo ngati ndi amphamvu kapena ofowoka, ochepa kapena ambiri.
og se, hvordan Landet er, og om Folket, som bor der, er stærkt eller svagt, faatalligt eller talrigt,
19 Nanga dziko limene akukhalako ndi lotani? Ndi labwino kapena loyipa? Mizinda imene akukhalamo ndi yotani? Kodi ilibe malinga kapena ndi ya malinga?
om Landet, de bor i, er godt eller daarligt, og om Byerne, de bor i, er Teltlejre eller Fæstninger,
20 Nthaka yake ndi yotani? Yachonde kapena yopanda chonde? Kodi dzikolo lili ndi mitengo kapena lilibe mitengo? Mukayesetse kubweretsako zipatso za mʼdzikomo.” (Inali nthawi yamphesa zoyamba kupsa).
og om Landet er fedt eller magert, om der findes Træer deri eller ej. Vær ved godt Mod og tag noget af Landets Frugt med tilbage!« Det var netop ved den Tid, de første Druer var modne.
21 Choncho anapita kukazonda dzikolo kuchokera ku chipululu cha Zini mpaka ku Rehobu, mopenyana ndi Lebo Hamati.
Saa drog de af Sted og undersøgte Landet lige fra Zins Ørken til Rehob, Egnen hen imod Hamat.
22 Anapita kudzera ku Negevi ndi kukafika ku Hebroni, kumene Ahimani, Sesai ndi Talimai, ana a Anaki ankakhala. (Anamanga Hebroni zaka zisanu ndi ziwiri asanamange Zowani ku Igupto).
Saa begav de sig op i Sydlandet og kom til Hebron; der boede Ahiman, Sjesjaj og Talmaj, Anaks Efterkommere. Men Hebron var grundlagt syv Aar før Zoan i Ægypten.
23 Atafika ku chigwa cha Esikolo, anadulako nthambi ya mpesa ya phava limodzi la mphesa ndipo anthu awiri ananyamulizana, natenganso makangadza ndi nkhuyu.
Da de naaede Esjkoldalen, afskar de en Ranke med en Drueklase, som der maatte to Mand til at bære paa en Bærestang, og plukkede nogle Granatæbler og Figener.
24 Malo amenewo anawatcha chigwa cha Esikolo chifukwa cha phava la mphesa limene Aisraeli anadula kumeneko.
Man kaldte dette Sted Esjkoldalen med Hentydning til den Drueklase, Israeliterne der skar af.
25 Patapita masiku makumi anayi, anthu aja anabwerako kokazonda dziko lija.
Efter fyrretyve Dages Forløb vendte de tilbage efter at have undersøgt Landet;
26 Ndipo atabwerako anapita kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa Aisraeli onse ku Kadesi mʼchipululu cha Parani. Kumeneko anafotokozera anthu onse nawaonetsanso zipatso za mʼdzikolo.
og de kom til Moses og Aron og hele Israeliternes Menighed i Parans Ørken i Kadesj og aflagde Beretning for dem og hele Menigheden og viste dem Landets Frugt.
27 Anthuwo anafotokozera Mose kuti, “Tinapita ku dziko komwe munatituma. Dzikolo ndi loyenda mkaka ndi uchi ndipo zipatso zake ndi izi.
De fortalte ham: »Vi kom til Landet, du sendte os til; det er virkelig et Land, der flyder med Mælk og Honning, og her er Flugt derfra;
28 Koma anthu amene amakhala mʼdzikomo ndi amphamvu, mizinda yawo ndi ya malinga aakulu kwambiri. Tinaonanso Aanaki kumeneko.
men stærkt er Folket, som bor i Landet, og Byerne er befæstede og meget store; ja, vi saa ogsaa Efterkommere af Anak der.
29 Aamaleki amakhala ku Negevi, Ahiti, Ayebusi ndi Aamori amakhala mʼdziko la mapiri ndipo Akanaani amakhala pafupi ndi nyanja, mʼmbali mwa Yorodani.”
Amalek bor i Sydlandet, Hetiterne, Jebusiterne og Amoriterne i Bjerglandet og Kana'anæerne ved Havet og langs Jordan.«
30 Koma Kalebe anawakhalitsa chete anthuwo pamaso pa Mose, ndipo anati, “Tiyeni tipite ndithu ndi kutenga dzikolo, pakuti tingathe kulitenga.”
Da søgte Kaleb at bringe Folket til Tavshed over for Moses og sagde: »Lad os kun drage op og underlægge os det, thi vi kan sikkert tage det!«
31 Koma anthu aja amene anapita naye anati, “Sitingathe kulimbana ndi anthuwo popeza ndi amphamvu kuposa ifeyo.”
Men de Mænd, der havde været med ham deroppe, sagde: »Vi kan ikke drage op imod dette Folk, thi det er stærkere end vi!«
32 Choncho anthuwo anafalitsa pakati pa Aisraeli mbiri yoyipa ya dziko lomwe anakalionalo. Iwo anati, “Dziko limene tinapita kukalizonda limawononga anthu okhala mʼmenemo. Ndipo anthu onse amene tinakawaona kumeneko ndi ataliatali.
Og de talte nedsættende til Israeliterne om Landet, som de havde undersøgt, og sagde: »Landet, som vi har rejst igennem og undersøgt, er et Land, der fortærer sine Indbyggere, og alle de Folk, vi saa der, var kæmpestore.
33 Kumeneko tinaona Anefili (ana a Aanaki ochokera kwa Nefili). Ifeyo timangodziona ngati ziwala mʼmaso mwawo, ndipo kwa iwo timaonekadi motero ndithu.”
Vi saa der Kæmperne — Anaks Sønner, der er af Kæmpeslægten — og vi forekom baade os selv og dem som Græshopper!«