< Numeri 12 >

1 Miriamu ndi Aaroni anayamba kuyankhula motsutsana ndi Mose chifukwa cha mkazi wa ku Kusi, popeza Moseyo anakwatira Mkusi.
UMiriyemu lo-Aroni basuka basebeqalisa ukusola uMosi ngenxa yomkakhe ongumKhushi, njengoba wayethethe umKhushi.
2 Iwowo anafunsa kuti, “Kodi Yehova anayankhula kudzera mwa Mose yekha? Kodi sanayankhule kudzeranso mwa ife?” Ndipo Yehova anamva zimenezi.
Babuzana bathi: “Kambe uMosi nguye yedwa ongumlomo kaThixo na? Kanti lathi kazange asenze izikhulumeli zakhe na?” UThixo wakuzwa lokhu.
3 (Koma Mose anali munthu wodzichepetsa kwambiri kuposa munthu aliyense pa dziko lapansi).
(UMosi wayeyindoda ethobeke kakhulu, ethobeke ukwedlula wonke amadoda asemhlabeni.)
4 Nthawi yomweyo Yehova anati kwa Mose, Aaroni ndi Miriamu, “Bwerani ku tenti ya msonkhano nonse atatu.” Ndipo atatuwo anapitadi kumeneko.
Khonokho nje uThixo wathi kuMosi, u-Aroni loMiriyemu, “Phumani lize ethenteni lokuhlangana, lonke lobathathu.” Lakanye beza bobathathu.
5 Tsono Yehova anatsika mu mtambo, nayima pa khomo la chihema. Kenaka anayitana Aaroni ndi Miriamu. Ndipo onse awiri atapita patsogolo,
UThixo wehla ngensika yeyezi; wema esangweni lethente wasebiza u-Aroni loMiriyemu. Kwathi lapho sebesondele bobabili,
6 Mulungu anati, “Mverani mawu anga: “Pakakhala mneneri wa Yehova pakati panu, ndimadzionetsera kwa iyeyo mʼmasomphenya, ndimayankhula naye mʼmaloto.
uThixo wasesithi, “Lalelani amazwi ami: Nxa kulomphrofethi kaThixo phakathi kwenu, ngiziveza kuye ngemibono, ngikhuluma laye emaphutsheni.
7 Koma sinditero ndi Mose mtumiki wanga; Iyeyu ndi wokhulupirika mʼnyumba yanga yonse.
Kodwa akunjalo ngenceku yami uMosi; uthembekile endlini yami yonke.
8 Ndimayankhula naye maso ndi maso, momveka bwino osati mophiphiritsa; ndipo amaona maonekedwe a Yehova. Nʼchifukwa chiyani simunaope kuyankhula motsutsana ndi Mose mtumiki wanga?”
Nxa ngikhuluma laye siqondana ubuso ngobuso, ngokucacileyo kungesikuphicana; uyasibona isimo sikaThixo. Kungani pho belingesabi ukusola inceku yami uMosi na?”
9 Ndipo Yehova anawakwiyira, nachoka.
Ulaka lukaThixo lwavutha phezu kwabo, uThixo wasesuka kubo.
10 Pamene mtambo unachoka pamwamba pa Chihema, taonani, Miriamu anagwidwa ndi khate. Aaroni atachewuka anaona Miriamu ali ndi khate;
Ekusukeni kweyezi phezu kwethente, kwabonakala uMiriyemu esemi lapho eselobulephero obunjengongqwaqwane. U-Aroni uthe emkhangela wambona eselobulephero;
11 ndipo Aaroni anawuza Mose kuti, “Pepani mbuye wanga, musatilange chifukwa cha tchimo limene tachita mopusa.
wasesithi kuMosi, “Awu, nkosi yami, ungasibeki icala ngenxa yesono esisenze ngobuwula.
12 Musalole kuti Miriamu akhale ngati mwana wobadwa wakufa kuchoka mʼmimba mwa amayi ake, thupi lake litawonongeka.”
Ungamyekeli enjengomntwana ozelwe efile, inyama yakhe idliwe nganxanye.”
13 Tsono Mose anafuwulira Yehova kuti, “Chonde Inu Mulungu, muchiritseni!”
Ngakho uMosi wakhala kuThixo wathi, “Nkulunkulu, ngiyakucela, msilise.”
14 Yehova anayankha Mose kuti, “Abambo ake akanamulavulira malovu mʼmaso, kodi sakanakhala wonyozeka masiku asanu ndi awiri? Mutsekereni kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri, kenaka mumulowetsenso.”
UThixo waphendula uMosi wathi, “Kambe ngabe uyise ubemkhafulele ebusweni, ubengayikuthwala ihlazo okwensuku eziyisikhombisa na? Mkhupheni ahlale ngaphandle kwezihonqo okwensuku eziyisikhombisa; ngemva kwalokho selingambuyisa.”
15 Choncho anamutsekera Miriamu kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri ndipo anthu sanayende ulendo wawo mpaka Miriamu atamulowetsanso.
Ngakho uMiriyemu wahlaliswa ngaphandle kwezihonqo okwensuku eziyisikhombisa, ngakho abantu kabaqhubekanga ngohambo waze waphenduka.
16 Pambuyo pake anthu ananyamuka ku Heziroti ndi kukamanga mʼchipululu cha Parani.
Ngemva kwalokho, abantu basuka eHazerothi bayamisa izihonqo enkangala yasePharani.

< Numeri 12 >