< Numeri 12 >

1 Miriamu ndi Aaroni anayamba kuyankhula motsutsana ndi Mose chifukwa cha mkazi wa ku Kusi, popeza Moseyo anakwatira Mkusi.
Cependant, Marie avec Aaron parla contre Moïse, à cause de la femme éthiopienne que Moïse avait épousée, car il avait pris une femme éthiopienne.
2 Iwowo anafunsa kuti, “Kodi Yehova anayankhula kudzera mwa Mose yekha? Kodi sanayankhule kudzeranso mwa ife?” Ndipo Yehova anamva zimenezi.
Et ils se dirent l'un à l'autre: Est-ce à Moïse seul que le Seigneur a parlé? Ne vous a-t-il pas parlé pareillement? Et le Seigneur entendit.
3 (Koma Mose anali munthu wodzichepetsa kwambiri kuposa munthu aliyense pa dziko lapansi).
Or, Moïse était le plus doux des hommes existant alors sur la terre.
4 Nthawi yomweyo Yehova anati kwa Mose, Aaroni ndi Miriamu, “Bwerani ku tenti ya msonkhano nonse atatu.” Ndipo atatuwo anapitadi kumeneko.
Soudain le Seigneur dit à Moïse, à Aaron et à Marie: Sortez tous les trois, allez au tabernacle du témoignage. Et ils sortirent tous les trois pour aller au tabernacle du témoignage.
5 Tsono Yehova anatsika mu mtambo, nayima pa khomo la chihema. Kenaka anayitana Aaroni ndi Miriamu. Ndipo onse awiri atapita patsogolo,
Le Seigneur descendit en une colonne de nuée, et il s'arrêta devant la porte du tabernacle du témoignage. Aaron et Marie furent appelés, et tous les deux s'avancèrent.
6 Mulungu anati, “Mverani mawu anga: “Pakakhala mneneri wa Yehova pakati panu, ndimadzionetsera kwa iyeyo mʼmasomphenya, ndimayankhula naye mʼmaloto.
Le Seigneur leur dit: Ecoutez ce que je vais dire: Lorsqu'il y aura parmi vous un prophète du Seigneur, je me manifesterai à lui en des visions, et je lui parlerai pendant son sommeil.
7 Koma sinditero ndi Mose mtumiki wanga; Iyeyu ndi wokhulupirika mʼnyumba yanga yonse.
Il n'en est pas ainsi de mon serviteur Moïse, qui m'est fidèle entre tous ceux de ma maison.
8 Ndimayankhula naye maso ndi maso, momveka bwino osati mophiphiritsa; ndipo amaona maonekedwe a Yehova. Nʼchifukwa chiyani simunaope kuyankhula motsutsana ndi Mose mtumiki wanga?”
A lui je parlerai bouche à bouche clairement, et non en termes obscurs; il a vu la gloire du Seigneur: comment donc n'avez-vous pas crainte de parler contre mon serviteur Moïse?
9 Ndipo Yehova anawakwiyira, nachoka.
Et la colère du Seigneur éclata contre eux, et le Seigneur partit.
10 Pamene mtambo unachoka pamwamba pa Chihema, taonani, Miriamu anagwidwa ndi khate. Aaroni atachewuka anaona Miriamu ali ndi khate;
La nuée s'éloigna du tabernacle, et aussitôt Marie se trouva couverte d'une lèpre blanche comme neige; Aaron la regarda, et voilà qu'elle était lépreuse.
11 ndipo Aaroni anawuza Mose kuti, “Pepani mbuye wanga, musatilange chifukwa cha tchimo limene tachita mopusa.
Et Aaron dit à Moïse: Je le conjure, Seigneur, ne nous fais pas porter la peine de notre péché, car nous avons commis une ignorance, nous avons péché.
12 Musalole kuti Miriamu akhale ngati mwana wobadwa wakufa kuchoka mʼmimba mwa amayi ake, thupi lake litawonongeka.”
Que ce mal n'aille pas la rendre semblable à un cadavre, à un avorton qui sort des entrailles de sa mère, et ronger la moitié de ses chairs.
13 Tsono Mose anafuwulira Yehova kuti, “Chonde Inu Mulungu, muchiritseni!”
Aussitôt, Moïse invoqua le Seigneur, et il dit: Dieu, je vous en conjure, guérissez-la.
14 Yehova anayankha Mose kuti, “Abambo ake akanamulavulira malovu mʼmaso, kodi sakanakhala wonyozeka masiku asanu ndi awiri? Mutsekereni kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri, kenaka mumulowetsenso.”
Le Seigneur répondit à Moïse: Si son père lui eut craché au visage, ne serait-elle pas sept jours dans sa honte? Qu'elle soit donc séparée sept jours hors du camp, ensuite elle y reviendra.
15 Choncho anamutsekera Miriamu kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri ndipo anthu sanayende ulendo wawo mpaka Miriamu atamulowetsanso.
Marie fut donc séparée sept jours hors du camp, et le peuple ne partit pas qu'elle ne fut purifiée.
16 Pambuyo pake anthu ananyamuka ku Heziroti ndi kukamanga mʼchipululu cha Parani.
Après cela le peuple, étant parti d'Aseroth, campa dans le désert de Pharan.

< Numeri 12 >