< Numeri 11 >
1 Anthu atadandaula kwa Yehova chifukwa cha mavuto awo, Yehovayo anamva ndipo anakwiya kwambiri. Kenaka moto wa Yehova unayaka pakati pawo ndi kutentha zigawo zina za kunja kwa msasa.
Cependant il s’éleva un murmure du peuple contre le Seigneur, comme se plaignant de la fatigue. Le Seigneur l’ayant entendu, fut irrité; et le feu du Seigneur allumé contre eux, dévora l’extrémité du camp.
2 Anthuwo analira kwa Mose ndipo Moseyo atapemphera kwa Yehova, motowo unazima.
Alors, comme le peuple cria vers Moïse, Moïse pria le Seigneur, et le feu s’éteignit.
3 Motero malowo anawatcha Tabera, chifukwa moto wa Yehova unayaka pakati pawo.
Et il appela ce lieu du nom d’Embrasement, parce que le feu du Seigneur s’y était allumé contre eux.
4 Anthu ena osokoneza amene anali pakati pa Aisraeli anayamba kukhumba chakudya cha ku Igupto ndipo Aisraeli nawonso anayamba kufuwula kwambiri nʼkumati, “Tikanangopeza nyama yoti nʼkudya!
Car une foule de gens de toute espèce, qui étaient montés avec eux, s’enflamma de convoitise, s’asseyant et pleurant, et les enfants d’Israël s’étant joints aussi à elle, elle dit: Qui nous donnera de la chair à manger?
5 Tikukumbukira nsomba zaulere zimene tinkadya ku Igupto komanso nkhaka, mavwende, anyezi wamitundumitundu ndi adyo.
Nous nous souvenons des poissons que nous mangions en Egypte pour rien: ils nous viennent à l’esprit, les concombres, les melons, les poireaux, les ognons et les aulx.
6 Koma tsopano chilakolako chathu chatha. Sitikuona kanthu kena kakudya koma mana basi!”
Notre âme est aride: nos yeux ne voient que la manne.
7 Mana ankafanana ndi mbewu zamapira ndipo maonekedwe ake anali ngati ulimbo wowuma.
Or la manne était comme de la graine de coriandre, de la couleur du bdellium.
8 Anthu ankapita kukatola manawo, nʼkumasinja mu mtondo kapena kupera. Ankawaphika mu mʼphika kapena kupanga makeke. Ndipo ankakoma ngati makeke ophikira mafuta a olivi.
Et le peuple allait autour du camp, et la recueillant, il la brisait sous la meule, ou il la pilait dans le mortier, la cuisant dans la marmite, et en faisant de petites miches d’une saveur semblable à celle du pain pétri avec de l’huile.
9 Mame akamagwa pa msasawo usiku ankagwera kumodzi ndi manawo.
Et lorsque la rosée descendait pendant la nuit sur le camp, la manne aussi descendait pareillement.
10 Mose anamva anthu a banja lililonse akufuwula, banja lililonse pa khomo la tenti yake. Yehova anakwiya kwambiri ndipo Mose anavutikanso mu mtima.
Moïse entendit donc le peuple pleurant dans les familles, chacun à la porte de sa tente. Alors la fureur du Seigneur fut extrêmement irritée; et la chose parut aussi à Moïse insupportable.
11 Mose anafunsa Yehova kuti, “Chifukwa chiyani mwabweretsa mavuto otere pa mtumiki wanune? Nʼchiyani chimene ndachita choti sichinakusangalatseni mpaka kundisenzetsa katundu wa anthu onsewa?
Et il dit au Seigneur: Pourquoi avez-vous affligé votre serviteur? pourquoi ne trouvé-je point grâce devant vous? et pourquoi avez-vous mis le poids de tout ce peuple sur moi?
12 Kodi Ndine amene ndinatenga pathupi pa anthu onsewa? Kodi ndinawabala ndine? Bwanji mukundiwuza kuti ndiwanyamule mʼmanja mwanga, monga momwe mlezi amanyamulira kamwana, kupita nawo ku malo omwe munalonjeza ndi lumbiro kwa makolo awo?
Est-ce moi qui ai conçu toute cette multitude, ou qui l’ai engendrée, pour que vous me disiez: Porte-les dans ton sein, comme la nourrice a coutume de porter son petit enfant, et conduis-les dans la terre au sujet de laquelle vous avez juré à leurs pères?
13 Ndingayipeze kuti nyama yoti anthu onsewa adye? Iwowa akulirira ine kuti, ‘Tipatse nyama tidye!’
D’où aurai-je de la chair pour en donner à une si grande multitude? ils pleurent contre moi, disant: Donne-nous de la chair, afin que nous en mangions.
14 Sindingathe kusamala anthu onsewa ndekha. Katundu ameneyu ndi wolemera kwambiri kwa ine.
Je ne puis seul soutenir tout ce peuple; parce qu’il est lourd pour moi.
15 Ngati umu ndi mmene muzichitira nane, chonde ingondiphani pompano. Koma ngati mwandikomera mtima ndiye ndisaonenso mavutowa.”
S’il ne vous en semble pas autrement, je demande instamment que vous me fassiez mourir, et que je trouve grâce à vos yeux, pour que je ne sois pas accablé de tant de maux.
16 Yehova anawuza Mose kuti, “Undibweretsere anthu 70 ochokera pakati pa akuluakulu a Aisraeli, amene umawadziwa kuti ndiwo atsogoleri komanso akuluakulu a mabanja. Abwere ku tenti ya msonkhano kuti ayime kumeneko pamodzi ndi iwe.
Et le Seigneur répondit à Moïse: Assemble-moi soixante dix hommes d’entre les anciens d’Israël, que tu sais être les anciens du peuple et les maîtres; et tu les conduiras à la porte du tabernacle d’alliance, et tu les feras rester là avec toi,
17 Ndidzatsika ndi kuyankhula nawe kumeneko, ndipo ndidzatenga mzimu umene uli pa iwe ndi kuyika pa iwowo. Adzakuthandiza kusenza nkhawa za anthuwa ndipo sudzasenzanso wekha.”
Pour que je descende et que je te parle, que je prenne ton esprit et que je leur donne, afin qu’ils soutiennent avec toi le fardeau du peuple, et que toi seul, tu ne sois pas surchargé.
18 “Uwawuze anthuwo kuti, ‘Mudziyeretse, kukonzekera mawa, pamene mudzadya nyama.’ Yehova anakumvani pamene munkalira kuti, ‘Zikanakhala bwino tikanapeza nyama yoti tidye! Tinkakhala bwino ku Igupto!’ Tsopano Yehova adzakupatsani nyama ndipo mudzayidyadi.
Tu diras aussi au peuple: Sanctifiez-vous, demain vous mangerez de la chair. Car moi-même je vous ai entendu dire: Qui nous donnera des aliments de chair? Nous étions bien en Egypte. Ainsi le Seigneur vous donnera de la chair, afin que vous en mangiez,
19 Simudzadya tsiku limodzi lokha, kapena masiku awiri, kapena asanu, khumi kapena masiku makumi awiri,
Non pas un jour, ni deux, ni cinq, ni dix, ni même vingt.
20 koma mwezi wonse, mpaka itakukolani ndi kutopa nayo chifukwa mwakana Yehova yemwe ali pakati panu ndipo mwalira pamaso pake kuti, ‘Bwanji tinachoka ku Igupto?’”
Mais pendant un mois de jours, jusqu’à ce qu’elle sorte par vos narines, qu’elle devienne nauséabonde, parce que vous avez rejeté le Seigneur, qui est au milieu de vous, et que vous avez pleuré devant lui, disant: Pourquoi sommes-nous sortis de l’Egypte?
21 Koma Mose anati, “Taonani pano ndili pakati pa anthu 600,000 amene ndi kuyenda nawo ndipo Inuyo mukuti, ‘Ndidzawapatsa nyama kuti adye mwezi wathunthu!’
Et Moïse dit: Il y a six cent mille hommes de pied dans ce peuple, et vous dites: Je leur donnerai des aliments de chair pendant un mois entier.
22 Kodi ngakhale titapha nkhosa ndi ngʼombe, zingawakwanire? Ngakhale titagwira nsomba zonse za mʼnyanja, kodi zingawakwanire iwowa?”
Est-ce qu’une multitude de brebis et de bœufs sera tuée, pour suffire à leur nourriture? ou bien tous les poissons de la mer seront-ils réunis, afin de les rassasier?
23 Yehova anayankha Mose kuti, “Kodi dzanja langa ndi lalifupi? Uwona tsopano ngati zimene ndanenazo zichitike kapena ayi.”
Le Seigneur lui répondit: Est-ce que la main du Seigneur est impuissante? Dès à présent tu verras si ma parole se réalisera.
24 Choncho Mose anatuluka nakawuza anthu zomwe Yehova ananena. Anasonkhanitsa pamodzi akuluakulu makumi asanu ndi awiri aja ndi kuwayimiritsa mozungulira Chihema.
Moïse vint donc et rapporta au peuple les paroles du Seigneur, rassemblant soixante-dix hommes d’entre les anciens d’Israël, qu’il plaça autour du tabernacle.
25 Ndipo Yehova anatsika mʼmitambo ndi kuyankhula naye ndipo anatengako mzimu womwe unali pa Mose ndi kuwuyika pa akuluakulu makumi asanu ndi awiri aja. Pamene mzimuwo unakhazikika pa akuluakuluwo, anayamba kunenera koma sanapitirize.
Alors le Seigneur descendit dans la nuée, et parla à Moïse, prenant de l’esprit qui était en lui, et le donnant aux soixante-dix hommes. Or, lorsque l’Esprit se fut reposé en eux, ils prophétisèrent et ne cessèrent plus.
26 Koma anthu ena awiri omwe mayina awo anali Elidadi ndi Medadi, anatsalira mu msasa. Anali nawo mʼgulu la olembedwa aja, koma sanapite nawo ku Chihema. Komabe mzimu unakhala pa iwo ndipo ananenera ali mu msasa.
Mais il était demeuré dans le camp deux hommes, dont l’un s’appelait Eldad, et l’autre Médad: l’Esprit se reposa sur eux; car ils avaient été enregistrés, et ils n’étaient pas sortis pour aller au tabernacle.
27 Mnyamata wina anathamanga kudzawuza Mose kuti, “Elidadi ndi Medadi akunenera mu msasa.”
Et, comme ils prophétisaient dans le camp, un enfant courut et l’annonça à Moïse, disant: Eldad et Médad prophétisent dans le camp.
28 Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Mose kuyambira ubwana wake, anayankha kuti, “Mbuye wanga Mose, aletseni!”
Aussitôt Josué, fils de Nun, serviteur de Moïse, et choisi dans le plus grand nombre, dit: Mon seigneur Moïse, empêchez-les.
29 Koma Mose anati, “Kodi ukuchita nsanje chifukwa cha ine? Ndikanakonda kuti anthu onse a Yehova akhale aneneri ndi kuti Yehova ayike mzimu wake pa iwo!”
Mais Moïse: Pourquoi, dit-il, es-tu jaloux pour moi? Plût à Dieu que tout le peuple prophétisât, et que le Seigneur leur donnât son esprit!
30 Mose ndi akuluakulu a Israeli aja anabwerera ku msasa.
Et Moïse revint, ainsi que les anciens d’Israël, dans le camp.
31 Pamenepo Yehova anawutsa mphepo yochokera ku nyanja imene inabweretsa zinziri. Zinzirizo zinagwera pansi kuzungulira msasa, mtunda wa kilomita imodzi mbali zonse ndipo msinkhu wake unali mita imodzi.
Mais un vent envoyé par le Seigneur, saisissant des cailles au-delà de la mer, les porta et les abattit dans le camp, de tout côté autour du camp, dans l’espace du chemin qu’on peut faire en un jour; et elles volaient en l’air à la hauteur de deux coudées au-dessus de la terre.
32 Tsiku limenelo masana onse mpaka usiku ndiponso tsiku lotsatiralo, anthu anatuluka kunja kukatola zinziri. Palibe amene anasonkhanitsa zochepera makilogalamu 1,000 ndipo anaziyanika kuzungulira msasa wonse.
Le peuple, se levant donc durant tout ce jour-là, toute la nuit, et le jour suivant, amassa des cailles, chacun au moins dix mesures; et ils les firent sécher autour du camp.
33 Koma pamene anthuwo ankadya nyamayo, asanayimeze nʼkomwe, ukali wa Yehova unafika pa iwo ndipo Iye anawakantha ndi mliri woopsa.
La chair était encore en leurs dents, et cet aliment n’était pas achevé; et voilà que la fureur du Seigneur excitée contre le peuple, le frappa d’une très grande plaie.
34 Nʼchifukwa chake malowo anawatcha Kibiroti Hatava chifukwa pamenepo anakwirirapo anthu osusuka aja.
Aussi ce lieu fut-il appelé: Sépulcres de la concupiscence; là, en effet, on ensevelit le peuple qui avait désiré de la chair. Mais sortis des Sépulcres de la concupiscence, ils vinrent à Haséroth et y demeurèrent.
35 Kuchoka pa Kibiroti Hatava anthuwo anayenda kupita ku Heziroti ndipo anakhala kumeneko kwa kanthawi.