< Numeri 11 >
1 Anthu atadandaula kwa Yehova chifukwa cha mavuto awo, Yehovayo anamva ndipo anakwiya kwambiri. Kenaka moto wa Yehova unayaka pakati pawo ndi kutentha zigawo zina za kunja kwa msasa.
One day the people complained to Yahweh about their troubles. When Yahweh heard what they were saying, he became angry. So he sent a fire which burned among the people at the edge of their camp.
2 Anthuwo analira kwa Mose ndipo Moseyo atapemphera kwa Yehova, motowo unazima.
Then the people cried out to Moses/me, and he/I prayed to Yahweh. Then the fire stopped burning.
3 Motero malowo anawatcha Tabera, chifukwa moto wa Yehova unayaka pakati pawo.
So they called that place Taberah, [which means ‘burning’], because the fire from Yahweh had burned among them.
4 Anthu ena osokoneza amene anali pakati pa Aisraeli anayamba kukhumba chakudya cha ku Igupto ndipo Aisraeli nawonso anayamba kufuwula kwambiri nʼkumati, “Tikanangopeza nyama yoti nʼkudya!
Then some troublemakers from other people-groups [who were traveling] with the Israelis began to want better food. And [when they started complaining] the Israeli people also started to complain.
5 Tikukumbukira nsomba zaulere zimene tinkadya ku Igupto komanso nkhaka, mavwende, anyezi wamitundumitundu ndi adyo.
They said, “We wish we had some meat!
6 Koma tsopano chilakolako chathu chatha. Sitikuona kanthu kena kakudya koma mana basi!”
We remember the fish that we ate while we were in Egypt, fish that was given to us without (cost/asking us to pay for it). And we had all the cucumbers, melons, leeks, onions, and garlic [that we wanted]. But now we do not have any desire to eat, because all we have to eat is this manna!”
7 Mana ankafanana ndi mbewu zamapira ndipo maonekedwe ake anali ngati ulimbo wowuma.
The manna resembled small white seeds.
8 Anthu ankapita kukatola manawo, nʼkumasinja mu mtondo kapena kupera. Ankawaphika mu mʼphika kapena kupanga makeke. Ndipo ankakoma ngati makeke ophikira mafuta a olivi.
[Each morning] the people would go out and gather some [from the surface of the ground]. Then they made flour by grinding it or pounding it with stones. Then they [added water and] boiled it in a pot, or they made flat cakes with it [and baked them]. The cakes tasted like bread that was baked with [olive] oil.
9 Mame akamagwa pa msasawo usiku ankagwera kumodzi ndi manawo.
Each night the manna came down on their ground where their tents were, like dew [from the sky].
10 Mose anamva anthu a banja lililonse akufuwula, banja lililonse pa khomo la tenti yake. Yehova anakwiya kwambiri ndipo Mose anavutikanso mu mtima.
Moses/I heard all the Israeli people complaining as they were standing in the entrances of their tents. Yahweh became very angry, and Moses/I was also very perturbed.
11 Mose anafunsa Yehova kuti, “Chifukwa chiyani mwabweretsa mavuto otere pa mtumiki wanune? Nʼchiyani chimene ndachita choti sichinakusangalatseni mpaka kundisenzetsa katundu wa anthu onsewa?
He/I [went into the Sacred Tent and] asked Yahweh, “Why have you caused me, your servant, to experience this trouble [RHQ]? Act mercifully to me! What wrong have I done, with the result that you have appointed me to take care of all of these people [RHQ]?
12 Kodi Ndine amene ndinatenga pathupi pa anthu onsewa? Kodi ndinawabala ndine? Bwanji mukundiwuza kuti ndiwanyamule mʼmanja mwanga, monga momwe mlezi amanyamulira kamwana, kupita nawo ku malo omwe munalonjeza ndi lumbiro kwa makolo awo?
(I am not their father./Am I their father?) [RHQ] Why have you told me to take care of them like a woman carries around her baby and (nurses it/gives it her milk) [MET, RHQ]? How can I take them to the land that you promised to give to our ancestors [RHQ]?
13 Ndingayipeze kuti nyama yoti anthu onsewa adye? Iwowa akulirira ine kuti, ‘Tipatse nyama tidye!’
Where can I get meat to feed all these people? They keep complaining to me, saying, ‘Give us some meat to eat!’
14 Sindingathe kusamala anthu onsewa ndekha. Katundu ameneyu ndi wolemera kwambiri kwa ine.
I cannot carry all these people’s burdens by myself! [They are like a heavy load [MET], and] I cannot carry this very heavy load any more.
15 Ngati umu ndi mmene muzichitira nane, chonde ingondiphani pompano. Koma ngati mwandikomera mtima ndiye ndisaonenso mavutowa.”
If you intend to act like this toward me, kill me now. If you are really concerned about me, be kind to me and [kill me to] end my misery [of trying to take care of them]!”
16 Yehova anawuza Mose kuti, “Undibweretsere anthu 70 ochokera pakati pa akuluakulu a Aisraeli, amene umawadziwa kuti ndiwo atsogoleri komanso akuluakulu a mabanja. Abwere ku tenti ya msonkhano kuti ayime kumeneko pamodzi ndi iwe.
Then Yahweh said to Moses/me, “Summon 70 men whom you know are leaders among the Israeli people. Tell them to stand with you in front of the Sacred Tent.
17 Ndidzatsika ndi kuyankhula nawe kumeneko, ndipo ndidzatenga mzimu umene uli pa iwe ndi kuyika pa iwowo. Adzakuthandiza kusenza nkhawa za anthuwa ndipo sudzasenzanso wekha.”
I will come down and talk with you there. Then I will take some of [the power of] my Spirit that you have, and I will put [that power] on them also. They will help you to take care of some of the things that the people are concerned about, in order that you will not need to do it alone.
18 “Uwawuze anthuwo kuti, ‘Mudziyeretse, kukonzekera mawa, pamene mudzadya nyama.’ Yehova anakumvani pamene munkalira kuti, ‘Zikanakhala bwino tikanapeza nyama yoti tidye! Tinkakhala bwino ku Igupto!’ Tsopano Yehova adzakupatsani nyama ndipo mudzayidyadi.
“Furthermore, say to the people, ‘Make yourselves acceptable to me, and tomorrow you will have meat to eat. You were complaining, and Yahweh heard you when you were saying, “We want some meat to eat. We had better food in Egypt!” Now Yahweh will give you some meat, and you will eat it.
19 Simudzadya tsiku limodzi lokha, kapena masiku awiri, kapena asanu, khumi kapena masiku makumi awiri,
You will eat meat not only for one or two days, nor only for five or ten or 20 days.
20 koma mwezi wonse, mpaka itakukolani ndi kutopa nayo chifukwa mwakana Yehova yemwe ali pakati panu ndipo mwalira pamaso pake kuti, ‘Bwanji tinachoka ku Igupto?’”
[You will eat meat every day] for one month, and then you will loathe/despise it, and it will cause you to want to vomit. [This will happen] because you have rejected Yahweh who is here among you, and you have wailed in his presence, saying [“We would have had better food to eat] if we had not left Egypt [RHQ].”’”
21 Koma Mose anati, “Taonani pano ndili pakati pa anthu 600,000 amene ndi kuyenda nawo ndipo Inuyo mukuti, ‘Ndidzawapatsa nyama kuti adye mwezi wathunthu!’
But Moses/I replied to Yahweh, “There are 600,000 men [plus women and children] here with me, so ([why] do you say ‘I will give them plenty of meat every day for a month!’?/it does not seem right for you to say ‘I will give them plenty of meat every day for a month!’) [RHQ]
22 Kodi ngakhale titapha nkhosa ndi ngʼombe, zingawakwanire? Ngakhale titagwira nsomba zonse za mʼnyanja, kodi zingawakwanire iwowa?”
Even if we killed all the sheep and cattle, that would not [RHQ] be enough [to provide meat for all of them] Even if we caught all the fish in the sea [and gave it to them], that would not be enough [RHQ]!”
23 Yehova anayankha Mose kuti, “Kodi dzanja langa ndi lalifupi? Uwona tsopano ngati zimene ndanenazo zichitike kapena ayi.”
But Yahweh said to Moses/me, “Do you think that I [SYN] have no power? You will now see if I can do what I say I will do.”
24 Choncho Mose anatuluka nakawuza anthu zomwe Yehova ananena. Anasonkhanitsa pamodzi akuluakulu makumi asanu ndi awiri aja ndi kuwayimiritsa mozungulira Chihema.
So Moses/I went out [from the Sacred Tent] and told the people what Yahweh had said. Then he/I gathered together the 70 leaders and told them to stand around the Sacred Tent.
25 Ndipo Yehova anatsika mʼmitambo ndi kuyankhula naye ndipo anatengako mzimu womwe unali pa Mose ndi kuwuyika pa akuluakulu makumi asanu ndi awiri aja. Pamene mzimuwo unakhazikika pa akuluakuluwo, anayamba kunenera koma sanapitirize.
Then Yahweh came down in the cloud [that was above the tent] and spoke to Moses/me. He took some of [the power of] the Spirit that he had given to Moses/me and gave it to the 70 leaders. By means of the power of the Spirit within them, they (prophesied/spoke messages that Yahweh gave them), but they did that only once.
26 Koma anthu ena awiri omwe mayina awo anali Elidadi ndi Medadi, anatsalira mu msasa. Anali nawo mʼgulu la olembedwa aja, koma sanapite nawo ku Chihema. Komabe mzimu unakhala pa iwo ndipo ananenera ali mu msasa.
Two of the leaders whom Moses/I appointed, Eldad and Medad, were not there when the rest of them gathered together. They had not left [their tents] to go and stand around the Sacred Tent. But Yahweh’s Spirit came on them also, and they started to (prophesy/speak messages from Yahweh).
27 Mnyamata wina anathamanga kudzawuza Mose kuti, “Elidadi ndi Medadi akunenera mu msasa.”
So a young man ran and told Moses/me, “Eldad and Medad are prophesying in all their tents!”
28 Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Mose kuyambira ubwana wake, anayankha kuti, “Mbuye wanga Mose, aletseni!”
Joshua, who had helped Moses/me since he was a young man, said, “Sir, tell them to stop doing that!”
29 Koma Mose anati, “Kodi ukuchita nsanje chifukwa cha ine? Ndikanakonda kuti anthu onse a Yehova akhale aneneri ndi kuti Yehova ayike mzimu wake pa iwo!”
But Moses/I replied, “(Are you worried that they might injure my reputation/Do you think that I want to be the only one who prophesies) [RHQ]? I wish that all Yahweh’s people could (prophesy/speak messages from Yahweh). I wish that Yahweh would give the power of his Spirit to all of them!”
30 Mose ndi akuluakulu a Israeli aja anabwerera ku msasa.
Then Moses/I and all the leaders went back to their/our tents.
31 Pamenepo Yehova anawutsa mphepo yochokera ku nyanja imene inabweretsa zinziri. Zinzirizo zinagwera pansi kuzungulira msasa, mtunda wa kilomita imodzi mbali zonse ndipo msinkhu wake unali mita imodzi.
Then Yahweh sent a strong wind from the sea. It blew quail into the area all around the camp for miles in every direction, [and caused the quail to fall onto the ground]. They were piled up on the ground about (3 feet/1 meter) high!
32 Tsiku limenelo masana onse mpaka usiku ndiponso tsiku lotsatiralo, anthu anatuluka kunja kukatola zinziri. Palibe amene anasonkhanitsa zochepera makilogalamu 1,000 ndipo anaziyanika kuzungulira msasa wonse.
So the people went out and gathered up the quail all that day, and all that night, and all of the following day. [It seemed as though] everyone gathered at least 50 bushels! They spread the quail out on the ground all around the camp, [so that the quail would dry out].
33 Koma pamene anthuwo ankadya nyamayo, asanayimeze nʼkomwe, ukali wa Yehova unafika pa iwo ndipo Iye anawakantha ndi mliri woopsa.
[Then they cooked them and started to eat them]. But while they were still eating the meat [MTY], Yahweh [showed that he] was very angry with them. He struck them with a severe plague/sickness, [and many people died].
34 Nʼchifukwa chake malowo anawatcha Kibiroti Hatava chifukwa pamenepo anakwirirapo anthu osusuka aja.
The people who died and were buried were the ones who had said they wanted to eat meat [like they had formerly eaten in Egypt]. So they called that place Kibroth-Hattaavah, [which means ‘graves of those who craved’].
35 Kuchoka pa Kibiroti Hatava anthuwo anayenda kupita ku Heziroti ndipo anakhala kumeneko kwa kanthawi.
From there, the Israelis continued walking [east] until they arrived at Hazeroth [town], where they stopped and stayed [for a long time].