< Numeri 11 >

1 Anthu atadandaula kwa Yehova chifukwa cha mavuto awo, Yehovayo anamva ndipo anakwiya kwambiri. Kenaka moto wa Yehova unayaka pakati pawo ndi kutentha zigawo zina za kunja kwa msasa.
And the people were as murmurers, speaking evil in the ears of Jehovah. And when Jehovah heard it, his anger was kindled, and the fire of Jehovah burnt among them, and devoured in the outermost part of the camp.
2 Anthuwo analira kwa Mose ndipo Moseyo atapemphera kwa Yehova, motowo unazima.
And the people cried to Moses. And Moses prayed to Jehovah, and the fire abated.
3 Motero malowo anawatcha Tabera, chifukwa moto wa Yehova unayaka pakati pawo.
And the name of that place was called Taberah, because the fire of Jehovah burnt among them.
4 Anthu ena osokoneza amene anali pakati pa Aisraeli anayamba kukhumba chakudya cha ku Igupto ndipo Aisraeli nawonso anayamba kufuwula kwambiri nʼkumati, “Tikanangopeza nyama yoti nʼkudya!
And the mixed multitude that was among them lusted exceedingly. And the sons of Israel also wept again, and said, Who shall give us flesh to eat?
5 Tikukumbukira nsomba zaulere zimene tinkadya ku Igupto komanso nkhaka, mavwende, anyezi wamitundumitundu ndi adyo.
We remember the fish which we ate in Egypt for nothing, the cucumbers, and the melons, and the leeks, and the onions, and the garlic,
6 Koma tsopano chilakolako chathu chatha. Sitikuona kanthu kena kakudya koma mana basi!”
but now our soul is dried away. There is nothing at all except this manna to look upon.
7 Mana ankafanana ndi mbewu zamapira ndipo maonekedwe ake anali ngati ulimbo wowuma.
And the manna was like coriander seed, and the appearance of it as the appearance of bdellium.
8 Anthu ankapita kukatola manawo, nʼkumasinja mu mtondo kapena kupera. Ankawaphika mu mʼphika kapena kupanga makeke. Ndipo ankakoma ngati makeke ophikira mafuta a olivi.
The people went about, and gathered it, and ground it in mills, or beat it in mortars, and boiled it in pots, and made cakes of it. And the taste of it was as the taste of fresh oil.
9 Mame akamagwa pa msasawo usiku ankagwera kumodzi ndi manawo.
And when the dew fell upon the camp in the night, the manna fell upon it.
10 Mose anamva anthu a banja lililonse akufuwula, banja lililonse pa khomo la tenti yake. Yehova anakwiya kwambiri ndipo Mose anavutikanso mu mtima.
And Moses heard the people weeping throughout their families, every man at the door of his tent. And the anger of Jehovah was kindled greatly, and Moses was displeased.
11 Mose anafunsa Yehova kuti, “Chifukwa chiyani mwabweretsa mavuto otere pa mtumiki wanune? Nʼchiyani chimene ndachita choti sichinakusangalatseni mpaka kundisenzetsa katundu wa anthu onsewa?
And Moses said to Jehovah, Why have thou dealt ill with thy servant? And why have I not found favor in thy sight, that thou lay the burden of all this people upon me?
12 Kodi Ndine amene ndinatenga pathupi pa anthu onsewa? Kodi ndinawabala ndine? Bwanji mukundiwuza kuti ndiwanyamule mʼmanja mwanga, monga momwe mlezi amanyamulira kamwana, kupita nawo ku malo omwe munalonjeza ndi lumbiro kwa makolo awo?
Have I conceived all this people? Have I brought them forth, that thou should say to me, Carry them in thy bosom, as a nurturing father carries the sucking child, to the land which thou swore to their fathers?
13 Ndingayipeze kuti nyama yoti anthu onsewa adye? Iwowa akulirira ine kuti, ‘Tipatse nyama tidye!’
From where should I have flesh to give to all this people? For they weep to me, saying, Give us flesh, that we may eat.
14 Sindingathe kusamala anthu onsewa ndekha. Katundu ameneyu ndi wolemera kwambiri kwa ine.
I am not able to bear all this people alone, because it is too heavy for me.
15 Ngati umu ndi mmene muzichitira nane, chonde ingondiphani pompano. Koma ngati mwandikomera mtima ndiye ndisaonenso mavutowa.”
And if thou deal thus with me, kill me, I pray thee, out of hand, if I have found favor in thy sight, and let me not see my wretchedness.
16 Yehova anawuza Mose kuti, “Undibweretsere anthu 70 ochokera pakati pa akuluakulu a Aisraeli, amene umawadziwa kuti ndiwo atsogoleri komanso akuluakulu a mabanja. Abwere ku tenti ya msonkhano kuti ayime kumeneko pamodzi ndi iwe.
And Jehovah said to Moses, Gather to me seventy men of the elders of Israel, whom thou know to be the elders of the people and officers over them. And bring them to the tent of meeting, that they may stand there with thee.
17 Ndidzatsika ndi kuyankhula nawe kumeneko, ndipo ndidzatenga mzimu umene uli pa iwe ndi kuyika pa iwowo. Adzakuthandiza kusenza nkhawa za anthuwa ndipo sudzasenzanso wekha.”
And I will come down and talk with thee there. And I will take of the spirit which is upon thee, and will put it upon them, and they shall bear the burden of the people with thee, that thou not bear it thyself alone.
18 “Uwawuze anthuwo kuti, ‘Mudziyeretse, kukonzekera mawa, pamene mudzadya nyama.’ Yehova anakumvani pamene munkalira kuti, ‘Zikanakhala bwino tikanapeza nyama yoti tidye! Tinkakhala bwino ku Igupto!’ Tsopano Yehova adzakupatsani nyama ndipo mudzayidyadi.
And say thou to the people, Sanctify yourselves against tomorrow, and ye shall eat flesh, for ye have wept in the ears of Jehovah, saying, Who shall give us flesh to eat? For it was well with us in Egypt. Therefore Jehovah will give you flesh, and ye shall eat.
19 Simudzadya tsiku limodzi lokha, kapena masiku awiri, kapena asanu, khumi kapena masiku makumi awiri,
Ye shall not eat one day, nor two days, nor five days, neither ten days, nor twenty days,
20 koma mwezi wonse, mpaka itakukolani ndi kutopa nayo chifukwa mwakana Yehova yemwe ali pakati panu ndipo mwalira pamaso pake kuti, ‘Bwanji tinachoka ku Igupto?’”
but a whole month, until it comes out at your nostrils, and it be loathsome to you, because ye have rejected Jehovah who is among you, and have wept before him, saying, Why did we come forth out of Egypt?
21 Koma Mose anati, “Taonani pano ndili pakati pa anthu 600,000 amene ndi kuyenda nawo ndipo Inuyo mukuti, ‘Ndidzawapatsa nyama kuti adye mwezi wathunthu!’
And Moses said, The people, among whom I am, are six hundred thousand footmen, and thou have said, I will give them flesh, that they may eat a whole month.
22 Kodi ngakhale titapha nkhosa ndi ngʼombe, zingawakwanire? Ngakhale titagwira nsomba zonse za mʼnyanja, kodi zingawakwanire iwowa?”
Shall flocks and herds be slain for them, to suffice them? Or shall all the fish of the sea be gathered together for them, to suffice them?
23 Yehova anayankha Mose kuti, “Kodi dzanja langa ndi lalifupi? Uwona tsopano ngati zimene ndanenazo zichitike kapena ayi.”
And Jehovah said to Moses, Is Jehovah's hand grown short? Now thou shall see whether my word shall come to pass to thee or not.
24 Choncho Mose anatuluka nakawuza anthu zomwe Yehova ananena. Anasonkhanitsa pamodzi akuluakulu makumi asanu ndi awiri aja ndi kuwayimiritsa mozungulira Chihema.
And Moses went out, and told the people the words of Jehovah. And he gathered seventy men of the elders of the people, and set them round about the tent.
25 Ndipo Yehova anatsika mʼmitambo ndi kuyankhula naye ndipo anatengako mzimu womwe unali pa Mose ndi kuwuyika pa akuluakulu makumi asanu ndi awiri aja. Pamene mzimuwo unakhazikika pa akuluakuluwo, anayamba kunenera koma sanapitirize.
And Jehovah came down in the cloud, and spoke to him, and took of the spirit that was upon him, and put it upon the seventy elders. And it came to pass, that, when the spirit rested upon them, they prophesied, but they did so no more.
26 Koma anthu ena awiri omwe mayina awo anali Elidadi ndi Medadi, anatsalira mu msasa. Anali nawo mʼgulu la olembedwa aja, koma sanapite nawo ku Chihema. Komabe mzimu unakhala pa iwo ndipo ananenera ali mu msasa.
But there remained two men in the camp, the name of the one was Eldad, and the name of the other Medad. And the spirit rested upon them. And they were of those who were written, but had not gone out to the tent. And they prophesied in the camp.
27 Mnyamata wina anathamanga kudzawuza Mose kuti, “Elidadi ndi Medadi akunenera mu msasa.”
And a young man ran, and told Moses, and said, Eldad and Medad do prophesy in the camp.
28 Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Mose kuyambira ubwana wake, anayankha kuti, “Mbuye wanga Mose, aletseni!”
And Joshua the son of Nun, the minister of Moses, one of his chosen men, answered and said, My lord Moses, forbid them.
29 Koma Mose anati, “Kodi ukuchita nsanje chifukwa cha ine? Ndikanakonda kuti anthu onse a Yehova akhale aneneri ndi kuti Yehova ayike mzimu wake pa iwo!”
And Moses said to him, Are thou jealous for my sake? Would that all of Jehovah's people were prophets, that Jehovah would put his spirit upon them!
30 Mose ndi akuluakulu a Israeli aja anabwerera ku msasa.
And Moses went into the camp, he and the elders of Israel.
31 Pamenepo Yehova anawutsa mphepo yochokera ku nyanja imene inabweretsa zinziri. Zinzirizo zinagwera pansi kuzungulira msasa, mtunda wa kilomita imodzi mbali zonse ndipo msinkhu wake unali mita imodzi.
And there went forth a wind from Jehovah, and brought quails from the sea, and let them fall by the camp, about a day's journey on this side, and a day's journey on the other side, round about the camp, and about two cubits above the face of the earth.
32 Tsiku limenelo masana onse mpaka usiku ndiponso tsiku lotsatiralo, anthu anatuluka kunja kukatola zinziri. Palibe amene anasonkhanitsa zochepera makilogalamu 1,000 ndipo anaziyanika kuzungulira msasa wonse.
And the people rose up all that day, and all the night, and all the next day, and gathered the quails. He who gathered least gathered ten homers. And they spread them all abroad for themselves round about the camp.
33 Koma pamene anthuwo ankadya nyamayo, asanayimeze nʼkomwe, ukali wa Yehova unafika pa iwo ndipo Iye anawakantha ndi mliri woopsa.
While the flesh was yet between their teeth, before it was chewed, the anger of Jehovah was kindled against the people, and Jehovah smote the people with a very great plague.
34 Nʼchifukwa chake malowo anawatcha Kibiroti Hatava chifukwa pamenepo anakwirirapo anthu osusuka aja.
And the name of that place was called Kibrothhattaavah, because there they buried the people who lusted.
35 Kuchoka pa Kibiroti Hatava anthuwo anayenda kupita ku Heziroti ndipo anakhala kumeneko kwa kanthawi.
From Kibrothhattaavah the people journeyed to Hazeroth, and they abode at Hazeroth.

< Numeri 11 >