< Numeri 10 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
И сказал Господь Моисею, говоря:
2 “Sula malipenga awiri a siliva, ndipo uziwagwiritsa ntchito posonkhanitsa anthu pamodzi ndiponso powasamutsa mʼmisasa.
сделай себе две серебряные трубы, чеканные сделай их, чтобы они служили тебе для созывания общества и для снятия станов;
3 Pamene akuliza malipenga onse awiri, anthu onse asonkhane kwa iwe pa khomo la tenti ya msonkhano.
когда затрубят ими, соберется к тебе все общество ко входу скинии собрания;
4 Akaliza limodzi lokha, atsogoleri, akulu a mafuko a Aisraeli, asonkhane kwa iwe.
когда одною трубою затрубят, соберутся к тебе князья и тысяченачальники Израилевы;
5 Akaliza lipenga lochenjeza, misasa yomwe ili kummawa iyambe kusamuka.
когда затрубите тревогу, поднимутся станы, становящиеся к востоку;
6 Akaliza lipenga lochenjeza lachiwiri, misasa yakummwera iyambe kusamuka. Kuliza kwa lipenga lochenjeza kudzakhala chizindikiro choyamba ulendo.
когда во второй раз затрубите тревогу, поднимутся станы, становящиеся к югу; когда затрубите в третий раз тревогу, поднимутся станы, становящиеся к морю; когда в четвертый раз затрубите тревогу, поднимутся станы, становящиеся к северу; тревогу пусть трубят при отправлении их в путь;
7 Pofuna kusonkhanitsa anthu, muziliza malipenga, koma mosiyana ndi mmene malipenga ochenjeza amalizidwira.
а когда надобно собрать собрание, трубите, но не тревогу;
8 “Ana a Aaroni, ansembe aja, ndiwo aziliza malipengawo. Zimenezi zikhale zokhazikika kwa inu ndi ku mibado yanu yonse.
сыны Аароновы, священники, должны трубить трубами: это будет вам постановлением вечным в роды ваши;
9 Pamene mukupita ku nkhondo mʼdziko lanu lomwe, kulimbana ndi mdani amene akukuzunzani, muziliza malipenga ochenjeza ndipo Yehova Mulungu wanu adzakukumbukirani ndi kukulanditsani mʼmanja mwa adani anu.
и когда пойдете на войну в земле вашей против врага, наступающего на вас, трубите тревогу трубами, - и будете воспомянуты пред Господом, Богом вашим, и спасены будете от врагов ваших;
10 Komanso pa nthawi yanu ya chisangalalo, pa maphwando anu oyikika ndi maphwando a mwezi watsopano, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zanu za chiyanjano, ndipo zidzakhala chikumbutso chanu pamaso pa Mulungu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.”
и в день веселия вашего, и в праздники ваши, и в новомесячия ваши трубите трубами при всесожжениях ваших и при мирных жертвах ваших, - и это будет напоминанием о вас пред Богом вашим. Я Господь, Бог ваш.
11 Pa chaka chachiwiri, mwezi wachiwiri, tsiku la 20, mtambo unachoka pamwamba pa chihema cha umboni.
Во второй год, во второй месяц, в двадцатый день месяца поднялось облако от скинии откровения;
12 Ndipo Aisraeli ananyamuka kuchoka mʼchipululu cha Sinai ndipo anayenda malo osiyanasiyana mpaka pamene mtambo unayima mʼchipululu cha Parani.
и отправились сыны Израилевы по станам своим из пустыни Синайской, и остановилось облако в пустыне Фаран.
13 Kameneka kanali koyamba kuti Aisraeli anyamuke monga momwe Yehova analamulira Mose.
И поднялись они в первый раз, по повелению Господню, данному чрез Моисея.
14 Magulu a msasa wa Yuda ndiwo anayamba kunyamuka potsata mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu lawo anali Naasoni mwana wa Aminadabu.
Поднято было во-первых знамя стана сынов Иудиных по ополчениям их; над ополчением их Наассон, сын Аминадава;
15 Mtsogoleri wa gulu la fuko la Isakara anali Netanieli mwana wa Zuwara,
и над ополчением колена сынов Иссахаровых Нафанаил, сын Цуара;
16 Eliabu mwana wa Heloni ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Zebuloni.
и над ополчением колена сынов Завулоновых Елиав, сын Хелона.
17 Kenaka anagwetsa chihema, ndipo Ageresoni ndi Amerari amene ananyamula chihemacho, ananyamuka.
И снята была скиния, и пошли сыны Гирсоновы и сыны Мерарины, носящие скинию.
18 Kenaka magulu a msasa wa fuko la Rubeni ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Elizuri mwana wa Sedeuri.
И поднято было знамя стана Рувимова по ополчениям их; и над ополчением его Елицур, сын Шедеура;
19 Mtsogoleri wa fuko la Simeoni anali Selumieli mwana wa Zurisadai,
и над ополчением колена сынов Симеоновых Шелумиил, сын Цуришаддая;
20 ndipo Eliyasafu mwana wa Deuweli ndiye ankatsogolera fuko la Gadi.
и над ополчением колена сынов Гадовых Елиасаф, сын Регуила.
21 Kenaka Akohati ananyamuka atanyamula zinthu zopatulika. Chihema chinkayenera kuyimikidwa iwo asanafike.
Потом пошли сыны Каафовы, носящие святилище; скиния же была поставляема до прихода их.
22 Magulu a msasa wa Aefereimu anatsatira potsatira mbendera yawo. Elisama mwana wa Amihudi ndiye anali mtsogoleri wawo.
И поднято было знамя стана сынов Ефремовых по ополчениям их; и над ополчением их Елишама, сын Аммиуда;
23 Gamalieli mwana wa Pedazuri ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Manase.
и над ополчением колена сынов Манассииных Гамалиил, сын Педацура;
24 Abidani mwana wa Gideoni ndiye anali mtsogoleri wa mtundu wa Benjamini.
и над ополчением колена сынов Вениаминовых Авидан, сын Гидеония.
25 Pambuyo pa magulu onse panali magulu a msasa wa Dani, omwe ankateteza magulu onsewa ndipo ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
Последним из всех станов поднято было знамя стана сынов Дановых с ополчениями их; и над ополчением их Ахиезер, сын Аммишаддая;
26 Pagieli mwana wa Okirani ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Aseri,
и над ополчением колена сынов Асировых Пагиил, сын Охрана;
27 ndipo mtsogoleri wa mtundu wa Nafutali anali Ahira mwana wa Enani.
и над ополчением колена сынов Неффалимовых Ахира, сын Енана.
28 Umenewu ndiwo unali mndandanda wa kayendedwe ka magulu a Aisraeli pamene ankanyamuka ulendo wawo mʼmagulumagulu.
Вот порядок шествия сынов Израилевых по ополчениям их. И отправились они.
29 Ndipo Mose anawuza Hobabu mwana wa Reueli Mmidiyani, mpongozi wa Mose kuti, “Tikunyamuka kupita ku malo amene Yehova anati, ‘Ndidzakupatsani.’ Tiye upite nafe ndipo tidzakusamalira bwino, pakuti Yehova analonjeza zinthu zabwino kwa Israeli.”
И сказал Моисей Ховаву, сыну Рагуилову, Мадианитянину, родственнику Моисееву: мы отправляемся в то место, о котором Господь сказал: вам отдам его; иди с нами, мы сделаем тебе добро, ибо Господь доброе изрек об Израиле.
30 Hobabu anayankha kuti, “Ayi, sindipita nanu, ndibwerera ku dziko la kwathu ndi kwa abale anga.”
Но он сказал ему: не пойду; я пойду в свою землю и на свою родину.
31 Ndipo Mose anati, “Pepa usatisiye popeza ukudziwa kumene tingamange misasa mʼchipululu muno ndipo udzakhala maso athu.
Моисей же сказал: не оставляй нас, потому что ты знаешь, как располагаемся мы станом в пустыне, и будешь для нас глазом;
32 Iweyo ukapita nafe, tidzagawana nawe zinthu zabwino zomwe Yehova adzatipatsa.”
если пойдешь с нами, то добро, которое Господь сделает нам, мы сделаем тебе.
33 Motero ananyamuka ku Phiri la Yehova nayenda ulendo wa masiku atatu. Bokosi la Chipangano cha Yehova linkayenda patsogolo pawo pa masiku atatuwo kuti apeze malo woti apumulepo.
И отправились они от горы Господней на три дня пути, и ковчег завета Господня шел пред ними три дня пути, чтоб усмотреть им место, где остановиться.
34 Mtambo wa Yehova unkawaphimba masana pamene ankasamuka pa misasa yawo.
И облако Господне осеняло их днем, когда они отправлялись из стана.
35 Nthawi iliyonse imene Bokosi la Chipangano likunyamuka, Mose ankanena kuti, “Dzukani, Inu Yehova! Adani anu abalalike; Odana nanu athawe pamaso panu.
Когда поднимался ковчег в путь, Моисей говорил: восстань, Господи, и рассыплются враги Твои, и побегут от лица Твоего ненавидящие Тебя!
36 “Pamene likupumula, ankanena kuti, “Bwererani, Inu Yehova, ku chinamtindi cha Aisraeli.”
А когда останавливался ковчег, он говорил: возвратись, Господи, к тысячам и тьмам Израилевым!