< Numeri 10 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke unto Moses, saying,
2 “Sula malipenga awiri a siliva, ndipo uziwagwiritsa ntchito posonkhanitsa anthu pamodzi ndiponso powasamutsa mʼmisasa.
Make unto thyself two trumpets of silver, beaten out of one piece shalt thou make them; and they shall serve thee for the calling of the congregation, and for the setting forward of the camps.
3 Pamene akuliza malipenga onse awiri, anthu onse asonkhane kwa iwe pa khomo la tenti ya msonkhano.
And when they shall blow with both, all the congregation shall assemble themselves unto thee at the door of the tabernacle of the congregation.
4 Akaliza limodzi lokha, atsogoleri, akulu a mafuko a Aisraeli, asonkhane kwa iwe.
And if they blow with but one, then shall assemble themselves unto thee the princes, the heads of the thousands of Israel.
5 Akaliza lipenga lochenjeza, misasa yomwe ili kummawa iyambe kusamuka.
And when ye blow an alarm, then shall set forward the camps that encamp on the east side.
6 Akaliza lipenga lochenjeza lachiwiri, misasa yakummwera iyambe kusamuka. Kuliza kwa lipenga lochenjeza kudzakhala chizindikiro choyamba ulendo.
And when ye blow an alarm the second time, then shall set forward the camps that encamp on the south side: an alarm shall they blow for their setting forward.
7 Pofuna kusonkhanitsa anthu, muziliza malipenga, koma mosiyana ndi mmene malipenga ochenjeza amalizidwira.
But at the assembling of the assembly, ye shall blow, but ye shall not sound an alarm.
8 “Ana a Aaroni, ansembe aja, ndiwo aziliza malipengawo. Zimenezi zikhale zokhazikika kwa inu ndi ku mibado yanu yonse.
And the sons of Aaron, the priests, shall blow with the trumpets; and they shall be to you for an ordinance for ever throughout your generations.
9 Pamene mukupita ku nkhondo mʼdziko lanu lomwe, kulimbana ndi mdani amene akukuzunzani, muziliza malipenga ochenjeza ndipo Yehova Mulungu wanu adzakukumbukirani ndi kukulanditsani mʼmanja mwa adani anu.
And if ye go to war in your land against the oppressor that oppresseth you, then shall ye blow an alarm with the trumpets; and ye shall be remembered before the Lord your God, and ye shall be saved from your enemies.
10 Komanso pa nthawi yanu ya chisangalalo, pa maphwando anu oyikika ndi maphwando a mwezi watsopano, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zanu za chiyanjano, ndipo zidzakhala chikumbutso chanu pamaso pa Mulungu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.”
And on the day of your gladness, and on your appointed festivals, and on the beginnings of your months, shall ye blow with the trumpets over your burnt-offerings, and over the sacrifices of your peace-offerings; and they shall be to you for a memorial before your God: I am the Lord your God.
11 Pa chaka chachiwiri, mwezi wachiwiri, tsiku la 20, mtambo unachoka pamwamba pa chihema cha umboni.
And it came to pass in the second year, in the second month, on the twentieth day of the month, that the cloud was taken up from off the tabernacle of the testimony.
12 Ndipo Aisraeli ananyamuka kuchoka mʼchipululu cha Sinai ndipo anayenda malo osiyanasiyana mpaka pamene mtambo unayima mʼchipululu cha Parani.
And the children of Israel set forward on their journeys from the wilderness of Sinai, and the cloud halted in the wilderness of Paran.
13 Kameneka kanali koyamba kuti Aisraeli anyamuke monga momwe Yehova analamulira Mose.
And they set forward for the first time at the order of the Lord by the hand of Moses.
14 Magulu a msasa wa Yuda ndiwo anayamba kunyamuka potsata mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu lawo anali Naasoni mwana wa Aminadabu.
And the standard of the camp of the children of Judah set forward at the first, according to their armies: and over their host was Nachshon the son of 'Amminadab.
15 Mtsogoleri wa gulu la fuko la Isakara anali Netanieli mwana wa Zuwara,
And over the host of the tribe of the children of Issachar was Nethanel the son of Zuar.
16 Eliabu mwana wa Heloni ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Zebuloni.
And over the host of the tribe of the children of Zebulun was Eliab the son of Chelon.
17 Kenaka anagwetsa chihema, ndipo Ageresoni ndi Amerari amene ananyamula chihemacho, ananyamuka.
And [in the mean time] the tabernacle was taken down; and then set forward the sons of Gershon and the sons of Merari, the bearers of the tabernacle.
18 Kenaka magulu a msasa wa fuko la Rubeni ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Elizuri mwana wa Sedeuri.
Then set forward the standard of the camp of Reuben, according to their armies: and over their host was Elizur the son of Shedeur.
19 Mtsogoleri wa fuko la Simeoni anali Selumieli mwana wa Zurisadai,
And over the host of the tribe of the children of Simeon was Shelumiel the son of Zurishaddai.
20 ndipo Eliyasafu mwana wa Deuweli ndiye ankatsogolera fuko la Gadi.
And over the host of the tribe of the children of Gad was Elyassaph the son of Deuel.
21 Kenaka Akohati ananyamuka atanyamula zinthu zopatulika. Chihema chinkayenera kuyimikidwa iwo asanafike.
And then set forward the Kehathites, the bearers of the sanctuary: and the others set up the tabernacle against they came.
22 Magulu a msasa wa Aefereimu anatsatira potsatira mbendera yawo. Elisama mwana wa Amihudi ndiye anali mtsogoleri wawo.
Then set forward the standard of the camp of the children of Ephraim according to their armies; and over their host was Elishama the son of 'Ammihud.
23 Gamalieli mwana wa Pedazuri ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Manase.
And over the host of the tribe of the children of Menasseh was Gamliel the son of Pedahzur.
24 Abidani mwana wa Gideoni ndiye anali mtsogoleri wa mtundu wa Benjamini.
And over the host of the tribe of the children of Benjamin was Abidan the son of Gidoni.
25 Pambuyo pa magulu onse panali magulu a msasa wa Dani, omwe ankateteza magulu onsewa ndipo ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
Then set forward the standard of the camp of the children of Dan, the rereward of all the camps, according to their hosts: and over their host was Achiezer the son of 'Ammishaddai.
26 Pagieli mwana wa Okirani ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Aseri,
And over the host of the tribe of the children of Asher was Pagiel the son of 'Ochran.
27 ndipo mtsogoleri wa mtundu wa Nafutali anali Ahira mwana wa Enani.
And over the host of the tribe of the children of Naphtali was Achira the son of 'Enan.
28 Umenewu ndiwo unali mndandanda wa kayendedwe ka magulu a Aisraeli pamene ankanyamuka ulendo wawo mʼmagulumagulu.
In this order were the journeyings of the children of Israel according to their armies, when they set forward.
29 Ndipo Mose anawuza Hobabu mwana wa Reueli Mmidiyani, mpongozi wa Mose kuti, “Tikunyamuka kupita ku malo amene Yehova anati, ‘Ndidzakupatsani.’ Tiye upite nafe ndipo tidzakusamalira bwino, pakuti Yehova analonjeza zinthu zabwino kwa Israeli.”
And Moses said unto Chobab, the son of Reuel the Midianite, the father-in-law of Moses, We are journeying unto the place of which the Lord hath said, This will I give unto you: come thou with us, and we will do thee good; for the Lord hath spoken [to bring] good upon Israel.
30 Hobabu anayankha kuti, “Ayi, sindipita nanu, ndibwerera ku dziko la kwathu ndi kwa abale anga.”
And he said unto him, I will not go; but to my own land, and to my birthplace will I go.
31 Ndipo Mose anati, “Pepa usatisiye popeza ukudziwa kumene tingamange misasa mʼchipululu muno ndipo udzakhala maso athu.
And he said, Do not, I pray thee, leave us; since thou didst find out the places where we were to encamp in the wilderness, and thou hast been to us instead of eyes.
32 Iweyo ukapita nafe, tidzagawana nawe zinthu zabwino zomwe Yehova adzatipatsa.”
And it shall be, if thou go with us, yea, it shall be, that the same goodness which the Lord may do unto us, will we do unto thee.
33 Motero ananyamuka ku Phiri la Yehova nayenda ulendo wa masiku atatu. Bokosi la Chipangano cha Yehova linkayenda patsogolo pawo pa masiku atatuwo kuti apeze malo woti apumulepo.
And they set forward from the mount of the Lord a three days' journey; and the ark of the covenant of the Lord went before them in the three days' journey, to search out for them a resting-place.
34 Mtambo wa Yehova unkawaphimba masana pamene ankasamuka pa misasa yawo.
And the cloud of the Lord was over them by day, when they set forward from the camp.
35 Nthawi iliyonse imene Bokosi la Chipangano likunyamuka, Mose ankanena kuti, “Dzukani, Inu Yehova! Adani anu abalalike; Odana nanu athawe pamaso panu.
And it came to pass, when the ark set forward, that Moses said, Rise up, Lord, and let thy enemies be scattered; and let those that hate thee flee before thy face.
36 “Pamene likupumula, ankanena kuti, “Bwererani, Inu Yehova, ku chinamtindi cha Aisraeli.”
And when it rested, he said, Return, O Lord, among thy myriads of the thousands of Israel.

< Numeri 10 >