< Numeri 10 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke to Moses, saying:
2 “Sula malipenga awiri a siliva, ndipo uziwagwiritsa ntchito posonkhanitsa anthu pamodzi ndiponso powasamutsa mʼmisasa.
Make thee two trumpets of beaten silver, wherewith thou mayest call together the multitude when the camp is to be removed.
3 Pamene akuliza malipenga onse awiri, anthu onse asonkhane kwa iwe pa khomo la tenti ya msonkhano.
And when thou shalt sound the trumpets, all the multitude shall gather unto thee to the door of the tabernacle of the covenant.
4 Akaliza limodzi lokha, atsogoleri, akulu a mafuko a Aisraeli, asonkhane kwa iwe.
If thou sound but once, the princes and the heads of the multitude of Israel shall come to thee.
5 Akaliza lipenga lochenjeza, misasa yomwe ili kummawa iyambe kusamuka.
But if the sound of the trumpets be longer, and with interruptions, they that are on the east side, shall first go forward.
6 Akaliza lipenga lochenjeza lachiwiri, misasa yakummwera iyambe kusamuka. Kuliza kwa lipenga lochenjeza kudzakhala chizindikiro choyamba ulendo.
And at the second sounding and like noise of the trumpet, they who lie on the south side shall take up their tents. And after this manner shall the rest do, when the trumpets shall sound for a march.
7 Pofuna kusonkhanitsa anthu, muziliza malipenga, koma mosiyana ndi mmene malipenga ochenjeza amalizidwira.
But when the people is to be gathered together, the sound of the trumpets shall be plain, and they shall not make a broken sound.
8 “Ana a Aaroni, ansembe aja, ndiwo aziliza malipengawo. Zimenezi zikhale zokhazikika kwa inu ndi ku mibado yanu yonse.
And the sons of Aaron the priest shall sound the trumpets: and this shall be an ordinance for ever in your generations.
9 Pamene mukupita ku nkhondo mʼdziko lanu lomwe, kulimbana ndi mdani amene akukuzunzani, muziliza malipenga ochenjeza ndipo Yehova Mulungu wanu adzakukumbukirani ndi kukulanditsani mʼmanja mwa adani anu.
If you go forth to war out of your land against the enemies that fight against you, you shall sound aloud with the trumpets, and there shall be a remembrance of you before the Lord your God, that you may be delivered out of the hands of your enemies.
10 Komanso pa nthawi yanu ya chisangalalo, pa maphwando anu oyikika ndi maphwando a mwezi watsopano, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zanu za chiyanjano, ndipo zidzakhala chikumbutso chanu pamaso pa Mulungu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.”
If at any time you shall have a banquet, and on your festival days, and on the first days of your months, you shall sound the trumpets over the holocausts, and the sacrifices of peace offerings, that they may be to you for a remembrance of your God. I am the Lord your God.
11 Pa chaka chachiwiri, mwezi wachiwiri, tsiku la 20, mtambo unachoka pamwamba pa chihema cha umboni.
The second year, in the second month, the twentieth day of the month, the cloud was taken up from the tabernacle of the covenant.
12 Ndipo Aisraeli ananyamuka kuchoka mʼchipululu cha Sinai ndipo anayenda malo osiyanasiyana mpaka pamene mtambo unayima mʼchipululu cha Parani.
And the children of Israel marched by their troops from the desert of Sinai, and the cloud rested in the wilderness of Pharan.
13 Kameneka kanali koyamba kuti Aisraeli anyamuke monga momwe Yehova analamulira Mose.
And the first went forward according to the commandment of the Lord by the hand of Moses.
14 Magulu a msasa wa Yuda ndiwo anayamba kunyamuka potsata mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu lawo anali Naasoni mwana wa Aminadabu.
The sons of Juda by their troops: whose prince was Nahasson the son of Aminadab.
15 Mtsogoleri wa gulu la fuko la Isakara anali Netanieli mwana wa Zuwara,
In the tribe of the sons of Issachar, the prince was Nathanael the son of Suar.
16 Eliabu mwana wa Heloni ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Zebuloni.
In the tribe of Zabulon, the prince was Eliab the son of Helon.
17 Kenaka anagwetsa chihema, ndipo Ageresoni ndi Amerari amene ananyamula chihemacho, ananyamuka.
And the tabernacle was taken down, and the sons of Gerson and Merari set forward, bearing it.
18 Kenaka magulu a msasa wa fuko la Rubeni ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Elizuri mwana wa Sedeuri.
And the sons of Ruben also marched, by their troops and ranks, whose prince was Helisur the son of Sedeur.
19 Mtsogoleri wa fuko la Simeoni anali Selumieli mwana wa Zurisadai,
And in the tribe of Simeon, the prince was Salamiel the son of Surisaddai.
20 ndipo Eliyasafu mwana wa Deuweli ndiye ankatsogolera fuko la Gadi.
And in the tribe of Cad, the prince was Eliasaph the son of Duel.
21 Kenaka Akohati ananyamuka atanyamula zinthu zopatulika. Chihema chinkayenera kuyimikidwa iwo asanafike.
Then the Caathites also marched carrying the sanctuary. So long was the tabernacle carried, till they same to the place of setting it up.
22 Magulu a msasa wa Aefereimu anatsatira potsatira mbendera yawo. Elisama mwana wa Amihudi ndiye anali mtsogoleri wawo.
The sons of Ephraim also moved their camp by their troops, in whose army the prince was Elisama the son of Ammiud.
23 Gamalieli mwana wa Pedazuri ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Manase.
And in the tribe of the sons of Manasses, the prince was Gamaliel the son of Phadassur.
24 Abidani mwana wa Gideoni ndiye anali mtsogoleri wa mtundu wa Benjamini.
And in the tribe of Benjamin, the prince was Abidan the son of Gedeon.
25 Pambuyo pa magulu onse panali magulu a msasa wa Dani, omwe ankateteza magulu onsewa ndipo ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
The last of all the camp marched the sons of Dan by their troops, in whose army the prince was Ahiezer the son of Ammisaddai.
26 Pagieli mwana wa Okirani ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Aseri,
And in the tribe of the sons of Aser, the prince was Phegiel the son of Ochran.
27 ndipo mtsogoleri wa mtundu wa Nafutali anali Ahira mwana wa Enani.
And in the tribe of the sons of Nephtali, the prince was Ahira the son of Enan.
28 Umenewu ndiwo unali mndandanda wa kayendedwe ka magulu a Aisraeli pamene ankanyamuka ulendo wawo mʼmagulumagulu.
This was the order of the camps, and marches of the children of Israel by their troops, when they set forward.
29 Ndipo Mose anawuza Hobabu mwana wa Reueli Mmidiyani, mpongozi wa Mose kuti, “Tikunyamuka kupita ku malo amene Yehova anati, ‘Ndidzakupatsani.’ Tiye upite nafe ndipo tidzakusamalira bwino, pakuti Yehova analonjeza zinthu zabwino kwa Israeli.”
And Moses said to Hobab the son of Raguel the Madianite, his kinsman: We are going towards the place which the Lord will give us: come with us, that we may do thee good: for the Lord hath promised good things to Israel.
30 Hobabu anayankha kuti, “Ayi, sindipita nanu, ndibwerera ku dziko la kwathu ndi kwa abale anga.”
But he answered him: I will not go with thee, but I will return to my country, wherein I was born.
31 Ndipo Mose anati, “Pepa usatisiye popeza ukudziwa kumene tingamange misasa mʼchipululu muno ndipo udzakhala maso athu.
And he said: Do not leave us: for thou knowest in what places we should encamp in the wilderness, and thou shalt be our guide.
32 Iweyo ukapita nafe, tidzagawana nawe zinthu zabwino zomwe Yehova adzatipatsa.”
And if thou comest with us, we will give thee what is the best of the riches which the Lord shall deliver to us.
33 Motero ananyamuka ku Phiri la Yehova nayenda ulendo wa masiku atatu. Bokosi la Chipangano cha Yehova linkayenda patsogolo pawo pa masiku atatuwo kuti apeze malo woti apumulepo.
So they marched from the mount of the Lord three days’ journey, and the ark of the covenant of the Lord went before them, for three days providing a place for the camp.
34 Mtambo wa Yehova unkawaphimba masana pamene ankasamuka pa misasa yawo.
The cloud also of the Lord was over them by day when they marched.
35 Nthawi iliyonse imene Bokosi la Chipangano likunyamuka, Mose ankanena kuti, “Dzukani, Inu Yehova! Adani anu abalalike; Odana nanu athawe pamaso panu.
And when the ark was lifted up, Moses said: Arise, O Lord, and let thy enemies be scattered, and let them that hate thee, flee from before thy face.
36 “Pamene likupumula, ankanena kuti, “Bwererani, Inu Yehova, ku chinamtindi cha Aisraeli.”
And when it was set down, he said: Return, O Lord, to the multitude of the host of Israel.