< Numeri 10 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
HERREN talede fremdeles til Moses og sagde:
2 “Sula malipenga awiri a siliva, ndipo uziwagwiritsa ntchito posonkhanitsa anthu pamodzi ndiponso powasamutsa mʼmisasa.
Du skal lave dig to Sølvtrompeter; i drevet Arbejde skal du lave dem. Dem skal du bruge, naar Menigheden skal kaldes sammen, og naar Lejrene skal bryde op.
3 Pamene akuliza malipenga onse awiri, anthu onse asonkhane kwa iwe pa khomo la tenti ya msonkhano.
Naar der blæses i dem begge to, skal hele Menigheden samle sig hos dig ved Indgangen til Aabenbaringsteltet.
4 Akaliza limodzi lokha, atsogoleri, akulu a mafuko a Aisraeli, asonkhane kwa iwe.
Blæses der kun i den ene, skal Øversterne, Overhovederne for Israels Stammer, samle sig hos dig.
5 Akaliza lipenga lochenjeza, misasa yomwe ili kummawa iyambe kusamuka.
Naar I blæser Alarm med dem, skal Lejrene paa Østsiden bryde op;
6 Akaliza lipenga lochenjeza lachiwiri, misasa yakummwera iyambe kusamuka. Kuliza kwa lipenga lochenjeza kudzakhala chizindikiro choyamba ulendo.
blæser Alarm anden Gang, skal Lejrene paa Sydsiden bryde op: tredje Gang skal Lejrene mod Vest bryde op, fjerde Gang Lejrene mod Nord; der skal blæses Alarm, naar de skal bryde op.
7 Pofuna kusonkhanitsa anthu, muziliza malipenga, koma mosiyana ndi mmene malipenga ochenjeza amalizidwira.
Men naar Forsamlingen skal sammenkaldes skal I blæse paa almindelig Vis, ikke Alarm.
8 “Ana a Aaroni, ansembe aja, ndiwo aziliza malipengawo. Zimenezi zikhale zokhazikika kwa inu ndi ku mibado yanu yonse.
Arons Sønner, Præsterne, skal blæse i Trompeterne; det skal være eder en evig gyldig Anordning fra Slægt til Slægt.
9 Pamene mukupita ku nkhondo mʼdziko lanu lomwe, kulimbana ndi mdani amene akukuzunzani, muziliza malipenga ochenjeza ndipo Yehova Mulungu wanu adzakukumbukirani ndi kukulanditsani mʼmanja mwa adani anu.
Naar I drager i Krig i eders Land mod en Fjende, der angriber eder, og blæser Alarm med Trompeterne, skal I ihukommes for HERREN eders Guds Aasyn og frelses fra eders Fjender.
10 Komanso pa nthawi yanu ya chisangalalo, pa maphwando anu oyikika ndi maphwando a mwezi watsopano, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zanu za chiyanjano, ndipo zidzakhala chikumbutso chanu pamaso pa Mulungu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.”
Og paa eders Glædesdage, eders Højtider og Nymaanedage, skal I blæse i Trompeterne ved eders Brændofre og Takofre; saa skal de tjene eder til Ihukommelse for eders Guds Aasyn. Jeg er HERREN eders Gud!
11 Pa chaka chachiwiri, mwezi wachiwiri, tsiku la 20, mtambo unachoka pamwamba pa chihema cha umboni.
Den tyvende Dag i den anden Maaned af det andet Aar løftede Skyen sig fra Vidnesbyrdets Bolig.
12 Ndipo Aisraeli ananyamuka kuchoka mʼchipululu cha Sinai ndipo anayenda malo osiyanasiyana mpaka pamene mtambo unayima mʼchipululu cha Parani.
Da brød Israeliterne op fra Sinaj Ørken, i den Orden de skulde bryde op i, og Skyen stod stille i Parans Ørken.
13 Kameneka kanali koyamba kuti Aisraeli anyamuke monga momwe Yehova analamulira Mose.
Da de nu første Gang brød op efter Guds Bud ved Moses,
14 Magulu a msasa wa Yuda ndiwo anayamba kunyamuka potsata mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu lawo anali Naasoni mwana wa Aminadabu.
var Judæernes Lejr den første, der brød op under sit Felttegn, Hærafdeling for Hærafdeling; deres Hær førtes af Nahasjon, Amminadabs Søn.
15 Mtsogoleri wa gulu la fuko la Isakara anali Netanieli mwana wa Zuwara,
Issakariternes Stammes Hær førtes af Netan'el, Zuars Søn,
16 Eliabu mwana wa Heloni ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Zebuloni.
og Zebuloniternes Stammes Hær af Eliab, Helons Søn.
17 Kenaka anagwetsa chihema, ndipo Ageresoni ndi Amerari amene ananyamula chihemacho, ananyamuka.
Da derpaa Boligen var taget ned, brød Gersoniterne og Merariterne op og bar Boligen.
18 Kenaka magulu a msasa wa fuko la Rubeni ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Elizuri mwana wa Sedeuri.
Saa brød Rubens Lejr op under sit Felttegn, Hærafdeling for Hærafdeling; deres Hær førtes af Elizur, Sjede'urs Søn.
19 Mtsogoleri wa fuko la Simeoni anali Selumieli mwana wa Zurisadai,
Simeoniternes Stammes Hær førtes af Sjelumiel, Zurisjaddajs Søn,
20 ndipo Eliyasafu mwana wa Deuweli ndiye ankatsogolera fuko la Gadi.
og Gaditernes Stammes Hær af Eljasaf, De'uels Søn.
21 Kenaka Akohati ananyamuka atanyamula zinthu zopatulika. Chihema chinkayenera kuyimikidwa iwo asanafike.
Saa brød Kehatiterne, der bar de hellige Ting, op; og før deres Komme havde man rejst Boligen.
22 Magulu a msasa wa Aefereimu anatsatira potsatira mbendera yawo. Elisama mwana wa Amihudi ndiye anali mtsogoleri wawo.
Saa brød Efraimiternes Lejr op under sit Felttegn, Hærafdeling for Hærafdeling; deres Hær førtes af Elisjama, Ammihuds Søn.
23 Gamalieli mwana wa Pedazuri ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Manase.
Manassiternes Stammes Hær førtes af Gamliel, Pedazurs Søn,
24 Abidani mwana wa Gideoni ndiye anali mtsogoleri wa mtundu wa Benjamini.
og Benjaminiternes Stammes Hær af Abidan, Gid'onis Søn.
25 Pambuyo pa magulu onse panali magulu a msasa wa Dani, omwe ankateteza magulu onsewa ndipo ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
Saa brød Daniternes Lejr op under sit Felttegn som Bagtrop i hele Lejrtoget, Hærafdeling for Hærafdeling; deres Hær førtes af Ahiezer, Ammisjaddajs Søn.
26 Pagieli mwana wa Okirani ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Aseri,
Aseriternes Stammes Hær førtes af Pag'iel, Okrans Søn,
27 ndipo mtsogoleri wa mtundu wa Nafutali anali Ahira mwana wa Enani.
og Naftaliternes Stammes Hær af Ahira, Enans Søn.
28 Umenewu ndiwo unali mndandanda wa kayendedwe ka magulu a Aisraeli pamene ankanyamuka ulendo wawo mʼmagulumagulu.
Saaledes foregik Israeliternes Opbrud, Hærafdeling for Hærafdeling. Saa brød de da op.
29 Ndipo Mose anawuza Hobabu mwana wa Reueli Mmidiyani, mpongozi wa Mose kuti, “Tikunyamuka kupita ku malo amene Yehova anati, ‘Ndidzakupatsani.’ Tiye upite nafe ndipo tidzakusamalira bwino, pakuti Yehova analonjeza zinthu zabwino kwa Israeli.”
Men Moses sagde til Midjaniten Hobab, Re'uels Søn, Moses's Svigerfader: »Vi bryder nu op for at drage til det Sted, HERREN har lovet at give os; drag med os! Vi skal lønne dig godt, thi HERREN har stillet Israel gode Ting i Udsigt.«
30 Hobabu anayankha kuti, “Ayi, sindipita nanu, ndibwerera ku dziko la kwathu ndi kwa abale anga.”
Men han svarede ham: »Jeg vil ikke drage med; nej, jeg drager til mit Land og min Slægt.«
31 Ndipo Mose anati, “Pepa usatisiye popeza ukudziwa kumene tingamange misasa mʼchipululu muno ndipo udzakhala maso athu.
Da sagde han: »Forlad os ikke! Du kender jo de Steder, hvor vi kan slaa Lejr i Ørkenen; vær Øje for os!
32 Iweyo ukapita nafe, tidzagawana nawe zinthu zabwino zomwe Yehova adzatipatsa.”
Drager du med os, skal vi give dig Del i alt det gode, HERREN vil give os.«
33 Motero ananyamuka ku Phiri la Yehova nayenda ulendo wa masiku atatu. Bokosi la Chipangano cha Yehova linkayenda patsogolo pawo pa masiku atatuwo kuti apeze malo woti apumulepo.
Derpaa brød de op fra HERRENS Bjerg og vandrede tre Dagsrejser frem, idet HERRENS Pagts Ark drog i Forvejen for at søge dem et Sted, hvor de kunde holde Hvil.
34 Mtambo wa Yehova unkawaphimba masana pamene ankasamuka pa misasa yawo.
Og HERRENS Sky svævede over dem om Dagen, naar de brød op fra Lejren.
35 Nthawi iliyonse imene Bokosi la Chipangano likunyamuka, Mose ankanena kuti, “Dzukani, Inu Yehova! Adani anu abalalike; Odana nanu athawe pamaso panu.
Og hver Gang Arken brød op, sagde Moses: »Staa op, HERRE, at dine Fjender maa splittes og dine Avindsmænd fly for dit Aasyn!«
36 “Pamene likupumula, ankanena kuti, “Bwererani, Inu Yehova, ku chinamtindi cha Aisraeli.”
Og hver Gang den standsede, sagde han: »Vend tilbage, HERRE, til Israels Stammers Titusinder!«

< Numeri 10 >