< Numeri 10 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
Jahve reče Mojsiju:
2 “Sula malipenga awiri a siliva, ndipo uziwagwiritsa ntchito posonkhanitsa anthu pamodzi ndiponso powasamutsa mʼmisasa.
“Napravi sebi dvije trube; napravi ih od kovana srebra. Neka ti služe za sazivanje zajednice i za pokretanje tabora.
3 Pamene akuliza malipenga onse awiri, anthu onse asonkhane kwa iwe pa khomo la tenti ya msonkhano.
Kad se u njih zatrubi, neka se sva zajednica skupi k tebi na ulazu u Šator sastanka.
4 Akaliza limodzi lokha, atsogoleri, akulu a mafuko a Aisraeli, asonkhane kwa iwe.
Ako li se zatrubi u jednu, neka se k tebi skupe glavari izraelski, tisućnici.
5 Akaliza lipenga lochenjeza, misasa yomwe ili kummawa iyambe kusamuka.
Kad popratite trubljenje bojnim poklikom, neka krenu logori utaboreni na istočnoj strani.
6 Akaliza lipenga lochenjeza lachiwiri, misasa yakummwera iyambe kusamuka. Kuliza kwa lipenga lochenjeza kudzakhala chizindikiro choyamba ulendo.
Kad popratite trubljenje bojnim poklikom po drugi put, neka krenu logori utaboreni s južne strane: neka se trubljenje poprati bojnim poklikom da oni krenu.
7 Pofuna kusonkhanitsa anthu, muziliza malipenga, koma mosiyana ndi mmene malipenga ochenjeza amalizidwira.
Trubite i da skupite zajednicu, ali bez bojnog poklika.
8 “Ana a Aaroni, ansembe aja, ndiwo aziliza malipengawo. Zimenezi zikhale zokhazikika kwa inu ndi ku mibado yanu yonse.
Neka u trube trube svećenici, sinovi Aronovi. Neka vam to bude trajnom uredbom za vaše naraštaje.
9 Pamene mukupita ku nkhondo mʼdziko lanu lomwe, kulimbana ndi mdani amene akukuzunzani, muziliza malipenga ochenjeza ndipo Yehova Mulungu wanu adzakukumbukirani ndi kukulanditsani mʼmanja mwa adani anu.
Kad u svojoj zemlji pođete u rat na neprijatelja koji vas pritisne, zaorite na trube s bojnim poklikom, i Jahve, Bog vaš, sjetit će se vas i bit ćete izbavljeni od svojih neprijatelja.
10 Komanso pa nthawi yanu ya chisangalalo, pa maphwando anu oyikika ndi maphwando a mwezi watsopano, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zanu za chiyanjano, ndipo zidzakhala chikumbutso chanu pamaso pa Mulungu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.”
Na dan svoje svečanosti, svojih blagdana ili svojih mjesečevih mlađaka, dok prinosite svoje paljenice i pričesnice, trubite u trube. Neka to za vas bude spomen pred Bogom vašim. Ja sam Jahve, Bog vaš.”
11 Pa chaka chachiwiri, mwezi wachiwiri, tsiku la 20, mtambo unachoka pamwamba pa chihema cha umboni.
Druge godine drugoga mjeseca dvadesetog dana u mjesecu diže se oblak iznad Prebivališta svjedočanstva.
12 Ndipo Aisraeli ananyamuka kuchoka mʼchipululu cha Sinai ndipo anayenda malo osiyanasiyana mpaka pamene mtambo unayima mʼchipululu cha Parani.
Tada se Izraelci zapute iz Sinajske pustinje na svoja putovanja. Oblak se zaustavi u pustinji Paranu.
13 Kameneka kanali koyamba kuti Aisraeli anyamuke monga momwe Yehova analamulira Mose.
Tako na Jahvinu zapovijed danu Mojsiju krenuše prvi put.
14 Magulu a msasa wa Yuda ndiwo anayamba kunyamuka potsata mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu lawo anali Naasoni mwana wa Aminadabu.
Prva je krenula zastava tabora Judinih sinova u svojim četama. Nad njihovom vojskom bijaše Nahšon, sin Aminadabov;
15 Mtsogoleri wa gulu la fuko la Isakara anali Netanieli mwana wa Zuwara,
nad vojskom plemena Jisakarovaca stajaše Netanel, sin Suarov,
16 Eliabu mwana wa Heloni ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Zebuloni.
a nad vojskom plemena Zebulunovaca bijaše Eliab, sin Helonov.
17 Kenaka anagwetsa chihema, ndipo Ageresoni ndi Amerari amene ananyamula chihemacho, ananyamuka.
Zatim, pošto je rastavljeno Prebivalište, krenuše Geršonovci i Merarijevci noseći Prebivalište.
18 Kenaka magulu a msasa wa fuko la Rubeni ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Elizuri mwana wa Sedeuri.
Potom krenu zastava tabora Rubenova u svojim četama. Nad njihovom vojskom bijaše Elisur, sin Šedeurov;
19 Mtsogoleri wa fuko la Simeoni anali Selumieli mwana wa Zurisadai,
nad vojskom plemena Šimunovaca stajao je Šelumiel, sin Surišadajev;
20 ndipo Eliyasafu mwana wa Deuweli ndiye ankatsogolera fuko la Gadi.
nad vojskom plemena Gadovaca bio je Elijasaf, sin Deuelov.
21 Kenaka Akohati ananyamuka atanyamula zinthu zopatulika. Chihema chinkayenera kuyimikidwa iwo asanafike.
Potom krenuše Kehatovci noseći posvećene predmete. Tako je Prebivalište bilo podignuto prije njihova dolaska.
22 Magulu a msasa wa Aefereimu anatsatira potsatira mbendera yawo. Elisama mwana wa Amihudi ndiye anali mtsogoleri wawo.
Onda krenu zastava tabora Efrajimovaca u svojim četama. Nad njihovom vojskom bijaše Elišama, sin Amihudov,
23 Gamalieli mwana wa Pedazuri ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Manase.
nad vojskom plemena Manašeovaca stajaše Gamliel, sin Pedahsurov;
24 Abidani mwana wa Gideoni ndiye anali mtsogoleri wa mtundu wa Benjamini.
nad vojskom plemena Benjaminovaca bijaše Abidan, sin Gidonijev.
25 Pambuyo pa magulu onse panali magulu a msasa wa Dani, omwe ankateteza magulu onsewa ndipo ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
A kao zalazna straža za sve tabore krenu, u svojim četama, zastava tabora Danovaca. Nad njihovom je vojskom stajao Ahiezer, sin Amišadajev.
26 Pagieli mwana wa Okirani ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Aseri,
Nad vojskom plemena Ašerovaca bio je Pagiel, sin Okranov;
27 ndipo mtsogoleri wa mtundu wa Nafutali anali Ahira mwana wa Enani.
a nad vojskom plemena Naftalijevaca bio je Ahira, sin Enanov.
28 Umenewu ndiwo unali mndandanda wa kayendedwe ka magulu a Aisraeli pamene ankanyamuka ulendo wawo mʼmagulumagulu.
Takav je bio red putovanja Izraelaca svrstanih u svoje čete. Tako su putovali.
29 Ndipo Mose anawuza Hobabu mwana wa Reueli Mmidiyani, mpongozi wa Mose kuti, “Tikunyamuka kupita ku malo amene Yehova anati, ‘Ndidzakupatsani.’ Tiye upite nafe ndipo tidzakusamalira bwino, pakuti Yehova analonjeza zinthu zabwino kwa Israeli.”
Mojsije reče Hobabu, sinu Midjanca Reuela, Mojsijeva tasta: “Zaputili smo se u kraj o kojemu je Jahve rekao: 'Dat ću vam ga!' Pođi s nama i dobro ćemo ti činiti, jer je Jahve obećao sreću Izraelu.”
30 Hobabu anayankha kuti, “Ayi, sindipita nanu, ndibwerera ku dziko la kwathu ndi kwa abale anga.”
“Ne idem”, odgovori mu, “nego se vraćam u svoju zemlju; k svojima se vraćam.”
31 Ndipo Mose anati, “Pepa usatisiye popeza ukudziwa kumene tingamange misasa mʼchipululu muno ndipo udzakhala maso athu.
“Molim te, ne ostavljaj nas!” - reče. “Budući da znaš gdje nam se treba u pustinji utaboriti, valjat ćeš nam kao oči.
32 Iweyo ukapita nafe, tidzagawana nawe zinthu zabwino zomwe Yehova adzatipatsa.”
Ako s nama pođeš, dobročinstva koja nam Jahve bude udijelio s tobom ćemo dijeliti.”
33 Motero ananyamuka ku Phiri la Yehova nayenda ulendo wa masiku atatu. Bokosi la Chipangano cha Yehova linkayenda patsogolo pawo pa masiku atatuwo kuti apeze malo woti apumulepo.
Od Jahvina brda putovali su tri dana hoda. Kovčeg Jahvina saveza išao je pred njima ta tri dana hoda da im potraži mjesto odmora.
34 Mtambo wa Yehova unkawaphimba masana pamene ankasamuka pa misasa yawo.
Danju je opet Jahvin oblak bio nad njima, kako bi se iz tabora zaputili.
35 Nthawi iliyonse imene Bokosi la Chipangano likunyamuka, Mose ankanena kuti, “Dzukani, Inu Yehova! Adani anu abalalike; Odana nanu athawe pamaso panu.
Kad bi Kovčeg polazio, Mojsije bi rekao: “Ustani, Jahve! Neprijatelji tvoji neka se rasprše! Koji tebe mrze nek' bježe pred tobom!”
36 “Pamene likupumula, ankanena kuti, “Bwererani, Inu Yehova, ku chinamtindi cha Aisraeli.”
A kad bi se zaustavljao, popratio bi: “Vrati se, o Jahve! Izraelu ti si tisuće bezbrojne!”