< Numeri 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
Locutusque est Dominus ad Moysen in deserto Sinai in tabernaculo foederis, prima die mensis secundi, anno altero egressionis eorum ex Aegypto, dicens:
2 “Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
Tollite summam universae congregationis filiorum Israel per cognationes et domos suas, et nomina singulorum, quidquid sexus est masculini
3 Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
a vigesimo anno et supra, omnium virorum fortium ex Israel, et numerabitis eos per turmas suas, tu et Aaron.
4 Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
Eruntque vobiscum principes tribuum ac domorum in cognationibus suis,
5 Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
quorum ista sunt nomina: De Ruben, Elisur filius Sedeur.
6 Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
de Simeon, Salamiel filius Surisaddai.
7 Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
de Iuda, Nahasson, filius Aminadab.
8 Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
de Issachar, Nathanael filius Suar.
9 Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
de Zabulon, Eliab filius Helon.
10 Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
Filiorum autem Ioseph, de Ephraim, Elisama filius Ammiud. de Manasse, Gamaliel filius Phadasseur.
11 Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
De Beniamin, Abidan filius Gedeonis.
12 Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
de Dan, Ahiezer filius Ammisaddai.
13 Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
de Aser, Phegiel filius Ochran.
14 Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
de Gad, Eliasaph filius Duel.
15 Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
de Nephthali, Ahira filius Enan.
16 Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
Hi nobilissimi principes multitudinis per tribus et cognationes suas, et capita exercitus Israel:
17 Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
quos tulerunt Moyses et Aaron cum omni vulgi multitudine:
18 ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
et congregaverunt primo die mensis secundi, recensentes eos per cognationes, et domos, ac familias, et capita, et nomina singulorum a vigesimo anno et supra,
19 monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
sicut praeceperat Dominus Moysi. Numeratique sunt in deserto Sinai.
20 Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
De Ruben primogenito Israelis per generationes et familias ac domos suas, et nomina capitum singulorum, omne quod sexus est masculini a vigesimo anno et supra, procedentium ad bellum,
21 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
quadraginta sex millia quingenti.
22 Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
De filiis Simeon per generationes et familias ac domos cognationum suarum recensiti sunt per nomina et capita singulorum, omne quod sexus est masculini a vigesimo anno et supra, procedentium ad bellum,
23 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
quinquaginta novem millia trecenti.
24 Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
De filiis Gad per generationes et familias ac domos cognationum suarum recensiti sunt per nomina singulorum a viginti annis et supra, omnes qui ad bella procederent,
25 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
quadragintaquinque millia sexcenti quinquaginta.
26 Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
De filiis Iuda per generationes et familias ac domos cognationum suarum, per nomina singulorum a vigesimo anno et supra, omnes qui poterant ad bella procedere,
27 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
recensiti sunt septuaginta quattuor millia sexcenti.
28 Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
De filiis Issachar, per generationes et familias ac domos cognationum suarum, per nomina singulorum a vigesimo anno et supra, omnes qui ad bella procederent,
29 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
recensiti sunt quinquaginta quattuor millia quadringenti.
30 Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
De filiis Zabulon per generationes et familias, ac domos cognationum suarum recensiti sunt per nomina singulorum a vigesimo anno et supra, omnes qui poterant ad bella procedere,
31 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
quinquaginta septem millia quadringenti.
32 Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
De filiis Ioseph, filiorum Ephraim per generationes, et familias, ac domos cognationum suarum recensiti sunt per nomina singulorum a vigesimo anno et supra, omnes qui poterant ad bella procedere,
33 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
quadraginta millia quingenti.
34 Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Porro filiorum Manasse per generationes et familias ac domos cognationum suarum recensiti sunt per nomina singulorum a viginti annis et supra, omnes qui poterant ad bella procedere,
35 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
triginta duo millia ducenti.
36 Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
De filiis Beniamin per generationes et familias ac domos cognationum suarum recensiti sunt nominibus singulorum a vigesimo anno et supra, omnes qui poterant ad bella procedere,
37 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
triginta quinque millia quadringenti.
38 Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
De filiis Dan per generationes, et familias ac domos cognationum suarum recensiti sunt nominibus singulorum a vigesimo anno et supra, omnes qui poterant ad bella procedere,
39 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
sexaginta duo millia septingenti.
40 Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
De filiis Aser per generationes et familias ac domos cognationum suarum recensiti sunt per nomina singulorum a vigesimo anno et supra, omnes qui poterant ad bella procedere,
41 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
quadraginta millia et mille quingenti.
42 Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
De filiis Nephthali per generationes et familias ac domos cognationum suarum recensiti sunt nominibus singulorum a vigesimo anno et supra, omnes qui poterant ad bella procedere,
43 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
quinquaginta tria millia quadringenti.
44 Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
Hi sunt, quos numeraverunt Moyses et Aaron, et duodecim principes Israel, singulos per domos cognationum suarum.
45 Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
Fueruntque omnis numerus filiorum Israel per domos et familias suas a vigesimo anno et supra, qui poterant ad bella procedere,
46 Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
sexcenta tria millia virorum quingenti quinquaginta.
47 Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
Levitae autem in tribu familiarum suarum non sunt numerati cum eis.
48 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
Locutusque est Dominus ad Moysen, dicens:
49 “Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
Tribum Levi noli numerare, neque pones summam eorum cum filiis Israel:
50 Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
sed constitue eos super tabernaculum testimonii et cuncta vasa eius, et quidquid ad ceremonias pertinet. Ipsi portabunt tabernaculum et omnia utensilia eius: et erunt in ministerio, ac per gyrum tabernaculi metabuntur.
51 Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
Cum proficiscendum fuerit, deponent Levitae tabernaculum: cum castrametanda, erigent. quisquis externorum accesserit, occidetur.
52 Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
Metabuntur autem castra filii Israel unusquisque per turmas et cuneos atque exercitum suum.
53 Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
Porro Levitae per gyrum tabernaculi figent tentoria, ne fiat indignatio super multitudinem filiorum Israel, et excubabunt in custodiis tabernaculi testimonii.
54 Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.
Fecerunt ergo filii Israel iuxta omnia quae praeceperat Dominus Moysi.

< Numeri 1 >