< Numeri 1 >
1 Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
Yahvé parla à Moïse dans le désert de Sinaï, dans la tente de la Rencontre, le premier jour du second mois, la deuxième année après leur sortie du pays d'Égypte, et il dit:
2 “Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
« Recense toute l'assemblée des enfants d'Israël, selon leurs familles, selon les maisons de leurs pères, d'après le nombre de leurs noms, tous les mâles, un par un,
3 Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
depuis l'âge de vingt ans et au-dessus, tous ceux qui sont en état de porter les armes en Israël. Toi et Aaron, vous les compterez selon leurs divisions.
4 Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
Il y aura avec vous un homme de chaque tribu, chacun à la tête de la maison de ses pères.
5 Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
Voici les noms des hommes qui se tiendront à vos côtés: De Reuben: Elizur, fils de Shedeur.
6 Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
De Siméon: Shelumiel, fils de Zurishaddai.
7 Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
De Juda: Nahshon, fils d'Amminadab.
8 Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
D'Issachar: Nethanel, fils de Zuar.
9 Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
De Zabulon: Eliab, fils de Helon.
10 Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
Des fils de Joseph: d'Éphraïm: Élischama, fils d'Ammihud; de Manassé: Gamaliel, fils de Pedahzur.
11 Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
De Benjamin: Abidan, fils de Gideoni.
12 Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
De Dan: Ahiezer, fils d'Ammishaddai.
13 Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
d'Asher: Pagiel, fils d'Ochran.
14 Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
De Gad: Eliasaph, fils de Deuel.
15 Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
Pour Nephtali: Ahira, fils d'Enan. »
16 Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
Voici les appelés de l'assemblée, les princes des tribus de leurs pères; ils étaient les chefs des milliers d'Israël.
17 Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
Moïse et Aaron prirent ces hommes qui sont mentionnés par leur nom.
18 ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
Ils convoquèrent toute l'assemblée le premier jour du second mois, et ils déclarèrent leurs ancêtres selon leurs familles, selon les maisons de leurs pères, d'après le nombre des noms, depuis l'âge de vingt ans et au-dessus, un par un.
19 monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
Comme Yahvé l'avait ordonné à Moïse, celui-ci les compta dans le désert de Sinaï.
20 Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Les fils de Ruben, premiers-nés d'Israël, selon leurs générations, selon leurs familles, selon les maisons de leurs pères, d'après le nombre des noms, un par un, tous les mâles depuis l'âge de vingt ans et au-dessus, tous ceux qui étaient en état de porter les armes.
21 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
Ceux de la tribu de Ruben dont on fit le dénombrement furent quarante-six mille cinq cents.
22 Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
On fit le dénombrement des fils de Siméon, selon leurs générations, selon leurs familles, selon les maisons de leurs pères, en comptant les noms, un par un, tous les mâles depuis l'âge de vingt ans et au-dessus, tous ceux qui étaient en état de porter les armes.
23 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
On fit le dénombrement des fils de la tribu de Siméon: cinquante-neuf mille trois cents.
24 Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
On enregistra les fils de Gad, selon leurs générations, selon leurs familles, selon les maisons de leurs pères, en comptant les noms depuis l'âge de vingt ans et au-dessus, tous ceux qui étaient en état de porter les armes.
25 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
On compta quarante-cinq mille six cent cinquante hommes de la tribu de Gad.
26 Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Des fils de Juda, selon leurs générations, selon leurs familles, selon les maisons de leurs pères, en comptant les noms depuis l'âge de vingt ans et au-dessus, tous ceux qui étaient propres à faire la guerre:
27 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
ceux de la tribu de Juda dont on fit le dénombrement furent soixante-quatorze mille six cents.
28 Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
On enregistra les fils d'Issacar, selon leurs familles, selon les maisons de leurs pères, d'après le nombre des noms, depuis l'âge de vingt ans et au-dessus, tous ceux qui étaient en état de porter les armes.
29 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
On fit le dénombrement des fils de la tribu d'Issacar: cinquante-quatre mille quatre cents.
30 Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
On enregistra les fils de Zabulon, selon leurs familles, selon les maisons de leurs pères, d'après le nombre des noms, depuis l'âge de vingt ans et au-dessus, tous ceux qui étaient propres à faire la guerre:
31 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
ceux de la tribu de Zabulon dont on fit le dénombrement furent cinquante-sept mille quatre cents.
32 Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Fils de Joseph: des fils d'Éphraïm, selon leurs générations, selon leurs familles, selon les maisons de leurs pères, en comptant les noms depuis l'âge de vingt ans et au-dessus, tous ceux qui étaient propres à faire la guerre:
33 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
ceux de la tribu d'Éphraïm dont on fit le dénombrement furent quarante mille cinq cents.
34 Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
On enregistra les fils de Manassé, selon leurs familles, selon les maisons de leurs pères, d'après le nombre des noms, depuis l'âge de vingt ans et au-dessus, tous ceux qui étaient propres à faire la guerre:
35 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
ceux de la tribu de Manassé dont on fit le dénombrement furent trente-deux mille deux cents.
36 Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
On enregistra les fils de Benjamin, selon leurs familles, selon les maisons de leurs pères, en comptant les noms depuis l`âge de vingt ans et au-dessus, tous ceux qui étaient propres à faire la guerre:
37 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
ceux de la tribu de Benjamin dont on fit le dénombrement furent trente-cinq mille quatre cents.
38 Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
On enregistra les fils de Dan, selon leurs familles, selon les maisons de leurs pères, d'après le nombre des noms, depuis l'âge de vingt ans et au-dessus, tous ceux qui étaient propres à faire la guerre:
39 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
ceux de la tribu de Dan dont on fit le dénombrement furent soixante-deux mille sept cents.
40 Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
On enregistra les fils d`Aser, selon leurs familles, selon les maisons de leurs pères, en comptant les noms depuis l`âge de vingt ans et au-dessus, tous ceux qui étaient propres à faire la guerre:
41 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
ceux de la tribu d'Aser dont on fit le dénombrement furent quarante et un mille cinq cents.
42 Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
On enregistra les fils de Nephthali, selon leurs familles, selon les maisons de leurs pères, d'après le nombre des noms, depuis l'âge de vingt ans et au-dessus, tous ceux qui étaient propres à faire la guerre:
43 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
ceux de la tribu de Nephthali dont on fit le dénombrement furent cinquante-trois mille quatre cents.
44 Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
Ce sont là ceux dont Moïse et Aaron firent le compte, et les douze hommes qui furent princes d'Israël, chacun pour sa maison de pères.
45 Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
Tous ceux des enfants d'Israël qui furent comptés selon leurs maisons de pères, depuis l'âge de vingt ans et au-dessus, tous ceux qui étaient en état de porter les armes en Israël -
46 Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
tous ceux qui furent comptés furent six cent trois mille cinq cent cinquante.
47 Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
Mais les Lévites, selon la tribu de leurs pères, ne furent pas comptés parmi eux.
48 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
Car Yahvé avait parlé à Moïse, en disant:
49 “Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
« Tu ne compteras pas la tribu de Lévi et tu ne la recenseras pas parmi les enfants d'Israël;
50 Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
mais tu établiras les Lévites sur le tabernacle du témoignage, sur tout son mobilier et sur tout ce qui lui appartient. Ils porteront le tabernacle et tous ses ustensiles; ils en prendront soin et camperont autour de lui.
51 Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
Lorsque le tabernacle devra être déplacé, les Lévites le descendront; et lorsque le tabernacle devra être dressé, les Lévites le dresseront. L'étranger qui s'approchera sera mis à mort.
52 Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
Les enfants d'Israël dresseront leurs tentes, chacun selon son camp, chacun selon sa bannière, selon leurs divisions.
53 Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
Les Lévites camperont autour de la tente du Témoignage, afin qu'il n'y ait pas de colère sur l'assemblée des enfants d'Israël. Les Lévites seront responsables du Tabernacle du Témoignage. »
54 Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.
Les enfants d'Israël firent ainsi. Ils firent tout ce que Yahvé avait ordonné à Moïse.