< Numeri 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
And the LORD spoke to Moses in the wilderness of Sinai, in the tabernacle of the congregation, on the first day of the second month, in the second year after they had come out of the land of Egypt, saying,
2 “Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
Take ye the sum of all the congregation of the children of Israel, after their families, by the house of their fathers, with the number of their names, every male by their polls;
3 Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
From twenty years old and upward, all that are able to go forth to war in Israel: thou and Aaron shall number them by their armies.
4 Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
And with you there shall be a man of every tribe; every one head of the house of his fathers.
5 Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
And these are the names of the men that shall stand with you: of the tribe of Reuben; Elizur the son of Shedeur.
6 Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
Of Simeon; Shelumiel the son of Zurishaddai.
7 Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
Of Judah; Nahshon the son of Amminadab.
8 Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
Of Issachar; Nethaneel the son of Zuar.
9 Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
Of Zebulun; Eliab the son of Helon.
10 Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
Of the children of Joseph: of Ephraim; Elishama the son of Ammihud: of Manasseh; Gamaliel the son of Pedahzur.
11 Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
Of Benjamin; Abidan the son of Gideoni.
12 Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
Of Dan; Ahiezer the son of Ammishaddai.
13 Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
Of Asher; Pagiel the son of Ocran.
14 Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
Of Gad; Eliasaph the son of Deuel.
15 Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
Of Naphtali; Ahira the son of Enan.
16 Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
These were the renowned of the congregation, princes of the tribes of their fathers, heads of thousands in Israel.
17 Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
And Moses and Aaron took these men who are mentioned by their names:
18 ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
And they assembled all the congregation on the first day of the second month, and they declared their genealogies after their families, by the house of their fathers, according to the number of the names, from twenty years old and upward, by their polls.
19 monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
As the LORD commanded Moses, so he numbered them in the wilderness of Sinai.
20 Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
And the children of Reuben, Israel’s eldest son, by their generations, after their families, by the house of their fathers, according to the number of the names, by their polls, every male from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
21 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
Those that were numbered of them, even of the tribe of Reuben, were forty and six thousand and five hundred.
22 Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Simeon, by their generations, after their families, by the house of their fathers, those that were numbered of them, according to the number of the names, by their polls, every male from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
23 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
Those that were numbered of them, even of the tribe of Simeon, were fifty and nine thousand and three hundred.
24 Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Gad, by their generations, after their families, by the house of their fathers, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
25 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
Those that were numbered of them, even of the tribe of Gad, were forty and five thousand six hundred and fifty.
26 Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Judah, by their generations, after their families, by the house of their fathers, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
27 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
Those that were numbered of them, even of the tribe of Judah, were seventy and four thousand and six hundred.
28 Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Issachar, by their generations, after their families, by the house of their fathers, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
29 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
Those that were numbered of them, even of the tribe of Issachar, were fifty and four thousand and four hundred.
30 Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Zebulun, by their generations, after their families, by the house of their fathers, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
31 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
Those that were numbered of them, even of the tribe of Zebulun, were fifty and seven thousand and four hundred.
32 Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Joseph, namely, of the children of Ephraim, by their generations, after their families, by the house of their fathers, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
33 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
Those that were numbered of them, even of the tribe of Ephraim, were forty thousand and five hundred.
34 Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Manasseh, by their generations, after their families, by the house of their fathers, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
35 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
Those that were numbered of them, even of the tribe of Manasseh, were thirty and two thousand and two hundred.
36 Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Benjamin, by their generations, after their families, by the house of their fathers, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
37 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
Those that were numbered of them, even of the tribe of Benjamin, were thirty and five thousand and four hundred.
38 Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Dan, by their generations, after their families, by the house of their fathers, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
39 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
Those that were numbered of them, even of the tribe of Dan, were sixty and two thousand and seven hundred.
40 Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Asher, by their generations, after their families, by the house of their fathers, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
41 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
Those that were numbered of them, even of the tribe of Asher, were forty and one thousand and five hundred.
42 Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Naphtali, throughout their generations, after their families, by the house of their fathers, according to the number of the names, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war;
43 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
Those that were numbered of them, even of the tribe of Naphtali, were fifty and three thousand and four hundred.
44 Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
These are those that were numbered, which Moses and Aaron numbered, and the princes of Israel, being twelve men: each one was for the house of his fathers.
45 Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
So were all those that were numbered of the children of Israel, by the house of their fathers, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war in Israel;
46 Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
Even all they that were numbered were six hundred thousand and three thousand and five hundred and fifty.
47 Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
But the Levites after the tribe of their fathers were not numbered among them.
48 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
For the LORD had spoken to Moses, saying,
49 “Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
Only thou shalt not number the tribe of Levi, neither take the sum of them among the children of Israel:
50 Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
But thou shalt appoint the Levites over the tabernacle of testimony, and over all its vessels, and over all things that belong to it: they shall bear the tabernacle, and all its vessels; and they shall minister to it, and shall encamp around the tabernacle.
51 Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
And when the tabernacle moveth forward, the Levites shall take it down: and when the tabernacle is to be pitched, the Levites shall set it up: and the stranger that cometh near shall be put to death.
52 Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
And the children of Israel shall pitch their tents, every man by his own camp, and every man by his own standard, throughout their hosts.
53 Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
But the Levites shall encamp around the tabernacle of testimony, that there may be no wrath upon the congregation of the children of Israel: and the Levites shall keep the charge of the tabernacle of testimony.
54 Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.
And the children of Israel did according to all that the LORD commanded Moses, so did they.

< Numeri 1 >