< Numeri 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
The Lord spake againe vnto Moses in the wildernesse of Sinai, in the Tabernacle of the Congregation, in the first day of the second moneth, in the second yere after they were come out of the land of Egypt, saying,
2 “Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
Take ye the summe of all the Congregation of the children of Israel, after their families, and housholdes of their fathers with the nomber of their names: to wit, all the males, man by man:
3 Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
From twentie yere olde and aboue, all that go forth to the warre in Israel, thou and Aaron shall number them, throughout their armies.
4 Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
And with you shalbe men of euery tribe, such as are the heads of the house of their fathers.
5 Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
And these are the names of the men that shall stand with you, of the tribe of Reuben, Elizur, the sonne of Shedeur:
6 Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
Of Simeon, Shelumiel the sonne of Zurishaddai:
7 Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
Of Iudah, Nahshon the sonne of Amminadab:
8 Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
Of Issachar, Nethaneel, the sonne of Zuar:
9 Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
Of Zebulun, Eliab, the sonne of Helon:
10 Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
Of the children of Ioseph: of Ephraim, Elishama the sonne of Ammihud: of Manasseh, Gamliel, the sonne of Pedahzur:
11 Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
Of Beiamin, Abida the sonne of Gideoni:
12 Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
Of Dan, Ahiezer, the sonne of Ammishaddai:
13 Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
Of Asher, Pagiel, the sonne of Ocran:
14 Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
Of Gad, Eliasaph, the sonne of Deuel:
15 Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
Of Naphtali, Ahira the sonne of Enan.
16 Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
These were famous in the Congregation, princes of the tribes of their fathers, and heads ouer thousands in Israel.
17 Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
The Moses and Aaron tooke these men which are expressed by their names.
18 ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
And they called all the Congregation together, in the first day of the second moneth, who declared their kindreds by their families, and by the houses of their fathers, according to the nomber of their names, from twentie yere olde and aboue, man by man.
19 monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
As the Lord had commanded Moses, so he nombred them in the wildernesse of Sinai.
20 Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
So were the sonnes of Reuben Israels eldest sonne by their generations, by their families, and by the houses of their fathers, according to the nomber of their names, man by man euery male from twentie yere olde and aboue, as many as went forth to warre:
21 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
The nomber of them, I say, of the tribe of Reuben, was sixe and fourtie thousande, and fiue hundreth.
22 Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sonnes of Simeon by their generatios, by their families, and by the houses of their fathers, the summe therof by the nomber of their names, man by man, euery male from twentie yeere olde and aboue, all that went forth to warre:
23 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
The summe of them, I say, of the tribe of Simeon was nine and fiftie thousande, and three hundreth.
24 Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sonnes of Gad by their generations, by their families, and by the houses of their fathers, according to the nomber of their names, from twentie yere olde and aboue, all that went forth to warre:
25 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
The number of them, I say, of the tribe of Gad was fiue and fourtie thousand, and six hundreth and fiftie.
26 Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sonnes of Iudah by their generations, by their families, and by the houses of their fathers, according to the nomber of their names, from twentie yere olde and aboue, all that went forth to warre:
27 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
The nomber of them, I say, of the tribe of Iudah was three score and fourteene thousande, and sixe hundreth.
28 Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sonnes of Issachar by their generations, by their families, and by the houses of their fathers, according to the nomber of their names, from twentie yeere olde and aboue, all that went forth to warre:
29 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
The nomber of them also of the tribe of Issachar was foure and fiftie thousande and foure hundreth.
30 Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sonnes of Zebulun by their generations, by their families, and by the houses of their fathers, according to the number of their names, from twentie yeere olde and aboue, all that went foorth to warre:
31 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
The nomber of them also of the tribe of Zebulun was seuen and fiftie thousand and foure hundreth.
32 Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sonnes of Ioseph, namely of the sonnes of Ephraim by their generations, by their families, and by the houses of their fathers, according to the nomber of their names, from twentie yeere olde and aboue, all that went foorth to warre:
33 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
The nomber of them also of the tribe of Ephraim was fourtie thousande and fiue hundreth.
34 Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sonnes of Manasseh by their generations, by their families, and by the houses of their fathers, according to the nomber of their names, from twentie yeere olde and aboue, all that went foorth to warre:
35 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
The nober of the also of ye tribe of Manasseh was two and thirtie thousand and two hundreth.
36 Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sonnes of Beniamin by their generations, by their families, and by the houses of their fathers, according to the nomber of their names, from twentie yeere olde and aboue, all that went foorth to warre:
37 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
The nomber of them also of the tribe of Beniamin was fiue and thirtie thousande and foure hundreth.
38 Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sonnes of Dan by their generations, by their families, and by the houses of their fathers, according to the nomber of their names, from twentie yeere olde and aboue, all that went foorth to warre:
39 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
The nomber of the also of ye tribe of Dan was three score and two thousand and seue hudreth.
40 Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sonnes of Asher by their generations, by their families, and by the houses of their fathers, according to the number of their names, from twentie yeere olde and aboue, all that went foorth to warre:
41 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
The nomber of them also of ye tribe of Asher was one and fourtie thousand and fiue hudreth.
42 Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the children of Naphtali, by their generations, by their families, and by the houses of their fathers, according to the nomber of their names, from twentie yeere olde and aboue, all that went to the warre:
43 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
The nomber of them also of the tribe of Naphtali, was three and fiftie thousand, and foure hundreth.
44 Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
These are the summes which Moses, and Aaron nombred, and the Princes of Israel, the twelue men, which were euery one for the house of their fathers.
45 Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
So this was all the summe of the sonnes of Israel, by the houses of their fathers, from twenty yeere olde and aboue, all that went to the warre in Israel,
46 Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
And all they were in nomber sixe hudreth and three thousande, fiue hundreth and fiftie.
47 Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
But the Leuites, after the tribes of their fathers were not nombred among them.
48 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
For the Lord had spoken vnto Moses, and said,
49 “Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
Onely thou shalt not number the tribe of Leui, neither take the summe of them among the children of Israel:
50 Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
But thou shalt appoynt the Leuites ouer the Tabernacle of the Testimonie, and ouer all the instruments thereof, and ouer all things that belong to it: they shall beare the Tabernacle, and all the instruments thereof, and shall minister in it, and shall dwell round about the Tabernacle.
51 Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
And when the Tabernacle goeth forth, the Leuites shall take it downe: and when the Tabernacle is to be pitched, ye Leuites shall set it vp: for the stranger that commeth neere, shalbe slaine.
52 Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
Also the children of Israel shall pitch their tentes, euery man in his campe, and euery man vnder his standerd throughout their armies.
53 Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
But the Leuites shall pitch rounde about the Tabernacle of the Testimonie, least vengeance come vpon the Congregation of the children of Israel, and the Leuites shall take the charge of the Tabernacle of the Testimonie.
54 Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.
So the children of Israel did according to all that ye Lord had comanded Moses: so did they.

< Numeri 1 >