< Numeri 1 >
1 Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
And the Lord spoke to Moses in the desert of Sinai in the tabernacle of the covenant, the first day of the second month, the second year of their going out of Egypt, saying:
2 “Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
Take the sum of all the congregation of the children of Israel by their families, and houses, and the names of every one, as many as are of the male sex,
3 Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
From twenty years old and upwards, of all the men of Israel fit for war, and you shall number them by their troops, thou and Aaron.
4 Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
And there shall be with you the princes of the tribes, and of the houses in their kindreds,
5 Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
Whose names are these: Of Ruben, Elisur the son of Sedeur.
6 Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
Of Simeon, Salamiel the son of Surisaddai.
7 Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
Of Juda, Nahasson the son of Aminadab.
8 Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
Of Issachar, Nathanael the son of Suar.
9 Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
Of Zabulon, Eliab the son of Helon.
10 Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
And of the sons of Joseph: of Ephraim, Elisama the son of Ammiud: of Manasses, Gamaliel the son of Phadassur.
11 Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
Of Benjamin, Abidan the son of Gedeon.
12 Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
Of Dan, Ahiezer the son of Ammisaddai.
13 Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
Of Aser, Phegiel the son of Ochran.
14 Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
Of Gad, Eliasaph the son of Duel.
15 Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
Of Nephtali, Ahira the son of Enan.
16 Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
These are the most noble princes of the multitude by their tribes and kindreds, and the chiefs of the army of Israel:
17 Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
Whom Moses and Aaron took with all the multitude of the common people:
18 ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
And assembled them on the first day of the second month, reckoning them up by the kindreds, and houses, and families, and heads, and names of every one from twenty years old and upward,
19 monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
As the Lord had commanded Moses. And they were numbered in the desert of Sinai.
20 Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of Ruben the eldest son of Israel, by their generations and families and houses and names of every head, all that were of the male sex, from twenty years old and upward, that were able to go forth to war,
21 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
Were forty-six thousand five hundred.
22 Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sons of Simeon by their generations and families, and houses of their kindreds, were reckoned up by the names and heads of every one, all that were of the male sex, from twenty years old and upward, that were able to go forth to war,
23 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
Fifty-nine thousand three hundred.
24 Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sons of Gad, by their generations and families and houses of their kindreds were reckoned up by the names of every one from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war,
25 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
Forty-five thousand six hundred and fifty.
26 Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sons of Juda, by their generations and families and houses of their kindreds, by the names of every one from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war,
27 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
Were reckoned up seventy-four thousand six hundred.
28 Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sons of Issachar, by their generations and families and houses of their kindreds, by the names of every one from twenty years old and upward, all that could go forth to war,
29 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
Were reckoned up fifty-four thousand four hundred.
30 Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sons of Zabulon, by the generations and families and houses of their kindreds, were reckoned up by the names of every one from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war,
31 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
Fifty-seven thousand four hundred.
32 Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sons of Joseph, namely, of the sons of Ephraim, by the generations and families and houses of their kindreds, were reckoned up by the names of every one, from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war,
33 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
Forty thousand five hundred.
34 Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Moreover of the sons of Manasses, by the generations and families and houses of their kindreds, were reckoned up by the names of every one from twenty years old and upward, all that could go forth to war,
35 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
Thirty-two thousand two hundred.
36 Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sons of Benjamin, by their generations and families and houses of their kindreds, were reckoned up by the names of every one from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war,
37 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
Thirty-five thousand four hundred.
38 Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sons of Dan, by their generations and families and houses of their kindreds, were reckoned up by the names of every one from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war,
39 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
Sixty-two thousand seven hundred.
40 Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sons of Aser, by their generations and families and houses of their kindreds, were reckoned up by the names of every one from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war,
41 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
Forty-one thousand and five hundred.
42 Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
Of the sons of Nephtali, by their generations and families and houses of their kindreds, were reckoned up by the names of every one from twenty years old and upward, all that were able to go forth to war,
43 Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
Fifty-three thousand four hundred.
44 Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
These era they who were numbered by Moses and Aaron, and the twelve princes of Israel, every one by the houses of their kindreds.
45 Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
And the whole number of the children of Israel by their houses and families, from twenty years old and upward, that were able to go to war,
46 Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
Were six hundred and three thousand five hundred and fifty men.
47 Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
But the Levites in the tribes of their families were not numbered with them.
48 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke to Moses, saying:
49 “Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
Number not the tribe of Levi, neither shalt thou put down the sum of them with the children of Israel:
50 Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
But appoint them over the tabernacle of the testimony, and all the vessels thereof, and whatsoever pertaineth to the ceremonies. They shall carry the tabernacle and all the furniture thereof: and they shall minister, and shall encamp round about the tabernacle.
51 Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
When you are to go forward, the Levites shall take down the tabernacle: when you are to camp, they shall set it up. What stranger soever cometh to it, shall be slain.
52 Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
And the children of Israel shall camp every man by his troops and bands and army.
53 Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
But the Levites shall pitch their tents round about the tabernacle, lest there come indignation upon the multitude of the children of Israel, and they shall keep watch, and guard the tabernacle of the testimony.
54 Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.
And the children of Israel did according to all things which the Lord had commanded Moses.