< Nehemiya 1 >

1 Awa ndi mawu a Nehemiya mwana wa Hakaliya: Pa mwezi wa Kisilevi, chaka cha makumi awiri, pamene ndinali mu mzinda wa Susa,
Paroles de Néhémie, fils de Hakhalia: "Au mois de Kislev, dans la vingtième année, alors que je me trouvais à Suse, la capitale,
2 Hanani mmodzi mwa abale anga, anabwera ndi anthu ena kuchokera ku Yuda, ndipo ine ndinawafunsa za Ayuda otsala amene sanatengedwe ukapolo, ndiponso za mzinda wa Yerusalemu.
il advint que Hanâni, un de mes frères, avec quelques autres hommes, arriva de Judée. Je les interrogeai sur les Judéens, ce groupe de libérés qui avaient été soustraits à la captivité, et sur Jérusalem.
3 Anandiyankha kuti, “Amene sanatengedwe ukapolo aja ali pa mavuto aakulu ndipo ali ndi manyazi. Khoma la Yerusalemu ndilogamukagamuka ndipo zipata zake zinatenthedwa ndi moto.”
Ils me répondirent "Ceux qui, échappés à la captivité, se sont fixés là-bas, dans la province, sont dans une situation très mauvaise et humiliante; les murs de Jérusalem gisent écroulés et ses portes sont consumées par le feu."
4 Nditamva zimenezi, ndinakhala pansi ndi kuyamba kulira. Ndinalira kwa masiku angapo. Ndinkasala zakudya ndi kumapemphera pamaso pa Mulungu Wakumwamba.
Quand j’entendis ces paroles, je m’affaissai en pleurant, et je fus dans la désolation pendant des jours. Je jeûnai et me répandis en prières devant le Dieu du ciel:
5 Ndinkati: “Inu Yehova, Mulungu wakumwamba, Mulungu wamkulu ndi woopsa. Mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu.
"De grâce, ô Eternel, dis-je, Dieu du ciel, Dieu grand et redoutable, qui gardes fidèlement le pacte de bienveillance à ceux qui t’aiment et obéissent à tes lois,
6 Tcherani khutu lanu ndi kutsekula maso anu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune limene ndikupemphera usana ndi usiku pamaso panu kupempherera Aisraeli, atumiki anu. Ndikuvomereza machimo a Aisraeli amene tinakuchimwirani. Ndithu, ine ndi banja la makolo anga tinakuchimwirani.
que ton oreille soit attentive et tes yeux ouverts pour entendre la prière de ton serviteur, qu’à présent j’élève vers toi jour et nuit en faveur de tes serviteurs, les enfants d’Israël, en confessant les péchés des enfants d’Israël que nous avons commis à ton égard; oui, moi aussi et la maison de mon père, nous avons péché.
7 Ife tinakuchitirani zoyipa zambiri. Sitinamvere mawu anu, malamulo ndi malangizo anu amene munapereka kwa mtumiki wanu Mose.
Nous t’avons gravement offensé, et nous n’avons pas observé les lois, les préceptes et les statuts que tu as prescrits à ton serviteur Moïse.
8 “Kumbukirani mawu amene munawuza mtumiki wanu Mose akuti, ‘Ngati mukhala osakhulupirika, ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina.
Souviens-toi donc de la déclaration dont tu as chargé Moïse, ton serviteur, à savoir: Si vous, vous devenez infidèles, moi, je vous disperserai parmi les nations.
9 Koma mukabwerera kwa Ine, mukamvera malamulo anga ndi kuwatsatadi, ndiye kuti ngakhale anthu anu atabalalika kutali chotani, Ine ndidzawasonkhanitsa kuchokera kumeneko ndi kubwera nawo ku malo amene ndinasankha kuti azidzayitanira dzina langa.’
Que si alors vous revenez à moi, si vous observez mes lois et les exécutez, dussent vos proscrits être relégués aux confins des cieux, de là je les rassemblerai pour les ramener à l’endroit que j’ai choisi pour en faire la résidence de mon nom."
10 “Iwo ndi atumiki anu ndi anthu anu, amene munawawombola ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu.
Or, ils sont tes serviteurs et ton peuple, que tu as délivrés par ta grande force et ta main puissante.
11 Inu Ambuye tcherani khutu lanu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune ndiponso pemphero la atumiki anu amene amakondwera kuchitira ulemu dzina lanu. Lolani kuti mtumiki wanune zinthu zindiyendere bwino lero ndi kuti mfumu indichitire chifundo.” Nthawi imeneyi nʼkuti ndili woperekera zakumwa kwa mfumu.
Ah! Seigneur, que ton oreille soit donc attentive à la prière de ton serviteur ainsi qu’à la prière de tes serviteurs, qui aspirent à révérer ton nom. De grâce, fais réussir ton serviteur en ce jour et concilie-lui la bienveillance de cet homme!" Je servais alors d’échanson au roi.

< Nehemiya 1 >