< Nehemiya 1 >
1 Awa ndi mawu a Nehemiya mwana wa Hakaliya: Pa mwezi wa Kisilevi, chaka cha makumi awiri, pamene ndinali mu mzinda wa Susa,
The words of Nehemias the son of Helchias. And it came to pass in the month of Casleu, in the twentieth year, as I was in the castle of Susa,
2 Hanani mmodzi mwa abale anga, anabwera ndi anthu ena kuchokera ku Yuda, ndipo ine ndinawafunsa za Ayuda otsala amene sanatengedwe ukapolo, ndiponso za mzinda wa Yerusalemu.
That Hanani one of my brethren came, he and some men of Juda; and I asked them concerning the Jews, that remained and were left of the captivity, and concerning Jerusalem.
3 Anandiyankha kuti, “Amene sanatengedwe ukapolo aja ali pa mavuto aakulu ndipo ali ndi manyazi. Khoma la Yerusalemu ndilogamukagamuka ndipo zipata zake zinatenthedwa ndi moto.”
And they said to me: They that have remained, and are left of the captivity there in the province, are in great affliction, and reproach: and the wall of Jerusalem is broken down, and the gates thereof are burnt with fire.
4 Nditamva zimenezi, ndinakhala pansi ndi kuyamba kulira. Ndinalira kwa masiku angapo. Ndinkasala zakudya ndi kumapemphera pamaso pa Mulungu Wakumwamba.
And when I had heard these words, I sat down, and wept, and mourned for many days: and I fasted, and prayed before the face of the God of heaven.
5 Ndinkati: “Inu Yehova, Mulungu wakumwamba, Mulungu wamkulu ndi woopsa. Mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu.
And I said: I beseech thee, O Lord God of heaven, strong, great, and terrible, who keepest covenant and mercy with those that love thee, and keep thy commandments:
6 Tcherani khutu lanu ndi kutsekula maso anu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune limene ndikupemphera usana ndi usiku pamaso panu kupempherera Aisraeli, atumiki anu. Ndikuvomereza machimo a Aisraeli amene tinakuchimwirani. Ndithu, ine ndi banja la makolo anga tinakuchimwirani.
Let thy ears be attentive, and thy eyes open, to hear the prayer of thy servant, which I pray before thee now, night and day, for the children of Israel thy servants: and I confess the sins of the children of Israel, by which they have sinned against thee: I and my father’s house have sinned.
7 Ife tinakuchitirani zoyipa zambiri. Sitinamvere mawu anu, malamulo ndi malangizo anu amene munapereka kwa mtumiki wanu Mose.
We have been seduced by vanity, and have not kept thy commandments, and ceremonies and judgments, which thou hast commanded thy servant Moses.
8 “Kumbukirani mawu amene munawuza mtumiki wanu Mose akuti, ‘Ngati mukhala osakhulupirika, ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina.
Remember the word that thou commandedst to Moses thy servant, saying: If you shall transgress, I will scatter you abroad among the nations:
9 Koma mukabwerera kwa Ine, mukamvera malamulo anga ndi kuwatsatadi, ndiye kuti ngakhale anthu anu atabalalika kutali chotani, Ine ndidzawasonkhanitsa kuchokera kumeneko ndi kubwera nawo ku malo amene ndinasankha kuti azidzayitanira dzina langa.’
But if you return to me, and keep my commandments, and do them, though you should be led away to the uttermost parts of the world, I will gather you from thence, and bring you back to the place which I have chosen for my name to dwell there.
10 “Iwo ndi atumiki anu ndi anthu anu, amene munawawombola ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu.
And these are thy servants, and thy people: whom thou hast redeemed by thy great strength, and by thy mighty hand.
11 Inu Ambuye tcherani khutu lanu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune ndiponso pemphero la atumiki anu amene amakondwera kuchitira ulemu dzina lanu. Lolani kuti mtumiki wanune zinthu zindiyendere bwino lero ndi kuti mfumu indichitire chifundo.” Nthawi imeneyi nʼkuti ndili woperekera zakumwa kwa mfumu.
I beseech thee, O Lord, let thy ear be attentive to the prayer of thy servant, and to the prayer of thy servants who desire to fear thy name: and direct thy servant this day, and give him mercy before this man. For I was the king’s cupbearer.