< Nehemiya 1 >

1 Awa ndi mawu a Nehemiya mwana wa Hakaliya: Pa mwezi wa Kisilevi, chaka cha makumi awiri, pamene ndinali mu mzinda wa Susa,
Nehemias, Hakalias Søns, Handeler. Og det skete udi Kislev Maaned, i det tyvende Aar, da jeg var i Susan paa Slottet,
2 Hanani mmodzi mwa abale anga, anabwera ndi anthu ena kuchokera ku Yuda, ndipo ine ndinawafunsa za Ayuda otsala amene sanatengedwe ukapolo, ndiponso za mzinda wa Yerusalemu.
da kom Hanani, en af mine Brødre, han og nogle Mænd fra Juda; og jeg spurgte dem om Jøderne, som vare undkomne, som vare overblevne af Fangenskabet, og om Jerusalem.
3 Anandiyankha kuti, “Amene sanatengedwe ukapolo aja ali pa mavuto aakulu ndipo ali ndi manyazi. Khoma la Yerusalemu ndilogamukagamuka ndipo zipata zake zinatenthedwa ndi moto.”
Og de sagde mig: De overblevne, som ere overblevne af Fangenskabet, ere der i Landskabet udi stor Ulykke og i Forsmædelse, og Jerusalems Mur er nedreven, og dens Porte ere opbrændte med Ild.
4 Nditamva zimenezi, ndinakhala pansi ndi kuyamba kulira. Ndinalira kwa masiku angapo. Ndinkasala zakudya ndi kumapemphera pamaso pa Mulungu Wakumwamba.
Og det skete, der jeg hørte disse Ord, satte jeg mig hen og græd og sørgede nogle Dage, og jeg fastede og bad for Guds Ansigt i Himmelen.
5 Ndinkati: “Inu Yehova, Mulungu wakumwamba, Mulungu wamkulu ndi woopsa. Mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu.
Og jeg sagde: Ak Herre, Himmelens Gud! den store og forfærdelige Gud, som holder Pagten og Miskundheden med dem, som ham elske og holde hans Bud!
6 Tcherani khutu lanu ndi kutsekula maso anu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune limene ndikupemphera usana ndi usiku pamaso panu kupempherera Aisraeli, atumiki anu. Ndikuvomereza machimo a Aisraeli amene tinakuchimwirani. Ndithu, ine ndi banja la makolo anga tinakuchimwirani.
Kære, lad dit Øre mærke derpaa, og dine Øjne være aabnede til at høre paa din Tjeners Bøn, som jeg beder for dit Ansigt i Dag, Dag og Nat for Israels Børn, dine Tjenere; og jeg bekender Israels Børns Synder, som vi have syndet imod dig, baade jeg og min Faders Hus have syndet.
7 Ife tinakuchitirani zoyipa zambiri. Sitinamvere mawu anu, malamulo ndi malangizo anu amene munapereka kwa mtumiki wanu Mose.
Vi have handlet saare slet imoi dig og ikke holdt de Bud og de Skikke og de Love, som du har budet Mose, din Tjener.
8 “Kumbukirani mawu amene munawuza mtumiki wanu Mose akuti, ‘Ngati mukhala osakhulupirika, ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina.
Kære, kom det Ord i Hu, som du bød Mose, din Tjener, sigende: Naar I forsynde eder, da skal jeg adsprede eder iblandt Folkene;
9 Koma mukabwerera kwa Ine, mukamvera malamulo anga ndi kuwatsatadi, ndiye kuti ngakhale anthu anu atabalalika kutali chotani, Ine ndidzawasonkhanitsa kuchokera kumeneko ndi kubwera nawo ku malo amene ndinasankha kuti azidzayitanira dzina langa.’
men naar I vende om til mig og holde mine Bud og gøre efter dem, om da end nogen af eder er bortdreven indtil Himmelens Ende, saa vil jeg dog samle dem derfra og føre dem til det Sted, som jeg har udvalgt, til at lade mit Navn bo der.
10 “Iwo ndi atumiki anu ndi anthu anu, amene munawawombola ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu.
De ere dog dine Tjenere og dit Folk, som du har forløst ved din store Kraft, og ved din stærke Haand.
11 Inu Ambuye tcherani khutu lanu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune ndiponso pemphero la atumiki anu amene amakondwera kuchitira ulemu dzina lanu. Lolani kuti mtumiki wanune zinthu zindiyendere bwino lero ndi kuti mfumu indichitire chifundo.” Nthawi imeneyi nʼkuti ndili woperekera zakumwa kwa mfumu.
Ak, Herre! Kære, lad dit Øre mærke paa din Tjeners Bøn og paa dine Tjeneres Bøn, deres, som have Velbehag i at frygte dit Navn, og lad det dog lykkes for din Tjener i Dag, og giv ham Barmhjertighed for denne Mands Ansigt. Men jeg var da Kongens Mundskænk.

< Nehemiya 1 >